Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Levitiko 27:30
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 30 “‘Chakhumi* chilichonse+ cha zinthu za m’dzikolo, kaya ndi zokolola m’munda kapena zipatso za m’mitengo, ndi cha Yehova. Chakhumi chimenechi ndi chopatulika kwa Yehova.

  • 2 Mbiri 31:5
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 5 Ana a Isiraeli+ atangomva mawuwo, anawonjezera zipatso zoyambirira zimene ankapereka za mbewu,+ vinyo watsopano,+ mafuta,+ uchi,+ ndi zokolola zonse zakumunda+ ndipo anabweretsa chakhumi cha zonsezi chochuluka zedi.+

  • Nehemiya 10:37
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 37 Komanso tinafunika kupititsa ufa woyambirira wamisere,+ zopereka zathu,+ zipatso za mtengo uliwonse,+ vinyo watsopano+ ndi mafuta+ kwa ansembe kumalo odyera+ m’nyumba ya Mulungu wathu. Tinafunikanso kupititsa chakhumi kwa Alevi+ pa zinthu zochokera m’nthaka yathu, pakuti Aleviwo anali kulandira chakhumi kuchokera m’mizinda yathu yonse ya zaulimi.

  • Nehemiya 12:44
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 44 Kuwonjezera apo, pa tsiku limenelo anaika amuna kuti aziyang’anira zipinda+ zosungiramo zinthu zosiyanasiyana,+ zopereka,+ mbewu zoyambirira+ ndi chakhumi.+ Anawapatsa udindo wosonkhanitsira m’zipindamo gawo loyenera kuperekedwa kwa ansembe ndi Alevi+ malinga ndi chilamulo,+ kuchokera m’minda yonse ya m’mizinda yawo. Yuda anali kusangalala chifukwa ansembe ndi Alevi+ anali kuchita utumiki wawo.

  • Nehemiya 13:12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Anthu onse a mu Yuda anabweretsa kumalo osungira zinthu+ chakhumi+ cha mbewu,+ cha vinyo watsopano+ ndiponso cha mafuta.+

  • Agalatiya 6:6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 6 Komanso, aliyense amene akuphunzitsidwa mawuwo+ agawane+ zinthu zonse zabwino ndi amene akumuphunzitsayo.+

  • Aheberi 7:5
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 5 Zoonadi, amuna ochokera mwa ana aamuna a Levi,+ amene amalandira udindo wa unsembe, amalamulidwa kulandira zakhumi+ kuchokera kwa anthu+ malinga ndi Chilamulo. Izi zikutanthauza kuti, amalandira zakhumizo kuchokera kwa abale awo, ngakhale kuti abale awowo anachokera m’chiuno mwa Abulahamu.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena