Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • bi12 Lamentations 1-5:22
  • Maliro

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Maliro
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Maliro

Maliro

א [ʼAʹleph]

1 Amene anali ndi anthu ambiri+ tsopano wakhala wopanda anthu.+

Amene anali ndi anthu ambiri pakati pa mitundu ina+ wakhala ngati mkazi wamasiye.+

Amene anali wolemekezeka pakati pa zigawo zina wayamba kugwira ntchito yaukapolo.+

ב [Behth]

 2 Iye akulira kwambiri usiku,+ ndipo misozi ikutsika pamasaya ake.+

Pakati pa onse amene anali kumukonda, palibe amene akumutonthoza.+

Anthu onse amene anali anzake amuchitira zachinyengo+ ndipo akhala adani ake.+

ג [Giʹmel]

 3 Yuda wakhala kapolo chifukwa cha nsautso+ ndiponso chifukwa cha kukula kwa ntchito yaukapolo imene akugwira.+

Iye wakhala pakati pa mitundu ina ya anthu,+ ndipo sanapeze malo ampumulo.

Onse amene anali kumuzunza amupeza pa nthawi ya mavuto ake.+

ד [Daʹleth]

 4 Njira zopita ku Ziyoni zikulira, chifukwa palibe amene akupita kuchikondwerero.+

Zipata zake zonse zasiyidwa.+ Ansembe+ ake akuusa moyo.*

Anamwali ake agwidwa ndi chisoni,+ ndipo iyeyo akumva kuwawa mumtima.

ה [Heʼ]

 5 Adani ake akumulamulira.+ Anthu odana naye sakuda nkhawa.+

Yehova wamuchititsa kukhala wachisoni chifukwa cha kuchuluka kwa machimo+ ake,

Ndipo ana ake ayenda patsogolo pa adani awo atagwidwa ukapolo.+

ו [Waw]

 6 Ulemerero+ wonse wamuchokera mwana wamkazi wa Ziyoni.

Akalonga ake akhala ngati mbawala zamphongo zimene zikusowa msipu.+

Iwo akuyenda mofooka+ pamaso pa wowazunza.*

ז [Zaʹyin]

 7 Yerusalemu anakumbukira zinthu zake zonse zabwino+ zimene anali nazo kuyambira kalekale.

Anazikumbukira m’masiku a masautso ake ndi a anthu ake osowa pokhala.

Anthu ake atagwidwa ndi adani, pamene iye analibe munthu womuthandiza,+

Adani akewo anamuona, ndipo anamuseka+ chifukwa chakuti wagwa.

ח [Chehth]

 8 Yerusalemu wachita tchimo+ lalikulu. N’chifukwa chake wakhala chinthu chonyansa.+

Onse amene anali kumulemekeza ayamba kumuona ngati chinthu chachabechabe,+ chifukwa aona maliseche+ ake.

Iyenso akuusa moyo+ ndipo watembenukira kwina chifukwa cha manyazi.

ט [Tehth]

 9 Zovala+ zake ndi zodetsedwa. Iye sanaganizire za tsogolo+ lake.

Wagwa modabwitsa ndipo alibe womutonthoza.+

Inu Yehova, onani kusautsika+ kwanga, pakuti mdani wanga akudzitukumula.+

י [Yohdh]

10 Mdani watambasula dzanja lake n’kutenga zinthu+ zake zonse zabwino.

Yerusalemu waona mitundu ina itabwera ndi kulowa m’malo ake opatulika,+

Mitundu imene munalamula kuti isalowe mumpingo wanu.

כ [Kaph]

11 Anthu ake onse akuusa moyo. Iwo akufunafuna chakudya.+

Asinthanitsa zinthu zawo zabwino ndi chakudya kuti adzitsitsimutse.+

Inu Yehova ndiyang’aneni. Onani kuti ndakhala ngati mkazi wachabechabe.+

ל [Laʹmedh]

12 Inu nonse amene mukudutsa m’njira, kodi mukuona ngati imeneyi ndi nkhani yaing’ono? Ndiyang’aneni kuti muone.+

Kodi palinso ululu wina woposa ululu umene ineyo ndalangidwa nawo,+

Ululu umene Yehova wandibweretsera nawo chisoni m’tsiku la mkwiyo+ wake woyaka moto?

מ [Mem]

13 Iye watumiza moto m’mafupa+ mwanga kuchokera kumwamba, ndipo wafooketsa fupa lililonse.

Watchera ukonde+ kuti ukole mapazi anga. Wandibweza kumbuyo.

Wandisandutsa mkazi wosiyidwa popanda thandizo. Ndikudwala tsiku lonse.+

נ [Nun]

14 Iye wakhala tcheru kuti aone machimo+ anga. Machimowo alukanalukana m’dzanja lake.

Amangidwa m’khosi+ mwanga, moti mphamvu zanga zatha.

Yehova wandipereka m’manja mwa anthu amene sindingathe kulimbana nawo.+

ס [Saʹmekh]

15 Yehova wandichotsera anthu anga onse amphamvu+ ndi kuwakankhira pambali.

Wandiitanitsira msonkhano kuti athyolethyole anyamata anga.+

Yehova wapondaponda moponderamo mphesa+ mwa namwali, mwana wamkazi wa Yuda.+

ע [ʽAʹyin]

16 Ndikulirira zinthu zimenezi ngati mkazi.+ Maso anga ine! Maso anga akutuluka misozi.+

Pakuti wonditonthoza, munthu woti anditsitsimule, ali kutali ndi ine.

Ana anga asiyidwa+ popanda thandizo, pakuti mdani wanga wadzitukumula.+

פ [Peʼ]

17 Ziyoni watambasula manja ake.+ Iye alibe womutonthoza.+

Yehova walamula onse ozungulira Yakobo kuti akhale adani ake.+

Yerusalemu wakhala chinthu chonyansa pakati pawo.+

צ [Tsa·dhehʹ]

18 Yehova ndi wolungama,+ koma ine ndapandukira+ mawu a pakamwa pake.

Anthu nonsenu, tamverani mawu anga, ndipo muone ululu umene ndikumva.

Anamwali anga ndi anyamata anga atengedwa kupita ku ukapolo.+

ק [Qohph]

19 Ndaitana anthu ondikonda kwambiri,+ koma anthuwo andichitira zachinyengo.

Ansembe anga ndiponso akuluakulu atha+ mumzinda.

Atha pamene anali kufunafuna chakudya choti adye kuti adzitsitsimutse.+

ר [Rehsh]

20 Taonani, inu Yehova. Inetu zandivuta. M’mimba mwanga mukubwadamuka.+

Mtima wanga wasweka,+ pakuti ndapanduka kwambiri.+

Panja, lupanga lapha+ ana. M’nyumba, anthu akufanso.+

ש [Shin]

21 Anthu amva mmene ndikuusira moyo ngati mkazi,+ koma palibe wonditonthoza.+

Adani anga onse amva za tsoka+ langa. Iwo akondwera,+ chifukwa ndinu mwachititsa zimenezi.

Inu mubweretsadi tsiku limene mwanena,+ kuti iwo akhale ngati ine.+

ת [Taw]

22 Kuipa kwawo konse kuonekere pamaso panu, ndipo muwalange+ koopsa.

Muwalange koopsa monga mmene mwandilangira ine chifukwa cha machimo+ anga onse.

Pakuti ndikuusa+ moyo kwambiri ndipo mtima wanga ukudwala.+

א [ʼAʹleph]

2 Chifukwa chokwiya, Yehova waphimba mwana wamkazi wa Ziyoni ndi mtambo+ wakuda.

Iye waponya pansi chokongoletsera+ Isiraeli kuchokera kumwamba.+

Sanakumbukire chopondapo mapazi+ ake pa tsiku la mkwiyo wake.

ב [Behth]

 2 Yehova wameza malo okhala a Yakobo. Sanamvere chisoni malo ake alionse.+

Mu ukali wake, iye wagwetsa mipanda yolimba kwambiri+ ya mwana wamkazi wa Yuda.

Waipitsa ufumu+ ndi akalonga+ ake ndipo wawagwetsera pansi.+

ג [Giʹmel]

 3 Mu mkwiyo wake wathyola nyanga* iliyonse ya Isiraeli.+

Adani athu atatiukira, iye sanatithandize.+

Mkwiyo wake ukuyakirabe Yakobo ngati moto umene wawononga ponseponse.+

ד [Daʹleth]

 4 Wakunga uta wake ngati mdani.+ Dzanja lake lamanja+ lakonzeka ngati la mdani,+

Ndipo wapitiriza kupha+ anthu onse ofunika kwambiri.

Ukali wake waukhuthula ngati moto+ m’hema+ wa mwana wamkazi wa Ziyoni.

ה [Heʼ]

 5 Yehova wakhala ngati mdani.+ Wameza Isiraeli.+

Iye wameza nsanja zonse za Isiraeli zokhalamo.+ Wawononga malo ake otetezedwa ndiponso mipanda yolimba kwambiri.+

Wachititsa kuti kulira ndi maliro+ zimveke mumzinda wa mwana wamkazi wa Yuda.

ו [Waw]

 6 Iye wapasula chisimba*+ chake ngati chisimba cha m’munda+ ndipo wathetsa zikondwerero zake.

Yehova wachititsa kuti zikondwerero+ ndi sabata ziiwalike mu Ziyoni,

Ndipo mu mkwiyo wake waukulu wakana mfumu ndi wansembe.+

ז [Zaʹyin]

 7 Yehova wataya guwa lake lansembe.+ Iye wanyoza malo ake opatulika.+

Wapereka m’manja mwa adani makoma* a nsanja zake zokhalamo.+

Iwo afuula m’nyumba ya Yehova ngati pa tsiku lachikondwerero.+

ח [Chehth]

 8 Yehova waganiza zogwetsa mpanda+ wa mwana wamkazi wa Ziyoni.

Watambasula chingwe choyezera.+ Sanabweze dzanja lake kuti lisabweretse chiwonongeko.+

Walilitsa+ chiunda chomenyerapo nkhondo ndi mpanda. Zonsezi zatha mphamvu.

ט [Tehth]

 9 Zipata+ zake zamira munthaka. Wawononga mipiringidzo yake ndipo waithyolathyola.

Mfumu yake ndi akalonga ake ali pakati pa mitundu ina.+ Malamulo sakutsatiridwa.+

Aneneri ake sakuonanso masomphenya ochokera kwa Yehova.+

י [Yohdh]

10 Akuluakulu a mwana wamkazi wa Ziyoni akhala pansi ndipo akhala chete.+

Iwo athira fumbi pamitu+ yawo ndipo avala ziguduli.*+

Anamwali a Yerusalemu aweramitsa mitu yawo mpaka padothi.+

כ [Kaph]

11 Maso anga atopa ndi kulira.+ M’mimba mwanga mukubwadamuka.+

Chiwindi changa chakhuthulidwa+ pansi chifukwa cha kuwonongedwa kwa mwana wamkazi wa anthu anga,+

Ndiponso chifukwa chakuti ana ndi makanda oyamwa akukomoka+ m’mabwalo a mzinda.

ל [Laʹmedh]

12 Iwo anali kufunsa amayi awo kuti: “Kodi chakudya ndi vinyo zili kuti?”+

Anali kufunsa chifukwa anali kukomoka m’mabwalo a mzinda ndi kugona pansi ngati anthu ophedwa,

Ndiponso chifukwa moyo wawo unali kukhuthukira pachifuwa cha amayi awo.

מ [Mem]

13 Kodi ndikusonyeze umboni wotani? Kodi ndingakuyerekezere ndi chiyani, iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu?+

Kodi ndikufananitse ndi chiyani kuti ndikutonthoze, namwali iwe, mwana wamkazi wa Ziyoni?+

Pakuti kuwonongeka+ kwako kwafalikira ngati kukula kwa nyanja. Ndani angakuchiritse?+

נ [Nun]

14 Aneneri ako aona masomphenya achabechabe ndi opanda pake+ onena za iwe.

Iwo sanaulule zolakwa zako kuti akuteteze n’cholinga choti usatengedwe kupita ku ukapolo,+

Koma anali kuona masomphenya achabechabe ndi osocheretsa+ onena za iwe.

ס [Saʹmekh]

15 Anthu onse odutsa mumsewu akakuona, akuwomba m’manja+ monyodola.

Akuimba mluzu+ ndi kupukusa mitu+ yawo poona mwana wamkazi wa Yerusalemu. Iwo akunena kuti:

“Kodi uwu ndi mzinda umene anali kunena kuti, ‘Ndi wokongola kwambiri, wotamandika padziko lonse lapansi’?”+

פ [Peʼ]

16 Adani ako onse akukutsegulira pakamwa.+

Akuimba mluzu ndi kukukukutira mano.+ Iwo akunena kuti: “Ameneyu timumeza.+

Ndithu, lero ndi tsiku limene takhala tikuyembekezera.+ Lafikadi! Taliona!”+

ע [ʽAʹyin]

17 Yehova wachita zimene anali kuganiza.+ Wakwaniritsa zimene ananena,+

Zimene analamula kalekale.+ Wapasula zinthu ndipo sanamve chisoni.+

Wachititsa adani ako kusangalala+ chifukwa cha zimene zakuchitikira. Wakweza nyanga ya adani+ ako.

צ [Tsa·dhehʹ]

18 Mtima wa anthuwo wafuulira Yehova,+ iwe mpanda wa mwana wamkazi wa Ziyoni.+

Gwetsa misozi ngati mtsinje usana ndi usiku.+

Usapume. Mwana wa diso lako asaleke kulira.

ק [Qohph]

19 Nyamuka! Lira mofuula usiku, pa nthawi yoyamba ulonda+ wam’mawa.

Khuthula+ mtima wako pamaso+ pa Yehova ngati madzi.

Pemphera utakweza manja+ ako kwa iye chifukwa cha ana ako,

Amene akukomoka ndi njala m’misewu.+

ר [Rehsh]

20 Inu Yehova, yang’anani kuti muone+ yemwe mwamulanga chotere.

Kodi amayi azidya zipatso za mimba yawo, ana awo athanzi?+

Kapena kodi wansembe ndi mneneri aziphedwa m’malo opatulika a Yehova?+

ש [Shin]

21 Anyamata ndi amuna okalamba+ agona pansi m’misewu.+

Anamwali anga ndi anyamata anga aphedwa ndi lupanga.+

Mwapha anthu pa tsiku la mkwiyo+ wanu. Onsewo mwawaphadi+ mopanda chisoni.+

ת [Taw]

22 Munaitana+ anthu kuchokera kumalo onse ozungulira, kumene akukhala monga alendo.

Pa tsiku la mkwiyo wa Yehova panalibe wothawa kapena wopulumuka.+

Ana onse athanzi amene ndinabereka ndi kuwalera, mdani wanga anawapha.+

א [ʼAʹleph]

3 Ine ndine mwamuna wamphamvu amene ndaona masautso+ chifukwa cha ndodo ya ukali wa Mulungu.

 2 Iye wanditsogolera ndi kundiyendetsa m’malo amdima, osati m’malo owala.+

 3 Ndithudi, iye amandimenya ndi dzanja lake mobwerezabwereza tsiku lonse.+

ב [Behth]

 4 Wafooketsa thupi langa ndipo wachititsa khungu langa kunyala.+ Iye waphwanyanso mafupa anga.+

 5 Wandimangira mpanda+ kuti chomera chakupha+ ndi mavuto zindizungulire.

 6 Wandichititsa kukhala m’malo amdima,+ ngati munthu woti anafa kalekale.+

ג [Giʹmel]

 7 Wanditsekereza ngati mmene mpanda wamiyala umatsekerezera, kuti ndisatuluke.+ Wandimanga ndi maunyolo olemera amkuwa.+

 8 Komanso ndikalira ndi kupempha thandizo mofuula, iye amatsekereza pemphero+ langa.

 9 Watsekereza njira zanga ndi miyala yosema.+ Wachititsa njira zanga kukhala zovuta kuyendamo.+

ד [Daʹleth]

10 Kwa ine, iye ali ngati chimbalangondo chimene chandibisalira,+ ndiponso ngati mkango umene wakhala pamalo obisika.+

11 Wasokoneza njira zanga ndipo wandichititsa kukhala wopanda chochita. Wandichititsanso kukhala wosiyidwa.+

12 Wakunga uta wake+ ndipo wandisandutsa chinthu cholasapo mivi+ yake.

ה [Heʼ]

