Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Salimo 15:1-5
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 15 Inu Yehova, ndi ndani amene angakhale mlendo mutenti yanu?

      Ndi ndani amene angakhale mʼphiri lanu lopatulika?+

       2 Ndi amene akuyenda mosalakwitsa zinthu,*+

      Amene amachita zinthu zabwino+

      Komanso kulankhula zoona mumtima mwake.+

       3 Iye sanena miseche ndi lilime lake,+

      Sachitira mnzake choipa chilichonse,+

      Ndipo sanyoza* anzake.+

       4 Iye sagwirizana ndi munthu aliyense wonyansa,+

      Koma amalemekeza anthu amene amaopa Yehova.

      Sasintha zimene walonjeza* ngakhale zinthu zitakhala kuti sizili bwino kwa iye.+

       5 Sakongoza ndalama zake kuti alandire chiwongoladzanja,+

      Ndipo salandira chiphuphu kuti akhotetse mlandu wa munthu wosalakwa.+

      Munthu aliyense amene amachita zimenezi, sadzagwedezeka.*+

  • Salimo 27:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  4 Ndapempha chinthu chimodzi kwa Yehova,

      Chimenecho ndi chimene ndikuchilakalaka.

      Chinthu chake nʼchakuti, ndikhale mʼnyumba ya Yehova masiku onse a moyo wanga,+

      Kuti ndione ubwino wa Yehova,

      Komanso kuti ndiyangʼane kachisi wake* moyamikira.*+

  • Salimo 65:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  4 Wosangalala ndi munthu amene inu mwamusankha nʼkumubweretsa pafupi ndi inu,

      Kuti akhale mʼmabwalo anu.+

      Tidzakhutira ndi zinthu zabwino zamʼnyumba yanu,+

      Kachisi wanu woyera.*+

  • Salimo 122:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 122 Ndinasangalala pamene anandiuza kuti:

      “Tiyeni tipite kunyumba ya Yehova.”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena