-
Salimo 15:1-5Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
15 Inu Yehova, ndi ndani amene angakhale mlendo mutenti yanu?
Ndi ndani amene angakhale mʼphiri lanu lopatulika?+
2 Ndi amene akuyenda mosalakwitsa zinthu,*+
Amene amachita zinthu zabwino+
Komanso kulankhula zoona mumtima mwake.+
Sasintha zimene walonjeza* ngakhale zinthu zitakhala kuti sizili bwino kwa iye.+
-
-
Salimo 84:1-4Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
Mtima wanga ndi thupi langa zikufuula mosangalala kwa Mulungu wamoyo.
3 Ngakhale mbalame zapeza malo okhala kumeneko
Ndipo namzeze wadzimangira chisa chake,
Mmene amasamaliramo ana ake
Pafupi ndi guwa lanu lansembe lalikulu, inu Yehova wa magulu ankhondo akumwamba,
Mfumu yanga ndi Mulungu wanga!
4 Osangalala ndi anthu amene akukhala mʼnyumba yanu!+
Iwo akupitiriza kukutamandani.+ (Selah)
-