13 Walasa impso zanga ndi mivi yotuluka m’kachikwama kake.+

14 Ndakhala chinthu choseketsa+ kwa anthu onse odana nane, ndipo amandiimba m’nyimbo yawo tsiku lonse.+

15 Wandipatsa zinthu zowawa zokwanira.+ Wandikhutitsa chitsamba chowawa.+

ו [Waw]

16 Wachititsa kuti mano anga aguluke ndi miyala.+ Wandipondaponda m’phulusa.+

17 Inu mwanditayira kutali, moti sindilinso pa mtendere. Sindikukumbukiranso zinthu zabwino.+

18 Nthawi zonse ndikunena kuti: “Ulemerero wanga ndi chiyembekezo changa mwa Yehova zatha.”+

ז [Zaʹyin]

19 Kumbukirani kuti ndine wosautsika ndi wosowa pokhala.+ Kumbukiraninso kuti ndimadya chitsamba chowawa ndi chomera chakupha.+

20 Ndithu mudzandikumbukira ndi kundiweramira kuti mundithandize.+

21 Ndidzakumbukira zimenezi mumtima mwanga.+ Pa chifukwa chimenechi, ndidzakhala ndi mtima wodikira.+

ח [Chehth]

22 Chifukwa cha kukoma mtima kosatha+ kwa Yehova, ife sitinafafanizidwe,+ ndipo chifundo chake sichidzatha.+

23 Chifundocho chimakhala chatsopano m’mawa uliwonse,+ pakuti inu ndinu wokhulupirika kwambiri.+

24 Ine ndanena kuti: “Yehova ndiye cholowa changa.+ Pa chifukwa chimenechi, ndidzakhala ndi mtima womudikira.”+

ט [Tehth]

25 Yehova ndi wabwino kwa munthu amene akumuyembekezera,+ kwa munthu amene akumufunafuna.+

26 Ndi bwino kuti munthu ayembekezere+ chipulumutso cha Yehova+ moleza mtima.+

27 Ndi bwino kuti mwamuna wamphamvu anyamule goli ali mnyamata.+

י [Yohdh]

28 Iye akhale payekha ndipo akhale chete,+ chifukwa Mulungu walola kuti zimenezi zimuchitikire.+

29 Iye awerame mpaka pakamwa pake pafike padothi.+ Mwina angakhale ndi chiyembekezo.+

30 Aperekere tsaya lake kwa munthu amene akumumenya.+ Alandire chitonzo chokwanira.+

כ [Kaph]

31 Pakuti Yehova sadzatitaya mpaka kalekale.*+

32 Ngakhale kuti watichititsa kumva chisoni,+ ndithu adzatichitira chifundo chifukwa kukoma mtima kwake kosatha n’kwakukulu.+

33 Pakuti iye sasangalala ndi kusautsa anthu kapena kuwamvetsa chisoni.+

ל [Laʹmedh]

34 Pajatu kupondaponda+ akaidi onse a padziko lapansi,+

35 Kukankhira pambali chilungamo cha mwamuna wamphamvu pamaso pa Wam’mwambamwamba,+

36 Ndi kupotoza chiweruzo cha munthu pa mlandu wake, Yehova savomereza zimenezi.+

מ [Mem]

37 Tsopano ndani ananenapo kuti chinthu chichitike, chinthucho n’kuchitikadi Yehova asanalamule?+

38 Zinthu zoipa ndi zabwino sizitulukira limodzi pakamwa pa Wam’mwambamwamba.+

39 Kodi munthu angadandaulirenji+ chifukwa cha zotsatirapo za tchimo lake?+

נ [Nun]

40 Tiyeni tifufuze njira zathu kuti tizidziwe,+ ndipo tibwerere kwa Yehova.+

41 Tiyeni tichonderere Mulungu kumwamba ndi mtima wonse, ndipo tikweze manja athu m’mwamba+ ndi kunena kuti:

42 “Ife taphwanya malamulo. Tachita zinthu zopanduka+ ndipo inu simunatikhululukire.+

ס [Saʹmekh]

