Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Deuteronomo 30
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

Zimene Zili Mʼbuku la Deuteronomo

      • Kubwerera kwa Yehova (1-10)

      • Malamulo a Yehova si ovuta kwambiri (11-14)

      • Kusankha moyo kapena imfa (15-20)

Deuteronomo 30:1

Mawu a M'munsi

  • *

    Mʼchilankhulo choyambirira, “mukadzawabweretsanso mumtima mwanu.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 11:26-28; 28:2, 15
  • +1Mf 8:47; Ne 1:9; Eze 18:28; Yow 2:13
  • +2Mf 17:6; 2Mb 36:20

Deuteronomo 30:2

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Yes 55:7; 1Yo 1:9
  • +De 4:29

Deuteronomo 30:3

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Yer 29:14
  • +Mlr 3:22
  • +Eza 1:2, 3; Sl 147:2; Yer 32:37; Eze 34:13

Deuteronomo 30:4

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 28:64; Zef 3:20

Deuteronomo 30:5

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ne 1:9

Deuteronomo 30:6

Mawu a M'munsi

  • *

    Mʼchilankhulo choyambirira, “adzachita mdulidwe.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Yer 32:37, 39
  • +De 6:5

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    6/1/2007, tsa. 13

Deuteronomo 30:7

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ge 12:2, 3; Yer 25:12; Mlr 3:64; Aro 12:19

Deuteronomo 30:9

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Yes 65:21, 22; Mki 3:10
  • +Yer 32:37, 41

Deuteronomo 30:10

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ne 1:9; Mac 3:19

Deuteronomo 30:11

Mawu a M'munsi

  • *

    Mʼchilankhulo choyambirira, “silili patali.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Yes 45:19

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    11/1/2009, tsa. 31

Deuteronomo 30:12

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Aro 10:6

Deuteronomo 30:14

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Aro 10:8
  • +Mt 7:21; Yak 1:25

Deuteronomo 30:15

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 11:26

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    11/1/2009, tsa. 31

Deuteronomo 30:16

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 6:5
  • +Le 18:5
  • +Le 25:18; De 30:5

Deuteronomo 30:17

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 29:18; Ahe 3:12
  • +De 4:19

Deuteronomo 30:18

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 8:19; Yos 23:15; 1Sa 12:25

Deuteronomo 30:19

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 11:26; 27:26; 28:2, 15
  • +Yos 24:15
  • +De 32:47

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo,

    Nsanja ya Olonda (Yogawira),

    No. 2 2018, tsatsa. 14-15

    Nsanja ya Olonda,

    2/15/2010, tsa. 28

    6/1/2006, tsa. 27

    7/15/1999, ptsa. 11-12

    6/15/1996, ptsa. 12-17

    Galamukani!,

    2/2009, tsa. 13

Deuteronomo 30:20

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 10:12
  • +De 4:4
  • +Ge 12:7; 15:18

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo,

    Nsanja ya Olonda (Yogawira),

    No. 2 2018, tsatsa. 14-15

    Nsanja ya Olonda,

    2/15/2010, tsa. 28

    11/1/2009, tsa. 31

    6/1/2006, ptsa. 28-29

    7/15/1999, ptsa. 11-12

    Galamukani!,

    2/2009, tsa. 13

Mabaibulo Ena

Dinani pa nambala ya vesi kuti muone mavesi a m'Baibulo lina ofanana ndi vesilo.

Malemba Ena

Deut. 30:1De 11:26-28; 28:2, 15
Deut. 30:11Mf 8:47; Ne 1:9; Eze 18:28; Yow 2:13
Deut. 30:12Mf 17:6; 2Mb 36:20
Deut. 30:2Yes 55:7; 1Yo 1:9
Deut. 30:2De 4:29
Deut. 30:3Yer 29:14
Deut. 30:3Mlr 3:22
Deut. 30:3Eza 1:2, 3; Sl 147:2; Yer 32:37; Eze 34:13
Deut. 30:4De 28:64; Zef 3:20
Deut. 30:5Ne 1:9
Deut. 30:6De 6:5
Deut. 30:6Yer 32:37, 39
Deut. 30:7Ge 12:2, 3; Yer 25:12; Mlr 3:64; Aro 12:19
Deut. 30:9Yes 65:21, 22; Mki 3:10
Deut. 30:9Yer 32:37, 41
Deut. 30:10Ne 1:9; Mac 3:19
Deut. 30:11Yes 45:19
Deut. 30:12Aro 10:6
Deut. 30:14Aro 10:8
Deut. 30:14Mt 7:21; Yak 1:25
Deut. 30:15De 11:26
Deut. 30:16De 6:5
Deut. 30:16Le 18:5
Deut. 30:16Le 25:18; De 30:5
Deut. 30:17De 29:18; Ahe 3:12
Deut. 30:17De 4:19
Deut. 30:18De 8:19; Yos 23:15; 1Sa 12:25
Deut. 30:19De 11:26; 27:26; 28:2, 15
Deut. 30:19Yos 24:15
Deut. 30:19De 32:47
Deut. 30:20De 10:12
Deut. 30:20De 4:4
Deut. 30:20Ge 12:7; 15:18
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
  • Werengani mu Baibulo la Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
  • 19
  • 20
Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Deuteronomo 30:1-20

Deuteronomo

30 “Mawu onsewa akadzakwaniritsidwa pa inu, madalitso ndi matemberero amene ndaika pamaso panu,+ ndipo mukadzawakumbukira*+ muli ku mitundu yonse kumene Yehova Mulungu wanu adzakubalalitsireni,+ 2 inu nʼkubwerera kwa Yehova Mulungu wanu+ komanso kumvera mawu ake ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse, mogwirizana ndi zonse zimene ndikukulamulani lero, inuyo ndi ana anu,+ 3 Yehova Mulungu wanu adzabweza kwawo anthu a mtundu wanu amene anagwidwa nʼkupita kudziko lina,+ ndipo adzakuchitirani chifundo+ nʼkukusonkhanitsaninso pamodzi kuchokera pakati pa anthu onse kumene Yehova Mulungu wanu anakubalalitsirani.+ 4 Ngakhale anthu a mtundu wanu amene anabalalitsidwawo atadzakhala kumalekezero kwa thambo, Yehova Mulungu wanu adzakusonkhanitsani nʼkukubweretsani kuchokera kumeneko.+ 5 Yehova Mulungu wanu adzakubweretsani mʼdziko limene makolo anu analitenga kuti likhale lawo, ndipo lidzakhala lanu. Iye adzachititsa kuti zinthu zikuyendereni bwino ndipo adzakuchulukitsani kwambiri kuposa makolo anu.+ 6 Yehova Mulungu wanu adzayeretsa* mitima yanu ndi mitima ya ana anu,+ kuti muzikonda Yehova Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse komanso moyo wanu wonse ndipo mudzakhala ndi moyo.+ 7 Ndiyeno Yehova Mulungu wanu adzabweretsa matemberero onsewa pa adani anu, amene ankadana nanu komanso kukuzunzani.+

8 Kenako inu mudzabwerera nʼkumvera mawu a Yehova komanso kutsatira malamulo ake onse amene ndikukupatsani lero. 9 Yehova Mulungu wanu adzachititsa kuti zinthu zikuyendereni bwino kwambiri pa ntchito iliyonse ya manja anu.+ Adzachulukitsa ana anu, ziweto zanu ndi zokolola zanu, chifukwa Yehova adzasangalalanso kuchititsa kuti zinthu zikuyendereni bwino, ngati mmene anachitira ndi makolo anu.+ 10 Chifukwa pa nthawiyo mudzamvera mawu a Yehova Mulungu wanu ndi kusunga malamulo komanso malangizo ake amene analembedwa mʼbuku ili la Chilamulo, ndipo mudzabwerera kwa Yehova Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse komanso moyo wanu wonse.+

11 Lamulo limene ndikukupatsani leroli si lovuta kwa inu kulitsatira, ndipo silili poti simungathe kulipeza.*+ 12 Silili kumwamba kuti munene kuti, ‘Ndani adzapite kumwamba kuti akatitengere lamulolo kuti ife tidzalimve nʼkulitsatira?’+ 13 Ndiponso silili tsidya lina la nyanja kuti munene kuti, ‘Ndani adzawoloke kupita tsidya lina la nyanja kuti akatitengere lamulolo kuti ife tidzalimve nʼkulitsatira?’ 14 Chifukwa mawu a chilamulowo ali pafupi kwambiri ndi inu, ali mʼkamwa mwanu ndi mumtima mwanu+ kuti muwatsatire.+

15 Taonani, ine ndikuika pamaso panu lero moyo ndi zinthu zabwino, imfa ndi zinthu zoipa.+ 16 Mukadzamvera malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani lero, pokonda Yehova Mulungu wanu,+ kuyenda mʼnjira zake ndi kusunga malamulo ake, malangizo ake ndi zigamulo zake, mudzakhala ndi moyo,+ mudzachulukana ndipo Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani mʼdziko limene mukupita kukalitenga kuti likhale lanu.+

17 Koma mtima wanu ukatembenukira kwina+ ndipo simukumvera, moti mwakopeka nʼkugwadira milungu ina ndi kuitumikira,+ 18 ndikukuuzani lero kuti mudzatheratu.+ Simudzakhala nthawi yaitali mʼdziko limene mukupita kukalitenga kuti likhale lanu mutawoloka Yorodano. 19 Lero ndaika moyo ndi imfa, dalitso ndi temberero pamaso panu.+ Kumwamba ndi dziko lapansi ndi mboni pa zochita zanu. Choncho inuyo ndi mbadwa zanu+ musankhe moyo kuti mukhalebe ndi moyo.+ 20 Musankhe moyo pokonda Yehova Mulungu wanu,+ kumvera mawu ake ndi kukhala okhulupirika kwa iye,+ chifukwa iye ndi amene amapereka moyo ndipo angakuthandizeni kuti mukhale ndi moyo kwa nthawi yaitali mʼdziko limene Yehova analumbira kuti adzalipereka kwa makolo anu, Abulahamu, Isaki ndi Yakobo.”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena