Numeri
9 M’mwezi woyamba*+ wa chaka chachiwiri, ana a Isiraeli atatuluka m’dziko la Iguputo, Yehova analankhula ndi Mose m’chipululu cha Sinai. Iye anati: 2 “Tsopano ana a Isiraeli akonze nsembe ya pasika+ pa nthawi yake yoikidwiratu.+ 3 Mukonze nsembeyo pa tsiku la 14 la mwezi uno, madzulo kuli kachisisira,*+ ndiyo nthawi yake yoikidwiratu. Muikonze malinga ndi malamulo ake onse, ndiponso motsatira njira zonse za kakonzedwe kake.”+
4 Pamenepo Mose analankhula kwa ana a Isiraeli kuti akonze nsembe ya pasika. 5 Iwo anakonza nsembe ya pasika pa tsiku la 14 la mwezi woyamba, madzulo kuli kachisisira, m’chipululu cha Sinai. Ana a Isiraeliwo anachita zonse malinga ndi zimene Yehova analamula Mose.+
6 Tsopano panali amuna ena amene anadzidetsa pokhudza mtembo wa munthu,+ moti sanathe kukonza nsembe ya pasika pa tsikulo. Chotero anakaonekera kwa Mose ndi Aroni pa tsikulo.+ 7 Ndipo iwo ananena kuti: “Ife ndife odetsedwa chifukwa takhudza mtembo wa munthu. Ngakhale kuti zili choncho, kodi tiyeneradi kuletsedwa kupereka nsembe+ kwa Yehova pakati pa ana a Isiraeli pa nthawi yake yoikidwiratu?” 8 Pamenepo Mose anawayankha kuti: “Dikirani pomwepo, ndimve zimene Yehova ati alamule zokhudza inu.”+
9 Ndiyeno Yehova anauza Mose kuti: 10 “Uza ana a Isiraeli kuti, ‘Munthu wina aliyense mwa inu kapena mwa mbadwa zanu, amene wadetsedwa pokhudza mtembo wa munthu,+ kapena amene ali pa ulendo wautali, akonzebe nsembe ya pasika yopereka kwa Yehova. 11 Azikonza nsembeyo m’mwezi wachiwiri+ pa tsiku la 14, madzulo kuli kachisisira. Azidya nyama ya nsembeyo pamodzi ndi mikate yopanda chofufumitsa, ndiponso masamba owawa.+ 12 Pasatsaleko iliyonse yoti ifike m’mawa,+ ndipo asaphwanye fupa lake lililonse.+ Aikonze motsatira malamulo onse a pasika.+ 13 Koma ngati munthu ali wosadetsedwa, kapena sanapite pa ulendo, ndipo wanyalanyaza kukonza nsembe ya pasika, munthuyo aphedwe kuti asakhalenso pakati pa anthu ake,+ chifukwa sanapereke nsembeyo kwa Yehova pa nthawi yake yoikidwiratu. Munthuyo adzafa chifukwa cha kuchimwa kwake.+
14 “‘Ngati pali mlendo amene akukhala pakati panu, iyenso azikonza nsembe ya pasika yopereka kwa Yehova.+ Aziikonza motsatira malamulo onse a pasika, ndiponso kakonzedwe kake ka nthawi zonse.+ Pakhale malamulo ofanana kwa nonsenu, kaya mlendo kapena mbadwa.’”+
15 Pa tsiku lomanga chihema chopatulika,+ mtambo unaima pamwamba pa chihema cha Umbonicho.+ Koma kuyambira madzulo mpaka m’mawa, moto+ unali kuoneka pamwamba pa chihema chopatulikacho. 16 Zinali kuchitika motero nthawi zonse. Mtambo unali kuima pamwamba pa chihemacho masana, ndipo usiku moto unali kuonekera pamwamba pake.+ 17 Mtambowo ukanyamuka pamwamba pa chihemacho, ana a Isiraeli anali kunyamuka nthawi yomweyo.+ Ndipo pamalo pamene mtambowo waima, m’pamene ana a Isiraeli anali kumangapo msasa.+ 18 Choncho Yehova akalamula, ana a Isiraeli anali kunyamuka, ndipo Yehova akalamula, anali kumanga msasa.+ Masiku onse amene mtambo unali pamwamba pa chihemacho, iwo anali kukhalabe pamsasapo. 19 Ngakhale mtambowo ukhale masiku ambiri pamwamba pa chihema, ana a Isiraeli ankamverabe Yehova, ndipo sankachoka pamalopo.+ 20 Nthawi zina mtambowo unali kungokhala masiku owerengeka pamwamba pa chihemapo. Yehova akalamula,+ iwo anali kukhalabe pamsasapo, ndipo Yehova akalamula, iwo anali kuchoka. 21 Nthawi zina mtambowo+ unali kukhalapo kuchokera madzulo kufika m’mawa, ndipo m’mawawo mtambowo unali kuchoka, anthuwo n’kunyamuka. Kaya mtambowo uchoke masana kapena usiku, iwonso anali kunyamuka.+ 22 Kaya mtambowo ukhale pamwamba pa chihemacho masiku awiri, mwezi, kapena masiku ambiri, ana a Isiraeli anali kukhalabe pamsasa osachoka. Koma mtambowo ukanyamuka, iwo anali kuchoka.+ 23 Yehova akalamula, iwo ankamanga msasa, ndipo Yehova akalamula, iwo ankanyamuka.+ Anali kumvera Yehova potsatira malangizo a Yehova odzera kwa Mose.+