43 Mwadzitchinga ndi mkwiyo wanu kuti tisakufikireni+ ndipo mukupitiriza kutithamangitsa.+ Mwapha anthu mopanda chisoni.+

44 Mwadzitchinga ndi mtambo waukulu+ kuti pemphero lisadutse ndi kufika kwa inu.+

45 Mwatisandutsa nyansi ndi zinyalala pakati pa anthu a mitundu ina.”+

פ [Peʼ]

46 Pakamwa pa adani athu onse pakutinenera zoipa.+

47 Ife tagwidwa ndi mantha ndipo tikusowa chochita.+ Tasiyidwa ndipo tawonongedwa.+

48 Maso anga akungotuluka misozi ngati mtsinje chifukwa cha kuwonongedwa kwa mwana wamkazi wa anthu anga.+

ע [ʽAʹyin]

49 Maso anga akungotuluka misozi mosalekeza,+

50 Kufikira Yehova atayang’ana pansi ndi kutiona ali kumwamba.+

51 Mtima wanga ukusautsika ndi zimene maso anga aona,+ zimene zachitikira ana onse aakazi a mzinda wanga.*+

צ [Tsa·dhehʹ]

52 Adani anga akundisaka ngati mbalame+ popanda chifukwa.+

53 Anali kufuna kuchotsa moyo wanga kuti andiponye m’dzenje+ ndipo anali kundiponya miyala.

54 Madzi asefukira ndi kumiza mutu wanga,+ moti ndanena kuti: “Ndifa basi!”+

ק [Qohph]

55 Inu Yehova, ndaitana dzina lanu mofuula ndili m’dzenje lakuya kwambiri.+

56 Mumve mawu anga.+ Musatseke khutu lanu pamene ndikupempha mpumulo ndiponso pamene ndikulirira thandizo.+

57 Pa tsiku limene ndinakuitanani,+ munandiyandikira ndi kundiuza kuti: “Usaope.”+

ר [Rehsh]

58 Inu Yehova, mwandiweruzira milandu yanga.+ Mwawombola moyo wanga.+

59 Inu Yehova, mwaona zoipa zimene andichitira.+ Chonde, ndiweruzireni mlandu wanga.+

60 Mwaona mtima wawo wokonda kubwezera ndiponso ziwembu zawo zonse zimene andikonzera.+

ש [Sin] kapena [Shin]

61 Inu Yehova, mwamva mawu awo otonza ndipo mwaona ziwembu zawo zonse zimene andikonzera.+

62 Mwamva mawu ochokera pakamwa pa anthu amene akundiukira.+ Mwamvanso zoipa zimene akundinenera monong’ona tsiku lonse.+

63 Onani zochita zawo zonse.+ Iwo akundiimba m’nyimbo yawo.+

ת [Taw]

64 Inu Yehova, mudzawabwezera mogwirizana ndi ntchito za manja awo.+

65 Mudzaumitsa mtima wawo,+ ndipo kuchita zimenezi n’kuwatemberera.+

66 Inu Yehova, mudzawakwiyira ndi kuwathamangitsa ndipo mudzawafafaniza+ padziko lanu lapansi.+

א [ʼAʹleph]

4 Golide amene anali kuwala, golide wabwino, sakuwalanso.+

Miyala yopatulika*+ aikhuthulira m’misewu yonse.+

ב [Behth]

 2 Ana okondedwa a Ziyoni+ amene anali amtengo wapatali ngati golide woyengeka bwino,

Tsopano ayamba kuonedwa ngati mitsuko ikuluikulu yadothi, ntchito ya manja a munthu woumba mbiya.+

ג [Giʹmel]

 3 Ngakhale mimbulu imapereka bere kwa ana ake kuti ayamwe.

Koma mwana wamkazi wa anthu anga wakhala wankhanza+ ngati nthiwatiwa m’chipululu.+

ד [Daʹleth]

 4 Lilime la ana oyamwa lamamatira kummero chifukwa cha ludzu.+

Ana apempha chakudya+ koma palibe amene akuwapatsa.+

ה [Heʼ]

