1 Mbiri
16 Motero analowetsa+ likasa la Mulungu woona muhema limene Davide anamanga, n’kuika likasalo pamalo ake muhemalo.+ Kenako iwo anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano kwa Mulungu woona.+ 2 Davide atamaliza kupereka nsembe yopsereza+ ndi nsembe zachiyanjano,+ anadalitsa+ anthu m’dzina la Yehova.+ 3 Kuwonjezera apo, Aisiraeli onse, mwamuna komanso mkazi, aliyense wa iwo anapatsidwa+ keke yozungulira, zipatso za kanjedza zouma zoumba pamodzi ndi mphesa zouma zoumba pamodzi. 4 Ndiyeno Davide anaika Alevi+ ena kukhala otumikira+ pa likasa la Yehova kuti azikumbutsa+ anthu, kuyamika,+ ndi kutamanda+ Yehova Mulungu wa Isiraeli. 5 Mtsogoleri wawo anali Asafu,+ wachiwiri wake anali Zekariya. Panalinso Yeyeli, Semiramoti, Yehiela, Matitiya, Eliyabu, Benaya, Obedi-edomu, ndi Yeyeli.+ Onsewa anali ndi zoimbira za zingwe ndi azeze,+ ndipo Asafu+ anali kuimba zinganga mokweza.+ 6 Benaya ndi Yahazieli, omwe anali ansembe, ankaimba malipenga+ nthawi zonse patsogolo pa likasa la pangano la Mulungu woona.
7 Pa tsiku limeneli m’pamene Davide anathandiza+ nawo kuyamika+ Yehova kudzera mwa Asafu+ ndi abale ake kwanthawi yoyamba, ndi nyimbo yakuti:
8 “Yamikani Yehova,+ anthu inu. Itanani pa dzina lake.+
Dziwitsani mitundu ya anthu ntchito zake!+
12 Kumbukirani ntchito zodabwitsa zimene wachita,+
Kumbukirani zozizwitsa zake ndi zigamulo zotuluka m’kamwa mwake,+
13 Inu mbadwa za Isiraeli mtumiki wake,+
Inu ana a Yakobo, osankhidwa mwapadera.+
14 Iye ndi Yehova Mulungu wathu.+ Zigamulo zake zili padziko lonse lapansi.+
15 Kumbukirani pangano lake mpaka kalekale,+
Kumbukirani lonjezo limene anapereka, ku mibadwo 1,000,+
16 Kumbukirani pangano limene anapangana ndi Abulahamu,+
Ndi lonjezo limene analumbira kwa Isaki.+
17 Pangano limene analikhazikitsa monga lamulo kwa Yakobo,+
Monga pangano lokhalapo mpaka kalekale kwa Isiraeli,+
18 Pamene anati: ‘Ndidzakupatsa dziko la Kanani,+
Kuti likhale gawo la cholowa chako.’+
19 Pamene ananena zimenezi n’kuti inu muli ochepa,+
N’kuti muli ochepa kwambiri, komanso muli alendo m’dzikolo.+
20 Iwo anapitiriza kuyendayenda pakati pa mitundu yosiyanasiyana,+
Anali kuchoka mu ufumu wina ndi kupita kukakhala ndi anthu a mtundu wina.+
21 Mulungu sanalole aliyense kuwachitira zachinyengo,+
Koma anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo.+
22 Iye anati: ‘Anthu inu musakhudze odzozedwa anga,
Ndipo aneneri anga musawachitire choipa chilichonse.’+
23 Imbirani Yehova, inu nonse okhala padziko lapansi!+
Tsiku ndi tsiku lengezani chipulumutso chimene amapereka!+
24 Fotokozani za ulemerero wake pakati pa anthu a mitundu ina,
Ndiponso za ntchito zake zodabwitsa pakati pa mitundu yonse ya anthu.
25 Pakuti Yehova ndi wamkulu ndi woyenera kutamandidwa kwambiri,+
Ndipo ndi woyenera kuopedwa kuposa milungu ina yonse.+
26 Chifukwa milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi milungu yopanda pake.+
Koma Yehova, ndiye anapanga kumwamba.+
28 Vomerezani Yehova, inu mabanja a mitundu ya anthu,
M’patseni Yehova ulemerero ndi kuvomereza kuti iye ndi wamphamvu.+
29 M’patseni Yehova ulemerero wa dzina lake,+
Tengani mphatso n’kubwera nayo pamaso pake.+
Gwadirani Yehova mutavala zovala zokongola ndi zopatulika.+
30 Njenjemerani ndi mantha* pamaso pake, inu anthu nonse okhala padziko lapansi!
Ndiponso dziko lapansi ndi lokhazikika,
Silidzagwedezeka ku nthawi zonse.+
31 Kumwamba kukondwere, ndipo dziko lapansi lisangalale,+
Ndipo anene pakati pa anthu a mitundu ina kuti: ‘Yehova wakhala mfumu!’+
32 Nyanja ichite mkokomo ndi zonse zimene zili mmenemo,+
Mtunda ukondwere ndi zonse zimene zili kumeneko.+
33 Pa nthawi imodzimodziyo, mitengo ya m’nkhalango ifuule mokondwera chifukwa cha Yehova,+
Pakuti iye wabwera kudzaweruza dziko lapansi.+
34 Yamikani Yehova anthu inu, chifukwa iye ndi wabwino,+
Pakuti kukoma mtima kwake kosatha kudzakhalapobe mpaka kalekale.+
35 Nenani kuti: ‘Tipulumutseni, inu Mulungu wachipulumutso chathu,+
Tisonkhanitseni pamodzi ndi kutilanditsa kwa anthu a mitundu ina,+
Kuti titamande dzina lanu loyera,+ ndiponso kuti tilankhule mokondwa pokutamandani.+
36 Adalitsike Yehova Mulungu wa Isiraeli kuyambira kalekale mpaka kalekale.’”+
Ndiyeno anthu onse ananena kuti, “Ame!”* n’kutamanda Yehova.+
37 Kenako Davide anasiya Asafu+ ndi abale ake kumeneko pamaso pa likasa la Yehova, kuti azitumikira+ pamaso pa Likasalo nthawi zonse, malinga ndi zofunikira pa tsiku lililonse.+ 38 Anasiyanso Obedi-edomu ndi abale ake okwanira 68, ndiponso Obedi-edomu mwana wa Yedutuni ndi Hosa kukhala alonda a pachipata. 39 Anasiyanso Zadoki+ wansembe ndi abale ake ansembe kuchihema cha Yehova chimene chinali pamalo okwezeka a ku Gibeoni,+ 40 kuti azipereka nsembe zopsereza kwa Yehova nthawi zonse paguwa lansembe zopsereza, m’mawa ndi madzulo, malinga ndi zonse zolembedwa m’chilamulo cha Yehova chimene analamula Aisiraeli.+ 41 Iwowa anali limodzi ndi Hemani+ ndi Yedutuni ndiponso amuna onse amene anasankhidwa+ mwa kutchulidwa mayina kuti aziyamika Yehova,+ chifukwa “kukoma mtima kwake kosatha kudzakhala mpaka kalekale.”+ 42 Anasiya Hemani+ ndi Yedutuni+ limodzi ndi amuna aja kuti aziimba malipenga,+ zinganga ndi zipangizo zina zoimbira nyimbo ya Mulungu woona, ndipo ana+ a Yedutuni anali alonda a pachipata. 43 Pambuyo pake anthu onse ananyamuka, ndipo aliyense anapita kunyumba kwake.+ Nayenso Davide anapita kunyumba kwake n’kukadalitsa banja lake.