Aroma
2 Choncho munthu iwe,+ kaya ukhale ndani, ulibe chifukwa chomveka chodzilungamitsira ngati umaweruza ena.+ Pakuti pa nkhani imene ukuweruza nayo wina, ukudzitsutsa wekha, chifukwa iwenso woweruzawe+ umachita zomwezo.+ 2 Tikudziwa kuti Mulungu amaweruza anthu amene amachita zimenezi kuti ndi oyenera kulandira chilango ndipo chiweruzo chake ndi chogwirizana ndi choonadi.+
3 Koma tsopano, iwe+ amene umaweruza anthu amene amachita zinthu zimene iwenso umachita, kodi ukuganiza kuti udzazemba chiweruzo cha Mulungu?+ 4 Kapena kodi ukunyoza kukoma mtima kwake kwakukulu,+ kusakwiya msanga+ kwake ndi kuleza mtima kwake,+ chifukwa chakuti sudziwa kuti cholinga cha kukoma mtima kwa Mulungu ndicho kukuthandiza kuti ulape?+ 5 Koma chifukwa chakuti ndiwe wosafuna kusintha khalidwe+ ndiponso wa mtima wosalapa,+ ukudzisungira mkwiyo wa Mulungu.+ Mulungu adzasonyeza mkwiyo+ umenewu pa tsiku loulula+ chiweruzo chake cholungama.+ 6 Iye adzaweruza aliyense malinga ndi ntchito zake motere:+ 7 Moyo wosatha kwa anthu amene popirira m’ntchito yabwino akuyesetsa kupeza ulemerero, ulemu ndi moyo wosakhoza kuwonongeka.+ 8 Koma adzapereka chilango ndi mkwiyo+ kwa okonda mikangano+ amenenso samvera choonadi+ koma amamvera zosalungama. 9 Aliyense wochita zoipa, kuyambira Myuda+ mpaka Mgiriki,+ adzaona nsautso ndi zowawa. 10 Koma aliyense wochita zabwino,+ choyamba Myuda+ kenako Mgiriki,+ adzalandira ulemerero, ulemu ndi mtendere. 11 Pakuti Mulungu alibe tsankho.+
12 Mwachitsanzo, onse amene anachimwa popanda chilamulo adzawonongekanso popanda chilamulo.+ Koma onse amene anachimwa ali ndi chilamulo+ adzaweruzidwa ndi chilamulo.+ 13 Pajatu akumva chabe chilamulo si amene amakhala olungama pamaso pa Mulungu, koma otsatira+ chilamulo ndiwo adzayesedwa olungama.+ 14 Nthawi zonse anthu a mitundu+ amene alibe chilamulo+ akamachita mwachibadwa zinthu za m’chilamulo,+ amakhala chilamulo kwa iwo eni ngakhale kuti alibe chilamulo. 15 Amenewa ndiwo amasonyeza kuti mfundo za m’chilamulo zinalembedwa m’mitima mwawo,+ pamene chikumbumtima chawo+ chimachitira umboni pamodzi ndi iwowo, ndipo maganizo awo amawatsutsa+ ngakhalenso kuwavomereza. 16 Zimenezi zidzaonekera pa tsiku limene Mulungu, kudzera mwa Khristu Yesu, adzaweruze+ zinthu zobisika+ za anthu,+ mogwirizana ndi uthenga wabwino umene ndikulengeza.+
17 Tsopano ngati ndiwe Myuda dzina lokha+ ndipo umadalira chilamulo+ ndi kunyadira Mulungu,+ 18 umadziwa chifuniro chake,+ umakondwera ndi zinthu zapamwamba kwambiri chifukwa chakuti unaphunzitsidwa Chilamulo ndi mawu a pakamwa,+ 19 komanso uli wotsimikiza kuti ndiwe wotsogolera akhungu,+ muuni wa anthu amene ali mu mdima,+ 20 wowongolera anthu opanda nzeru,+ wophunzitsa tiana,+ womvetsa+ zinthu zofunika kuzidziwa ndi choonadi+ zopezeka m’Chilamulo . . . 21 kodi iwe wophunzitsa enawe, sudziphunzitsa wekha?+ Iwe amene umalalikira kuti “Usabe,”+ umabanso kodi?+ 22 Iwe amene umanena kuti “Usachite chigololo,”+ kodi umachitanso chigololo? Iweyo amene umalankhula zosonyeza kuti umanyansidwa ndi mafano, umabanso+ za mu akachisi kodi? 23 Iwe wonyadira chilamulo, kodi umachitiranso Mulungu chipongwe mwa kuphwanya Chilamulo?+ 24 Pakuti “dzina la Mulungu likunyozedwa pakati pa anthu amitundu chifukwa cha inu”+ monga mmene Malemba amanenera.
25 Pajatu mdulidwe+ ndi waphindu pokhapokha ngati iweyo umatsatiradi chilamulo.+ Koma ngati umaphwanya chilamulo, ndiye kuti mdulidwe+ wako ndi wopanda tanthauzo.+ 26 Chotero ngati munthu wosadulidwa+ akusunga miyezo yolungama+ ya m’Chilamulo, kusadulidwa kwake kudzaonedwa ngati kudulidwa, kodi si choncho?+ 27 Munthu amene mwachibadwa ndi wosadulidwa, mwa kutsatira Chilamulo adzakuweruza iwe.+ Adzakuweruza iweyo amene umaphwanya malamulo, amene uli ndi malamulo olembedwa ndiponso ndiwe wodulidwa. 28 Pakuti iye amene ali Myuda kunja kokha si Myuda ayi,+ ndiponso mdulidwe wakunja kokha wochitidwa pathupi, si mdulidwe ayi.+ 29 Koma Myuda ndi amene ali wotero mkati,+ ndipo mdulidwe wake ndi wa mumtima+ wochitidwa ndi mzimu, osati ndi malamulo olembedwa.+ Munthu woteroyo satamandidwa+ ndi anthu koma ndi Mulungu.+