 5 Anthu amene anali kudya zinthu zabwino adzidzimuka ndipo agwidwa ndi mantha m’misewu.+

Anthu amene akula akuvala zovala zamtengo wapatali*+ agona pamilu ya phulusa.+

ו [Waw]

 6 Chilango chimene mwana wamkazi wa anthu anga walandira chifukwa cha zolakwa zake, n’chachikulu kuposa chimene mzinda wa Sodomu unalandira chifukwa cha machimo ake.+

Mzinda umenewu unawonongedwa mwadzidzidzi m’kanthawi kochepa, ndipo palibe dzanja limene linauthandiza.+

ז [Zaʹyin]

 7 Anaziri+ ake anali oyera kuposa chipale chofewa.+ Analinso oyera kuposa mkaka.

Ndipotu anali ofiira+ kuposa miyala yamtengo wapatali ya korali. Analinso osalala ngati mwala wa safiro.+

ח [Chehth]

 8 Tsopano ayamba kuoneka akuda kuposa makala. Anthu sakuwazindikiranso mumsewu.+

Khungu lawo lafota moti lamamatira kumafupa awo.+ Langoti gwaa ngati mtengo.

ט [Tehth]

 9 Amene anaphedwa ndi lupanga+ aliko bwino kusiyana ndi amene anafa ndi njala,+

Pakuti amene anafa ndi njala anafooka chifukwa chosowa chakudya, ndipo anakhala ngati apyozedwa ndi lupanga.

י [Yohdh]

10 Ngakhale amayi, amene amakhala achifundo, afika pophika ana awo ndi manja awo.+

Anawo akhala ngati chakudya chotonthoza anthu pa nthawi ya kuwonongedwa kwa mwana wamkazi wa anthu anga.+

כ [Kaph]

11 Yehova wasonyeza ukali wake wonse.+ Wakhuthula mkwiyo wake woyaka moto.+

Iye wayatsa moto m’Ziyoni, umene wanyeketsa maziko ake.+

ל [Laʹmedh]

12 Mafumu a padziko lapansi ndiponso anthu onse okhala panthaka ya dziko lapansi,+

Sanayembekezere kuti mdani angadzalowe pazipata za Yerusalemu.+

מ [Mem]

13 Zimenezi zinachitika chifukwa cha machimo a aneneri ake ndi zolakwa za ansembe ake,+

Amene anakhetsa magazi a anthu olungama a mumzindawo.+

נ [Nun]

14 Ansembe ndi aneneriwo akungoyendayenda mumsewu ngati anthu akhungu.+ Aipitsidwa ndi magazi,+

Moti palibe amene akukhudza zovala zawo.+

ס [Saʹmekh]

15 Anthu akuwafuulira kuti: “Chokani! Ndinu odetsedwa!+ Chokani! Chokani! Musatikhudze!”+

Ansembe ndi aneneriwo alibe pokhala+ ndipo akungoyendayenda.+ Anthu a mitundu ina akunena kuti: “Amenewa sapitiriza kukhala kuno.+

פ [Peʼ]

16 Yehova wawabalalitsa+ ndipo sadzawayang’ananso.+

Anthu sadzaganiziranso ansembe.+ Sadzachitiranso chifundo amuna okalamba.”+

ע [ʽAʹyin]

17 Pamene tili ndi moyo, maso athu akulefuka chifukwa choyembekezera thandizo lomwe silikubwera.+

Pofunafuna thandizo, tadalira mtundu wa anthu amene sangabweretse chipulumutso.+

צ [Tsa·dhehʹ]

18 Akutisakasaka kulikonse kumene tikupita,+ moti palibe amene akuyenda m’mabwalo a mizinda yathu.

Mapeto athu ayandikira. Masiku athu akwanira, pakuti mapeto athu afika.+

ק [Qohph]

19 Otithamangitsawo ndi aliwiro kuposa ziwombankhanga zouluka m’mwamba.+

Iwo atithamangitsa pamapiri.+ Atibisalira m’chipululu.+

ר [Rehsh]

20 Wodzozedwa wa Yehova,+ amene ndi mpweya wotuluka mphuno mwathu,+ wagwidwa m’dzenje lawo lalikulu.+

Ponena za ameneyu, ife tinati: “Tidzakhala mumthunzi wake+ pakati pa mitundu ya anthu.”+

