Yoswa
19 Maere+ achiwiri anagwera Simiyoni, kapena kuti fuko la ana a Simiyoni,+ potsata mabanja awo. Cholowa chawo chinali pakati pa cholowa cha ana a Yuda.+ 2 M’gawo la cholowa chawo munali Beere-seba+ kuphatikizapo Sheba, Molada,+ 3 Hazara-suali,+ Bala, Ezemu,+ 4 Elitoladi,+ Betuli, Horima, 5 Zikilaga,+ Beti-marikaboti, Hazara-susa,+ 6 Beti-lebaoti,+ ndi Saruheni. Mizinda 13 ndi midzi yake. 7 Munalinso Aini,+ Rimoni,+ Eteri, ndi Asani.+ Mizinda inayi ndi midzi yake, 8 ndiponso midzi yonse yozungulira mizinda imeneyi mpaka kukafika ku Baalati-beere,+ komwe ndi ku Rama+ wa kum’mwera. Ichi chinali cholowa cha fuko la ana a Simiyoni potsata mabanja awo. 9 Cholowa cha ana a Simiyoni chinali m’gawo la ana a Yuda chifukwa ana a Yuda gawo lawo linawakulira.+ Choncho ana a Simiyoni anapatsidwa malo pakati pa cholowa chawo.+
10 Maere achitatu+ anagwera ana a Zebuloni+ potsata mabanja awo. Malire a cholowa chawo anayambira ku Saridi 11 n’kulowera chakumadzulo, kukafika ku Marala. Anapitirira kukafika ku Dabeseti mpaka kuchigwa chimene chili kutsogolo kwa Yokineamu.+ 12 Kenako malirewo anakhota n’kubwerera kulowera kum’mawa kwa Saridi mpaka kumalire a Kisilotu-tabori. Ndiyeno anapitirira kukafika ku Daberati+ mpaka ku Yafiya. 13 Kuchokera kumeneko, malirewo analowera chakum’mawa n’kukafika ku Gati-heferi,+ ku Eti-kazini, ndi ku Rimoni, mpaka ku Nea. 14 Malirewo anazungulira kumpoto kwa Nea kukafika ku Hanatoni, n’kukathera kuchigwa cha Ifita-eli, 15 komanso ku Katati, Nahalala, Simironi,+ Idala, ndi ku Betelehemu.+ Mizindayi inalipo 12 ndi midzi yake. 16 Ichi chinali cholowa+ cha ana a Zebuloni potsata mabanja awo,+ ndipo imeneyi inali mizinda yawo ndi midzi yake.
17 Maere achinayi anagwera Isakara,+ kapena kuti ana a Isakara potsata mabanja awo. 18 Malire a gawo lawo anakafika ku Yezereeli,+ Kesulotu, Sunemu,+ 19 Hafaraimu, Sioni, Anaharati, 20 Rabiti, Kisioni, Ebezi, 21 Remeti, Eni-ganimu,+ Eni-hada, ndi Beti-pazezi. 22 Malirewo anakafika ku Tabori,+ ku Sahazuma, ndi ku Beti-semesi n’kukathera ku Yorodano. Mizinda 16 ndi midzi yake. 23 Ichi chinali cholowa cha fuko la ana a Isakara potsata mabanja awo,+ ndipo imeneyi inali mizinda yawo ndi midzi yake.
24 Maere achisanu+ anagwera fuko la ana a Aseri,+ potsata mabanja awo. 25 Malire a gawo lawo anadutsa ku Helikati,+ Hali, Beteni, Akasafu,+ 26 Alameleki, Amadi, ndi Misali.+ Analowera chakumadzulo ku Karimeli+ ndi ku Sihori-libanati. 27 Kenako anakhota n’kubwerera kulowera kotulukira dzuwa ku Beti-dagoni, n’kukafika ku Zebuloni+ ndi kumpoto kwa chigwa cha Ifita-eli. Anakafikanso ku Beti-emeki ndi ku Nehieli n’kupitirira mpaka ku Kabulu chakumanzere. 28 Anapitirira mpaka ku Eburoni, Rehobu, Hamoni, Kana, mpaka kumzinda wa anthu ambiri wa Sidoni.+ 29 Malirewo anakhota n’kubwerera ku Rama, mpaka kukafika kumzinda wa Turo+ wokhala ndi mpanda wolimba kwambiri. Kenako anakhotanso n’kubwerera ku Hosa n’kukathera kunyanja, m’chigawo cha Akizibu.+ 30 Anakafikanso ku Uma, Afeki,+ ndi Rehobu.+ Mizindayi inalipo 22 ndi midzi yake. 31 Ichi chinali cholowa cha fuko la ana a Aseri potsata mabanja awo,+ ndipo imeneyi inali mizinda yawo ndi midzi yake.
32 Maere a 6+ anagwera ana a Nafitali+ potsata mabanja awo. 33 Malire a gawo lawo anayambira ku Helefi, ndi kumtengo waukulu wa ku Zaananimu,+ mpaka ku Adami-nekebi, ndi ku Yabineeli, n’kukafika ku Lakumu n’kukathera ku Yorodano. 34 Malirewo anakhotera kumadzulo n’kubwerera ku Azinotu-tabori, n’kupitirira mpaka kukafika ku Hukoku ndi ku Zebuloni+ kum’mwera. Anakafikanso ku Aseri+ kumadzulo, ndi kotulukira dzuwa ku Yuda,+ kumtsinje wa Yorodano. 35 Mizinda yake yokhala ndi mipanda yolimba kwambiri inali Zidimu, Zere, Hamati,+ Rakati, Kinereti,+ 36 Adama, Rama, Hazori,+ 37 Kedesi,+ Edirei, Eni-hazori, 38 Yironi, Migidala-eli, Horemu, Beti-anati, ndi Beti-semesi.+ Mizinda 19 ndi midzi yake. 39 Ichi chinali cholowa+ cha fuko la ana a Nafitali potsata mabanja awo,+ ndipo imeneyi inali mizinda yawo ndi midzi yake.
40 Maere a 7+ anagwera fuko la ana a Dani+ potsata mabanja awo. 41 Malire a gawo la cholowa chawo anadutsa ku Zora,+ Esitaoli, Iri-semesi, 42 Saalabini,+ Aijaloni,+ Itila, 43 Eloni, Timuna,+ Ekironi,+ 44 Eliteke, Gebetoni,+ Baalati,+ 45 Yehuda, Bene-beraki, Gati-rimoni,+ 46 Me-jarikoni, Rakoni, n’kukafika kumalire amene ali kutsogolo kwa Yopa.+ 47 Gawo la ana a Dani linawachepera,+ choncho anapita kukachita nkhondo ku Lesemu.+ Analanda mzindawo n’kupha anthu ake ndi lupanga. Kenako anautenga n’kuyamba kukhalamo ndipo anautcha Lesemu Dani, potengera dzina la kholo lawo Dani.+ 48 Ichi chinali cholowa cha fuko la ana a Dani potsata mabanja awo, ndipo imeneyi inali mizinda yawo ndi midzi yake.
49 Apa m’pamene anamalizira kugawa dzikolo m’zigawozigawo kuti akhalemo. Kenako ana a Isiraeli anam’patsa cholowa Yoswa mwana wa Nuni pakati pawo. 50 Molamulidwa ndi Yehova, anam’patsa mzinda umene anapempha+ wa Timinati-sera,+ m’dera lamapiri la Efuraimu ndipo iye anayamba kumanga mzindawo n’kumakhalamo.
51 Zimenezi ndiye zigawo za cholowa chimene wansembe Eleazara, Yoswa mwana wa Nuni, ndi atsogoleri a mafuko a ana a Isiraeli, anagawira anthu.+ Anagawa dzikolo pochita maere ku Silo+ pamaso pa Yehova, pakhomo la chihema chokumanako,+ ndipo anamaliza kuligawa dzikolo.