Akolose
1 Ine Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwa kufuna kwa Mulungu,+ pamene ndili limodzi ndi Timoteyo+ m’bale wathu, 2 ndikulembera oyera ndi abale okhulupirika amene ali ogwirizana+ ndi Khristu ku Kolose, kuti:
Kukoma mtima kwakukulu ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate wathu zikhale nanu.+
3 Nthawi zonse tikamakupemphererani,+ timayamika+ Mulungu, Atate wa Ambuye wathu Yesu Khristu. 4 Timatero chifukwa tinamva za chikhulupiriro chanu mwa Khristu Yesu, ndi chikondi chanu pa oyera onse,+ 5 chimene muli nacho chifukwa cha chiyembekezo+ chodzalandira zimene akusungirani kumwamba.+ Munamva za chiyembekezo chimenechi pamene choonadi cha uthenga wabwino chinalengezedwa kwa inu.+ 6 Uthenga wabwinowu unafika kwa inu popeza ukubala zipatso+ ndipo ukuwonjezeka+ m’dziko lonse.+ Ukuteronso pakati panu, kuyambira tsiku limene munamva ndi kudziwa molondola za kukoma mtima kwakukulu+ kwa Mulungu monga mmene kulilidi.+ 7 Zimenezi mwaziphunzira kwa Epafura,+ kapolo mnzathu wokondedwa, amene ndi mtumiki wokhulupirika wa Khristu m’malo mwa ife. 8 Iye ndi amenenso anatidziwitsa za chikondi chanu+ chimene munachikulitsa mothandizidwa ndi mzimu wa Mulungu.
9 N’chifukwa chake ifenso, kuyambira tsiku limene tinamva zimenezo, sitinaleke kukupemphererani.+ Takhala tikupemphanso kuti mukhale odziwa molondola+ chifuniro chake, ndiponso kuti mukhale ndi nzeru+ zonse komanso muzimvetsetsa zinthu zauzimu.+ 10 Tikupemphereranso kuti muziyenda mogwirizana ndi zimene Yehova+ amafuna,+ kuti muzimukondweretsa pa chilichonse,+ pamene mukupitiriza kubala zipatso m’ntchito iliyonse yabwino, ndi kuwonjezera kumudziwa Mulungu molondola.+ 11 Tikupemphereranso kuti mulandire mphamvu zazikulu chifukwa cha mphamvu zake zaulemerero,+ kuti muthe kupirira+ zinthu zonse ndi kukhala oleza mtima ndiponso achimwemwe, 12 komanso muziyamika Atate, amene anakuyeneretsani kuti mupatsidweko gawo pa cholowa+ cha oyerawo,+ amene ali m’kuwala.+
13 Iye anatilanditsa ku ulamuliro+ wa mdima, n’kutisamutsira+ mu ufumu+ wa Mwana wake wokondedwa.+ 14 Mwa Mwana wakeyo, tinamasulidwa ndi dipo,* kutanthauza kuti machimo athu anakhululukidwa.+ 15 Iye ndiye chifaniziro+ cha Mulungu wosaonekayo,+ woyamba kubadwa+ wa chilengedwe chonse, 16 chifukwa kudzera mwa iye+ zinthu zina zonse zinalengedwa, zakumwamba ndi zapadziko lapansi. Inde, zinthu zooneka ndi zinthu zosaoneka, kaya ndi mipando yachifumu, kapena ambuye, kapena maboma, kapena maulamuliro.+ Zinthu zina zonse zinalengedwa kudzera mwa iye,+ ndiponso chifukwa cha iye. 17 Ndiponso, iye ali patsogolo pa zinthu zina zonse,+ ndipo zinthu zina zonse zinakhalapo kudzera mwa iye.+ 18 Iye ndiyenso mutu wa thupilo, lomwe ndi mpingo.+ Iye ndiye chiyambi, woyamba kubadwa kuchokera kwa akufa,+ kuti adzakhale woyamba+ pa zinthu zonse. 19 Zili motero chifukwa kunamukomera Mulungu kuti zinthu zonse+ zikhale mwa mwana wakeyo ndipo zidzazemo bwino. 20 Kuti kudzera mwa mwana wakeyo iye agwirizanitsenso+ zinthu zina zonse ndi iyeyo,+ pokhazikitsa mtendere+ mwa magazi+ amene iye anakhetsa pamtengo wozunzikirapo,*+ kaya zikhale zinthu zapadziko lapansi kapena zinthu zakumwamba.
21 Ndithudi, inu amene kale munali otalikirana+ naye ndiponso adani ake chifukwa maganizo anu anali pa ntchito zoipa,+ 22 tsopano wagwirizana+ nanunso pogwiritsa ntchito thupi lanyama la mwanayo kudzera mu imfa yake.+ Wachita izi kuti akuperekeni pamaso pa iyeyo, muli opatulika ndi opanda chilema,+ ndiponso opanda chifukwa chokunenezerani.+ 23 Adzaterodi, malinga ngati mupitirizabe m’chikhulupiriro,+ muli okhazikika pamaziko+ ndiponso olimba, osasunthika+ pa chiyembekezo cha uthenga wabwino umene munamva,+ umenenso unalalikidwa+ m’chilengedwe chonse+ cha pansi pa thambo. Uthenga wabwino umenewu ndi umene ineyo Paulo ndinakhala mtumiki wake.+
24 Ndikusangalala tsopano ndi masautso amene ndikukumana nawo chifukwa cha inu.+ Ndipo inenso kumbali yanga, ndikuona kuti sindinazunzikebe mokwanira+ monga chiwalo cha thupi la Khristu, limene ndi mpingo.+ 25 Ndinakhala mtumiki+ wa mpingo umenewu mogwirizana ndi udindo+ umene Mulungu anandipatsa, woti ndilalikire mawu a Mulungu mokwanira, kuti inuyo mupindule. 26 Mawuwo ndi chinsinsi chopatulika+ chimene chinabisidwa nthawi* zakale,+ ndiponso kwa mibadwo yakale. Koma tsopano chaululidwa+ kwa oyera ake. 27 Mulungu anaululira anthu a mitundu ina chinsinsi chopatulikachi,+ chimene chili chodzaza ndi ulemerero ndi chuma chauzimu.+ Chinsinsicho n’chakuti Khristu+ ndi wogwirizana ndi inuyo, zimene zikutanthauza kuti muli ndi chiyembekezo chodzalandira ulemerero pamodzi naye.+ 28 Tikulengeza,+ kuchenjeza, ndi kuphunzitsa munthu aliyense za ameneyu mu nzeru zonse,+ kuti tipereke munthu aliyense kwa Mulungu ali wokhwima mwauzimu+ mogwirizana ndi Khristu. 29 Ineyo ndikugwira ntchito mwakhama kuti ndichite zimenezi, poyesetsa kwambiri+ mogwirizana ndi mphamvu+ yake imenenso ikugwira ntchito mwa ine.+