1 Timoteyo
2 Choncho, poyamba ndikuchonderera nonse kuti muzipereka mapembedzero kwa Mulungu, muzipereka mapemphero,+ muzipemphererana, ndipo muzipereka mapemphero oyamika Mulungu m’malo mwa anthu onse, kaya akhale a mtundu wotani.+ 2 Muchite zimenezi m’malo mwa mafumu+ ndi m’malo mwa anthu onse apamwamba,+ kuti tikhale ndi moyo wabata ndi wamtendere, ndiponso kuti tikhale odzipereka kwa Mulungu mokwanira komanso tikhale oganiza bwino.+ 3 Zimenezi ndi zabwino ndiponso ndi zovomerezeka+ kwa Mpulumutsi wathu Mulungu,+ 4 amene chifuniro chake n’chakuti anthu, kaya akhale a mtundu wotani,+ apulumuke+ ndi kukhala odziwa choonadi+ molondola.+ 5 Pakuti pali Mulungu mmodzi+ ndi mkhalapakati mmodzi+ pakati pa Mulungu+ ndi anthu.+ Ameneyo ndiye munthuyo Khristu Yesu.+ 6 Iye anadzipereka kuti akhale dipo* lokwanira ndendende m’malo mwa onse.+ Zimenezi ndi zimene adzazichitire umboni pa nthawi zake. 7 Chifukwa cha umboni umenewu,+ ine ndinasankhidwa kuti ndikhale mlaliki ndi mtumwi.+ Ndikunenatu zoona,+ sindikunama ayi. Ndinasankhidwa kuti ndikhale mphunzitsi wophunzitsa anthu a mitundu ina+ za chikhulupiriro+ ndi choonadi.
8 Choncho, ndikufuna kuti kulikonse amuna apitirize kupemphera, kukweza m’mwamba manja awo oyera+ popanda kukwiyirana+ ndi kutsutsana.+ 9 Mofanana ndi zimenezi, ndikufunanso kuti akazi azidzikongoletsa ndi zovala zoyenera, povala mwaulemu+ ndi mwanzeru, osati kudzikongoletsa ndi masitayilo omangira tsitsi, golide, ngale, kapena zovala zamtengo wapatali.+ 10 Koma azidzikongoletsa mogwirizana ndi mmene akazi amene amati amalemekeza Mulungu amayenera kudzikongoletsera.+ Azidzikongoletsa ndi ntchito zabwino.+
11 Pophunzira, mkazi azikhala chete ndipo azikhala wogonjera ndi mtima wonse.+ 12 Sindikuvomereza kuti mkazi aziphunzitsa+ kapena kukhala ndi ulamuliro pa mwamuna,+ koma azikhala chete. 13 Pakuti Adamu ndiye anayamba kupangidwa, kenako Hava.+ 14 Komanso, Adamu sananyengedwe,+ koma mkaziyo ndiye amene ananyengedwa+ ndipo anachimwa.+ 15 Komabe, mkazi adzatetezeka mwa kubereka ana,+ malinga ngati akupitiriza kukhala ndi chikhulupiriro, chikondi, ndi kukhala woyera ndiponso woganiza bwino.+