ש [Sin]

21 Kondwa ndipo usangalale,+ iwe mwana wamkazi wa Edomu,+ amene ukukhala m’dziko la Uzi.+

Iwenso kapuyo ikupeza.+ Udzaledzera ndipo anthu adzakuona uli maliseche.+

ת [Taw]

22 Iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, chilango chimene anakupatsa chifukwa cha zolakwa zako chatha.+ Sadzakutenganso kupita nawe ku ukapolo.+

Tsopano iwe mwana wamkazi wa Edomu, Mulungu watembenukira kwa iwe kuti aone zolakwa zako. Machimo ako wawaika poyera.+

5 Inu Yehova, kumbukirani zimene zatichitikira.+ Tiyang’aneni kuti muone chitonzo chathu.+

 2 Cholowa chathu chaperekedwa kwa anthu achilendo. Nyumba zathu zaperekedwa kwa alendo.+

 3 Ife takhala anthu amasiye opanda bambo.+ Amayi athu akhala ngati akazi amasiye.+

 4 Madzi akumwa ndi nkhuni, tikuchita kugula.+

 5 Akutithamangitsa ndipo atsala pang’ono kutigwira.+ Tatopa ndipo tikusowa mpumulo.+

 6 Kuti tipeze chakudya chokwanira, tikudalira Iguputo+ ndi Asuri.+

 7 Makolo athu ndi amene anachimwa.+ Iwo anafa, koma ifeyo ndi amene tikuvutika ndi zolakwa zawozo.+

 8 Antchito wamba ndi amene akutilamulira.+ Palibe amene akutilanditsa m’manja mwawo.+

 9 Kuti tipeze chakudya, timaika moyo wathu pachiswe+ chifukwa cha anthu amene ali ndi malupanga m’chipululu.

10 Khungu lathu latentha kwambiri ngati ng’anjo, chifukwa cha njala yaikulu.+

11 Achitira zachipongwe+ akazi athu amene ali m’Ziyoni ndi anamwali amene ali m’mizinda ya Yuda.

12 Akalonga athu awapachika dzanja limodzi lokha.+ Anthuwo sanalemekezenso ngakhale amuna okalamba.+

13 Anyamata awanyamulitsa mphero,+ ndipo tianyamata tadzandira polemedwa ndi mitolo ya nkhuni.+

14 Pazipata sipakupezekanso amuna achikulire+ ndipo anyamata sakuimbanso nyimbo ndi zipangizo zawo zoimbira.+

15 Chisangalalo cha mumtima mwathu chatha. Kuvina kwathu kwasanduka kulira maliro.+

16 Chisoti chathu chachifumu chagwa.+ Tsoka kwa ife chifukwa tachimwa!+

17 Pa chifukwa chimenechi, mtima wathu wadwala.+ Chifukwa cha zinthu zimenezi, maso athu achita mdima.+

18 Nkhandwe zayamba kuyendayenda paphiri la Ziyoni chifukwa lasanduka bwinja.+

19 Koma inu Yehova mudzakhala pampando wanu wachifumu mpaka kalekale.+ Mpando wanu wachifumuwo udzakhalapo ku mibadwomibadwo.+

20 N’chifukwa chiyani mwatiiwala kwamuyaya+ ndi kutisiya kwa masiku ambiri?+

21 Inu Yehova, tibwezeni+ kwa inu ndipo ife tibwerera mwamsanga. Mubwezeretse zinthu zonse kuti zikhale ngati mmene zinalili kale.+

22 Koma inu mwatikanitsitsa.+ Mwatikwiyira kwambiri.+

Onani Matanthauzo a Mawu Ena.

Kapena kuti “wowathamangitsa.”

Onani mawu a m’munsi pa 1Sa 2:1.

Ena amati “khumbi,” kapena “chitala.”

Ena amati “zipupa,” kapena “zikupa.”

Ena amati “masaka.”

Onani Matanthauzo a Mawu Ena.

Kapena kuti “midzi yozungulira.”

Kapena kuti “miyala ya pamalo opatulika.”

Mawu ake enieni, “zovala zofiira,” kutanthauza zovala zofiira zamtengo wapatali.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena