Maliro
א [ʼAʹleph]
1 Amene anali ndi anthu ambiri+ tsopano wakhala wopanda anthu.+
Amene anali ndi anthu ambiri pakati pa mitundu ina+ wakhala ngati mkazi wamasiye.+
Amene anali wolemekezeka pakati pa zigawo zina wayamba kugwira ntchito yaukapolo.+
ב [Behth]
2 Iye akulira kwambiri usiku,+ ndipo misozi ikutsika pamasaya ake.+
Pakati pa onse amene anali kumukonda, palibe amene akumutonthoza.+
Anthu onse amene anali anzake amuchitira zachinyengo+ ndipo akhala adani ake.+
ג [Giʹmel]
3 Yuda wakhala kapolo chifukwa cha nsautso+ ndiponso chifukwa cha kukula kwa ntchito yaukapolo imene akugwira.+
Iye wakhala pakati pa mitundu ina ya anthu,+ ndipo sanapeze malo ampumulo.
Onse amene anali kumuzunza amupeza pa nthawi ya mavuto ake.+
ד [Daʹleth]
4 Njira zopita ku Ziyoni zikulira, chifukwa palibe amene akupita kuchikondwerero.+
Zipata zake zonse zasiyidwa.+ Ansembe+ ake akuusa moyo.*
Anamwali ake agwidwa ndi chisoni,+ ndipo iyeyo akumva kuwawa mumtima.
ה [Heʼ]
5 Adani ake akumulamulira.+ Anthu odana naye sakuda nkhawa.+
Yehova wamuchititsa kukhala wachisoni chifukwa cha kuchuluka kwa machimo+ ake,
Ndipo ana ake ayenda patsogolo pa adani awo atagwidwa ukapolo.+
ו [Waw]
6 Ulemerero+ wonse wamuchokera mwana wamkazi wa Ziyoni.
Akalonga ake akhala ngati mbawala zamphongo zimene zikusowa msipu.+
ז [Zaʹyin]
7 Yerusalemu anakumbukira zinthu zake zonse zabwino+ zimene anali nazo kuyambira kalekale.
Anazikumbukira m’masiku a masautso ake ndi a anthu ake osowa pokhala.
Anthu ake atagwidwa ndi adani, pamene iye analibe munthu womuthandiza,+
Adani akewo anamuona, ndipo anamuseka+ chifukwa chakuti wagwa.
ח [Chehth]
8 Yerusalemu wachita tchimo+ lalikulu. N’chifukwa chake wakhala chinthu chonyansa.+
Onse amene anali kumulemekeza ayamba kumuona ngati chinthu chachabechabe,+ chifukwa aona maliseche+ ake.
Iyenso akuusa moyo+ ndipo watembenukira kwina chifukwa cha manyazi.
ט [Tehth]
9 Zovala+ zake ndi zodetsedwa. Iye sanaganizire za tsogolo+ lake.
Wagwa modabwitsa ndipo alibe womutonthoza.+
Inu Yehova, onani kusautsika+ kwanga, pakuti mdani wanga akudzitukumula.+
י [Yohdh]
10 Mdani watambasula dzanja lake n’kutenga zinthu+ zake zonse zabwino.
Yerusalemu waona mitundu ina itabwera ndi kulowa m’malo ake opatulika,+
Mitundu imene munalamula kuti isalowe mumpingo wanu.
כ [Kaph]
11 Anthu ake onse akuusa moyo. Iwo akufunafuna chakudya.+
Asinthanitsa zinthu zawo zabwino ndi chakudya kuti adzitsitsimutse.+
Inu Yehova ndiyang’aneni. Onani kuti ndakhala ngati mkazi wachabechabe.+
ל [Laʹmedh]
12 Inu nonse amene mukudutsa m’njira, kodi mukuona ngati imeneyi ndi nkhani yaing’ono? Ndiyang’aneni kuti muone.+
Kodi palinso ululu wina woposa ululu umene ineyo ndalangidwa nawo,+
Ululu umene Yehova wandibweretsera nawo chisoni m’tsiku la mkwiyo+ wake woyaka moto?
מ [Mem]
13 Iye watumiza moto m’mafupa+ mwanga kuchokera kumwamba, ndipo wafooketsa fupa lililonse.
Watchera ukonde+ kuti ukole mapazi anga. Wandibweza kumbuyo.
Wandisandutsa mkazi wosiyidwa popanda thandizo. Ndikudwala tsiku lonse.+
נ [Nun]
14 Iye wakhala tcheru kuti aone machimo+ anga. Machimowo alukanalukana m’dzanja lake.
Amangidwa m’khosi+ mwanga, moti mphamvu zanga zatha.
Yehova wandipereka m’manja mwa anthu amene sindingathe kulimbana nawo.+
ס [Saʹmekh]
15 Yehova wandichotsera anthu anga onse amphamvu+ ndi kuwakankhira pambali.
Wandiitanitsira msonkhano kuti athyolethyole anyamata anga.+
Yehova wapondaponda moponderamo mphesa+ mwa namwali, mwana wamkazi wa Yuda.+
ע [ʽAʹyin]
16 Ndikulirira zinthu zimenezi ngati mkazi.+ Maso anga ine! Maso anga akutuluka misozi.+
Pakuti wonditonthoza, munthu woti anditsitsimule, ali kutali ndi ine.
Ana anga asiyidwa+ popanda thandizo, pakuti mdani wanga wadzitukumula.+
פ [Peʼ]
17 Ziyoni watambasula manja ake.+ Iye alibe womutonthoza.+
Yehova walamula onse ozungulira Yakobo kuti akhale adani ake.+
Yerusalemu wakhala chinthu chonyansa pakati pawo.+
צ [Tsa·dhehʹ]
18 Yehova ndi wolungama,+ koma ine ndapandukira+ mawu a pakamwa pake.
Anthu nonsenu, tamverani mawu anga, ndipo muone ululu umene ndikumva.
Anamwali anga ndi anyamata anga atengedwa kupita ku ukapolo.+
ק [Qohph]
19 Ndaitana anthu ondikonda kwambiri,+ koma anthuwo andichitira zachinyengo.
Ansembe anga ndiponso akuluakulu atha+ mumzinda.
Atha pamene anali kufunafuna chakudya choti adye kuti adzitsitsimutse.+
ר [Rehsh]
20 Taonani, inu Yehova. Inetu zandivuta. M’mimba mwanga mukubwadamuka.+
ש [Shin]
21 Anthu amva mmene ndikuusira moyo ngati mkazi,+ koma palibe wonditonthoza.+
Adani anga onse amva za tsoka+ langa. Iwo akondwera,+ chifukwa ndinu mwachititsa zimenezi.
Inu mubweretsadi tsiku limene mwanena,+ kuti iwo akhale ngati ine.+
ת [Taw]
22 Kuipa kwawo konse kuonekere pamaso panu, ndipo muwalange+ koopsa.
Muwalange koopsa monga mmene mwandilangira ine chifukwa cha machimo+ anga onse.
א [ʼAʹleph]
2 Chifukwa chokwiya, Yehova waphimba mwana wamkazi wa Ziyoni ndi mtambo+ wakuda.
Iye waponya pansi chokongoletsera+ Isiraeli kuchokera kumwamba.+
Sanakumbukire chopondapo mapazi+ ake pa tsiku la mkwiyo wake.
ב [Behth]
2 Yehova wameza malo okhala a Yakobo. Sanamvere chisoni malo ake alionse.+
Mu ukali wake, iye wagwetsa mipanda yolimba kwambiri+ ya mwana wamkazi wa Yuda.
Waipitsa ufumu+ ndi akalonga+ ake ndipo wawagwetsera pansi.+
ג [Giʹmel]
3 Mu mkwiyo wake wathyola nyanga* iliyonse ya Isiraeli.+
Adani athu atatiukira, iye sanatithandize.+
Mkwiyo wake ukuyakirabe Yakobo ngati moto umene wawononga ponseponse.+
ד [Daʹleth]
4 Wakunga uta wake ngati mdani.+ Dzanja lake lamanja+ lakonzeka ngati la mdani,+
Ndipo wapitiriza kupha+ anthu onse ofunika kwambiri.
Ukali wake waukhuthula ngati moto+ m’hema+ wa mwana wamkazi wa Ziyoni.
ה [Heʼ]
5 Yehova wakhala ngati mdani.+ Wameza Isiraeli.+
Iye wameza nsanja zonse za Isiraeli zokhalamo.+ Wawononga malo ake otetezedwa ndiponso mipanda yolimba kwambiri.+
Wachititsa kuti kulira ndi maliro+ zimveke mumzinda wa mwana wamkazi wa Yuda.
ו [Waw]
6 Iye wapasula chisimba*+ chake ngati chisimba cha m’munda+ ndipo wathetsa zikondwerero zake.
Yehova wachititsa kuti zikondwerero+ ndi sabata ziiwalike mu Ziyoni,
Ndipo mu mkwiyo wake waukulu wakana mfumu ndi wansembe.+
ז [Zaʹyin]
7 Yehova wataya guwa lake lansembe.+ Iye wanyoza malo ake opatulika.+
Wapereka m’manja mwa adani makoma* a nsanja zake zokhalamo.+
Iwo afuula m’nyumba ya Yehova ngati pa tsiku lachikondwerero.+
ח [Chehth]
8 Yehova waganiza zogwetsa mpanda+ wa mwana wamkazi wa Ziyoni.
Watambasula chingwe choyezera.+ Sanabweze dzanja lake kuti lisabweretse chiwonongeko.+
Walilitsa+ chiunda chomenyerapo nkhondo ndi mpanda. Zonsezi zatha mphamvu.
ט [Tehth]
9 Zipata+ zake zamira munthaka. Wawononga mipiringidzo yake ndipo waithyolathyola.
Mfumu yake ndi akalonga ake ali pakati pa mitundu ina.+ Malamulo sakutsatiridwa.+
Aneneri ake sakuonanso masomphenya ochokera kwa Yehova.+
י [Yohdh]
10 Akuluakulu a mwana wamkazi wa Ziyoni akhala pansi ndipo akhala chete.+
Iwo athira fumbi pamitu+ yawo ndipo avala ziguduli.*+
Anamwali a Yerusalemu aweramitsa mitu yawo mpaka padothi.+
כ [Kaph]
11 Maso anga atopa ndi kulira.+ M’mimba mwanga mukubwadamuka.+
Chiwindi changa chakhuthulidwa+ pansi chifukwa cha kuwonongedwa kwa mwana wamkazi wa anthu anga,+
Ndiponso chifukwa chakuti ana ndi makanda oyamwa akukomoka+ m’mabwalo a mzinda.
ל [Laʹmedh]
12 Iwo anali kufunsa amayi awo kuti: “Kodi chakudya ndi vinyo zili kuti?”+
Anali kufunsa chifukwa anali kukomoka m’mabwalo a mzinda ndi kugona pansi ngati anthu ophedwa,
Ndiponso chifukwa moyo wawo unali kukhuthukira pachifuwa cha amayi awo.
מ [Mem]
13 Kodi ndikusonyeze umboni wotani? Kodi ndingakuyerekezere ndi chiyani, iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu?+
Kodi ndikufananitse ndi chiyani kuti ndikutonthoze, namwali iwe, mwana wamkazi wa Ziyoni?+
Pakuti kuwonongeka+ kwako kwafalikira ngati kukula kwa nyanja. Ndani angakuchiritse?+
נ [Nun]
14 Aneneri ako aona masomphenya achabechabe ndi opanda pake+ onena za iwe.
Iwo sanaulule zolakwa zako kuti akuteteze n’cholinga choti usatengedwe kupita ku ukapolo,+
Koma anali kuona masomphenya achabechabe ndi osocheretsa+ onena za iwe.
ס [Saʹmekh]
15 Anthu onse odutsa mumsewu akakuona, akuwomba m’manja+ monyodola.
Akuimba mluzu+ ndi kupukusa mitu+ yawo poona mwana wamkazi wa Yerusalemu. Iwo akunena kuti:
“Kodi uwu ndi mzinda umene anali kunena kuti, ‘Ndi wokongola kwambiri, wotamandika padziko lonse lapansi’?”+
פ [Peʼ]
16 Adani ako onse akukutsegulira pakamwa.+
Akuimba mluzu ndi kukukukutira mano.+ Iwo akunena kuti: “Ameneyu timumeza.+
Ndithu, lero ndi tsiku limene takhala tikuyembekezera.+ Lafikadi! Taliona!”+
ע [ʽAʹyin]
17 Yehova wachita zimene anali kuganiza.+ Wakwaniritsa zimene ananena,+
Zimene analamula kalekale.+ Wapasula zinthu ndipo sanamve chisoni.+
Wachititsa adani ako kusangalala+ chifukwa cha zimene zakuchitikira. Wakweza nyanga ya adani+ ako.
צ [Tsa·dhehʹ]
18 Mtima wa anthuwo wafuulira Yehova,+ iwe mpanda wa mwana wamkazi wa Ziyoni.+
Gwetsa misozi ngati mtsinje usana ndi usiku.+
Usapume. Mwana wa diso lako asaleke kulira.
ק [Qohph]
19 Nyamuka! Lira mofuula usiku, pa nthawi yoyamba ulonda+ wam’mawa.
Khuthula+ mtima wako pamaso+ pa Yehova ngati madzi.
Pemphera utakweza manja+ ako kwa iye chifukwa cha ana ako,
Amene akukomoka ndi njala m’misewu.+
ר [Rehsh]
20 Inu Yehova, yang’anani kuti muone+ yemwe mwamulanga chotere.
Kodi amayi azidya zipatso za mimba yawo, ana awo athanzi?+
Kapena kodi wansembe ndi mneneri aziphedwa m’malo opatulika a Yehova?+
ש [Shin]
21 Anyamata ndi amuna okalamba+ agona pansi m’misewu.+
Anamwali anga ndi anyamata anga aphedwa ndi lupanga.+
Mwapha anthu pa tsiku la mkwiyo+ wanu. Onsewo mwawaphadi+ mopanda chisoni.+
ת [Taw]
22 Munaitana+ anthu kuchokera kumalo onse ozungulira, kumene akukhala monga alendo.
Pa tsiku la mkwiyo wa Yehova panalibe wothawa kapena wopulumuka.+
Ana onse athanzi amene ndinabereka ndi kuwalera, mdani wanga anawapha.+
א [ʼAʹleph]
3 Ine ndine mwamuna wamphamvu amene ndaona masautso+ chifukwa cha ndodo ya ukali wa Mulungu.
2 Iye wanditsogolera ndi kundiyendetsa m’malo amdima, osati m’malo owala.+
3 Ndithudi, iye amandimenya ndi dzanja lake mobwerezabwereza tsiku lonse.+
ב [Behth]
4 Wafooketsa thupi langa ndipo wachititsa khungu langa kunyala.+ Iye waphwanyanso mafupa anga.+
5 Wandimangira mpanda+ kuti chomera chakupha+ ndi mavuto zindizungulire.
6 Wandichititsa kukhala m’malo amdima,+ ngati munthu woti anafa kalekale.+
ג [Giʹmel]
7 Wanditsekereza ngati mmene mpanda wamiyala umatsekerezera, kuti ndisatuluke.+ Wandimanga ndi maunyolo olemera amkuwa.+
8 Komanso ndikalira ndi kupempha thandizo mofuula, iye amatsekereza pemphero+ langa.
9 Watsekereza njira zanga ndi miyala yosema.+ Wachititsa njira zanga kukhala zovuta kuyendamo.+
ד [Daʹleth]
10 Kwa ine, iye ali ngati chimbalangondo chimene chandibisalira,+ ndiponso ngati mkango umene wakhala pamalo obisika.+
11 Wasokoneza njira zanga ndipo wandichititsa kukhala wopanda chochita. Wandichititsanso kukhala wosiyidwa.+
12 Wakunga uta wake+ ndipo wandisandutsa chinthu cholasapo mivi+ yake.
ה [Heʼ]
13 Walasa impso zanga ndi mivi yotuluka m’kachikwama kake.+
14 Ndakhala chinthu choseketsa+ kwa anthu onse odana nane, ndipo amandiimba m’nyimbo yawo tsiku lonse.+
15 Wandipatsa zinthu zowawa zokwanira.+ Wandikhutitsa chitsamba chowawa.+
ו [Waw]
16 Wachititsa kuti mano anga aguluke ndi miyala.+ Wandipondaponda m’phulusa.+
17 Inu mwanditayira kutali, moti sindilinso pa mtendere. Sindikukumbukiranso zinthu zabwino.+
18 Nthawi zonse ndikunena kuti: “Ulemerero wanga ndi chiyembekezo changa mwa Yehova zatha.”+
ז [Zaʹyin]
19 Kumbukirani kuti ndine wosautsika ndi wosowa pokhala.+ Kumbukiraninso kuti ndimadya chitsamba chowawa ndi chomera chakupha.+
20 Ndithu mudzandikumbukira ndi kundiweramira kuti mundithandize.+
21 Ndidzakumbukira zimenezi mumtima mwanga.+ Pa chifukwa chimenechi, ndidzakhala ndi mtima wodikira.+
ח [Chehth]
22 Chifukwa cha kukoma mtima kosatha+ kwa Yehova, ife sitinafafanizidwe,+ ndipo chifundo chake sichidzatha.+
23 Chifundocho chimakhala chatsopano m’mawa uliwonse,+ pakuti inu ndinu wokhulupirika kwambiri.+
24 Ine ndanena kuti: “Yehova ndiye cholowa changa.+ Pa chifukwa chimenechi, ndidzakhala ndi mtima womudikira.”+
ט [Tehth]
25 Yehova ndi wabwino kwa munthu amene akumuyembekezera,+ kwa munthu amene akumufunafuna.+
26 Ndi bwino kuti munthu ayembekezere+ chipulumutso cha Yehova+ moleza mtima.+
27 Ndi bwino kuti mwamuna wamphamvu anyamule goli ali mnyamata.+
י [Yohdh]
28 Iye akhale payekha ndipo akhale chete,+ chifukwa Mulungu walola kuti zimenezi zimuchitikire.+
29 Iye awerame mpaka pakamwa pake pafike padothi.+ Mwina angakhale ndi chiyembekezo.+
30 Aperekere tsaya lake kwa munthu amene akumumenya.+ Alandire chitonzo chokwanira.+
כ [Kaph]
31 Pakuti Yehova sadzatitaya mpaka kalekale.*+
32 Ngakhale kuti watichititsa kumva chisoni,+ ndithu adzatichitira chifundo chifukwa kukoma mtima kwake kosatha n’kwakukulu.+
33 Pakuti iye sasangalala ndi kusautsa anthu kapena kuwamvetsa chisoni.+
ל [Laʹmedh]
34 Pajatu kupondaponda+ akaidi onse a padziko lapansi,+
35 Kukankhira pambali chilungamo cha mwamuna wamphamvu pamaso pa Wam’mwambamwamba,+
36 Ndi kupotoza chiweruzo cha munthu pa mlandu wake, Yehova savomereza zimenezi.+
מ [Mem]
37 Tsopano ndani ananenapo kuti chinthu chichitike, chinthucho n’kuchitikadi Yehova asanalamule?+
38 Zinthu zoipa ndi zabwino sizitulukira limodzi pakamwa pa Wam’mwambamwamba.+
39 Kodi munthu angadandaulirenji+ chifukwa cha zotsatirapo za tchimo lake?+
נ [Nun]
40 Tiyeni tifufuze njira zathu kuti tizidziwe,+ ndipo tibwerere kwa Yehova.+
41 Tiyeni tichonderere Mulungu kumwamba ndi mtima wonse, ndipo tikweze manja athu m’mwamba+ ndi kunena kuti:
42 “Ife taphwanya malamulo. Tachita zinthu zopanduka+ ndipo inu simunatikhululukire.+
ס [Saʹmekh]
43 Mwadzitchinga ndi mkwiyo wanu kuti tisakufikireni+ ndipo mukupitiriza kutithamangitsa.+ Mwapha anthu mopanda chisoni.+
44 Mwadzitchinga ndi mtambo waukulu+ kuti pemphero lisadutse ndi kufika kwa inu.+
45 Mwatisandutsa nyansi ndi zinyalala pakati pa anthu a mitundu ina.”+
פ [Peʼ]
46 Pakamwa pa adani athu onse pakutinenera zoipa.+
47 Ife tagwidwa ndi mantha ndipo tikusowa chochita.+ Tasiyidwa ndipo tawonongedwa.+
48 Maso anga akungotuluka misozi ngati mtsinje chifukwa cha kuwonongedwa kwa mwana wamkazi wa anthu anga.+
ע [ʽAʹyin]
49 Maso anga akungotuluka misozi mosalekeza,+
50 Kufikira Yehova atayang’ana pansi ndi kutiona ali kumwamba.+
51 Mtima wanga ukusautsika ndi zimene maso anga aona,+ zimene zachitikira ana onse aakazi a mzinda wanga.*+
צ [Tsa·dhehʹ]
52 Adani anga akundisaka ngati mbalame+ popanda chifukwa.+
53 Anali kufuna kuchotsa moyo wanga kuti andiponye m’dzenje+ ndipo anali kundiponya miyala.
54 Madzi asefukira ndi kumiza mutu wanga,+ moti ndanena kuti: “Ndifa basi!”+
ק [Qohph]
55 Inu Yehova, ndaitana dzina lanu mofuula ndili m’dzenje lakuya kwambiri.+
56 Mumve mawu anga.+ Musatseke khutu lanu pamene ndikupempha mpumulo ndiponso pamene ndikulirira thandizo.+
57 Pa tsiku limene ndinakuitanani,+ munandiyandikira ndi kundiuza kuti: “Usaope.”+
ר [Rehsh]
58 Inu Yehova, mwandiweruzira milandu yanga.+ Mwawombola moyo wanga.+
59 Inu Yehova, mwaona zoipa zimene andichitira.+ Chonde, ndiweruzireni mlandu wanga.+
60 Mwaona mtima wawo wokonda kubwezera ndiponso ziwembu zawo zonse zimene andikonzera.+
ש [Sin] kapena [Shin]
61 Inu Yehova, mwamva mawu awo otonza ndipo mwaona ziwembu zawo zonse zimene andikonzera.+
62 Mwamva mawu ochokera pakamwa pa anthu amene akundiukira.+ Mwamvanso zoipa zimene akundinenera monong’ona tsiku lonse.+
63 Onani zochita zawo zonse.+ Iwo akundiimba m’nyimbo yawo.+
ת [Taw]
64 Inu Yehova, mudzawabwezera mogwirizana ndi ntchito za manja awo.+
65 Mudzaumitsa mtima wawo,+ ndipo kuchita zimenezi n’kuwatemberera.+
66 Inu Yehova, mudzawakwiyira ndi kuwathamangitsa ndipo mudzawafafaniza+ padziko lanu lapansi.+
א [ʼAʹleph]
ב [Behth]
2 Ana okondedwa a Ziyoni+ amene anali amtengo wapatali ngati golide woyengeka bwino,
Tsopano ayamba kuonedwa ngati mitsuko ikuluikulu yadothi, ntchito ya manja a munthu woumba mbiya.+
ג [Giʹmel]
3 Ngakhale mimbulu imapereka bere kwa ana ake kuti ayamwe.
Koma mwana wamkazi wa anthu anga wakhala wankhanza+ ngati nthiwatiwa m’chipululu.+
ד [Daʹleth]
ה [Heʼ]
5 Anthu amene anali kudya zinthu zabwino adzidzimuka ndipo agwidwa ndi mantha m’misewu.+
Anthu amene akula akuvala zovala zamtengo wapatali*+ agona pamilu ya phulusa.+
ו [Waw]
6 Chilango chimene mwana wamkazi wa anthu anga walandira chifukwa cha zolakwa zake, n’chachikulu kuposa chimene mzinda wa Sodomu unalandira chifukwa cha machimo ake.+
Mzinda umenewu unawonongedwa mwadzidzidzi m’kanthawi kochepa, ndipo palibe dzanja limene linauthandiza.+
ז [Zaʹyin]
7 Anaziri+ ake anali oyera kuposa chipale chofewa.+ Analinso oyera kuposa mkaka.
Ndipotu anali ofiira+ kuposa miyala yamtengo wapatali ya korali. Analinso osalala ngati mwala wa safiro.+
ח [Chehth]
8 Tsopano ayamba kuoneka akuda kuposa makala. Anthu sakuwazindikiranso mumsewu.+
Khungu lawo lafota moti lamamatira kumafupa awo.+ Langoti gwaa ngati mtengo.
ט [Tehth]
9 Amene anaphedwa ndi lupanga+ aliko bwino kusiyana ndi amene anafa ndi njala,+
Pakuti amene anafa ndi njala anafooka chifukwa chosowa chakudya, ndipo anakhala ngati apyozedwa ndi lupanga.
י [Yohdh]
10 Ngakhale amayi, amene amakhala achifundo, afika pophika ana awo ndi manja awo.+
Anawo akhala ngati chakudya chotonthoza anthu pa nthawi ya kuwonongedwa kwa mwana wamkazi wa anthu anga.+
כ [Kaph]
11 Yehova wasonyeza ukali wake wonse.+ Wakhuthula mkwiyo wake woyaka moto.+
Iye wayatsa moto m’Ziyoni, umene wanyeketsa maziko ake.+
ל [Laʹmedh]
12 Mafumu a padziko lapansi ndiponso anthu onse okhala panthaka ya dziko lapansi,+
Sanayembekezere kuti mdani angadzalowe pazipata za Yerusalemu.+
מ [Mem]
13 Zimenezi zinachitika chifukwa cha machimo a aneneri ake ndi zolakwa za ansembe ake,+
Amene anakhetsa magazi a anthu olungama a mumzindawo.+
נ [Nun]
14 Ansembe ndi aneneriwo akungoyendayenda mumsewu ngati anthu akhungu.+ Aipitsidwa ndi magazi,+
Moti palibe amene akukhudza zovala zawo.+
ס [Saʹmekh]
15 Anthu akuwafuulira kuti: “Chokani! Ndinu odetsedwa!+ Chokani! Chokani! Musatikhudze!”+
Ansembe ndi aneneriwo alibe pokhala+ ndipo akungoyendayenda.+ Anthu a mitundu ina akunena kuti: “Amenewa sapitiriza kukhala kuno.+
פ [Peʼ]
16 Yehova wawabalalitsa+ ndipo sadzawayang’ananso.+
Anthu sadzaganiziranso ansembe.+ Sadzachitiranso chifundo amuna okalamba.”+
ע [ʽAʹyin]
17 Pamene tili ndi moyo, maso athu akulefuka chifukwa choyembekezera thandizo lomwe silikubwera.+
Pofunafuna thandizo, tadalira mtundu wa anthu amene sangabweretse chipulumutso.+
צ [Tsa·dhehʹ]
18 Akutisakasaka kulikonse kumene tikupita,+ moti palibe amene akuyenda m’mabwalo a mizinda yathu.
Mapeto athu ayandikira. Masiku athu akwanira, pakuti mapeto athu afika.+
ק [Qohph]
ר [Rehsh]
20 Wodzozedwa wa Yehova,+ amene ndi mpweya wotuluka mphuno mwathu,+ wagwidwa m’dzenje lawo lalikulu.+
Ponena za ameneyu, ife tinati: “Tidzakhala mumthunzi wake+ pakati pa mitundu ya anthu.”+
ש [Sin]
21 Kondwa ndipo usangalale,+ iwe mwana wamkazi wa Edomu,+ amene ukukhala m’dziko la Uzi.+
Iwenso kapuyo ikupeza.+ Udzaledzera ndipo anthu adzakuona uli maliseche.+
ת [Taw]
22 Iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, chilango chimene anakupatsa chifukwa cha zolakwa zako chatha.+ Sadzakutenganso kupita nawe ku ukapolo.+
Tsopano iwe mwana wamkazi wa Edomu, Mulungu watembenukira kwa iwe kuti aone zolakwa zako. Machimo ako wawaika poyera.+
5 Inu Yehova, kumbukirani zimene zatichitikira.+ Tiyang’aneni kuti muone chitonzo chathu.+
2 Cholowa chathu chaperekedwa kwa anthu achilendo. Nyumba zathu zaperekedwa kwa alendo.+
3 Ife takhala anthu amasiye opanda bambo.+ Amayi athu akhala ngati akazi amasiye.+
4 Madzi akumwa ndi nkhuni, tikuchita kugula.+
5 Akutithamangitsa ndipo atsala pang’ono kutigwira.+ Tatopa ndipo tikusowa mpumulo.+
6 Kuti tipeze chakudya chokwanira, tikudalira Iguputo+ ndi Asuri.+
7 Makolo athu ndi amene anachimwa.+ Iwo anafa, koma ifeyo ndi amene tikuvutika ndi zolakwa zawozo.+
8 Antchito wamba ndi amene akutilamulira.+ Palibe amene akutilanditsa m’manja mwawo.+
9 Kuti tipeze chakudya, timaika moyo wathu pachiswe+ chifukwa cha anthu amene ali ndi malupanga m’chipululu.
10 Khungu lathu latentha kwambiri ngati ng’anjo, chifukwa cha njala yaikulu.+
11 Achitira zachipongwe+ akazi athu amene ali m’Ziyoni ndi anamwali amene ali m’mizinda ya Yuda.
12 Akalonga athu awapachika dzanja limodzi lokha.+ Anthuwo sanalemekezenso ngakhale amuna okalamba.+
13 Anyamata awanyamulitsa mphero,+ ndipo tianyamata tadzandira polemedwa ndi mitolo ya nkhuni.+
14 Pazipata sipakupezekanso amuna achikulire+ ndipo anyamata sakuimbanso nyimbo ndi zipangizo zawo zoimbira.+
15 Chisangalalo cha mumtima mwathu chatha. Kuvina kwathu kwasanduka kulira maliro.+
16 Chisoti chathu chachifumu chagwa.+ Tsoka kwa ife chifukwa tachimwa!+
17 Pa chifukwa chimenechi, mtima wathu wadwala.+ Chifukwa cha zinthu zimenezi, maso athu achita mdima.+
18 Nkhandwe zayamba kuyendayenda paphiri la Ziyoni chifukwa lasanduka bwinja.+
19 Koma inu Yehova mudzakhala pampando wanu wachifumu mpaka kalekale.+ Mpando wanu wachifumuwo udzakhalapo ku mibadwomibadwo.+
20 N’chifukwa chiyani mwatiiwala kwamuyaya+ ndi kutisiya kwa masiku ambiri?+
21 Inu Yehova, tibwezeni+ kwa inu ndipo ife tibwerera mwamsanga. Mubwezeretse zinthu zonse kuti zikhale ngati mmene zinalili kale.+
22 Koma inu mwatikanitsitsa.+ Mwatikwiyira kwambiri.+
Onani Matanthauzo a Mawu Ena.
Kapena kuti “wowathamangitsa.”
Onani mawu a m’munsi pa 1Sa 2:1.
Ena amati “khumbi,” kapena “chitala.”
Ena amati “zipupa,” kapena “zikupa.”
Ena amati “masaka.”
Onani Matanthauzo a Mawu Ena.
Kapena kuti “midzi yozungulira.”
Kapena kuti “miyala ya pamalo opatulika.”
Mawu ake enieni, “zovala zofiira,” kutanthauza zovala zofiira zamtengo wapatali.