Yobu
1 Kudziko la Uzi+ kunali munthu wina dzina lake Yobu.+ Iye anali munthu wopanda cholakwa,+ wowongoka mtima,+ woopa Mulungu+ ndiponso wopewa zoipa.+ 2 Yobu anali ndi ana aamuna 7, ndi ana aakazi atatu.+ 3 Iye anali ndi ziweto+ izi: Nkhosa 7,000, ngamila 3,000, ng’ombe 1,000 zomwe zinali kugwira ntchito zili ziwiriziwiri, ndi abulu aakazi 500. Analinso ndi antchito ochuluka zedi, ndipo iye anali munthu wolemekezeka kwambiri pa anthu onse a Kum’mawa.+
4 Ana ake aamuna anali kuchita phwando+ kunyumba ya aliyense wa iwo, tsiku lina kwa wina, tsiku lina kwa wina, ndipo anali kuitana alongo awo atatu kuti adzadye ndi kumwera limodzi. 5 Akamaliza kuchita maphwando kunyumba zawo zonse, Yobu anali kutumiza uthenga n’kuwauza kuti adziyeretse.+ Kenako iye anali kudzuka m’mawa kwambiri n’kupereka nsembe zopsereza+ mogwirizana ndi chiwerengero cha ana ake onse, popeza iye ankati, “mwina ana anga achimwa ndipo anyoza+ Mulungu mumtima mwawo.”+ Umu ndi mmene Yobu anali kuchitira nthawi zonse.+
6 Tsopano linafika tsiku limene ana a Mulungu woona+ ankapita kukaonekera pamaso pa Yehova,+ ndipo ngakhalenso Satana+ anapita nawo limodzi.+
7 Kenako Yehova anafunsa Satana kuti: “Kodi ukuchokera kuti iwe?” Satanayo anamuyankha Yehova kuti: “Ndinali kuzungulirazungulira m’dziko lapansi+ ndi kuyendayendamo.”+ 8 Ndiyeno Yehova anafunsanso Satana kuti: “Kodi mtima wako uli pa mtumiki wanga Yobu, poti palibe wina wokhala ngati iyeyo padziko lapansi?+ Iyetu ndi munthu wopanda cholakwa+ ndi wowongoka mtima,+ woopa Mulungu+ ndi wopewa zoipa.”+ 9 Pamenepo Satana anamuyankha Yehova kuti: “Kodi mukuganiza kuti Yobu amangoopa Mulungu pachabe?+ 10 Kodi inuyo simwam’tchinga iyeyo?+ Mwatchingiranso nyumba yake ndi chilichonse chimene ali nacho. Mwadalitsa ntchito ya manja ake+ ndipo ziweto zake zachuluka kwambiri padziko lapansi. 11 Koma tsopano tatambasulani dzanja lanu ndi kukhudza zonse zimene ali nazo, ndipo muona, akutukwanani m’maso muli gwa!”+ 12 Choncho Yehova anauza Satana kuti: “Chabwino, chilichonse chimene ali nacho chikhale m’manja mwako. Koma iyeyo usam’tambasulire dzanja lako ndi kum’khudza.” Pamenepo Satana anachoka pamaso pa Yehova.+
13 Tsopano linafika tsiku limene ana a Yobu, aamuna ndi aakazi, anali kudya ndi kumwa vinyo m’nyumba ya m’bale* wawo woyamba kubadwa.+ 14 Kenako kunabwera munthu+ kwa Yobu kudzanena uthenga wakuti: “Ng’ombe zinali kulima+ ndipo abulu aakazi anali kudya msipu chapambali pake. 15 Ndiyeno kunabwera Asabeya+ omwe alanda ziwetozo n’kupha abusa ake ndi lupanga. Ine ndekha ndi amene ndapulumuka kuti ndidzakuuzeni.”+
16 Uyu ali mkati molankhula kunabwera munthu wina kudzanena kuti: “Moto wa Mulungu watsika kuchokera kumwamba,+ ndipo wayaka pakati pa nkhosa ndi abusa n’kupsereza nkhosazo ndi abusawo. Ine ndekha ndi amene ndapulumuka kuti ndidzakuuzeni.”
17 Ameneyu ali mkati molankhula kunabwera munthu wina kudzanena kuti: “Kunabwera magulu atatu a Akasidi+ omwe anafika mwaliwiro kwambiri, n’kulanda ngamila ndi kupha abusa ake ndi lupanga. Ine ndekha ndi amene ndapulumuka kuti ndidzakuuzeni.”
18 Ameneyu ali mkati molankhula kunabwera munthu winanso kudzanena kuti: “Ana anu aamuna ndi aakazi anali kudya ndi kumwa vinyo+ m’nyumba ya m’bale wawo woyamba kubadwa. 19 Kenako kunabwera chimphepo+ kuchokera kudera la kuchipululu chomwe chinawomba makona anayi a nyumbayo, ndipo nyumbayo yagwera anawo n’kuwapha. Ine ndekha ndi amene ndapulumuka kuti ndidzakuuzeni.”
20 Yobu atamva zimenezi anaimirira n’kung’amba+ malaya ake akunja odula manja. Anametanso tsitsi+ kumutu kwake, kenako anagwada pansi+ n’kuwerama mpaka nkhope yake pansi,+ 21 n’kuyamba kunena kuti:
“Ndinatuluka m’mimba mwa mayi anga ndili wamaliseche,+
Ndipo ndidzabwerera mmenemo ndilinso wamaliseche.+
Yehova wapereka,+ ndipo Yehova yemweyo watenga.+
Dzina la Yehova lipitirize kutamandidwa.”+
22 M’zonsezi Yobu sanachimwe, kapena kunena kuti Mulungu wachita zosayenera.+
2 Pambuyo pa zimenezi, linafika tsiku limene ana a Mulungu woona ankapita kukaonekera pamaso pa Yehova, ndipo nayenso Satana anapita nawo limodzi kukaonekera pamaso pa Yehova.+
2 Kenako Yehova anafunsa Satana kuti: “Kodi ukuchokera kuti iwe?” Satanayo anamuyankha Yehova kuti: “Ndinali kuzungulirazungulira m’dziko lapansi ndi kuyendayendamo.”+ 3 Ndiyeno Yehova anafunsanso Satana kuti: “Kodi mtima wako uli pa mtumiki wanga Yobu,+ poti palibe wina wokhala ngati iyeyo padziko lapansi? Iyetu ndi munthu wopanda cholakwa ndi wowongoka mtima,+ woopa Mulungu+ ndiponso wopewa zoipa.+ Komabe iye akadali ndi mtima wosagawanika+ ngakhale kuti iweyo ukundiumiriza+ kuti ndimuwononge popanda chifukwa.”+ 4 Koma Satana+ anamuyankha Yehova kuti: “Khungu kusinthanitsa ndi khungu. Munthu angalolere kupereka chilichonse chimene ali nacho kuti apulumutse moyo wake.+ 5 Tsopano tatambasulani dzanja lanu ndi kukhudza mnofu wake mpaka fupa lake, ndipo muona, akutukwanani m’maso muli gwa!”+
6 Choncho Yehova anauza Satana kuti: “Chabwino, ndam’pereka m’manja mwako. Koma samala kuti usakhudze moyo wake.” 7 Kenako Satana anachoka pamaso pa Yehova+ n’kukagwetsera Yobu zilonda zopweteka,+ kuyambira kuphazi mpaka kumutu. 8 Ndiyeno Yobu anatenga phale loti azidzikanda nalo ndipo anali kukhala paphulusa.+
9 Patapita nthawi, mkazi wake anam’funsa kuti: “Kodi mukupitirizabe kukhala ndi mtima wosagawanika?+ Tukwanani Mulungu mufe!” 10 Koma Yobu anamuyankha kuti: “Ukulankhula ngati mmene amalankhulira akazi opusa.+ Kodi tizingolandira zabwino zokha kuchokera kwa Mulungu woona osalandiranso zoipa?”+ M’zonsezi Yobu sanachimwe ndi milomo yake.+
11 Tsopano anzake atatu a Yobu anamva za tsoka lonse limene linamugwera ndipo aliyense wa iwo anabwera kuchokera kwawo. Mayina awo anali Elifazi wa ku Temani,+ Bilidadi wa ku Shuwa+ ndi Zofari wa ku Naama.+ Iwo anakumana pamodzi atachita kupangana+ kuti apite kukazonda Yobu ndi kukamulimbikitsa.+ 12 Atakweza maso awo ali chapatali, sanamuzindikire poyamba. Kenako anayamba kulira mokweza mawu ndipo aliyense anang’amba+ malaya ake akunja odula manja, n’kuwaza fumbi m’mwamba pamwamba pa mitu yawo.+ 13 Kenako anakhala+ naye limodzi pansi masiku 7 usana ndi usiku, ndipo palibe amene anali kumulankhula chilichonse popeza iwo anaona kuti ululu+ wake unali waukulu kwambiri.
3 Pambuyo pa zimenezi m’pamene Yobu anatsegula pakamwa pake n’kuyamba kutemberera tsiku limene anabadwa.+ 2 Tsopano Yobu anati:
3 “Liwonongeke tsiku limene ndinabadwa,+
Ndiponso usiku umene wina ananena kuti, ‘Mwamuna wamphamvu wapangika m’mimba.’
6 Usiku umenewo utengedwe ndi mdima.+
Usasangalale pakati pa masiku a pachaka,
Pachiwerengero cha miyezi, usalowe nawo.
9 Nyenyezi za m’chisisira cha m’mawa mwake zizime.
Lidikire kuwala koma lisakuone,
Ndipo lisaone kuwala kwa m’bandakucha.
12 N’chifukwa chiyani mawondo anakumana nane,
Ndipo mabere+ ndinakumana nawo chifukwa chiyani kuti ndiyamwe?
13 Panopa bwenzi nditagona kuti ndisasokonezedwe,+
Bwenzi ndili m’tulo pa nthawiyo, ndipo bwenzi pano ndikupuma+
14 Limodzi ndi mafumu ndi aphungu a padziko lapansi,+
Amene anadzimangira malo omwe tsopano ali bwinja.+
15 Kapena ndi akalonga amene ali ndi golide,
Amene amadzaza nyumba zawo ndi siliva.
16 Kapena ngati pakati pomwe papita pachabe mosadziwa,+ bwenzi ine kulibe,
Mofanana ndi ana amene sanaone kuwala.+
20 N’chifukwa chiyani Mulungu amapereka kuwala kwa munthu amene ali ndi mavuto,
Ndiponso moyo kwa opwetekedwa mtima?+
21 N’chifukwa chiyani anthu ena amadikirira imfa, koma siwabwerera,+
Ngakhale amakumba pansi poifunafuna, kuposa mmene amakumbira chuma chobisika?
22 Amenewa amasangalala kwadzaoneni,
Amakondwera akapeza manda.
23 N’chifukwa chiyani Mulungu amapereka kuwala kwa mwamuna wamphamvu amene njira yake yabisika,+
Amene Mulungu akum’pingapinga?+
24 Pakuti chakudya changa chimabwera limodzi ndi kuusa moyo,*+
Ndipo ngati madzi, kubuula kwanga kumakhuthuka.+
25 Chinthu chochititsa mantha chimene ndinali kuchita nacho mantha, chandibwerera,
Ndipo chimene ndinali kuchiopa chabwera kwa ine.+
26 Sindinali wopanda nkhawa kapena wopanda mavuto,
Komanso sindinali pa mtendere, komabe zosautsa mtima zandibwerera.”
4 Tsopano Elifazi+ wa ku Temani anayankha kuti:
2 “Munthu akayesa kukulankhula, kodi utopa?
Koma ndani angathe kudziletsa kuti asalankhule?
5 Koma panopa zili pa iwe, ndipo watopa nazo,
Zakhudza iwe, ndipo wasokonezeka nazo.
6 Popeza umaopa Mulungu, kodi sukuyenera kulimba mtima?
Kodi ulibe chiyembekezo, munthu woti ukuyenda ndi mtima wosagawanika?+
7 Takumbukira: Kodi ndani wosalakwa amene anawonongedwapo?
Ndipo n’kuti kumene anthu owongoka mtima+ anafafanizidwapo?
8 Malinga ndi zimene ine ndaona, anthu okonzera anzawo zopweteka,
Ndi ofesa mavuto, amakolola zomwezo.+
9 Iwo amawonongeka ndi mpweya wa Mulungu,
Ndipo ndi mphamvu ya mkwiyo wake, amatha.
10 Mkango umabangula, ndipo mkango wamphamvu umamveka kulira,
Koma ngakhale mano a mkango wamphamvu, amathyoka.
11 Mkango umafa posowa nyama yoti udye,
Ndipo ana a mkango amalekanitsidwa.
12 Tsopano mawu anabwera kwa ine mwakachetechete,
Ndipo khutu langa linamva kunong’ona kwa mawuwo.+
13 Ndinakhala ndi malingaliro osautsa chifukwa cha masomphenya amene ndinaona usiku,
Pa nthawi imene anthu amakhala ali m’tulo tofa nato.
14 Ndinachita mantha kwambiri ndiponso ndinanjenjemera,
Ndipo mafupa anga onse anadzaza mantha.
15 Mzimu unadutsa kumaso kwanga,
Ndipo ubweya wa pathupi langa unayamba kuimirira.
16 Mzimuwo unaima chilili,
Koma sindinazindikire maonekedwe ake.
Chinthu chinaima pamaso panga.
Kunali bata, kenako ndinamva mawu akuti:
17 ‘Kodi munthu angakhale wolungama kuposa Mulungu?
Kapena kodi munthu angakhale woyera kuposa amene anam’panga?’
19 Nanga kuli bwanji anthu okhala m’nyumba zadothi,
Amene maziko awo ali m’fumbi?+
Iwo amathudzulidwa mosavuta kuposa kadziwotche.
20 Kuyambira m’mawa mpaka madzulo, amakhala akunyenyedwa.
Amawonongeka kwamuyaya, popanda aliyense kukhudzika nazo.
21 Kodi chingwe cha hema wawo chimene chili mkati mwawo, sichinasololedwe?
Iwo amafa chifukwa chosowa nzeru.
2 Chifukwa wopusa, mkwiyo udzamupha,
Ndipo nsanje ya munthu wosachedwa kukopeka idzamupha.
5 Zimene iye amakolola, munthu wanjala amazidya.
Ngakhale nyama yake imene waipha n’kuikoloweka pangowe, wina amadzaitenga,
Ndipo msampha umawalanda zofunika pa moyo wawo.
6 Pajatu zopweteka sizichokera m’fumbi,
Ndipo mavuto satuluka m’nthaka.
7 Pakuti munthu amabadwa kuti akumane ndi mavuto,
Monga momwe mbaliwali zimathethekera m’mwamba kuchokera pamoto.
8 Koma ndikanakhala ine, ndikanafunsa kwa Mulungu,
Ndipo kwa Mulunguyo, ndikanatula mlandu wanga.+
9 Kwa Iye amene amachita zinthu zazikulu ndi zosatheka kuzifufuza,
Zinthu zodabwitsa zosawerengeka.+
10 Kwa Iye amene amapereka mvula padziko lapansi,+
Ndi kupititsa madzi pabwalo.+
11 Kwa Iye amene amaika anthu onyozeka pamalo okwezeka,+
Mwakuti anthu achisoni amakhala pamwamba, pomwe amapezapo chipulumutso.
12 Kwa Iye amene amalepheretsa zolinga za ochenjera,+
Mwakuti ntchito imene manja awo amagwira siioneka.
13 Kwa Iye amene amakola anzeru m’kuchenjera kwawo,+
Iye amene amachititsa kuti malangizo a ochenjera abweretse chisokonezo.+
14 Iwo amakumana ndi mdima ngakhale masana,
Ndipo amafufuzafufuza masanasana ngati kuti ndi usiku.+
15 Kwa Iye amene amapulumutsa munthu ku lupanga lochokera m’kamwa mwa oipa,
Ndi kupulumutsa wosauka m’manja mwa wamphamvu.+
16 Mwakuti wonyozeka amapeza chiyembekezo,+
Koma anthu opanda chilungamo amatseka pakamwa pawo.+
17 Tamvera! N’ngodala munthu amene Mulungu amam’dzudzula,+
Ndipo chilango* cha Wamphamvuyonse usachikane.
18 Pakuti iye amayambitsa kupweteka, koma amamanga chilonda chopwetekacho.
Amaphwanya anthu, koma manja ake ndi amene amawachiritsa.
20 Pa nthawi yanjala, adzakulanditsa ndithu ku imfa,+
Ndipo pa nkhondo adzakupulumutsa ku mphamvu ya lupanga.
21 Udzabisidwa ku lilime lomenya ngati chikwapu,+
Ndipo sudzachita mantha ikadzafika nthawi yowononga.
22 Pa nthawi yowononga ndi yanjala, iweyo udzaseka,
Ndipo nyama zakutchire sudzaziopa.
24 Udzaona ndithu kuti mtendere ndiwo hema wako,
Ndipo ukapita kukayendera malo ako odyetserako ziweto, udzaona kuti palibe chimene chikusowa.
25 Ndithu udzaona kuti ana ako ndi ambiri,+
Ndipo mbadwa zako zidzakhala ngati zomera za padziko lapansi.+
26 Udzakhala ndi mphamvube mpaka kulowa m’manda,+
Mofanana ndi ngala zokhwima za tirigu, zimene amazisanjikiza pamodzi pamalo opunthira tirigu pa nyengo yake.
27 Izi n’zimene tafufuza ndipo zilidi choncho.
Imva zimenezi ndi kuzitsatira.”
6 Tsopano Yobu anayankha kuti:
2 “Zikanakhala bwino masautso anga+ onse akanayezedwa kulemera kwake,
Ndiponso pa nthawi yomweyo mavuto anga akanaikidwa pasikelo.
4 Pakuti mivi ya Wamphamvuyonse yandilasa,+
Ndipo ine ndikumwa poizoni wa miviyo.+
Zoopsa zochokera kwa Mulungu zasonkhana kuti zilimbane nane.+
7 Moyo wanga wakana kukhudza zinthu zoterozo.
Zili ngati matenda m’chakudya changa.
8 Zikanakhala bwino pempho langa likanayankhidwa,
Ndiponso Mulungu akanandipatsa chiyembekezo.
10 Ngakhale zimenezo, bwenzi zili zonditonthoza.
Ndikadadumpha ndi chisangalalo+ ngakhale kuti ndikumva ululu wosalekeza,
Chifukwa sindinabise mawu+ a Woyerayo,+ ngakhale kuti iye sakanandichitira chisoni.
11 Kodi ndili ndi mphamvu zochuluka motani, kuti ndizidikirabe?+
Ndipo kodi mapeto anga ndi otani, kuti ndipitirize kutalikitsa moyo wanga?
12 Kodi mphamvu zanga ndi mphamvu za miyala?
Kapena kodi mnofu wanga ndi wamkuwa?
13 Ndilibenso mphamvu zodzithandizira,
Ndipo sindingathenso kugwira ntchito bwinobwino.
15 Ngakhale abale anga amene, achita zachinyengo+ ngati mtsinje woyenda nthawi yozizira,
Ngati makwawa a mitsinje yoyenda nthawi yozizira, imene imauma.
16 Mitsinjeyo imakhala ndi madzi akuda chifukwa cha kusungunuka kwa madzi oundana,
Ndipo chipale chofewa nachonso chimasungunukira momwemo.
18 Njira zawo zimakhala zokhotakhota.
Mitsinjeyo imapita kumalo opanda kanthu, n’kutha.
22 Kodi ndinanena kuti, ‘Mundipatse kanthu,
Kapena mutapeko pa chuma chanu n’kundiperekera mphatso?
23 Kapena mundipulumutse m’manja mwa mdani,+
Ndi kundiwombola m’manja mwa anthu ankhanza?’+
26 Kodi mwapangana kuti mudzudzule mawu anga,
Chonsecho mawu a munthu wopanda chiyembekezo+ amatengedwa ndi mphepo?+
29 Chonde sinthani maganizo anu, kuti pachitike chilungamo.
Ndithu sinthani maganizo. Inetu ndikadali wolungama.+
30 Kodi palilime panga pali zosalungama?
Kapena kodi m’kamwa mwanga simuzindikira mavuto?
7 “Kodi si paja munthu amagwira ntchito yokakamiza+ padziko lapansi?
Ndipo kodi masiku ake sali ngati masiku a munthu waganyu?+
2 Monga kapolo, iye amakhala wefuwefu kufunafuna mthunzi,+
Ndipo ngati munthu waganyu, amadikirira malipiro ake.+
3 Chotero ndalandira miyezi yachabechabe ngati cholowa,+
Ndipo kuvutika usiku uliwonse+ ndiwo malipiro anga.
4 Ndikagona ndimanena kuti, ‘Kodi ndidzuka nthawi yanji?’+
Kukada ndimangokhalira kutembenukatembenuka mpaka m’mawa kuli mbuu.
5 Mnofu wanga wakutidwa ndi mphutsi+ ndipo wamatirira fumbi,+
Khungu langa lang’ambika n’kumatuluka mafinya.+
6 Masiku anga akufulumira+ kuposa mmene chimathamangira chowombera nsalu,
Iwo afika pamapeto popanda chiyembekezo.+
8 Diso la iye amene amandiona silidzandionanso,
Maso anu adzandiyang’ana, koma ine kudzakhala kulibe.+
9 Mtambo umafika kumapeto ake n’kutha.
Chimodzimodzi ndi munthu amene wapita ku Manda,* sadzabwerako.+
11 Choncho, ine sinditseka pakamwa panga.
Ndilankhula chifukwa cha kuvutika mumtima,+
Ndilankhula za nkhawa zanga, chifukwa moyo wanga ukupweteka.
13 Ndikanena kuti, ‘Bedi langa linditonthoza,
Bedi langa lindithandiza kusenza nkhawa zanga,’
14 Inuyo mumandiopseza ndi maloto,
Ndipo mumandichititsa mantha ndi masomphenya.
15 Chotero moyo wanga wasankha kubanika,
Wasankha imfa+ m’malo mwa mafupa angawa.
16 Moyo ndaukana,+ sindikufuna kukhala ndi moyo mpaka kalekale.*
Ndisiyeni chifukwa masiku anga ndi ochepa kwambiri.+
17 Kodi munthu ndani+ kuti mumulere,
Ndi kuti muzimuganizira?
18 Iye ndani kuti muzimuganizira m’mawa uliwonse,
Ndi kuti muzimuyesa nthawi zonse?+
20 Ngati ndachimwa, ndingakuchiteni chiyani Inu amene mumaonetsetsa anthu?+
N’chifukwa chiyani mwalunjika ine, kuti ndikhale cholemetsa kwa inu?
21 N’chifukwa chiyani simukundikhululukira machimo anga,+
Ndi kunyalanyaza zolakwa zanga?
Pakuti tsopano ndigona m’fumbi.+
Mudzandifunafuna koma ine kudzakhala kulibe.”
8 Kenako Bilidadi wa ku Shuwa+ anati:
2 “Kodi ukhala ukulankhula zimenezi mpaka liti,+
Pamene zolankhula za m’kamwa mwako zili ngati mphepo yamphamvu?+
4 Ngati ana ako amuchimwira,
Mwakuti iye wawalanga chifukwa cha kupanduka kwawo,
Ndi kuchonderera Wamphamvuyonse,
6 Ngati uli woyera ndi wowongoka mtima,+
Bwenzi panopa atadzuka kuti akumvere,
Ndipo ndithu akanabwezeretsa malo ako olungama pamene unali kukhala.
7 Komanso chiyambi chako chikanaoneka ngati chaching’ono,
Koma mapeto ako akanakhala aakulu kwambiri.+
9 Pakuti ife tabadwa dzulo,+ ndipo sitikudziwa kalikonse,
Chifukwa masiku athu padziko lapansi ali ngati mthunzi.+
10 Kodi iwo sadzakulangiza, sadzakuuza?
Ndipo kodi iwo sadzalankhula kuchokera mumtima mwawo?
11 Kodi gumbwa*+ amamera n’kutalika pamalo pamene si padambo?
Ndipo kodi bango limakula popanda madzi?
13 Ndi mmene zilili njira za onse oiwala Mulungu,+
Ndipo chiyembekezo cha wampatuko chidzatha.+
14 Iye amene chidaliro chake chimatha,
15 Iye adzatsamira nyumba yake, koma siidzakhala chiimire.
Adzaigwira, koma siidzakhalitsa.
16 Iye ali ngati chomera chachiwisi bwino chomwe chikuwombedwa dzuwa.
M’munda mwake, nthambi zake zimakula.+
17 Mizu yake imapiringizanapiringizana pamulu wa miyala.
Iye amaona kuti miyalayo ndi nyumba yake.
20 Mulungutu sangakane munthu wopanda cholakwa,
Ndipo sangagwire dzanja la ochita zoipa.
21 Adzadzaza m’kamwa mwako ndi kuseka,
Ndipo milomo yako adzaidzaza ndi mfuu yachisangalalo.
9 Tsopano Yobu anayankha kuti:
2 “Ndikudziwa bwino kuti zili choncho.
Koma kodi munthu angakhale bwanji wosalakwa pa mlandu wotsutsana ndi Mulungu?+
7 Amauza dzuwa kuti lisawale,
Ndipo amaphimba nyenyezi.+
8 Kumwamba anakutambasula yekha,+
Ndipo amayenda pamafunde aatali a m’nyanja.+
9 Anapanga gulu la nyenyezi la Asi, gulu la nyenyezi la Kesili,
Gulu la nyenyezi la Kima+ ndi zipinda zamkati za Kum’mwera.
10 Amachita zinthu zazikulu ndi zosatheka kuzifufuza,+
Ndiponso zinthu zodabwitsa zosawerengeka.+
14 N’chifukwa chake ndikamamuyankha,
Ndiyenera kusankha bwino mawu anga.+
15 Choncho, sindingamuyankhe ngakhale nditakhala kuti ndikunena zoona.+
Ndingachonderere amene akutsutsana nane pa mlandu.+
16 Nditamuitana, kodi angandiyankhe?+
Sindikukhulupirira kuti angandimvetsere.
17 Iye amene wandikantha ndi mavuto onga mphepo yamkuntho,
Wachulukitsa zilonda zanga popanda chifukwa.+
19 Ngati kuli wamphamvu kwambiri, ndi iyeyo.+
Ngati pali wolimbikitsa chilungamo, ndikufuna andiitane.
20 Ndikanakhala kuti ndikulondola, pakamwa panga pomwe pakanandinena kuti ndine wolakwa.
Ndikanakhala wosalakwa, iye akanandinena kuti ndine wachinyengo.
21 Ngakhale ndikanakhala wosalakwa, sindikanadziwa zimenezo,
Ndipo ndikanakana moyo wanga.
22 N’chifukwa chake ndikunena kuti zonsezo mfundo yake ndi imodzi, yakuti:
‘Iye amapha osalakwa komanso oipa.’+
23 Anthu atati afe mwadzidzidzi chifukwa cha kusefukira kwa madzi,
Iye angaseke anthu osalakwa akuvutika.
24 Dziko lapansi laperekedwa m’manja mwa woipa.+
Iye amaphimba nkhope za oweruza ake.
Ngati si iyeyo, ndiye ndi ndani?
25 Komanso masiku anga akufulumira kwambiri kuposa munthu wothamanga.+
Iwo athawa ndipo ndithu sadzaona zabwino.
26 Ayenda ngati ngalawa za bango,
Ngati chiwombankhanga chimene chimauluka uku ndi uko pofunafuna chakudya.+
30 Nditati ndisambe madzi a chipale chofewa,
Ndi kusamba m’manja ndi sopo,+
31 Inuyo mungandiviike m’dzenje,
Ndipo zovala zanga zinganyansidwe nane ndithu.
35 Ndilankhule ndipo ndisachite naye mantha,
Chifukwa ine sindiopa kulankhula naye.
10 “Ineyo ndikunyansidwa ndi moyo wanga.+
Ndilankhula mwamphamvu za nkhawa zanga.
Ndilankhula chifukwa cha kuwawa kwa moyo wanga.
2 Ndimuuza Mulungu kuti, ‘Musanene kuti ndine woipa.
Ndiuzeni chifukwa chimene mukulimbanirana nane.
3 Kodi ndi bwino kuti inuyo muchite zoipa,+
Kuti mukane chinthu chimene manja anu anagwira ntchito mwamphamvu pochipanga,+
Ndiponso kuti muvomereze malangizo a anthu oipa?
5 Kodi masiku anu ali ngati masiku a munthu,+
Kapena kodi zaka zanu zili ngati masiku a mwamuna wamphamvu,
6 Kuti muyese kupeza cholakwa changa,
Ndi kuti muzifunafuna tchimo langa?+
8 Manja anu omwe ndi amene anandiumba, ndipo anandipanga+
Kuzungulira thupi langa lonse, koma tsopano mukufuna kundimeza.
12 Mwandipatsa moyo ndi kundisonyeza kukoma mtima kosatha,+
Ndipo mwa kundisamalira+ mumateteza moyo wanga.
13 Zinthu zimenezi mwazibisa mumtima mwanu.
Ndikudziwa bwino kuti zinthu zimenezi zili ndi inu.
14 Ngati ndachimwa ndipo inu mwaona zonsezo,+
Ndiponso simunandikhululukire zolakwa zanga,+
15 Ngati ndine wolakwa, tsoka kwa ine!+
Ngati ndine wosalakwa, ndisadzutse mutu wanga.+
Ndachita manyazi kwambiri ndipo ndadzazidwa ndi mavuto.+
16 Mutu wanga ukadzikweza,+ mudzandisaka ngati kuti ndinu mkango wamphamvu,+
Ndipo mudzandichitira chinthu chinanso chodabwitsa.
17 Mudzabweretsa mboni zanu zatsopano pamaso panga,
Ndipo mudzakulitsa mkwiyo wanu pa ine.
Mavuto anga akungotsatizanatsatizana.
18 Kodi munanditulutsiranji m’mimba?+
Zikanakhala bwino ndikanafa kuti diso ndi limodzi lomwe lisandione.
19 Bwenzi nditakhala ngati sindinakhaleko.
Ndikanangochokera m’mimba n’kupita kumanda.’
20 Kodi masiku anga si paja ndi ochepa?+ Iye andisiye,
Asiye kundiyang’anitsitsa kuti ndisangalaleko+ pang’ono
21 Ndisanapite. Ndikapita sindibweranso,+
Ndikapita kudziko lamdima wandiweyani,+
22 Kudziko lopanda kuwala, lamdima wandiweyani
Ndi lachisokonezo, losaona kuwala mofanana ndi malo amdima.”
11 Tsopano Zofari wa ku Naama+ anayankha kuti:
2 “Kodi mawu ambirimbiri anganenedwe osayankhidwa?
Kapena kodi munthu wongodzitama angakhale wosalakwa?
3 Kodi zolankhula zako zopanda pake zingachititse anthu kukhala chete?
Ndipo kodi upitirizabe kunyoza popanda wokudzudzula?+
4 Komanso ukunena kuti, ‘Zimene ndimaphunzitsa + ndi zoyera,
Ndipo Mulungu amandiona kuti ndine woyera.’+
6 Bwenzi atakuuza chinsinsi cha nzeru,
Chifukwa zinthu za nzeru ndiponso zopindulitsa n’zambiri.
Komanso bwenzi utadziwa kuti Mulungu wachititsa kuti zolakwa zako zina ziiwalike.+
7 Kodi ungazindikire zinthu zozama za Mulungu,+
Kapena kodi ungadziwe mapeto a kukula kwa Wamphamvuyonse?
8 N’zofika kutali kuposa kumwamba. Ungachite chiyani iwe?
N’zozama kuposa Manda.+ Ungadziwe chiyani iwe?
9 N’zazitali kuposa kutalika kwa dziko lapansi,
N’zazikulu kuposa nyanja.
10 Iye akadutsa n’kupereka winawake,
N’kumuitanitsira bwalo, ndani angatsutsane naye?
12 Ngati mbidzi yooneka ngati bulu ingabadwe munthu,
Ndiye kuti munthu wanzeru zoperewera angamvetse zinthu.
13 Ngati iweyo ungakonzekeretsedi mtima wako,
Ndi kutambasulira manja ako kwa iye,+
14 Ndiponso ngati m’manja mwako muli choipa, uchikankhire kutali,
Ndipo m’mahema ako musakhale zopanda chilungamo.
16 Pakuti iweyo udzaiwala mavuto.
Ndipo udzawakumbukira ngati madzi amene anadutsa.
18 Udzalimba mtima chifukwa chakuti pali chiyembekezo.
Udzayang’anayang’ana paliponse mosamala, ndipo udzagona mopanda mantha.+
19 Ndithu udzadziwongola popanda aliyense wokuopsa.
Anthu ambiri adzakupangira zinthu zokuchititsa kuwakomera mtima.+
Ndipo malo othawirako sadzawapeza.+
Chiyembekezo chawo chidzakhala imfa.”+
12 Tsopano Yobu anayankha kuti:
2 “Zoonadi, amuna inu ndinu anthu,
Ndipo nzeru zidzathera limodzi ndi inu.+
3 Inenso ndili ndi zolinga zabwino+ ngati inuyo.
Si ine wonyozeka kwa inu,+
Ndipo ndani amene alibe zinthu ngati zimenezi?
4 Ine ndakhala chinthu choseketsa kwa anthu anzanga,+
Ndakhala munthu woitana kwa Mulungu kuti amuyankhe.+
Munthu wolungama ndi wosalakwa wakhala choseketsa.
5 Amene ali pa mtendere amanyoza tsoka n’kumaganiza kuti+
Limagwera okhawo amene mapazi awo amaterereka.+
6 Mahema a anthu olanda amakhala opanda nkhawa,+
Ndipo anthu okwiyitsa Mulungu amakhala pa mtendere
Wofanana ndi wa munthu amene watenga mulungu* m’manja mwake.+
9 Ndani pa zonsezi sadziwa bwino
Kuti dzanja la Yehova ndi limene lachita zimenezi?+
10 Iye amene moyo+ wa aliyense uli m’dzanja lake,
Ndiponso mzimu wa anthu onse.+
11 Kodi khutu si paja limasiyanitsa mawu+
Ngati mmene m’kamwa+ mumasiyanitsira kakomedwe ka chakudya?
12 Kodi okalamba si paja amakhala ndi nzeru,+
Ndipo amene akhala masiku ambiri si paja amamvetsa zinthu?
14 Iyetu amagwetsa zinthu kuti zisamangidwe,+
Zimene iye watseka, palibe munthu amene angazitsegule.+
16 Iye ali ndi mphamvu ndi nzeru zopindulitsa.+
Kwa iye kuli wochimwa mosazindikira ndi wochimwitsa ena.+
17 Amachititsa alangizi kuyenda opanda nsapato,+
Ndipo oweruza amawachititsa misala.
19 Amachititsa ansembe kuyenda opanda nsapato,+
Ndipo amene akhazikika amawawononga.+
20 Okhulupirika, iye amawakhalitsa chete,
Ndipo amuna okalamba, iye amawachotsera nzeru.
21 Iye amanyoza anthu olemekezeka,+
Ndipo amakhwepetsa lamba wa anthu amphamvu.
22 Amavundukula zinthu zozama zimene zinali pamdima,+
Ndipo amaunika pamdima wandiweyani.
23 Amapatsa mphamvu mitundu kuti aiwononge.+
Amafutukula mitundu kuti aichotse.
24 Amachotsa nzeru za atsogoleri a anthuwo,
Kuti iwo aziyendayenda kumalo kopanda kanthu,+ kumene kulibe njira.
25 Iwo amafufuzafufuza mu mdima+ mopanda kuwala,
Kuti awachititse kuyendayenda ngati munthu woledzera.+
13 “Tamverani! Zonsezi maso anga aziona,
Ndipo khutu langa lamva ndi kuziganizira.
7 Kodi amuna inu mulankhula zopanda chilungamo m’malo mwa Mulungu?
Mulankhula zachinyengo m’malo mwa iye?+
9 Kodi zingakhale bwino kuti iye akufufuzeni?+
Kapena mungam’pusitse ngati mmene mungapusitsire munthu?
10 Iye adzakudzudzulani ndithu,+
Mukadzayesera kuchita zinthu zokondera mwakabisira.+
11 Kodi kulemekezeka kwake sikudzakuchititsani mantha?
Kodi iye sadzakuchititsani kuti muope?+
12 Mawu anu osaiwalika ndiwo miyambi yopanda pake ngati phulusa.
Mayankho anu odziteteza ali ngati zishango zadothi.+
13 Khalani chete pamaso panga, kuti ineyo ndilankhule.
Kenako chilichonse chondifikira chindifikire.
15 Ngati iye atandipha, kodi sindidzadikirira?+
Komabe ndingatsutsane naye pamasom’pamaso za njira zanga.
20 Pali zinthu ziwiri zokha zoti musandichitire.
Mukatero sindidzabisala pamaso panu.+
21 Ikani dzanja lanu kutali ndi ine,
Ndipo kuopsa kwanu kusandichititse mantha.+
22 Muitane kuti ine ndivomere.
Kapena ndilankhule ndipo inu mundiyankhe.
23 Kodi ine ndinalakwa ndiponso kuchimwa mwa njira yanji?
Ndidziwitseni kulakwa kwanga ndiponso tchimo langa.
25 Kodi mukuopseza ine tsamba lachabechabe louluzika ndi mphepo?
Kapena mukuthamangitsa ine udzu wouma wachabechabe?
26 Pakuti inu mukupitiriza kundilembera zinthu zowawa,+
Ndipo mukundipatsa zotsatira za zolakwa zimene ndinachita ndili mnyamata.+
27 Ndiponso simukuchotsa mapazi anga m’matangadza,+
Ndipo mumayang’anitsitsa njira zanga zonse.
Mapazi anga mumawalembera malire.
5 Masiku a munthu ndi odziwika,+
Ndipo chiwerengero cha miyezi yake chili ndi inu.
Mwamuikira lamulo kuti asalipitirire.
6 Siyani kumuyang’anitsitsa kuti apumule,+
Mpaka apeze chisangalalo ngati mmene amachitira waganyu pakutha pa tsiku.
7 Ngakhale mtengo umakhala ndi chiyembekezo.
Ukadulidwa umaphukanso,+
Ndipo nthambi yake idzakhalapo mpaka kalekale.
8 Muzu wake ukakalamba m’nthaka,
Ndipo chitsa chake chikafa m’fumbi,
9 Ukadzangomva fungo la madzi udzaphukira,+
Ndipo udzamera nthambi ngati mtengo watsopano.+
10 Koma mwamuna wamphamvu amafa ndipo amagona pansi atagonjetsedwa.
Munthu wochokera kufumbi amatha. Kodi ali kuti?+
12 Anthu nawonso amagona pansi osadzuka.+
Sadzadzuka mpaka kumwamba kutachoka,+
Sadzadzutsidwa ku tulo tawo.+
14 Munthu akafa, kodi angakhalenso ndi moyo?+
Ndidzadikira masiku onse a ntchito yanga yokakamiza,+
Mpaka mpumulo wanga utafika.+
18 Ngakhale phiri limagwa n’kugumukagumuka,
Ngakhale thanthwe limasunthidwa pamalo ake.
19 Madzi amaperesa ngakhale miyala.
Akamathamanga amakokolola dothi la padziko lapansi.
Inunso mwawononga chiyembekezo cha munthu.
21 Ana ake amalemekezedwa, koma iye sadziwa zimenezo.+
Iwo amakhala opanda pake, koma iye sawaganizira.
22 Mnofu wake umawawa adakali nawo,
Ndipo moyo wake umapitiriza kulira udakali mwa iye.”
15 Tsopano Elifazi wa ku Temani anayankha kuti:
2 “Kodi munthu wanzeru angayankhe ndi nzeru zopanda pake,+
Kapena angadzaze mimba yake ndi mphepo ya kum’mawa?+
3 Kungodzudzula ndi mawu n’kopanda ntchito,
Ndipo mawu ndi osathandiza paokha.
4 Koma chifukwa cha iweyo kuopa Mulungu kwatha,
Ndipo ukupeputsa phindu losinkhasinkha pamaso pa Mulungu.
5 Chifukwa zolakwa zako zimaphunzitsa pakamwa pako zoti palankhule,
Ndipo umasankha lilime la akathyali.
6 Pakamwa pako m’pamene pakunena kuti ndiwe wolakwa, osati ine,
Ndipo milomo yako ikuyankha motsutsana nawe.+
7 Kodi iwe unali munthu woyamba kubadwa?+
Kodi unabadwa ndi zowawa za pobereka, mapiri asanakhaleko?+
11 Kodi chitonthozo cha Mulungu sichikukukwanira?
Kapena kulankhula nawe mawu odekha sikunakukwanire?
12 N’chifukwa chiyani mtima wako ukudzikweza?
Ndipo n’chifukwa chiyani maso ako akuwala?
13 Pakuti mtima wako watembenukira Mulungu,
Ndipo iwe watulutsa mawu oipa ndi pakamwa pako.
Dikira ndikuuze zimene ndaziona,
Ndiponso zimene sanabise, zochokera kwa makolo awo.
19 Dziko linaperekedwa kwa iwo okha,
Ndipo palibe mlendo amene anadutsa pakati pawo.
20 Woipa amavutika ndi zowawa masiku ake onse,
Ngakhale pa zaka zonse zimene zasungidwira wolamulira wankhanza.
23 Amayendayenda pofunafuna chakudya. Kodi chili kuti?+
Akudziwa bwino kuti tsiku la mdima+ layandikira.
24 Zowawa ndi zozunza zimangokhalira kumuchititsa mantha.+
Zimamugonjetsa ngati mfumu yomwe yakonzekera nkhondo.
25 Popeza amatambasula dzanja lake motsutsana ndi Mulungu,
Ndipo amayesera kuti akhale wamkulu kuposa Wamphamvuyonse,+
26 Popeza iye amalimbana ndi Mulungu mwaliuma,
Ndi zishango zake zokhala ndi mfundo zochindikala,
27 Popeza nkhope yake yaphimbika ndi mafuta a m’thupi mwake,
Ndipo wanenepa m’chiuno mwake,+
28 Iye amakhala m’mizinda imene idzafafanizidwe,
M’nyumba zimene anthu sadzapitiriza kukhalamo,
Zimene mosakayikira zidzakhala milu ya miyala.
29 Iye sadzalemera ndipo chuma chake sichidzachuluka.
Zinthu zimene adzatenge kwa iwo, sadzazimwaza padziko lapansi.+
30 Iye sadzachoka mu mdima,
Moto udzaumitsa nthambi yake,
Ndipo adzachotsedwa ndi mpweya wa m’kamwa mwa Mulungu.+
31 Iye asakhulupirire zopanda pake n’kusocheretsedwa,
Chifukwa zopanda pake n’zimene zidzakhale malipiro ake.
32 Zimenezi zidzakwaniritsidwa tsiku la woipayo lisanafike,
Ndipo mphukira yake sidzakula mosangalala.+
33 Adzathothola mphesa zake zosapsa ngati mtengo wa mpesa,
Ndipo adzayoyola maluwa ake ngati mtengo wa maolivi.
34 Pakuti msonkhano wa ampatuko ndi wopanda phindu,+
Ndipo moto uyenera kunyeketsa mahema a anthu aziphuphu.+
16 Tsopano Yobu anayankha kuti:
2 “Ndamva zinthu zambiri ngati zimenezi.
Nonsenu ndinu otonthoza onditopetsa!+
4 Inenso ndikanatha kulankhula ngati mmene mukuchitiramu,
Moyo wanu ukanakhala ngati mmene ulili moyo wanga,
Kodi ndikanalankhula mawu ogometsa okunenani?+
Ndipo kodi ndikanakupukusirani mutu?+
5 Ndikanakulimbikitsani ndi mawu a m’kamwa mwanga,+
Ndipo chitonthozo cha milomo yanga chikanachepetsa . . .
8 Komanso inu mwandigwira. Umenewu wakhala umboni,+
Mwakuti kuwonda kwanga kwandiukira ndipo kukuchitira umboni pankhope panga.
9 Mkwiyo wa Mulungu wandikhadzula. Iye ali nane chidani+
Ndipo akundikukutira mano.+
Mdani wanga akundiyang’ana ndi diso lozonda.+
10 Iwo ayasamula kukamwa kwawo kuti andimeze.+
Andimenya mbama ndi mnyozo.
Asonkhana ambirimbiri kuti alimbane nane.+
12 Ine ndinali pa mtendere koma iye anandikhutchumula.+
Anandigwira kumbuyo kwa khosi n’kundimenyetsa pansi,
Ndipo walunjikitsa mivi yake pa ine.
13 Anthu ake oponya mivi ndi uta+ andizungulira.
Iye wandiboola impso+ koma osamva chisoni,
Wakhuthulira ndulu yanga pansi.
16 Nkhope yanga yafiira chifukwa cholira,+
Ndipo pazikope zanga pali mdima wandiweyani,+
17 Chonsecho manja anga sanachite zachiwawa,
Ndipo pemphero langa ndi loyera.+
20 Anzanga asanduka ondilankhulira otsutsana nane.+
Diso langa lakhala likuyang’ana kwa Mulungu osagona.+
21 Chiweruzo chiperekedwe pakati pa mwamuna wamphamvu ndi Mulungu,
Mofanana ndi pakati pa mwana wa munthu ndi mnzake.+
3 Chonde, mundisungire chotsimikizira changa.+
Palinso ndani amene angagwirane nane chanza+ monga chikole?
7 Chifukwa cha kuzunzika, diso langa layamba kuchita mdima.+
Ziwalo zanga zonse zakhala ngati mthunzi.
8 Anthu owongoka mtima akuyang’ana zimenezi modabwa,
Ndipo ngakhale munthu wosalakwa wakwiyira wopanduka.
10 Komabe, amuna nonsenu mungathe kuyambiranso kundinena. Chotero pitirizani,
Chifukwa sindikuonapo wanzeru pakati panu.+
12 Anzanga akungokhalira kunena zabodza m’malo monena zoona.*+ Iwo akunena kuti:
‘Kuwala kuli pafupi, pamene ine ndikungoona mdima wokhawokha.’
14 Ndidzaitana dzenje+ kuti, ‘Ndinu bambo anga!’
Kwa mphutsi+ ndidzati, ‘Mayi anga ndi mlongo wanga!’
15 Chotero, kodi chiyembekezo changa chili kuti?+
Kodi pali amene akuona kuti ine ndili ndi chiyembekezo?
16 Iwo adzatsikira ku Manda otsekedwa ndi zitsulo,
Pa nthawi imene tonsefe tidzatsikira limodzi kufumbi.”+
18 Tsopano Bilidadi wa ku Shuwa anayankha kuti:
2 “Kodi zikutengerani nthawi yaitali bwanji anthu inu kuti musiye kulankhula?
Muyenera kumvetsa kuti kenako tilankhule.
4 Iwe amene ukukhadzula moyo wako mumkwiyo wako,
Kodi dziko lapansi lingasiyidwe chifukwa cha iwe?
Kapena mwala ungasunthe pamalo ake chifukwa cha iwe?
10 Chingwe choti chim’kole chabisidwa pansi,
Ndipo msampha woti um’gwire uli panjira yake.
11 Paliponse, zoopsa zadzidzidzi zimamuchititsa mantha,+
Ndipo zimamuthamangitsa zili pafupi naye kwambiri.
13 Mwana woyamba wa imfa azidzanyotsola khungu la munthuyo n’kumadya.
Iye adzadya ziwalo zake.
18 Adzamuchotsa powala n’kumukankhira kumdima.
Adzamuthamangitsa panthaka ya padziko lapansi.
19 Iye sadzasiya ana kapena mbadwa pakati pa anthu ake,+
Ndipo sipadzakhala wopulumuka pamalo amene iye akukhala monga mlendo.
20 Pa tsiku la tsoka lake anthu a Kumadzulo adzayang’ana modabwa,
Ndipo anthu a Kum’mawa adzanjenjemera.
21 Izi n’zimene zimachitikira malo okhala munthu woipa,
Ndipo awa ndiwo malo a munthu wosadziwa Mulungu.”
19 Tsopano Yobu anayankha kuti:
2 “Kodi amuna inu musautsa moyo wanga mpaka liti,+
Ndi kundilasa ndi mawu?+
5 Ngati amuna inu mukudzikweza polimbana nane,+
Ndipo mukuonetsa kuti chitonzo changa n’chondiyenerera,+
6 Dziwani kuti Mulungu mwiniwakeyo ndi amene wandisocheretsa,
Ndipo wandizunguliza ndi ukonde wake wosakira nyama.+
7 Inetu ndakhala ndikukuwa kuti, ‘Chiwawa!’ koma palibe woyankha.+
Ndakhala ndikufuula popempha thandizo, koma chilungamo sichikupezeka.+
8 Iye watchinga njira yanga ndi mpanda wamiyala+ mwakuti sindingathe kudutsa.
Ndiponso waika mdima panjira zanga.+
10 Akundikokera pansi mbali zonse, ine n’kuchoka.
Wazula chiyembekezo changa ngati mtengo.
12 Asilikali ake agwirizana n’kubwera kudzamanga njira yawo kuti alimbane nane,+
Ndipo azungulira hema wanga.
14 Anzanga apamtima anditaya.+
Anthu amene ndinali kuwadziwa andiiwala,
15 Iwo amene anali kukhala m’nyumba mwanga monga alendo.+ Akapolo anga aakazi akukhala ngati sakundidziwa.
Ndakhala mlendo weniweni m’maso mwawo.
16 Ndaitana wantchito wanga koma sakundiyankha.
Ndikukhalira kumuchonderera ndi pakamwa panga kuti andimvere chisoni.
17 Mpweya wanga wasanduka wonyansa kwa mkazi wanga,+
Ndipo ndakhala wonunkha kwa ana obadwa kwa mayi anga.
19 Amuna onse amene anali anzanga apamtima akudana nane,+
Ndipo amene ndinali kuwakonda anditembenukira.+
22 N’chifukwa chiyani amuna inu mukungokhalira kundizunza ngati mmene akuchitira Mulungu?+
Kodi simunatope ndi kundinenera zoipa?
23 Tsopano ndikulakalaka mawu anga akanalembedwa!
Ndithu akanalembedwa m’buku!
24 Akanalembedwa ndi chitsulo chogobera+ n’kukhuthulirapo mtovu,
Akanalembedwa pathanthwe mochita kugoba kuti akhale kwamuyaya.
25 Ineyo ndikudziwa bwino kuti wondiwombola+ ali moyo,
Ndipo adzabwera pambuyo panga n’kuimirira+ pafumbi.
26 Pambuyo pa khungu langa limene alisenda, zidzakhala chonchi.
Koma ndili wowonda choncho, ndidzaona Mulungu.
Maso angawa, osati a mlendo winawake, adzamuonadi Mulungu.*
Impso zanga zasiya kugwira ntchito mkati mwanga.
28 Pakuti amuna inu mukunena kuti, ‘N’chifukwa chiyani tikungokhalira kumuzunza?’+
Chonsecho muzu wa nkhaniyo ndine.
Chifukwa lupanga limaukira ochita zoipa,
Kuti amuna inu mudziwe kuti kuli woweruza.”+
20 Tsopano Zofari wa ku Naama anayankha kuti:
2 “N’chifukwa chake malingaliro anga osautsa akundiyankha,
Chifukwa cha mkwiyo wa mumtima mwanga.
3 Ndikumva mawu ondinyoza,
Ndipo munthu wa mtima wopanda nzeru ngati zimene ine ndili nazo, akundiyankha.
4 Kodi wakhala ukudziwa zimenezi kuyambira kalekale,
Kuyambira pamene munthu anaikidwa padziko lapansi?+
5 Kuti mfuu yachisangalalo ya anthu oipa sikhalitsa,+
Ndiponso kuti kusangalala kwa wampatuko kumakhala kwa kanthawi?
6 Ngakhale kuti ulemerero wake umafika mpaka kumwamba,+
Ndipo mutu wake umafika m’mitambo?
7 Adzatheratu mofanana ndi ndowe zake.+
Amene ankamuona adzati, ‘Ali kuti kodi?’+
10 Ana ake adzafunafuna kuti anthu onyozeka awachitire chifundo.
Manja ake adzabweza zinthu zake zamtengo wapatali.+
12 Ngati zoipa zimatsekemera* m’kamwa mwake,
Ngati amazibulumunya kuseri kwa lilime lake,
13 Ngati amazikonda ndipo sazisiya,
Ngati amazivumata m’kamwa mwake,
14 Chakudya chake chidzasintha m’matumbo mwake.
Chidzakhala poizoni wa mamba m’thupi mwake.
15 Wameza chuma, koma adzachisanza.
Mulungu adzachithamangitsa m’mimba mwake.
18 Adzabweza chuma chimene anachipeza ndipo sadzachimeza.
Chumacho chidzakhala ngati chuma chochokera ku malonda ake chimene sadzachidyerera.+
21 Palibe chimene chatsala choti ameze,
N’chifukwa chake ulemerero wake sudzakhalitsa.
23 Mulungu atumize mkwiyo wake woyaka moto pa iye,
N’kuudzaza m’mimba mwake.+
Auvumbitsire pa iye kuti ufike mpaka m’matumbo mwake.
25 Muvi udzatulukira kumsana kwake,
Ndipo chida chonyezimira chidzaboola ndulu yake.+
Zida zoopsa zidzam’pweteka.+
26 Zinthu zake zapamtima zidzakumana ndi mdima wokhawokha.
Moto wopanda woukolezera udzamunyeketsa.+
Munthu wotsala muhema wake zinthu zidzamuipira.
28 Mvula yamphamvu idzakokolola nyumba yake.
Zinthu zambiri zidzam’gwera pa tsiku la mkwiyo wa Mulungu.+
21 Tsopano Yobu anayankha kuti:
2 “Amuna inu, mvetserani mwatcheru mawu anga.
Zimenezi zikhale zokutonthozani.
3 Ndilezereni mtima kuti ndilankhule.
Ndikamaliza kulankhula, aliyense wa inu akhoza kuyamba kunyoza.+
4 Kodi ineyo ndauza munthu nkhawa zanga?
Kapena n’chifukwa chiyani mzimu wanga sukukwiya?
6 Ndikakumbukira, zikundisokoneza maganizo,
Ndipo thupi langa lonse likumanjenjemera.
8 Ana awo akhazikika nawo limodzi pamaso pawo,
Ndiponso mbadwa zawo zakhazikika iwo akuona.
10 Ng’ombe zawo zamphongo zimapereka bere, ndipo siziwononga mphamvu zobereketsa.
Ng’ombe zawo zazikazi zimabereka+ ndipo sizibereka ana akufa.
11 Iwo amalola ana awo kutuluka panja ngati nkhosa,
Ndipo anawo amakhala akudumphadumpha pabwalo.
16 Komatu, ulemerero wawo saupeza chifukwa cha mphamvu zawo.+
Malangizo a anthu oipa atalikirana nane.+
Kodi ndi kangati pamene Mulungu amawakwiyira ndi kuwalanga?+
18 Kodi iwo amakhala ngati udzu wouluzika ndi mphepo?+
Kapena ngati mankhusu* ouluka ndi mphepo yamkuntho?
19 Zoipa zimene munthu anachita, Mulungu adzazisungira ana ake omwe,+
Adzam’patsa mphoto yake, ndipo iye adzaidziwa.+
21 Kodi adzatha kusangalala ndi ana ake iyeyo atapita,
Chiwerengero cha miyezi yake chitadulidwa pakati?+
23 Munthu ameneyo adzafa ali wokhutira.+
Adzafa ali pa mtendere ndiponso wosatekeseka.
24 Ntchafu zake zitadzaza mafuta,
Ndiponso mafuta a m’mafupa mwake akadali ofewa.
27 Inetu ndikudziwa bwino maganizo anu amuna inu,
Ndiponso zachiwawa zimene mungapangane kuti mundichitire.+
28 Popeza mukuti, ‘Kodi nyumba ya wolemekezeka ili kuti,
Ndipo hema wa oipa ali kuti? Kodi malo awo okhala ali kuti?’+
29 Kodi simunafunse anthu oyenda m’misewu,
Ndipo simuonetsetsa zizindikiro zawo,
30 Kuti pa tsiku la tsoka woipa amapulumuka,+
Ndipo pa tsiku la mkwiyo amawomboledwa?
33 Kwa iye zibuma za dothi lochokera m’chigwa* zidzakhala zotsekemera.+
Pambuyo pake adzakoka anthu onse,+
Ndipo amene anapita iye asanapite n’ngosawerengeka.
34 Choncho, amuna inu mukungodzivuta poyesa kunditonthoza,+
Ndipo mayankho anu ndi mabodza okhaokha.”
22 Tsopano Elifazi wa ku Temani anayankha kuti:
2 “Kodi mwamuna wamphamvu angakhale waphindu kwa Mulungu?+
Kodi aliyense wozindikira angakhale waphindu kwa iye?
3 Kodi Wamphamvuyonse amasangalala kuti ndiwe wolungama?+
Kapena amapindula chilichonse chifukwa chakuti suchita cholakwa?+
6 Umalanda abale ako chikole popanda chifukwa,+
Umalanda zovala anthu osauka n’kuwasiya ali maliseche.
10 N’chifukwa chake misampha ya mbalame yakuzungulira,+
Ndipo ukusokonezeka ndi zoopsa zadzidzidzi.
11 N’chifukwa chake pali mdima, moti sungathe kuona,
Ndipo madzi osefukira akumiza.
13 Komabe iwe wanena kuti: ‘Mulungu akudziwa chiyani?
Kodi angathe kuweruza pali mdima wandiweyani?
14 Mitambo imamutchingira malo moti saona,
Ndipo iye amayenda pamwamba pa thambo.’
15 Kodi upitiriza kuyenda panjira yakalekale
Imene anthu ochita zoipa anayendamo,
16 Anthu amene anatengedwa nthawi yawo isanakwane,+
Amene maziko+ awo amakhuthulidwa ngati madzi a mumtsinje,
17 Ndiponso amene amauza Mulungu woona kuti: ‘Tichokereni!+
Kodi Wamphamvuyonse angatichite chiyani?’
18 Chonsecho iye wadzaza nyumba zawo ndi zinthu zabwino,+
Ndipo malangizo a anthu oipa ali kutali ndi ine.+
19 Olungama adzaona chiwonongeko chawo n’kusangalala,+
Ndipo wosalakwa adzawaseka kuti:
20 ‘Zoonadi adani athu afafanizidwa,
Ndipo zimene azisiya, moto udzazinyeketsa.’
21 Um’dziwe bwino Mulungu ndi kukhala naye pa mtendere.
Ukatero zinthu zabwino zidzabwera kwa iwe.
23 Ukabwerera kwa Wamphamvuyonse,+ udzabwezeretsedwa mwakale.
Ukaika zosalungama kutali ndi hema wako,
24 Ndipo ukataya golide wako wamtengo wapatali m’fumbi,
Ukataya golide wa ku Ofiri+ m’miyala ya m’zigwa,*
25 Ndithu Wamphamvuyonse adzakhala golide wako wamtengo wapatali,
Ndiponso siliva wako wabwino kwambiri.+
30 Adzapulumutsa munthu wosalakwa,+
Ndipo iwe udzapulumutsidwa chifukwa chakuti manja ako ndi oyera.”+
23 Tsopano Yobu anayankha kuti:
2 “Ngakhale lero, sindikusangalala ndi mmene zinthu zilili pa moyo wanga. Chotero ndikudandaula.+
Dzanja langa likulemera chifukwa chakuti ndikuusa moyo.
4 Bwenzi nditapita pamaso pake ndi nkhani yoti aweruze.
M’kamwa mwanga bwenzi nditadzazamo mfundo zodziikira kumbuyo.
5 Bwenzi nditadziwa mawu amene amanena pondiyankha,
Ndipo bwenzi nditaganizira zimene amandiuza.+
7 Kumeneko, wowongoka mtima adzathetsa nkhani zake ndi iye,
Ndipo ine ndikanapulumuka kwa woweruza wanga mpaka kalekale.
8 Ndikapita kum’mawa, iye kulibe.
Ndikabwerako, sindimuona.+
9 Ndimapita kumanzere kumene iye akugwira ntchito, koma sindimuona.
Amatembenukira kudzanja lamanja, koma ine osamuona,
10 Pakuti iye amadziwa bwino njira imene ine ndimadutsa.+
Akamaliza kundiyesa, ndidzakhala ngati golide.+
12 Sindisiya malamulo otuluka pakamwa pake.+
Ndasunga mosamala mawu a pakamwa pake+ kuposa zimene akufuna kuti ndichite.
17 Pakuti sindinaletsedwe kulankhula chifukwa cha mdima,
Kapenanso chifukwa chakuti mdima wandiweyani waphimba nkhope yanga.
24 “N’chifukwa chiyani Wamphamvuyonse sanakhazikitse nthawi yachiweruzo,+
Ndipo n’chifukwa chiyani omudziwa sanaone masiku ake achiweruzo?+
3 Amathamangitsa ngakhale bulu wamphongo wa ana amasiye,*
Amalanda ng’ombe yamphongo ya mkazi wamasiye ngati chikole.+
Osaukawo amapita kukafunafuna chakudya.
Chipululu chimapatsa aliyense chakudya cha ana ake.
6 M’munda wa munthu wina, osauka amakololamo chakudya cha ziweto,
Ndipo iwo amalanda msangamsanga zinthu za m’munda wa mpesa wa munthu woipa.
8 Amanyowa ndi mvula yamkuntho ya m’mapiri,
Ndipo chifukwa chakuti alibe pobisala,+ amakupatira thanthwe.
9 Oipa amalanda mwana wamasiye kum’chotsa pabere.+
Amatenga ngati chikole chovala chimene wozunzika wavala.+
12 Anthu amene akufa amamveka kubuula kunja kwa mzinda,
Moyo wa anthu amene akufa chifukwa chovulala umafuula popempha thandizo,+
Ndipo Mulungu saziona ngati zolakwika.+
13 Oipawo amasonyeza kuti ali pakati pa opanduka omwe amatsutsana ndi kuwala.+
Iwo sanazindikire njira zake,
Ndipo sanakhale m’misewu yake.
14 Kukangocha, wakupha amadzuka
Kupita kukapha wozunzika ndi wosauka,+
Ndipo usiku iye amakhala wakuba.+
15 Diso la wachigololo+ limadikira kuti mdima ugwe madzulo.+
Iye amati, ‘Palibe diso limene lindione,’+
Ndipo amaphimba kumaso kwake.
16 Mu mdima iye amathyola nyumba za anthu,
Masana iwo amadzitsekera m’nyumba,
Ndipo saona kuwala kwa masana.+
17 Kwa iwo m’mawa n’chimodzimodzi ndi mdima wandiweyani,+
Chifukwa zoopsa zadzidzidzi za mu mdima wandiweyani amazidziwa.
18 Woipa amatengedwa mwamsanga ndi madzi.
Malo awo adzakhala otembereredwa padziko lapansi.+
Sadzapatukira kunjira yopita kuminda ya mpesa.
19 Chilala ndi kutentha zimatenga madzi a chipale chofewa.
Ndi mmenenso Manda amachitira ndi anthu amene achimwa.+
20 Mimba idzamuiwala, mphutsi zidzamumva kutsekemera pomuyamwa,+
Ndipo iye sadzakumbukiridwanso.+
Kupanda chilungamo kudzathyoledwa ngati mtengo.+
21 Woipa amachita zoipa ndi mkazi wouma amene sabereka,
Komanso ndi mkazi wamasiye+ amene woipayo sam’chitira zabwino.
22 Ndi mphamvu zake, Mulungu adzakoka anthu anyonga.
Oipa adzakhala apamwamba n’kumakayikira za moyo wawo.
23 Mulungu adzachititsa oipawo kuti azidzidalira+ n’cholinga choti azitha kudzisamalira.
Maso ake adzakhala panjira zawo.+
24 Oipawo amakhala okwezeka kwa kanthawi, kenako n’kutha.+
Iwo amatsitsidwa,+ ndipo mofanana ndi wina aliyense amathotholedwa.
Amadulidwa mofanana ndi nsonga ya ngala za tirigu.
25 Choncho ndani amene anganene kuti ndine wabodza?
Kapena kunena kuti mawu anga ndi achabechabe?”
25 Tsopano Bilidadi+ wa ku Shuwa anayankha kuti:
2 “Ulamuliro ndi wake ndipo iye ndi wochititsa mantha.+
Iye amakhazikitsa mtendere kumwamba.
3 Kodi asilikali ake angatheke kuwawerenga?
Ndipo ndani amene kuwala kwake sikum’fika?
4 Choncho, kodi munthu angakhale bwanji wolungama pamaso pa Mulungu?+
Kapena kodi munthu wobadwa kwa mkazi angakhale bwanji woyera?+
5 Kulitu mwezi koma si wowala.
Ndipo nyenyezi si zoyera m’maso mwake.
26 Tsopano Yobu anayankha kuti:
2 “Koma ndiyetu wathandiza munthu wopanda mphamvu!
Ukuona ngati wapulumutsa dzanja lopanda nyonga,+
3 Walangiza munthu wopanda nzeru.+
Komanso ukuona ngati anthu ochuluka wawadziwitsa nzeru zopindulitsa.
4 Kodi wauza ndani mawu ako,
Ndipo zimene ukunenazi zachokera kuti?
7 Iye anatambasula kumpoto pamwamba pa malo opanda kanthu,+
Ndipo anakoloweka dziko lapansi m’malere.
8 Iye anakulunga madzi m’mitambo yake,+
Moti mitamboyo sing’ambika pansi pa madziwo.
9 Anaphimba mpando wake wachifumu,
Poukuta ndi mtambo wake.+
11 Zipilala za kumwamba zimagwedezeka,
Ndipo zimadabwa chifukwa cha kudzudzula kwake.
14 Komatu zimenezi ndi kambali kakang’ono chabe ka zochita zake,+
Ndipo timangomva kunong’ona kwapansipansi kwa mawu ake.
Koma kodi mabingu ake amphamvu, angawamvetse ndani?”+
27 Tsopano Yobu anayambanso kulankhula mwandakatulo+ kuti:
2 “Pali Mulungu wamoyo+ amene wandimana chilungamo,+
Ndiponso pali Wamphamvuyonse wamoyo amene wachititsa moyo wanga kupweteka,+
3 Pamene mpweya wanga udakali wonse mwa ine,
Ndiponso pamene mzimu wa Mulungu udakali m’mphuno mwanga,+
4 Milomo yanga sidzalankhula zopanda chilungamo,
Ndipo lilime langa silidzalankhula zachinyengo.
5 Inetu sindingayerekeze n’komwe kunena kuti amuna inu ndinu olungama.+
Mpaka ine kumwalira, sindidzasiya kukhala ndi mtima wosagawanika.+
10 Kodi iye angasangalale ndi Wamphamvuyonse?
Kodi angapemphere kwa Mulungu nthawi zonse?
13 Gawo la munthu woipa lochokera kwa Mulungu,+
Zomwe adzalandire kwa Wamphamvuyonse monga cholowa cha ozunza anzawo, ndi izi:
16 Iye akaunjika siliva ngati fumbi,
Ndipo akakonza zovala zake ngati dothi,
17 Ngakhale akonze zovalazo, wolungama ndi amene adzazivale.+
Ndipo silivayo, wosalakwa ndi amene adzam’tenge.
19 Adzagona ali wolemera, koma palibe chimene chidzasonkhanitsidwe.
Adzatsegula maso ake, koma sipadzakhala kalikonse.+
28 “Zoonadi, siliva ali ndi malo amene amapezekako,
Ndiponso kuli malo a golide yemwe amayengedwa.+
2 Chitsulo chimatengedwa m’fumbi,+
Ndipo mkuwa umakhuthulidwa kuchokera m’miyala.
4 Amakumba mgodi kutali ndi kumene anthu amakhala monga alendo,+
Kumalo oiwalika, kutali ndi phazi.
Anthu ena amatsikira pansi n’kumagwira ntchito cholendewera.
5 Padziko lapansi pamamera chakudya,+
Koma pansi pake pasandulizidwa ngati kuti pasakazidwa ndi moto.
8 Zilombo zamphamvu zakutchire sizinapondepondemo,
Mkango wamphamvu sunayendeyendemo.
9 Anthu amatenga mwala wolimba,
Amagwetsa mapiri kuyambira pansi penipeni.
10 M’miyala amakumbamo ngalande zodzaza ndi madzi,+
Ndipo maso awo aona zinthu zonse zamtengo wapatali.
11 Kumalo kumene kumayambira mitsinje, amakumbako madamu.+
Ndipo chinthu chobisika amachibweretsa poyera.
17 Golide ndi galasi sizingayerekezedwe ndi nzeru,
Ndipo sangazisinthanitse ndi chiwiya chilichonse cha golide woyengeka bwino.
18 Mwala wamtengo wapatali wa korali+ ndi wa kulusitalo sizingayerekezedwe n’komwe ndi nzeruzo.
Ndipo thumba lodzaza ndi nzeru ndi lamtengo wapatali kuposa thumba lodzaza ndi ngale.+
19 Sizingayerekezedwe ndi miyala ya topazi+ ya ku Kusi,
Ngakhale golide woyenga bwino sangagulire nzeru.
21 Zabisika ngakhale kumaso kwa munthu aliyense wamoyo,+
Ndipo n’zobisika kwa zolengedwa zouluka m’mlengalenga.
22 Chiwonongeko ndi imfa zanena kuti,
‘Ndi makutu athu, tamva nkhani zokhudza nzeruzo.’
23 Mulungu ndi amene amamvetsa njira zake,+
Ndipo iye ndiye amadziwa malo ake.
24 Pakuti iye amayang’ana kumapeto kwenikweni kwa dziko lapansi.+
Amaona pansi ponse pa thambo,
25 Kuti mphepo aipatse mphamvu.+
Ndipo iye amagawa madzi ndi choyezera.+
26 Pamene ankapangira mvula lamulo,+
Ndiponso pamene ankapangira njira mtambo wa mvula ya mabingu,
27 M’pamene anaona nzeru n’kuyamba kulankhula zinthu zokhudza nzeruzo.
Iye anazikonza n’kuzifufuza bwinobwino.
28 Ndiyeno anauza munthu kuti,
‘Tamvera, kuopa Yehova ndiko nzeru,+
Ndipo kupatuka pa choipa ndiko kumvetsa zinthu.’”+
29 Yobu anayambanso kulankhula mwandakatulo kuti:
2 “Ndikulakalaka ndikanakhala ngati mmene ndinalili m’miyezi yakale,+
Ngati mmene ndinalili m’masiku amene Mulungu anali kundiyang’anira,+
3 Pamene anachititsa nyale yake kuwala pamutu panga,
Pamene ndinkayenda mu mdima iye akundiunikira ndi kuwala kwake.+
4 Ngati mmene ndinalili m’masiku amene ndinali mnyamata,+
Pamene Mulungu anali bwenzi langa lapamtima, ndipo anali pahema wanga,+
5 Pamene Wamphamvuyonse anali nane,
Pamene antchito anga onse anandizungulira,
6 Pamene ndinkasambitsa mapazi anga m’mafuta a mkaka,
Ndiponso pamene miyala inkanditulutsira mitsinje ya mafuta.+
7 Ndikapita kuchipata cha mzinda,+
Ndinkakonzako malo anga okhala pabwalo la mzinda.+
11 Khutu likamva, linkanena kuti ndine wodala,
Ndipo diso likaona, linkandichitira umboni.
12 Pakuti ndinkapulumutsa wosautsika wopempha thandizo,+
Ndiponso mwana wamasiye* ndi aliyense amene analibe womuthandiza.+
13 Madalitso+ a munthu amene watsala pang’ono kuwonongedwa ankabwera kwa ine,
Ndipo ndinkasangalatsa mtima wa mkazi wamasiye.+
14 Ndinkavala chilungamo, ndipo icho chinkandiveka.+
Chilungamo changa chinali ngati malaya akunja odula manja, ndi nduwira.*
16 Ndinali bambo weniweni kwa osauka,+
Ndipo mlandu wa munthu amene sindinali kumudziwa ndinkaufufuza.+
17 Ndinkaphwanya nsagwada za wochita zoipa,+
Ndipo wogwidwa, ndinkamulanditsa kukamwa kwa wochita zoipayo.
20 Ulemerero wanga ndili nawobe,
Ndipo uta umene uli m’manja mwanga uziponya mivi mobwerezabwereza.’
23 Iwo ankandidikirira ngati akudikira mvula,+
Ndipo ankayasama kuti m’kamwa mwawo mugwere mvula yomalizira.+
25 Ndinkawasankhira njira, ndipo ndinkakhala pansi patsogolo pawo.
Ndinali ngati mfumu pakati pa asilikali ake,+
Ndiponso ngati wotonthoza olira.+
30 “Tsopano anthu amene ndi ana aang’ono poyerekeza ndi ine,+
Akundiseka.+
Anthu amene abambo awo sindikanalola
Kuwaika pamodzi ndi agalu oweta nkhosa zanga.
3 Chifukwa cha njala ndiponso kusowa, iwo ali ngati akufa.
Amatafuna dera lopanda madzi,+
Limene dzulo kunali mphepo yamkuntho ndi chiwonongeko.
4 Iwo anali kubudula chitsamba cha mchere m’tchire,
Ndipo mizu ya timitengo ndiyo inali chakudya chawo.
7 Amalira mokuwa ali pakati pa zitsamba,
Amaunjikana pansi pa zitsamba zaminga.
8 Ana a munthu wopusa,+ komanso ana a munthu wopanda dzina.
Iwo akwapulidwa n’kuthamangitsidwa m’dziko.
11 Pakuti iye anakhwefula chingwe cha uta wanga n’kunditsitsa,
Ndipo zingwe za pakamwa pa hatchi,* iwo anazisiya zomasula chifukwa cha ine.
12 Iwo aimirira kudzanja langa lamanja ngati kagulu ka anthu oipa.
Amasula mapazi anga,
Koma andiikira zopinga zovulaza kwambiri.+
14 Amabwera ngati akudutsa pampata waukulu,
Amakokoloka ndi madzi a mvula yamkuntho.
15 Zoopsa zadzidzidzi zandibwerera.
Ulemerero wanga wachoka ngati kuti wauluzika ndi mphepo,
Ndipo chipulumutso changa chapita ngati mtambo.
18 Chifukwa cha kuchuluka kwa mphamvu, chovala* changa chimasintha,
Ndipo chimandithina ngati kolala yothina.
19 Iye wanditsitsa mpaka m’dothi,
Moti ndikukhala ngati fumbi ndi phulusa.
22 Mwandiuluza ndi mphepo, mwandinyamula nayo.
Kenako mwandisungunula ndi mkokomo wake.
24 Koma palibe amene amatambasula dzanja lake polimbana ndi mulu wa zinthu zowonongeka.+
Komanso pa kuwonongeka kwa munthu, palibe amene amapempha thandizo la zinthu zimenezo.
25 Ndithu, ndalirira munthu amene zinthu sizikumuyendera bwino.+
Moyo wanga walirira munthu wosauka.+
26 Ngakhale kuti ndinkadikirira zabwino, zoipa n’zimene zinabwera.+
Ndinkadikirira kuwala, koma kunabwera mdima.
27 Matumbo anga anawira ndipo sanakhale chete.
Masiku a masautso anandipeza.
28 Ndinayendayenda mwachisoni+ pamene kunalibe kuwala.
Ndinaimirira mumpingo, ndipo ndinkangofuula popempha thandizo.
30 Khungu langa linakhala lakuda+ ndipo linayoyoka pathupi panga.
Mafupa anga anatentha chifukwa chouma.
31 Zeze wanga anangokhala wolirirapo,
Ndipo chitoliro changa chinangokhala choimbapo mawu a anthu olira.
2 Kodi pali gawo lanji lochokera kwa Mulungu+ kumwamba,
Kapena cholowa chochokera kwa Wamphamvuyonse m’mwamba?
3 Kodi si paja wochita zoipa amakumana ndi zosautsa,+
Ndipo ochitira anzawo zopweteka tsoka limawagwera?
5 Ngati ndayenda ndi anthu osanena zoona,+
Ndipo phazi langa lathamangira ku chinyengo,+
6 Iye adzandiyeza pasikelo zolondola,+
Ndipo Mulungu adzadziwa kuti ndili ndi mtima wosagawanika.+
7 Ngati ndaponda kumbali kusiya njira,+
Kapena ngati mtima wanga ukungotsatira maso anga,+
Kapenanso ngati cholakwa chilichonse chamatirira m’manja mwanga,+
8 Ine ndibzale mbewu wina n’kudya,+
Ndipo mbadwa zanga zichotsedwe padziko.
9 Ngati mtima wanga wakopeka ndi mkazi,+
Ndipo ndinali kudikirira+ pakhomo lolowera kunyumba kwa mnzanga,
10 Mkazi wanga aperere ufa mwamuna wina,
Ndipo amuna ena agone naye.+
11 Chifukwa limenelo lingakhale khalidwe lotayirira,
Ndipo chimenecho chingakhale cholakwa chofunika kupita nacho kwa oweruza.+
12 Pakuti umenewu ndi moto umene unganyeketse zinthu mpaka kuziwononga,+
Ndipo unganyeketse mbewu zanga zonse ndi mizu yomwe.
13 Ngati ndinkalepheretsa chiweruzo cha kapolo wanga wamwamuna,
Kapena cha kapolo wanga wamkazi pa mlandu ndi ine,
14 Ndiye ndingatani Mulungu akaimirira,
Ndipo akandifunsa ndingamuyankhe chiyani?+
15 Kodi amene anandipanga m’mimba si amene anapanganso iyeyo?+
Kodi si mmodzi yemweyo amene anatipanga tonsefe m’mimba?
16 Ngati ndinkakaniza anthu onyozeka zopempha zawo,+
Ndipo ngati ndinkachititsa chisoni maso a mkazi wamasiye,+
17 Ngati ndinkanyema chakudya changa n’kumadya ndekha,
18 (Pakuti kuyambira ubwana wanga iye wakula ndi ine ngati bambo ake,
Ndipo kuyambira m’mimba mwa mayi anga ndakhala ndikutsogolera mkazi wamasiyeyo).
19 Ngati ndinkaona munthu akuzunzika chifukwa chosowa chovala,+
Kapena kuona kuti wosauka alibe chofunda,
20 Ngati iye* sanandidalitse,+
Ndipo ngati sanavale ubweya+ wometedwa ku nkhosa zanga zamphongo zazing’ono kuti afundidwe,
21 Ngati ndili pachipata ndinaonapo mwana wamasiye akufunika thandizo langa,+
Koma ine n’kumuopseza ndi dzanja langa,+
22 Fupa la paphewa langa ligwe kuchoka m’malo mwake,
Ndipo fupa lakumtunda la dzanja langa lithyoke.
23 Chifukwa ine ndinkaopa tsoka lochokera kwa Mulungu,
Ndipo ulemu wake+ sindikanatha kulimbana nawo.
25 Ngati ndinkasangalala chifukwa chakuti ndinali ndi katundu wambiri,+
Ndiponso chifukwa chakuti dzanja langa linapeza zinthu zambiri,+
26 Ngati ndinkaona kuwala kukamanyezimira,
Kapena mwezi wamtengo wapatali ukuyenda,+
27 Ndipo mtima wanga unayamba kukopeka mobisa,+
Komanso dzanja langa linapsompsona pakamwa panga,
28 Chimenechonso chikanakhala cholakwa chofunika kupita nacho kwa oweruza,
Chifukwa ndikanakhala nditakana Mulungu woona wakumwamba.
29 Ngati ndinkasangalala ndi kutha kwa munthu amene ankadana nane kwambiri,+
Kapena ngati ndinkakondwera chifukwa chakuti zoipa zam’gwera . . .
30 Ine sindinalole m’kamwa mwanga kuchimwa,
Popempha lumbiro loipira moyo wake.+
31 Ngati amuna a m’hema wanga sananene kuti,
‘Ndani angabwere ndi munthu amene sanakhute chakudya cha iye?’+ . . .
32 Palibe mlendo amene ankagona panja usiku.+
Zitseko zanga ndinkazisiya zotsegula kwa odutsa m’njira.
33 Ngati ndinabisa zolakwa zanga monga munthu wochokera kufumbi,+
Pobisa machimo anga m’thumba la malaya . . .
34 Chifukwa choopa khamu lalikulu,
Ndiponso chifukwa choopa kunyozedwa ndi mabanja,
Ndinkakhala chete, sindinkatuluka pakhomo.
35 Ndikulakalaka ndikanakhala ndi wina wondimvetsera,+
Kuti mogwirizana ndi chizindikiro changa chochita kulemba, Wamphamvuyonse andiyankhe.+
Ndikulakalaka munthu amene ali nane pa mlandu akanalemba chikalata.
36 Ndithu ndikanachinyamula paphewa.
Ndikanachizunguliza kumutu kwanga ngati chisoti chachikulu chachifumu.
38 Ngati nthaka yanga ikanandilirira popempha thandizo,
Ndipo ngati mizere yake ikanalirira pamodzi,
39 Ngati ndadya zipatso zake osapereka ndalama,+
Ndipo ndachititsa moyo wa olima ake kupumira m’mwamba,+
40 M’malo mwa tirigu, pamere chitsamba chaminga,+
Ndipo m’malo mwa balere, pamere zitsamba zonunkha.”
Mawu a Yobu athera pamenepa.
32 Choncho amuna atatuwa anasiya kumuyankha Yobu, chifukwa iye anali kudziona kuti ndi wolungama.+ 2 Koma Elihu mwana wa Barakeli mbadwa ya Buza+ wa m’banja la Ramu anakwiya kwambiri. Anakwiyira Yobu chifukwa Yobuyo ankanena kuti anali wolungama, osati Mulungu.+ 3 Iye anakwiyiranso anzake atatu aja chifukwa chakuti iwo sanapeze yankho koma ankanena kuti Mulungu ndi woipa.+ 4 Elihu anali ndi mawu koma anadikira kuti Yobu amalize, chifukwa anthuwo anali aakulu kwa Elihuyo.+ 5 M’kupita kwa nthawi, Elihu anaona kuti amuna atatuwo analibe choyankha+ ndipo mkwiyo wake unakulirakulira. 6 Kenako Elihu mwana wa Barakeli mbadwa ya Buza anati:
“Ine ndine wamng’ono
Ndipo amuna inu ndinu achikulire.+
N’chifukwa chake ndinabweza mawu anga ndipo ndinaopa
Kukuuzani zimene ndikudziwa.
8 Ndithudi, mzimu wa anthu
Ndiponso mpweya wa Wamphamvuyonse n’zimene zimawachititsa kumvetsa zinthu.+
9 Si anthu a masiku ambiri okha amene amakhala ndi nzeru,+
Ndipo si okalamba okha amene amadziwa kuweruza.+
10 Chotero ndinati, ‘Ndimvereni.
Ndikufuna kunena zimene ndikudziwa.’
11 Inetu ndimadikira kuti inu mulankhule.
Ndakhala ndikumvetsera maganizo anu,+
Kufikira mutapeza mawu oti munene.
12 Ndakhala ndikukumvetserani mwachidwi,
Ndipo palibe aliyense amene akum’dzudzula Yobu.
Palibe aliyense wa inu amene akuyankha zonena zake,
13 Kuti musanene kuti, ‘Tapeza nzeru.+
Mulungu ndiye akumuthamangitsa, osati munthu.’
14 Popeza sanalankhule mawu ondinena,
Ine sindimuyankha ndi mawu anu.
15 Iwo achita mantha, sakuyankhanso.
Mawu awathera.
16 Ine ndadikira, chifukwa sakupitiriza kulankhula.
Pakuti anangoima chilili, sanayankhenso.
17 Ine ndifotokozapo maganizo anga.
Ndinena zimene ndikudziwa,
18 Chifukwa ndili ndi mawu ambiri.
Mzimu wandikanikiza+ m’mimba mwanga.
Ndipo sindipereka dzina laulemu kwa munthu aliyense wochokera kufumbi.+
22 Chifukwa sindikudziwa kuti ndingapereke bwanji dzina laulemu kwa munthu.
Pakuti amene anandipanga+ angandichotse mosavuta.
33 “Tsopano inu a Yobu, imvani mawu anga,
Ndipo tcherani khutu ku zonena zanga zonse.
3 Zonena zanga zikusonyeza kuwongoka kwa mtima wanga,+
Ndipo milomo yanga imanena nzeru moona mtima.+
5 Ngati mungathe ndiyankheni.
Ndifotokozereni mawu anu, ndipo khalani pamalo anu.
8 Komabe inu mwanena m’makutu anga,
Ndipo ine ndakhala ndikumva mawu anu akuti,
9 ‘Ndine woyera, wopanda tchimo,+
Ndilibe chondidetsa, ndilibe cholakwa.+
14 Pakuti Mulungu amalankhula koyamba,
Kenako kachiwiri,+ ngakhale anthu asamvere.
15 Iye amawalankhula m’maloto+ ndi m’masomphenya+ a usiku,
Anthu akakhala m’tulo tofa nato,
Akamagona pabedi.+
16 Pa nthawi imeneyi m’pamene amatsegula anthu makutu,+
Pa chilimbikitso chake kwa iwo, amadindapo chidindo,
17 Kuti achotse munthu pa zochita zake,+
Ndi kuti mwamuna wamphamvu am’bisire kunyada.+
19 Kuwawa kumam’dzudzula iye ali pabedi pake,
Mafupa ake amangokhalira kukangana.
21 Mnofu wake umatha, osaonekanso.
Mafupa ake amene sanali kuoneka amakhala pamtunda.
23 Ngati iye ali ndi mthenga,
Womulankhulira mmodzi pa omulankhulira 1,000,
Kuti auze munthu zimene zili zowongoka,
24 Mulungu amasangalatsidwa naye ndi kunena kuti,
‘M’pulumutseni kuti asapite m’dzenje,+
25 Mnofu wake usalale kuposa mmene unalili ali mnyamata.+
Abwerere ku masiku ake aunyamata pamene anali ndi mphamvu.’+
26 Adzadandaulira Mulungu kuti asangalale naye,+
Adzaona nkhope yake akufuula mosangalala,
Ndipo Mulungu adzabwezera kwa munthu kulungama kwa Mulunguyo.
27 Adzaimbira anthu n’kunena kuti,
‘Ndachimwa,+ ndakhotetsa zimene zinali zowongoka,
Ndipo sindinayenere kuchita zimenezi.
29 Mulungutu amachita zinthu zonsezi.
Kawiri kapena katatu konse, amachitira zimenezi mwamuna wamphamvu,
30 Kum’bweza kuti asapite kudzenje,+
Kuti aunikiridwe ndi kuwala kwa anthu amene ali moyo.+
31 Tcherani khutu inu a Yobu. Ndimvereni!
Khalani chete, ndipo ine ndipitiriza kulankhula.
32 Ngati muli ndi mawu, ndiyankheni.
Lankhulani chifukwa ine ndakondwera ndi kulungama kwanu.
34 Elihu anapitiriza kulankhula kuti:
2 “Mvetserani mawu anga, anthu anzeru inu.
Ndipo anthu odziwa zinthu inu, ndimvereni.
4 Tiyeni tidzisankhire chiweruzo.
Tidziwe tokha pakati pathu chimene chili chabwino.
6 Kodi ndikunama za mmene chiweruzo changa chiyenera kukhalira?
Chilonda changa chachikulu sichikupola ngakhale kuti sindinachimwe.’+
8 Iye ndithu ali pa ulendo wokachita ubwenzi ndi anthu ochita zopweteka ena,
Komanso ali pa ulendo wokayenda ndi anthu oipa.+
10 Choncho inu amuna a mtima+ womvetsa zinthu, ndimvereni.
Mulungu woona sangachite zoipa m’pang’ono pomwe,+
Ndipo Wamphamvuyonse sangachite zinthu zopanda chilungamo ngakhale pang’ono.+
11 Pakuti iye amapereka mphoto kwa munthu wochokera kufumbi malinga ndi zochita zake,+
Ndipo amam’bweretsera zinthu zogwirizana ndi njira yake.
13 Ndani wam’patsa dziko lapansi?
Ndipo ndani wam’patsa ulamuliro panthaka yonse?
14 Akaika mtima wake pa munthu aliyense,
Akatenga mzimu* ndi mpweya wa munthuyo,+
15 Zamoyo zonse zimafera limodzi,
Ndipo munthu amabwerera kufumbi.+
16 Choncho ngati mumamvetsa zinthu, mvetserani izi.
Mvetserani mawu anga.
17 Kodi zoonadi munthu wodana ndi chilungamo angalamulire?+
Ngati munthu wamphamvu ali wolungama, kodi munganene kuti ndi woipa?+
18 Kodi munthu anganene kwa mfumu kuti, ‘Ndinu wopanda pake’?
Kapena angauze anthu olemekezeka kuti, ‘Ndinu oipa’?+
19 Alipo amene sanakonderepo akalonga,
Ndipo saganizira kwambiri wolemekezeka kuposa wonyozeka,+
Chifukwa onsewo anapangidwa ndi manja ake.+
20 Iwo amafa mwadzidzidzi,+ ngakhale pakati pa usiku.+
Anthuwo amagwedezeka uku ndi uku n’kufa,
Ndipo amphamvu amachoka popanda dzanja lowachotsa.+
23 Pakuti iye saikiratu nthawi yoti munthu aliyense
Apite kukaweruzidwa ndi Mulungu.
26 Amawamenya monga oipa,
Pamalo pomwe ena akuonerera.+
27 Chifukwa asiya kumutsatira,+
Ndipo sasamala za njira zake zonse,+
28 Kuti achititse kulira kwa wonyozeka kupita kwa iye.
Choncho iye amamva kulira kwa osautsika.+
29 Iye akachititsa bata, ndani angamudzudzule?
Ndipo akabisa nkhope yake,+ ndani angamuone?
Kaya abisire nkhope yake mtundu+ kapena munthu, n’chimodzimodzi.
31 Kodi munthu ndithu anganene kwa Mulungu kuti,
‘Ndapirira ngakhale kuti sindinachite cholakwa?+
32 Ngakhale kuti sindikuona chilichonse, inuyo ndiphunzitseni?
Ngati ndachita chosalungama chilichonse,
Sindidzachichitanso?’+
33 Kodi iye angakulipire mogwirizana ndi mmene ukuganizira, chifukwa chakuti ukukana chiweruzo chake?
Chifukwa chakuti iweyo wasankha wekha, osati ine?
Tsopano nena zimene ukudziwa.
34 Anthu a mtima womvetsa zinthu+ adzandiuza,
Ngakhale munthu wanzeru komanso wamphamvu amene akundimvetsera adzandiuza kuti,
35 ‘Yobu sadziwa zimene akunena,+
Ndipo amanena mawu osonyeza kuti iye ndi wosazindikira.’
36 Atate anga, Yobu ayesedwe mpaka pamapeto
Chifukwa cha zimene anali kuyankha pakati pa amuna ochita zopweteka anzawo.+
37 Chifukwa pa tchimo lake akuwonjezerapo kupanduka.+
Akuwomba m’manja pakati pathu ndipo akuchulutsa zonena zake zotsutsana ndi Mulungu woona.”+
35 Elihu anapitiriza kulankhula kuti:
2 “Kodi mukuona ngati chimenechi n’chilungamo?
Inuyo mwanena kuti, ‘Ndine wolungama kuposa Mulungu.’+
3 Mwanena kuti, ‘Kodi kulungamako n’kwantchito yanji kwa inu?+
Kodi kundipindulitsa chiyani kuposa chimene ndikanapindula pochimwa?’+
6 Mukachimwa, kodi mumapindula chiyani chotsutsana naye?+
Ndipo kupanduka kwanu kukawonjezeka, kodi mumam’chitira chiyani chomuipira?
7 Ngati ndinudi wosalakwa, kodi mumam’patsa chiyani?
Kodi amalandira chiyani kuchokera m’manja mwanu?+
8 Kuipa kwanu kungapweteke munthu ngati inu nomwe,+
Ndipo chilungamo chanu chingakomere mwana wa munthu wochokera kufumbi.+
9 Chifukwa cha kuchuluka kwa kuponderezedwa, iwo amangokhalira kufuula popempha thandizo.+
Amangokhalira kulirira thandizo chifukwa cha dzanja la amphamvu.+
10 Koma palibe wanena kuti, ‘Kodi Mulungu, Wondipanga Wamkulu,+ ali kuti,
Amene amapatsa anthu nyimbo usiku?’+
11 Iye ndiye amatiphunzitsa+ zambiri kuposa nyama zakutchire,+
Ndipo amatipatsa nzeru kuposa ngakhale zolengedwa zouluka m’mlengalenga.
14 Nanga kuli bwanji mukanena kuti simumuona?+
Mlanduwo uli pamaso pake, choncho muzimuyembekezera ndi nkhawa.+
16 Yobu akatsegula pakamwa pake amalankhula zopanda pake.
Amachulukitsa mawu osonyeza kuti palibe chimene akudziwa.”+
36 Elihu anapitiriza kunena kuti:
2 “Ndilezereni mtima kwa kanthawi kochepa ndipo ndikuuzani
Kuti mawu alipobe oti ndinene m’malo mwa Mulungu.
3 Zimene ndinene ndizitenga kutali,
Ndipo ndilengeza kuti amene anandipanga, ndiye mwiniwake wa chilungamo.+
5 Mulungutu ndi wamphamvu+ ndipo sadzakana munthu.
Iye ali ndi mphamvu zazikulu zomvetsa zinthu.
6 Iye sadzasiya woipa aliyense ali wamoyo,+
Koma adzapereka chiweruzo cholungama kwa osautsika.+
7 Sadzachotsa maso ake pa aliyense wolungama.+
Adzaika mafumu pamipando yachifumu,+
Adzawachititsa kuti alamulire kwamuyaya, ndipo iwo adzakhala ndi mphamvu zambiri.
9 Ndiyeno iye adzawauza za momwe iwo amachitira zinthu
Ndiponso zolakwa zawo, chifukwa iwo amadzikuza.
10 Iye adzatsegula makutu awo kuti iwo amve pamene iye akuwalimbikitsa,+
Ndipo adzawauza kuti asiye kuchita zopweteka ena.+
15 Iye adzapulumutsa wozunzika m’masautso ake,
Ndipo adzatsegula makutu awo pamene akuponderezedwa.
16 Ndithu iye adzakukopani n’kukuchotsani pakamwa pa zowawa.+
M’malomwake padzakhala malo otakasuka,+ osati opanikiza,
Ndipo chitonthozo cha patebulo panu chidzakhala chodzaza ndi mafuta.+
18 Samalani kuti mkwiyo+ usakuchititseni kuwomba m’manja chifukwa cha njiru,
Ndipo dipo lalikulu+ lisakusocheretseni.
19 Kodi kulira kwanu kopempha thandizo kudzakupindulirani?+ Ayi, sikudzakupindulirani ngakhalenso pa mavuto,
Ngakhale muyesetse mwamphamvu bwanji.+
20 Musapumire m’mwamba polakalaka usiku,
Pamene anthu amabwera kuchokera kumene anali.
21 Samalani kuti musabwerere ku zinthu zopweteka ena,+
Chifukwa mwasankha zimenezi m’malo mwa masautso.+
22 Mulungutu amachita zinthu zapamwamba ndi mphamvu zake.
Kodi mphunzitsi winanso ndani wofanana naye?
27 Pakuti iye amakoka madontho a madzi.+
Madonthowo amasefeka n’kutsika ngati mvula ndi nkhungu,
Imakhetsa madzi ochuluka pa anthu.
3 Amakuchititsa kumveka pansi ponse pa thambo,
Ndipo mphezi yake+ imafika kumalekezero a dziko lapansi.
4 Pambuyo pake pamamveka phokoso.
Iye amabangula+ ndi mawu ake amphamvu.+
Mawu ake akamveka, iye saletsa mphezizo.+
5 Mulungu amabangula ndi mawu ake+ mochititsa chidwi kwambiri.
Amachita zinthu zazikulu zimene sitingazidziwe.+
6 Chifukwa chipale chofewa amachiuza kuti, ‘Gwera padziko lapansi.’+
Amauzanso mvula zimenezi, ngakhalenso mvula yamphamvu ikamakhuthuka.+
7 Iye amatseka dzanja la munthu aliyense,
Kuti anthu onse adziwe ntchito ya Mulungu.
11 Iye amalemetsa mitambo ndi chinyontho.
Kuwala kwake+ kumamwaza mitambo younjikana pamodzi.
12 Amaizunguliza ndi kuiwongolera kuti igwire ntchito yake
Kulikonse kumene amailamula+ panthaka ya padziko lapansi.
13 Amagwiritsa ntchito mitamboyo kuti ipereke chilango,+ kuti inyowetse dziko lake,+
Komanso kuti iye asonyeze kukoma mtima kwake kosatha.+
15 Kodi mukudziwa nthawi imene Mulungu anapangana nazo,+
Komanso pamene anachititsa kuunika kwa mtambo wake kuti kuwale?
16 Kodi mukudziwa mmene mtambo umaimira,+
Ndiponso ntchito zodabwitsa za yemwe amadziwa zinthu bwino kwambiri?+
18 Kodi limodzi ndi iyeyo mungagangate* kuthambo,+
Komwe kuli ngati galasi lolimba lopangidwa ndi chitsulo chosungunula?
19 Tidziwitseni zoti timuuze.
Sitingathe kutulutsa mawu chifukwa cha mdima.
38 Tsopano Yehova anamuyankha Yobu kuchokera mumphepo yamkuntho+ kuti:
2 “Kodi amene akuphimba malangizo anga
Ndi mawu ake opanda nzeruyu ndani?+
3 Takokera chovala chako n’kuchimanga m’chiuno ngati mwamuna wamphamvu.
Ndikufuna ndikufunse mafunso ndipo iweyo undiyankhe.+
5 Ndani anaika miyezo yake, ngati ukudziwa,
Kapena ndani anatambasulirapo chingwe choyezera?
6 Kodi maziko ake anazikidwa pa chiyani?+
Kapena ndani anaika mwala wake wapakona,
7 Pamene nyenyezi za m’mawa+ zinafuula pamodzi mokondwera,
Ndiponso pamene ana onse a Mulungu+ anayamba kufuula ndi chisangalalo?
8 Ndani anatseka nyanja ndi zitseko,+
Imene inayamba kuyenda ngati kuti ikutumphuka m’mimba?
9 Pamene ndinaika mtambo ngati chovala chake,
Ndi mdima wandiweyani ngati nsalu yoikulungira.
10 Ndipo ndinaiikira lamulo,
Ndinaiikiranso mpiringidzo ndi zitseko.+
11 Kenako ndinaiuza kuti, ‘Ukhoza kufika apa, koma usapitirirepo,+
Ndipo mafunde ako aatali azilekezera pamenepa.’+
12 Kodi kuyambira masiku ako oyambirira unalamula m’mawa?+
Kodi ndiwe unachititsa m’bandakucha kudziwa malo ake,
13 Kuti kuwala kwake kufike mpaka kumalekezero a dziko lapansi,
Kuti anthu oipa asansidwe n’kuchotsedwamo?+
14 Dzikolo limadzisintha ngati dongo+ pansi pa chodindira,
Ndipo zinthu zimakhala pamalo awo ngati kuti zavala zovala.
19 Kodi njira yopita kumene kuwala kumakhala ili kuti?+
Nanga mdima, kwawo n’kuti,
20 Kuti uzipititse kumalire awo,
Ndi kuti udziwe njira zopita kunyumba kwawo?
21 Kodi ukudziwa popeza pa nthawiyo unali utabadwa,+
Ndiponso chifukwa chakuti masiku ako ndi ochuluka?
22 Kodi unalowapo munkhokwe ya chipale chofewa,+
Kapena umaziona nkhokwe za matalala,+
23 Zimene ndazisungira nthawi ya zowawa,
Ndi tsiku lomenyana komanso lankhondo?+
24 Kodi njira imene kuwala kumadzigawira ili kuti,
Ndiponso njira imene mphepo ya kum’mawa+ imamwazikira padziko lapansi ili kuti?
25 Ndani anagawa ngalande ya madzi osefukira,
Ndi njira ya mtambo wa mvula yamabingu,+
26 Kuti achititse mvula kugwa padziko pamene palibe munthu,+
Ndi kuchipululu kumene kulibe munthu aliyense,
27 Kuti inyowetse malo owonongeka ndi mvula yamkuntho ndiponso ouma,
Komanso kuti imeretse udzu?+
29 Kodi madzi oundana amachokera m’mimba mwa ndani,
Ndipo mame oundana+ a m’mlengalenga anawabereka ndani?
31 Kodi ungamange zingwe gulu la nyenyezi la Kima,
Kapena kodi ungamasule zingwe za gulu la nyenyezi la Kesili?+
32 Kodi ungatulutse gulu la nyenyezi la Mazaroti pa nthawi yake?
Ndipo kodi ungatsogolere gulu la nyenyezi la Asi pamodzi ndi ana ake?
35 Kodi ungauze mphezi kuti zibwere kwa iwe
N’kudzakuuza kuti, ‘Ndife pano, tabwera’?
37 Ndani amene ali ndi nzeru zoti angathe kudziwa chiwerengero cholondola cha mitambo,
Kapena zosungira madzi akumwamba, ndani angathe kuzipendeketsa,+
38 Fumbi likasanduka matope n’kumayenderera ngati chitsulo chosungunula,
Ndiponso zibuma zadothi zikamatana?
39 Kodi mkango ungausakire nyama,
Ndipo kodi ungakhutiritse mikango yamphamvu yanjala kwambiri,+
40 Ikamyata m’malo amene imabisala,+
Kapena ikabisala patchire kuti igwire nyama?
41 Ndani amakonzera khwangwala chakudya,+
Ana ake akamalirira Mulungu kuti awathandize,
Akamadzandira chifukwa chosowa chakudya?
39 “Kodi ukudziwa nthawi yoikidwiratu imene mbuzi za m’mapiri zokhala m’matanthwe zimabereka?+
Kodi unaona nthawi imene mphoyo zimabereka+ ndi zowawa za pobereka?
2 Kodi umawerenga miyezi imene zimakwanitsa,
Kapena ukudziwa nthawi yoikidwiratu imene zimabereka?
3 Zimagwada zikamaswa ana awo,
Ululu wawo ukamatha.
4 Ana awo amakhala amphamvu ndi athanzi, ndipo amakulira m’tchire.
Amachoka osabwereranso kwa makolo awo.
5 Ndani anapatsa mbidzi+ ufulu wongodziyendera,
Ndipo ndani anamasula zingwe za bulu wam’tchire,
6 Amene ndinam’patsa chipululu monga nyumba yake,
Ndiponso amene amakhala kudera la nthaka yamchere?+
9 Kodi ng’ombe yamphongo yam’tchire* imafuna kukutumikira,+
Kapena ingagone pafupi ndi chodyeramo ziweto zako?
11 Kodi ungaikhulupirire chifukwa ili ndi mphamvu zochuluka,
Kapena ungaisiyire ntchito yako?
12 Kodi ungaidalire kuti ikubweretsere mbewu zako,
Ndi kuti izitutire popunthira?
13 Kodi nthiwatiwa yaikazi imakupiza mapiko ake mosangalala,
Kapena kodi ili ndi mapiko ndi nthenga zofanana ndi za dokowe?+
14 Pakuti imasiya mazira ake munthaka,
Ndipo imawatenthetsa m’fumbi.
15 Imaiwala kuti phazi linalake likhoza kuwaphwanya,
Kapenanso kuti nyama yakutchire ikhoza kuwaponda.
16 Imachitira nkhanza ana ake ngati kuti si ake,+
Ndipo imagwira ntchito pachabe chifukwa ilibe mantha.
18 Ikatambasula mapiko ake ndi kuwakupiza,
Imaseka hatchi ndi wokwerapo wake.
23 Kachikwama koika mivi kamachita phokoso kakamagunda m’nthiti mwake
Limodzi ndi mkondo ndi nthungo.*
24 Imatha mtunda mwamgugu ndiponso mosangalala.
Ikamva kulira kwa lipenga sikhulupirira chifukwa cha chisangalalo.
25 Lipenga likangolira, imati eyaa!
Imanunkhiza nkhondo ili kutali,
Imamva phokoso la mafumu ndi mfuu yankhondo.+
26 Kodi kuzindikira kwako n’kumene kumachititsa kabawi kuuluka pamwamba,
Ndi kutambasulira mapiko ake mphepo yakum’mwera?
27 Kapena kodi lamulo lako n’limene limachititsa chiwombankhanga+ kuulukira m’mwamba,
Ndi kumanga chisa chake pamwamba kwambiri,+
28 Kukhala pathanthwe ndi kugona pomwepo usiku,
Pansonga penipeni pa thanthwe ndi pamalo povuta kufikapo?
40 Tsopano Yehova anafunsa Yobu kuti:
2 “Kodi munthu ayenera kum’tola chifukwa Wamphamvuyonse, n’kutsutsana naye?+
Amene akudzudzula Mulungu ayankhe.”+
3 Ndiyeno Yobu anamuyankha Yehova kuti:
4 “Ine tsopano ndakhala wopanda pake.+
Kodi ndingakuyankheni chiyani?
Ndaika dzanja langa pakamwa.+
5 Ndalankhula kamodzi ndipo sindiyankhanso.
Sindionjezera chilichonse pa mawu amene ndalankhula kawiri.”
6 Tsopano Yehova anamuyankha Yobu kuchokera mumphepo yamkuntho+ kuti:
7 “Takokera chovala chako n’kuchimanga m’chiuno ngati mwamuna wamphamvu.+
Ndikufuna ndikufunse mafunso ndipo iweyo undiyankhe.+
8 Kodi ndithu ukuchititsa chilungamo changa kukhala chopanda pake?
Kodi ukunena kuti ine ndine wolakwa kuti iweyo ukhale wolondola?+
9 Kapena kodi uli ndi dzanja ngati la Mulungu woona?+
Kodi ungachititse mabingu kugunda ndi mawu ngati a Mulungu?+
Uphimbe nkhope zawo m’malo obisika,
14 Ndipo ineyo ndidzakuyamikira,
Chifukwa chakuti dzanja lako lamanja lingakupulumutse.
15 Ine ndinapanga mvuu* ndipo ndinapanganso iweyo.
Iyo imadya udzu wobiriwira+ ngati ng’ombe yamphongo.
17 Imapindira pansi mchira wake ngati mtengo wa mkungudza,
Mitsempha ya m’ntchafu mwake ndi yolukanalukana.
18 Mafupa ake ali ngati mapaipi amkuwa,
Mafupa ake olimba ali ngati ndodo zachitsulo.
22 Mitengo yaminga imaitchinga ndi mthunzi wawo.
Mitengo ya msondodzi ya kuchigwa* imazungulira mvuuyo.
23 Mtsinje ukakalipa iyo sichita mantha n’kuthawa.
Sitekeseka ngakhale madzi a mu Yorodano+ asefukire n’kumainyowetsa kumaso.
24 Kodi alipo amene angaigwire iyo ikuona?
Kodi alipo amene angakole mphuno yake ndi ngowe?
3 Kodi iyo ingachonderere kambirimbiri kwa iwe,
Kapena kodi ingalankhule nawe mofatsa?
4 Kodi ingachite nawe pangano,
Kuti uitenge ngati kapolo mpaka kalekale?
5 Kodi ungasewere nayo ngati mbalame,
Kapena kodi ungaimange kuti izisangalatsa ana ako aakazi?
6 Kodi ochita malonda angaigule posinthanitsa ndi chinthu china?
Kodi angaigawe pakati pa amalonda?
8 Ika dzanja lako pa iyo.
Kumbukira nkhondoyo. Usadzachitenso.
9 Ndithu, zimene munthu anali kuyembekezera adzakhumudwa nazo,
Komanso adzagwa pansi akangoiona.
11 Ndani wayamba kundipatsa kanthu, kuti ndim’patse mphoto?+
Zinthu zonse za pansi pa thambo ndi zanga.+
12 Sindikhala chete osanena za ziwalo zake,
Kapena za mphamvu zake ndi kukongola kwa thupi lake loumbidwa bwino.
13 Ndani angaivule chovala chake?
Ndani angalowe pakati pa nsagwada zake?
14 Ndani watsegula zitseko za kumaso kwake?
Mano ake onse ndi ochititsa mantha.
15 Mizere ya mamba ake ndiyo kudzikuza kwake.
Iwo ndi otsekeka ngati anachita kuwamatirira pamodzi.
16 Ndi othithikana kwambiri,
Moti ngakhale mpweya sungadutse pakati pawo.
17 Onse anamatirirana.
Anagwirana ndipo sizingatheke kuwalekanitsa.
18 Ikamatulutsa mpweya, pamaoneka kuwala.
Maso ake ali ngati kuwala kwa m’bandakucha.
19 M’kamwa mwake mumatuluka kung’anima kwa mphezi,
Ngakhale moto wothetheka umatulukamo.
20 M’mphuno mwake mumatuluka utsi,
Ngati ng’anjo imene yayatsidwa ndi udzu.
21 Moyo wake umayatsa makala.
Ngakhale lawi la moto limatuluka m’kamwa mwake.
22 M’khosi mwake mumakhala mphamvu,
Ndipo pamaso pake, kutaya mtima kumadumpha.
23 Minofu yake yokwinyika imamatana.
Imakhala ngati anaiumbira pomwepo ndipo sisunthika.
24 Mtima wake anauumba kuti ukhale wolimba ngati mwala.
Anauumbadi ngati mwala wapansi wa mphero.
31 Imachititsa madzi akuya kuwira ngati mphika.
Imachititsa nyanja kukhala ngati mphika wa mafuta onunkhira.
32 Imachititsa njira kuwala m’mbuyo mwake.
Munthu angaone madzi akuya ngati kuti ndi imvi.
33 Pafumbi palibe chofanana nayo.
Iyo inapangidwa kuti isamachite mantha.
34 Imaona chilichonse chokwezeka.
Iyo ndi mfumu ya zilombo zonse zakutchire.”
42 Tsopano Yobu anamuyankha Yehova kuti:
2 “Ndadziwa kuti inu mumatha kuchita zinthu zonse,+
Ndipo palibe zimene simungakwanitse.+
3 Inu munati, ‘Kodi amene akuphimba malangizo anga mopanda nzeruyu ndani?’+
Chotero ine ndinalankhula, koma sindinali kuzindikira
Zinthu zodabwitsa kwambiri kwa ine, zimene sindikuzidziwa.+
5 Ndinkangomva za inu,
Koma tsopano diso langa lakuonani.
7 Yehova atanena mawu amenewa kwa Yobu, Yehovayo anauza Elifazi wa ku Temani kuti:
“Mkwiyo wanga wayakira iweyo ndi anzako awiriwo+ chifukwa inu simunanene zoona za ine,+ monga wachitira Yobu mtumiki wanga. 8 Tsopano utenge ng’ombe zamphongo 7 ndi nkhosa zamphongo 7.+ Upite nazo kwa mtumiki wanga Yobu,+ ndipo inuyo mukadziperekere nsembe yopsereza. Ndiyeno Yobu mtumiki wanga akakupemphererani.+ Ine ndimvera iye yekhayo basi kuti ndisakuchititseni manyazi chifukwa cha zopusa zimene mwachita, popeza simunanene zoona za ine monga wachitira Yobu mtumiki wanga.”+
9 Chotero Elifazi wa ku Temani, Bilidadi wa ku Shuwa ndi Zofari wa ku Naama anapita n’kukachita monga mmene Yehova anawauzira. Choncho Yehova anamva pemphero la Yobu.
10 Tsopano Yehova anathetsa masautso a Yobu+ pamene iye anapempherera anzake aja.+ Kuwonjezera pamenepo Yehova anayamba kum’patsa Yobu zonse zimene anali nazo, kuwirikiza kawiri.+ 11 Abale ake onse, alongo ake onse ndi onse amene anali kumudziwa kale+ ankabwera kwa iye. Iwo anayamba kudyera naye pamodzi mkate+ m’nyumba mwake, komanso anali kumulimbikitsa ndi kum’pepesa chifukwa cha tsoka lonse limene Yehova analola kuti lim’gwere. Aliyense wa iwo anapatsa Yobu mphatso ya ndalama ndi mphete yagolide.
12 Yehova anadalitsa+ kwambiri mapeto a Yobu kuposa chiyambi chake+ moti iye anakhala ndi nkhosa 14,000, ngamila 6,000, ng’ombe 2,000 zimene zinkagwira ntchito zili ziwiriziwiri, ndi abulu aakazi 1,000. 13 Anakhalanso ndi ana aamuna 7 ndi ana aakazi atatu.+ 14 Mwana wake wamkazi woyamba anam’patsa dzina lakuti Yemima, wachiwiri Keziya ndipo wachitatu Kereni-hapuki. 15 M’dziko lonselo munalibe akazi okongola ngati ana aakazi a Yobu, ndipo bambo awo anawapatsa cholowa pamodzi ndi abale awo.+
16 Pambuyo pa zimenezi, Yobu anakhala ndi moyo zaka 140+ ndipo anaona ana ake ndi zidzukulu zake+ mpaka m’badwo wachinayi. 17 Pomalizira pake Yobu anamwalira ali wokalamba ndiponso wokhutira ndi masiku ake.+
Kapena kuti “mchimwene.”
M’Chiheberi, “Leviyatani.”
Onani Matanthauzo a Mawu Ena.
Kapena kuti “amithenga.”
Mawu ake enieni, “woyera.”
Onani Mawu a m’munsi pa Miy 1:2.
Ena amati “manthova,” kapena “mambidza.”
Onani Zakumapeto 5.
Onani Matanthauzo a Mawu Ena.
Onani Matanthauzo a Mawu Ena.
Mawu ake enieni, “nyumba.”
Ena amati “nthota.”
Kutanthauza, “fano.”
Mawu ake enieni, “kunyamula mnofu wanga ndi mano.”
Kapena kuti “munthu uyu.” M’Chiheberi, “iye” kutanthauza “Yobu.”
Mawu achiheberi amene tawamasulira kuti “njenjete” amatanthauza mtundu wa kachilombo kotchedwa kadziwotche kooneka ngati gulugufe, kamene kamadya zovala ngati mmene njenjete imachitira.
Mawu ake enieni, “oyera.”
Ena amati “masaka.”
Mawu ake enieni, “Anzanga akungokhalira kuika usiku m’malo mwa masana.”
Mawu ake enieni, “ndapulumuka ndi khungu la mano anga.”
Mawu ake enieni, “amene maso anga adzamuonadi, koma osati mlendo.”
Ena amati “zimanzuna.”
“Mankhusu” ndi makoko amene amachotsa ku mbewu ngati mpunga popuntha, ndipo amatha kuwauluza ndi mphepo.
Onani mawu a m’munsi pa Ge 26:17.
Mawu ake enieni, “ana aamuna opanda bambo.”
Onani mawu a m’munsi pa Ge 26:17.
Mawu ake enieni, “ana aamuna opanda bambo.”
Mwina “wachiwawa” ameneyu ndi chilombo cha m’nyanja.
Ena amati “kulasa.”
Ena amati “khumbi,” kapena “chitala.”
Mawu ake enieni, “mwana wamwamuna wopanda bambo.”
“Nduwira” ndi chovala chansalu chakumutu chimene amachimanga ngati duku.
Onani mawu a m’munsi pa Ge 26:17.
Ena amati “hosi,” kapena “kavalo.”
N’kutheka kuti akutanthauza “khungu.”
Mawu ake enieni, “mwana wamwamuna wopanda bambo.”
Mawu ake enieni, “chiuno chake.”
Onani Matanthauzo a Mawu Ena.
Onani Zakumapeto 4.
Ena amati “kutchaya,” kapena “kutsendera.”
Mwina nyama imeneyi inali yooneka ngati njati.
Tikati “nthungo” tikutanthauza mkondo waung’ono, wopepukirako.
M’Chiheberi, “Behemoti.”
Onani mawu a m’munsi pa Ge 26:17.
M’Chiheberi, “Leviyatani.”
Mawu ake enieni, “mlulu.”
Umenewu ndi mpaliro umene mwina unali ndi mano oyang’ana kumbuyo ngati dzino la mbedza.
Gulaye ndi chipangizo choponyera miyala ndi dzanja chimene amachita kupukusa. M’madera ena amati mvuluma kapena ulaya.