Masalimo*
BUKU LOYAMBA
(Masalimo 1 – 41)
1 Wodala+ ndi munthu amene sayenda motsatira malangizo a anthu oipa,+
Saima m’njira ya anthu ochimwa,+
Ndipo sakhala pansi pamodzi ndi anthu onyoza.+
2 Koma amakondwera ndi chilamulo cha Yehova,+
Ndipo amawerenga ndi kusinkhasinkha chilamulo chake usana ndi usiku.+
3 Munthu ameneyo adzakhala ngati mtengo wobzalidwa m’mphepete mwa mitsinje ya madzi,+
Umene umabala zipatso m’nyengo yake,+
Umenenso masamba ake safota,+
Ndipo zochita zake zonse zidzamuyendera bwino.+
2 N’chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akuchita chipolowe,+
Ndiponso n’chifukwa chiyani mitundu ya anthu ikung’ung’udza za chinthu chopanda pake?+
2 Mafumu a dziko lapansi aima pamalo awo,+
Ndipo nduna zapamwamba zasonkhana pamodzi mogwirizana.+
Atero kuti alimbane ndi Yehova+ komanso wodzozedwa wake.+
3 Iwo akunena kuti: “Tiyeni tidule zomangira zawo,+
Ndipo titaye zingwe zawo kutali ndi ife!”+
5 Pa nthawiyo, adzawalankhula mu mkwiyo wake,+
Adzawasokoneza ataipidwa kwambiri.+
7 Ndinene za lamulo la Yehova.
Iye wandiuza kuti: “Iwe ndiwe mwana wanga,+
Lero, ine ndakhala bambo ako.+
8 Tandipempha,+ ndipo ndikupatsa mitundu ya anthu kukhala cholowa chako,+
Ndikupatsa dziko lonse lapansi kukhala lako.+
9 Mitunduyo udzaiswa ndi ndodo yachifumu yachitsulo,+
Udzaiphwanya ngati mbiya yadothi, n’kukhala zidutswazidutswa.”+
10 Tsopano inu mafumu, sonyezani kuzindikira,
Lolani kuti maganizo anu akonzedwe, inu oweruza a dziko lapansi.+
12 Psompsonani mwanayo+ kuopera kuti Mulungu angakwiye,
Ndipo mungawonongeke ndi kuchotsedwa panjirayo.+
Pakuti mkwiyo wake umatha kuyaka mofulumira.+
Odala ndi onse amene akuthawira kwa iye.+
Nyimbo ya Davide pamene anali kuthawa mwana wake Abisalomu.+
3 Inu Yehova, n’chifukwa chiyani adani anga achuluka chotere?+
N’chifukwa chiyani anthu ondiukira achuluka?+
7 Nyamukani,+ inu Yehova! Ndipulumutseni+ inu Mulungu wanga!+
Pakuti mudzakantha adani anga onse pachibwano.+
Mano a anthu oipa mudzawaphwanyaphwanya.+
Kwa wotsogolera nyimbo: Nyimboyi iimbidwe ndi zipangizo za zingwe.+ Nyimbo ya Davide.
4 Ndikaitana, mundiyankhe inu Mulungu wanga wolungama.+
M’masautso anga mundiimiritse pamalo otakasuka.
Mundikomere mtima+ ndipo imvani pemphero langa.
2 Inu ana a anthu, kodi mudzandinyoza chifukwa cha ulemerero wanga+ kufikira liti?
Mudzakonda zinthu zopanda pake kufikira liti?
Mudzafunafuna nkhani yoti mundinamizire kufikira liti? [Seʹlah.]
4 Ngati mwakwiya, musachimwe.+
Lankhulani mumtima mwanu, muli pabedi panu,+ ndipo mukhale chete. [Seʹlah.]
6 Pali ambiri amene akunena kuti: “Ndani adzationetsa zinthu zabwino?”
Inu Yehova, tiunikeni ndi kuwala kwa nkhope yanu.+
7 Mudzasangalatsadi mtima wanga,+
Kuposanso mmene iwo amasangalalira, mbewu ndi vinyo wawo watsopano zikachuluka.+
8 Ndidzagona pansi ndi kupeza tulo mu mtendere,+
Pakuti inu nokha Yehova mumandichititsa kukhala wotetezeka.+
Kwa wotsogolera nyimbo pa Nehiloti.* Nyimbo ya Davide.
2 Imvani kufuula kwanga kopempha thandizo,+
Inu Mfumu yanga+ ndi Mulungu wanga, chifukwa ndimapemphera kwa inu.+
4 Pakuti inu sindinu Mulungu wokondwera ndi zoipa,+
Palibe munthu woipa amene angakhale ndi inu ngakhale kwa kanthawi kochepa.+
5 Palibe anthu odzitama amene angaime pamaso panu.+
Mumadana ndi onse ochita zopweteka ena.+
6 Mudzawononga olankhula bodza.+
Munthu wokhetsa magazi+ ndi wachinyengo,+ Yehova amaipidwa naye.
7 Koma ine ndidzalowa m’nyumba yanu+
Chifukwa cha kuchuluka kwa kukoma mtima kwanu kosatha.+
Ndidzawerama nditayang’ana kumene kuli kachisi wanu wopatulika chifukwa chokuopani.+
8 Inu Yehova, nditsogolereni m’chilungamo chanu+ chifukwa adani anga andizungulira.+
Salazani njira yanu kuti ndiyendemo popanda chopunthwitsa.+
9 Pakuti m’kamwa mwawo simutuluka mawu okhulupirika.+
Mitima yawo yadzaza ndi zinthu zoipa.+
Mmero wawo ndi manda otseguka.+
Iwo amalankhula ndi lilime lachinyengo.+
10 Mulungu adzawapeza ndi mlandu.+
Adzagwa ndi ziwembu zawo zomwe.+
Muwamwaze chifukwa cha kuchuluka kwa zolakwa zawo,+
Chifukwa iwo akupandukirani.+
11 Koma onse othawira kwa inu adzakondwa.+
Adzafuula mokondwera mpaka kalekale.*+
Ndipo inu mudzawateteza.
Okonda dzina lanu adzakondwa chifukwa cha inu.+
12 Pakuti inu Yehova mudzadalitsa aliyense wolungama.+
Mudzamutchinga ndi chivomerezo chanu+ ngati kuti mukum’teteza ndi chishango chachikulu.+
Kwa wotsogolera nyimbo: Nyimboyi iimbidwe chapansipansi* ndi zoimbira za zingwe.+ Nyimbo ya Davide.
2 Ndikomereni mtima, inu Yehova, chifukwa ndikulefuka.+
Ndichiritseni,+ inu Yehova, chifukwa mafupa anga agwedezeka.
4 Bwererani+ mudzapulumutse moyo wanga, inu Yehova.+
Ndipulumutseni chifukwa cha kukoma mtima kwanu kosatha.+
6 Ndalefuka chifukwa cha kuusa moyo* kwanga.+
Usiku wonse ndimanyowetsa bedi langa.+
Ndimakhathamitsa bedi langa ndi misozi.+
7 Maso anga achita mdima chifukwa cha chisoni changa.+
Maso anga akalamba chifukwa cha anthu onse ondichitira zoipa.+
8 Ndichokereni pamaso panga inu nonse ochita zopweteka ena,+
Chifukwa Yehova adzamva ndithu mawu a kulira kwanga.+
10 Adani anga onse adzachita manyazi kwambiri+ ndipo adzasokonezeka.
Adzabwerera, ndipo nthawi yomweyo adzachita manyazi.+
Nyimbo yoimba polira* imene Davide anaimbira Yehova, yonena za mawu a Kusi M’benjamini.
7 Inu Yehova Mulungu wanga,+ ine ndathawira kwa inu.+
Ndipulumutseni kwa onse ondizunza ndipo mundilanditse,+
2 Kuti pasapezeke wondikhadzulakhadzula ngati mmene mkango umachitira,+
Pasapezeke wondikwatula popanda wondilanditsa.+
3 Inu Yehova Mulungu wanga, ngati ndachita cholakwa chilichonse,+
Ngati manja anga achita zosalungama zilizonse,+
4 Ngati munthu wondichitira zabwino ndamubwezera zoipa,+
Kapena ngati ndafunkha zinthu za aliyense wondichitira zoipa amene sanaphule kanthu,+
5 Mdani wanga afunefune moyo wanga,+
Ndipo aupeze ndi kuupondaponda pafumbi.
Ulemerero wanga aukwirire m’fumbi. [Seʹlah.]
6 Nyamukani, inu Yehova, mu mkwiyo wanu.+
Imirirani ndi kukhaulitsa amene andisonyeza mkwiyo ndi kundichitira zoipa.+
Dzukani ndi kundithandiza,+ pakuti mwalamula kuti chiweruzo chiperekedwe.+
7 Mitundu ya anthu isonkhane ndi kukuzungulirani,
Ndipo inu mubwerere kumwamba ndi kuwakhaulitsa.
8 Yehova adzapereka chigamulo ku mitundu ya anthu.+
Ndiweruzeni inu Yehova, mogwirizana ndi chilungamo changa,+
Komanso mogwirizana ndi mtima wanga wosagawanika.+
10 Chishango changa chili ndi Mulungu,+ Mpulumutsi wa anthu owongoka mtima.+
12 Ngati munthu sadzabwerera kusiya zoipa,+ Mulungu adzanola lupanga lake,+
Adzakunga uta wake ndi kukonzekera kulasa.+
14 Taonani! Wina ali ndi pakati pa zinthu zoipa,+
Watenga pakati pa mavuto ndipo ndithu adzabereka chinyengo.+
17 Ndidzatamanda Yehova chifukwa cha chilungamo chake.+
Ndidzaimba nyimbo motsatizana ndi zipangizo zoimbira, kutamanda dzina+ la Yehova Wam’mwambamwamba.+
Kwa wotsogolera nyimbo pa Gititi.*+ Nyimbo ya Davide.
8 Inu Yehova Ambuye wathu, dzina lanu ndi lalikulu padziko lonse lapansi,+
Inuyo ulemerero wanu ukusimbidwa kumwambamwamba!+
2 M’kamwa mwa ana aang’ono ndi ana oyamwa mwakhazikitsamo zamphamvu,+
Chifukwa cha amene akukuchitirani zoipa.+
Mwatero kuti mugonjetse mdani wanu komanso amene akufuna kukubwezerani zoipa.+
3 Ndikayang’ana kumwamba, ntchito ya zala zanu,+
Mwezi ndi nyenyezi zimene munapanga,+
4 Ndimaganiza kuti: Munthu+ ndani kuti muzimuganizira,+
Ndipo mwana wa munthu wochokera kufumbi ndani kuti muzimusamalira?+
5 Munamuchepetsa pang’ono poyerekeza ndi ena onga Mulungu,*+
Kenako munamuveka ulemerero+ ndi ulemu monga chisoti chachifumu.+
7 Nkhosa, mbuzi ndi ng’ombe zamphongo, zonse zimenezi,+
Komanso zilombo zakutchire.+
8 Mbalame zam’mlengalenga ndi nsomba za m’nyanja,+
Chilichonse choyenda m’njira za pansi pa nyanja.+
9 Inu Yehova Ambuye wathu, dzina lanu ndi lalikulu padziko lonse lapansi!+
Kwa wotsogolera nyimbo pa Mutilabeni.* Nyimbo ya Davide.
א [ʼAʹleph]
2 Ndidzakondwera ndi kusangalala chifukwa cha inu,+
Ndidzaimba nyimbo motsagana ndi zipangizo zoimbira, kutamanda dzina lanu, inu Wam’mwambamwamba.+
ב [Behth]
4 Chifukwa mwandiweruzira mlandu wanga ndi dandaulo langa.+
Mwakhala pampando wachifumu ndipo mukuweruza mwachilungamo.+
ג [Giʹmel]
5 Mwadzudzula anthu a mitundu ina,+ mwawononga oipa.+
Dzina lawo mwalifafaniza mpaka kalekale, mwalifafaniza mpaka muyaya.+
6 Kusakaza kwa mdani kwatheratu tsopano,+
Mizinda imene mwaifafaniza, nayonso yatheratu.+
Dzina la mdani wanu silidzatchulidwanso.+
ה [Heʼ]
7 Koma Yehova adzakhala pampando wachifumu mpaka kalekale,+
Adzakhazikitsa mpando wake wachifumu kuti aweruze.+
8 Iye adzaweruza anthu padziko lapansi mwachilungamo.+
Adzazenga mlandu mitundu ya anthu moyenerera.+
ו [Waw]
9 Yehova adzakhala malo okwezeka ndiponso achitetezo kwa aliyense woponderezedwa,+
Adzakhala malo okwezeka ndiponso achitetezo m’nthawi za masautso.+
10 Anthu odziwa dzina lanu adzakukhulupirirani,+
Pakuti simudzasiya ndithu anthu okufunafunani, inu Yehova.+
ז [Zaʹyin]
11 Anthu inu, imbani nyimbo motsagana ndi zipangizo zoimbira, kutamanda Yehova amene akukhala m’Ziyoni.+
Fotokozani ntchito zake kwa mitundu ya anthu.+
12 Pofunafuna okhetsa magazi,+ iye adzakumbukira ndithu anthu osautsidwa.+
Sadzaiwala ndithu kulira kwawo.+
ח [Chehth]
13 Ndikomereni mtima inu Yehova. Onani mmene anthu odana nane akundisautsira,+
Inu Mulungu amene mukundinyamula kundichotsa pazipata za imfa.+
14 Ndichitireni zimenezi kuti ndilengeze ntchito zanu zonse zotamandika+
Pazipata+ za mwana wamkazi wa Ziyoni,+
Kuti ndikondwere ndi chipulumutso chanu.+
ט [Tehth]
16 Yehova amadziwika ndi ziweruzo zimene amapereka.+
Woipa wakodwa mumsampha wa ntchito ya manja ake.+
Higayoni.* [Seʹlah.]
י [Yohdh]
18 Pakuti waumphawi sadzaiwalidwa nthawi zonse,+
Ndiponso chiyembekezo cha ofatsa sichidzatha konse.+
כ [Kaph]
20 Ikani mantha m’mitima yawo, inu Yehova,+
Kuti anthu a mitundu ina adziwe kuti iwo ndi anthu ochokera kufumbi.+ [Seʹlah.]
ל [Laʹmedh]
10 N’chifukwa chiyani inu Yehova mukuima kutali?+
N’chifukwa chiyani mukubisala pa nthawi ya masautso?+
2 Modzikweza, woipa amathamangitsa wosautsika,+
Ndipo wosautsikayo amakodwa ndi maganizo amene woipa walingalira.+
3 Pakuti woipa amadzitamandira ndi zilakolako zake zadyera,+
Ndipo wopanga phindu lachinyengo+ amadzitamanda.
נ [Nun]
Iye amanyoza Yehova.+
4 Chifukwa cha kutukumuka mtima kwake, woipa safufuza kuti adziwe Mulungu.+
Iye amangoganiza kuti: “Kulibe Mulungu.”+
5 Zochita zake zimayenda bwino nthawi zonse.+
Zigamulo zanu zili pamwamba kwambiri pamene iye sangathe kuziona.+
Onse omuchitira zoipa amawanyodola.+
6 Mumtima mwake amanena kuti: “Sindidzagwedezeka.+
Palibe chimene chidzandichitikira ku mibadwomibadwo.”+
פ [Peʼ]
7 M’kamwa mwake mwadzaza matemberero, chinyengo ndi kupondereza ena.+
Pansi pa lilime lake pamatuluka mavuto ndi zopweteka ena.+
ע [ʽAʹyin]
Maso ake amafunafuna waumphawi.+
9 Amadikirira anthu pamalo obisika ngati mkango pamalo ake obisalapo.+
Amawadikirira+ kuti atenge mokakamiza munthu wosautsika.
Amakulunga wosautsika mu ukonde wake ndi kumutenga mokakamiza.+
10 Wosautsikayo amaponderezedwa, amawerama ndi chisoni,
Ndipo khamu la anthu achisoni limagwera m’manja amphamvu a woipayo.+
11 Mumtima mwake+ amanena kuti: “Mulungu waiwala zochita zanga.+
Wabisa nkhope yake.+
Ndithudi, sadzaona kalikonse.”+
ק [Qohph]
ר [Rehsh]
14 Inu mwaona mavuto ndi masautso.
Mumawayang’anabe kuti muchitepo kanthu.+
Waumphawi,+ mwana wamasiye,* amadziikiza m’manja mwanu.
Inu mwakhala mthandizi wake.+
ש [Shin]
15 Thyolani dzanja la woipa ndi wankhanzayo.+
Fufuzani zoipa zake zonse ndi kumulanga kufikira zoipazo zitatha.+
ת [Taw]
17 Mudzamva kuchonderera kwa anthu ofatsa,+ inu Yehova.
Mudzakonzekeretsa mitima yawo.+
Mudzatchera khutu lanu,+
18 Kuti muweruze mwana wamasiye komanso woponderezedwa.+
Mudzatero kuti munthu wamba wochokera kufumbi asachititsenso anthu ena kunjenjemera.+
Kwa wotsogolera nyimbo. Salimo la Davide.
11 Ine ndathawira kwa Yehova.+
Kodi mulibe mantha? Mukundiuza kuti:
“Thawirani kumapiri anu ngati mbalame!+
Akonzekeretsa mivi yawo kuti aiponye ndi uta,
Kuti alase anthu owongoka mtima kuchokera pamalo amdima.+
4 Yehova ali m’kachisi wake wopatulika.+
Yehova, mpando wake wachifumu uli kumwamba.+
Maso ake amaona, maso ake owala amasanthula+ ana a anthu.
5 Yehova amasanthula anthu olungama ndi oipa omwe,+
Ndipo Mulungu amadana kwambiri ndi aliyense wokonda chiwawa.+
6 Iye adzavumbitsira oipa misampha, moto ndi sulufule,+
Komanso mphepo yotentha, monga gawo limene ayenera kumwa.+
7 Pakuti Yehova ndi wolungama.+ Amakonda ntchito zolungama.+
Anthu owongoka mtima ndi amene adzaona nkhope yake.+
Kwa wotsogolera nyimbo: Iimbidwe chapansipansi.*+ Nyimbo ya Davide.
12 Ndipulumutseni,+ inu Yehova, pakuti anthu okhulupirika atha.+
Anthu okhulupirika atheratu pakati pa ana a anthu.
3 Yehova adzadula milomo yonse yolankhula zachinyengo
Ndi lilime lolankhula modzikuza.+
4 Iye adzadula anthu onena kuti: “Ndi lilime lathu tidzapambana.+
Timalankhula chilichonse chimene tikufuna ndi milomo yathu. Ndani angatilamulire?”
5 Tsopano Yehova wanena kuti: “Chifukwa cha kuponderezedwa kwa osautsika, chifukwa cha kuusa moyo kwa anthu osauka,+
Ndidzanyamuka pa nthawiyo,+
Ndidzawateteza kwa aliyense wowanyodola.”+
6 Mawu a Yehova ndi oyengeka bwino,+
Ngati siliva woyengedwa nthawi zokwanira 7 mung’anjo ya m’nthaka.
Kwa wotsogolera nyimbo. Nyimbo ya Davide.
13 Kodi mudzandiiwala kufikira liti, inu Yehova?+ Mpaka muyaya?+
Mudzandibisira nkhope yanu kufikira liti?+
2 Kodi ndidzalimbana ndi masautso anga kufikira liti?
Kodi masiku a moyo wanga adzakhala odzaza ndi chisoni kufikira liti?
Kodi mdani wanga adzadzikweza pamaso panga kufikira liti?+
3 Ndiyang’aneni. Ndiyankheni, inu Yehova Mulungu wanga.
Walitsani maso anga+ kuti ndisagone mu imfa.+
4 Chitani zimenezi kuti mdani wanga asanene kuti: “Ndamugonjetsa!”
Kutinso adani anga asakondwere chifukwa chakuti ine ndadzandira.+
5 Koma ine ndakhulupirira kukoma mtima kwanu kosatha.+
Mtima wanga ukondwere chifukwa cha chipulumutso chanu.+
6 Ndidzaimbira Yehova chifukwa wandifupa ndi zinthu zabwino.+
Kwa wotsogolera nyimbo. Salimo la Davide.
14 Wopusa amanena mumtima mwake kuti:
“Kulibe Yehova.”+
Anthu oterewa amachita zoipa,+ ndipo amachita zinthu zonyansa.
Palibe amene akuchita zabwino.+
2 Koma kuchokera kumwamba, Yehova wayang’ana ana a anthu padziko lapansi,+
Kuti aone ngati pali aliyense wozindikira, aliyense amene akufunafuna Yehova.+
3 Onse apatuka,+ ndipo onsewo ndi achinyengo.+
Palibe aliyense amene akuchita zabwino,+
Palibiretu ndi mmodzi yemwe.+
4 Kodi palibe aliyense wozindikira mwa anthu ochita zopweteka anzawowa,+
Amene akudya anthu anga ngati chakudya?+
Iwo sanaitane pa Yehova.+
7 Haa! Zikanakhala bwino m’Ziyoni mukanapezeka chipulumutso cha Isiraeli.+
Yehova akadzasonkhanitsa ndi kubwezeretsa anthu ake amene anagwidwa ndi kutengedwa kupita kudziko lina,+
Yakobo adzasangalale, Isiraeli adzakondwere.+
Nyimbo ya Davide.
15 Inu Yehova, ndani amene angakhale mlendo m’chihema chanu?+
Ndani angakhale m’phiri lanu lopatulika?+
2 Ndi amene akuyenda mosalakwitsa zinthu,+ amene amachita chilungamo,+
Ndi kulankhula zoona mumtima mwake.+
3 Iye sanena miseche ndi lilime lake.+
Sachitira mnzake choipa,+
Ndipo satonza bwenzi lake lapamtima.+
4 Iye sagwirizana ndi munthu aliyense wonyansa,+
Koma anthu oopa Yehova amawalemekeza.+
Akalumbira kuchita zinthu zimene kenako zakhala zoipa kwa iye, sasintha malingaliro ake.+
5 Sapereka ndalama zake kuti alandire chiwongoladzanja,+
Ndipo salandira chiphuphu kuti akhotetse mlandu wa munthu wosalakwa.+
Wochita zinthu zimenezi, sadzagwedezeka konse.+
Mikitamu* ya Davide.
16 Ndisungeni, inu Mulungu, pakuti ndathawira kwa inu.+
2 Ndauza Yehova kuti: “Inu ndinu Yehova. Ubwino wanga sungakupindulitseni,+
3 Koma ungapindulitse oyera amene ali padziko lapansi.
Anthu aulemerero amenewo, ndi amene ndimakondwera nawo.”+
4 Zopweteka zimachuluka kwa anthu amene amati akaona mulungu wina, amamuthamangira.+
Ine sindidzatsanula nsembe zawo zachakumwa zothira magazi,+
Ndipo sindidzatchula dzina lawo ndi milomo yanga.+
5 Yehova ndiye gawo langa, gawo limene ndinapatsidwa,+ komanso chikho changa.+
Inu mukundisungira bwino kwambiri cholowa changa.
8 Ndaika Yehova patsogolo panga nthawi zonse.+
Popeza kuti ali kudzanja langa lamanja, sindidzagwedezeka.+
11 Mudzandidziwitsa njira ya moyo.+
Chifukwa cha nkhope yanu, munthu adzakondwera mokwanira.+
Kudzanja lanu lamanja kuli chimwemwe mpaka muyaya.+
Pemphero la Davide.
17 Imvani dandaulo lolungama, inu Yehova. Mvetserani kulira kwanga kochonderera.+
Tcherani khutu ku pemphero langa limene likutuluka pamilomo yopanda chinyengo.+
3 Mwasanthula mtima wanga, mwandifufuza usiku,+
Ndipo mwandiyenga. Mudzaona kuti sindinaganizire kuchita choipa chilichonse.+
Pakamwa panga sipadzaphwanya malamulo.+
4 Kunena za ntchito za anthu,
Ndakhala wosamala mwa kusunga mawu a pakamwa panu, kuti ndisatengere njira ya wachifwamba.+
6 Ine ndikuitana pa inu, chifukwa mudzandiyankha, inu Mulungu.+
Tcherani khutu kwa ine. Imvani mawu anga.+
7 Sonyezani kukoma mtima kosatha mwa kuchita zodabwitsa,+ inu Mpulumutsi wa anthu othawira kwa inu,
Amene akuthawa anthu ogalukira dzanja lanu lamanja.+
8 Ndisungeni monga mwana wa diso,+
Ndibiseni mumthunzi wa mapiko anu,+
9 Chifukwa cha anthu oipa amene akundipondereza.
Adani a moyo wanga atsala pang’ono kundipeza.+
10 Mitima yawo siimva chisoni,*+
Ndipo amalankhula modzikuza ndi pakamwa pawo.+
11 Tsopano adaniwo atizungulira, kulikonse kumene tingapite.+
Akutiyang’anitsitsa kuti atigwetse.+
12 Aliyense wa iwo akuoneka ngati mkango umene ukufunitsitsa kukhadzula nyama.+
Akuonekanso ngati mkango wamphamvu umene wabisalira nyama.
13 Nyamukani, inu Yehova, yang’anizanani naye maso ndi maso woipayo.+
M’gonjetseni. Pulumutsani moyo wanga kwa woipayo ndi lupanga lanu.+
14 Ndipulumutseni kwa anthu ndi dzanja lanu, inu Yehova,+
Ndipulumutseni kwa anthu a m’nthawi* ino,+ amene gawo lawo lili m’moyo uno.+
Anthu amene mimba zawo mwazidzaza ndi chuma chanu chobisika,+
Amene ali ndi ana aamuna ochuluka,+
Ndipo amakundikira ana awo chuma.+
Kwa wotsogolera nyimbo. Salimo la mtumiki wa Yehova, Davide, amene anauza Yehova mawu a m’nyimbo iyi pa tsiku limene Yehova anamulanditsa m’manja mwa adani ake onse komanso m’manja mwa Sauli.+ Iye anati:
18 Ndidzakukondani inu Yehova, mphamvu yanga.+
2 Yehova ndiye thanthwe langa, malo anga achitetezo ndiponso Wopereka chipulumutso kwa ine.+
Mulungu wanga ndiye thanthwe langa. Ine ndidzathawira kwa iye.+
Iye ndiye chishango changa, nyanga* yanga ya chipulumutso ndiponso ndiye malo anga okwezeka achitetezo.+
6 Pa nthawi ya zowawa zanga ndinaitana Yehova,
Ndinafuulira Mulungu wanga kuti andithandize.+
Iye anamva mawu anga ali m’kachisi wake.+
Pamenepo makutu ake anamva kulira kwanga kopempha thandizo.+
7 Dziko lapansi linayamba kugwedezekera uku ndi uku ndiponso kutekeseka.+
Maziko a mapiri anagwedezeka,+
Anagwedezekera uku ndi uku chifukwa Mulungu anakwiya.+
8 Utsi unatuluka m’mphuno mwake, ndipo moto wotuluka m’kamwa mwake unanyeketsa.+
Makala onyeka anatuluka mwa iye.
10 Iye anafika atakwera pakerubi wouluka.+
Mulungu anali kuuluka mwaliwiro pamapiko a cholengedwa chauzimu.*+
11 Kenako anapanga mdima kukhala malo ake obisalamo,+
Panali madzi akuda ndi mtambo wakuda,
Zimene zinamuzungulira ngati msasa wake.+
12 M’kuwala kochokera pamaso pake munatuluka mitambo yake,+
Munatulukanso matalala ndi makala onyeka a moto.+
13 Ali kumwamba, Yehova anayamba kugunda ngati mabingu,+
Wam’mwambamwamba anayamba kutulutsa mawu ake,+
Anatulutsanso matalala ndi makala onyeka a moto.
15 Ndipo ngalande za pansi pa madzi zinaonekera,+
Maziko a dziko lapansi anakhala poonekera.+
Zinatero chifukwa cha kudzudzula kwanu, inu Yehova, chifukwa cha mphamvu ya mpweya wa m’mphuno mwanu.+
17 Anandilanditsa kwa mdani wanga wamphamvu,+
Anandilanditsa kwa odana nane chifukwa anali amphamvu kuposa ine.+
20 Yehova amandipatsa mphoto mogwirizana ndi chilungamo changa.+
Amandibwezera mogwirizana ndi kuyera kwa manja anga.+
21 Pakuti ndasunga njira za Yehova,+
Sindinachoke kwa Mulungu wanga. Ndikanatero, ndikanachita chinthu choipa.+
24 Yehova andibwezere mogwirizana ndi chilungamo changa,+
Andibwezere mogwirizana ndi kuyera kwa manja anga pamaso pake.+
25 Munthu wokhulupirika, mudzamuchitira mokhulupirika.+
Munthu wamphamvu wopanda cholakwa, mudzamuchitira mwachilungamo.+
26 Kwa munthu wokhalabe woyera, mudzadzisonyeza kuti ndinu woyera,+
Kwa munthu wopotoka maganizo mudzadzisonyeza kuti ndinu wochenjera,+
27 Chifukwa anthu osautsika mudzawapulumutsa,+
Koma anthu odzikweza mudzawatsitsa.+
29 Pakuti ndi thandizo lanu, ndingathamangitse gulu la achifwamba.+
Ndi thandizo la Mulungu wanga ndingakwere khoma.+
30 Njira ya Mulungu woona ndi yangwiro.+
Mawu a Yehova ndi oyengeka bwino.+
Iye ndi chishango kwa onse othawira kwa iye.+
32 Mulungu woona Ndiye amandilimbitsa,*+
Ndipo adzasalaza njira yanga.+
33 Iye adzachititsa mapazi anga kukhala aliwiro ngati a mbawala zazikazi,+
Ndipo adzandiimiritsabe pamalo okwezeka kwa ine.+
35 Inu mudzandipatsa chishango chanu cha chipulumutso,+
Dzanja lanu lamanja lidzandichirikiza,+
Ndipo kudzichepetsa kwanu n’kumene kudzandikweza.+
40 Koma mudzachititsa adani anga kugonja* pamaso panga,+
Anthu odana nane kwambiri, ndidzawakhalitsa chete.+
41 Adzafuula kupempha thandizo, koma sipadzapezeka wowapulumutsa,+
Adzafuulira Yehova, koma sadzawayankha.+
43 Inu mudzandipulumutsa kwa anthu a mtundu wanga onditola zifukwa.+
Mudzandiika kukhala mtsogoleri wa mitundu yonse.+
Anthu amene sindikuwadziwa adzanditumikira.+
44 Anthu akangomva mphekesera chabe zokhudza ine, adzandimvera.+
Alendo adzabwera kwa ine akunthunthumira.+
46 Yehova ndi wamoyo.+ Lidalitsike Thanthwe langa.+
Mulungu wa chipulumutso changa akhale wokwezeka.+
47 Mulungu woona ndiye Wobwezera adani anga.+
Iye amagonjetsa mitundu ya anthu ndi kuiika kunsi kwa mapazi anga.+
48 Iye amandipulumutsa kwa adani anga olusa.+
Ndipo mudzandikweza pamwamba pa anthu amene amandiukira.+
Mudzandilanditsa kwa munthu wachiwawa.+
49 N’chifukwa chake ndidzakutamandani, inu Yehova pakati pa mitundu.+
Ndipo ndidzaimba nyimbo zotamanda dzina lanu.+
50 Iye akuchita ntchito zazikulu za chipulumutso kwa mfumu yake,+
Ndipo akusonyeza kukoma mtima kosatha kwa wodzozedwa wake,+
kwa Davide ndi mbewu yake mpaka kalekale.+
Kwa wotsogolera nyimbo. Nyimbo ya Davide.
19 Zakumwamba zikulengeza ulemerero wa Mulungu.+
Ndipo m’mlengalenga mukufotokoza ntchito ya manja ake.+
4 Zingwe zawo zoyezera zafika padziko lonse lapansi,+
Mawu awo amveka kumalekezero a dziko lapansi kumene kuli anthu.+
Kumwambako Mulungu wamangira dzuwa hema.+
5 Dzuwalo limaoneka ngati mkwati amene akutuluka m’chipinda chake,+
Limakondwa ngati mmene mwamuna wamphamvu amachitira akamathamanga m’njira.+
6 Limatuluka kuchokera kumalekezero ena a kumwamba,
Ndi kuzungulira mpaka kumalekezero enanso.+
Palibe chinthu chilichonse chimene sichimva kutentha kwake.+
7 Chilamulo+ cha Yehova ndi changwiro,+ chimabwezeretsa moyo.+
Zikumbutso+ za Yehova ndi zodalirika,+ zimapatsa nzeru munthu wosadziwa zinthu.+
9 Kuopa+ Yehova n’koyera, ndipo kudzakhalapo kwamuyaya.
Zigamulo+ za Yehova n’zolondola,+ ndipo pa mbali iliyonse zasonyezadi kuti ndi zolungama.+
10 N’zolakalakika kuposa golide, kuposa golide wambiri woyengeka bwino.+
N’zotsekemera* kuposa uchi,+ inde kuposa uchi umene ukukha m’zisa.+
12 Ndani angazindikire yekha zinthu zimene walakwitsa?+
Mundikhululukire machimo amene ndachita mosadziwa.+
13 Komanso mundiletse kuchita modzikuza, ine mtumiki wanu.+
Musalole kuti kudzikuza kundilamulire.+
Pamenepo ndidzakhala wopanda chifukwa,+
Ndipo ndidzakhalabe wopanda milandu yambiri yophwanya malamulo.
14 Mawu a pakamwa panga ndi kusinkhasinkha kwa mtima wanga,+
Zikukondweretseni, inu Yehova, Thanthwe langa+ ndi Wondiwombola.+
Kwa wotsogolera nyimbo. Nyimbo ya Davide.
3 Akumbukire nsembe zanu zonse zimene munapereka monga mphatso.+
Alandire mafuta a nsembe zanu zopsereza.+ [Seʹlah.]
5 Tidzafuula mokondwera chifukwa cha chipulumutso chanu,+
Tidzakweza mbendera zathu m’dzina la Mulungu wathu.+
Yehova akwaniritse zopempha zanu zonse.+
6 Tsopano ndadziwa kuti Yehova amapulumutsa wodzozedwa wake.+
Amamuyankha kuchokera kumwamba kwake koyera,+
Amamupulumutsa ndi dzanja lake lamanja lamphamvu zopulumutsa.+
7 Ena akunena za magaleta* ndipo ena akunena za mahatchi,*+
Koma ife tidzanena za dzina la Yehova Mulungu wathu.+
Kwa wotsogolera nyimbo. Nyimbo ya Davide.
21 Inu Yehova, mfumu ikukondwera mu mphamvu zanu.+
Ndipo idzapitiriza kukondwera mu chipulumutso chanu.+
3 Munaidalitsa ndi kuipatsa zinthu zabwino,+
Ndipo pamutu pake munaika chisoti chachifumu chagolide woyengeka bwino.+
4 Mfumuyo inakupemphani moyo. Ndipo munaipatsadi,+
Munaipatsa masiku ochuluka kuti ikhale mpaka kalekale, ndithu mpaka muyaya.+
6 Mwaichititsa kukhala yodalitsika kwambiri mpaka muyaya.+
Mwaikondweretsa ndi kuisangalatsa pamaso panu.+
7 Pakuti mfumu imakhulupirira Yehova,+
Imakhulupirira kukoma mtima kosatha kwa Wam’mwambamwamba. Iyo siidzagwedezeka.+
9 Mudzawakhalitsa ngati oponyedwa mung’anjo yamoto pa nthawi ya kuonekera kwanu.+
Yehova adzawameza mu mkwiyo wake, ndipo moto udzawanyeketsa.+
10 Mudzawononga ana awo kuwachotsa padziko lapansi,+
Ndipo ana awo mudzawachotsa pakati pa ana a anthu.+
12 Inu mudzawachititsa kutembenuka ndi kuthawa.+
Mudzachita zimenezi ndi zingwe za mauta amene mwakonzekera kuwalasa nawo pankhope.+
Kwa wotsogolera nyimbo: Nyimboyi iimbidwe motsatira Mbawala Yaikazi ya M’bandakucha. Nyimbo ya Davide.
22 Mulungu wanga, Mulungu wanga, mwandisiyiranji ine?+
N’chifukwa chiyani mukuchedwa kundipulumutsa?+
N’chifukwa chiyani simukumva mawu a kubuula kwanga?+
2 Inu Mulungu wanga, ine ndimaitana usana koma simundiyankha.+
Usiku ndimaitanabe, moti sindikukhala chete.+
5 Iwo anali kufuulira inu,+ ndipo anali kupulumuka.+
Anali kudalira inu, ndipo simunawachititse manyazi.+
7 Anthu onse ondiona amandinyodola.+
Iwo amandinyogodola ndi pakamwa pawo, ndipo amapukusa mitu yawo mondinyoza.+ Iwo amati:
9 Pakuti ndinu amene munanditulutsa m’mimba,+
Amene munandichititsa kumva kuti ndine wotetezeka pamene ndinali kuyamwa mabere a mayi anga.+
10 Ndinaponyedwa m’manja mwanu kuchokera m’mimba.+
Kuyambira ndili m’mimba mwa mayi anga, inu mwakhala Mulungu wanga.+
11 Musakhale kutali ndi ine, chifukwa zondisautsa zili pafupi,+
Ndiponso chifukwa ndilibe mthandizi winanso.+
12 Ng’ombe zazing’ono zamphongo zochuluka zandizungulira.+
Nkhunzi zamphamvu za ku Basana zandizinga.+
14 Ndathiridwa pansi ngati madzi.+
Mafupa anga onse alekanalekana.+
Mtima wanga wakhala ngati phula,+
Wasungunuka mkati mwanga.+
15 Mphamvu yanga yauma gwaa, ngati phale.+
Lilime langa lamamatira kunkhama zanga,+
Ndipo mwandikhazika m’fumbi la imfa.+
20 Landitsani moyo wanga ku lupanga,+
Moyo wanga wokhawu umene ndili nawo muulanditse m’kamwa mwa galu.+
21 Ndipulumutseni m’kamwa mwa mkango,+
Ndipo mundiyankhe ndi kundipulumutsa ku nyanga za ng’ombe zamphongo zam’tchire.+
23 Inu oopa Yehova, m’tamandeni!+
Inu nonse mbewu ya Yakobo, m’patseni ulemerero!+
Ndipo muopeni, inu nonse mbewu ya Isiraeli.+
Kapena kunyansidwa ndi nsautso ya munthu wosautsidwa.+
Ndipo sanam’bisire nkhope yake.+
Pamene anamulirira kuti amuthandize, iye anamva.+
25 Chifukwa cha zimene mwachita ndidzakutamandani mumpingo waukulu.+
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga pamaso pa anthu oopa iye.+
26 Ofatsa adzadya ndi kukhuta.+
Ofunafuna Yehova adzamutamanda.+
Mitima yanu ikhale ndi moyo kosatha.+
27 Anthu onse okhala kumalekezero a dziko lapansi adzakumbukira Yehova ndi kubwerera kwa iye.+
Ndipo mafuko onse a anthu a mitundu ina adzagwada pamaso panu.+
29 Anthu onse a padziko lapansi onyada chifukwa cha chuma chawo adzadya ndi kuwerama.+
Onse otsikira kufumbi adzawerama pamaso pake,+
Ndipo palibe amene adzapulumutsa moyo wake.+
31 Adzafika ndi kunena za chilungamo chake,+
Adzauza anthu amene adzabadwe kuti iye ndiye wachita zimenezi.+
Nyimbo ya Davide.
4 Ngakhale ndikuyenda m’chigwa cha mdima wandiweyani,+
Sindikuopa kanthu,+
Pakuti inu muli ndi ine.+
Chibonga chanu ndi ndodo yanu ndi zimene zimandilimbikitsa.+
5 Mumandipatsa chakudya patebulo, pamaso pa anthu ondichitira zoipa.+
Mwadzoza mutu wanga ndi mafuta.+
Chikho changa ndi chodzaza bwino.+
6 Ndithudi, ubwino ndi kukoma mtima kosatha zidzanditsata masiku onse a moyo wanga.+
Ndipo ine ndidzakhala m’nyumba ya Yehova mpaka kalekale.+
Salimo la Davide.
24 Dziko lapansi ndi zonse zili mmenemo ndi za Yehova,+
Nthaka ndi yake pamodzi ndi onse okhala panthakapo.+
4 Aliyense wopanda mlandu m’manja mwake ndi woyera mumtima mwake,+
Amene sanaone Moyo wanga ngati wopanda pake,+
Kapena kulumbira mwachinyengo.+
5 Ameneyo adzalandira madalitso kuchokera kwa Yehova,+
Adzalandira chilungamo kuchokera kwa Mulungu wa chipulumutso chake.+
6 Umenewo ndiwo m’badwo wa amene amafunafuna Mulungu,
M’badwo wa anthu ofunafuna nkhope yanu, inu Mulungu wa Yakobo.+ [Seʹlah.]
7 “Tukulani mitu yanu, inu zipata,+
Ndipo dzitukuleni, inu makomo akale lomwe,+
Kuti Mfumu yaulemerero ilowe!”+
8 “Kodi Mfumu yaulemerero imeneyi ndani?”+
“Ndi Yehova, wanyonga ndi wamphamvu,+
Yehova wamphamvu mu nkhondo.”+
9 “Tukulani mitu yanu, inu zipata,+
Tukulani mitu, inu makomo akale lomwe,
Kuti Mfumu yaulemerero ilowe!”+
10 “Kodi Mfumu yaulemerero imeneyi ndani?”
“Ndi Yehova wa makamu. Iye ndiye Mfumu yaulemerero.”+ [Seʹlah.]
Salimo la Davide.
א [ʼAʹleph]
25 Ndapereka moyo wanga kwa inu Yehova.+
ב [Behth]
2 Inu Mulungu wanga, chikhulupiriro changa chili mwa inu.+
Musalole kuti ndichite manyazi.
Adani anga asakondwere chifukwa cha masautso anga.+
ג [Giʹmel]
3 Ndithudi, palibe aliyense amene adzachita manyazi mwa anthu amene chiyembekezo chawo chili mwa inu.+
Amene adzachite manyazi ndi amene akuchita zinthu mwachinyengo koma osaphula kanthu.+
ד [Daʹleth]
ה [Heʼ]
5 Ndiyendetseni m’choonadi chanu ndi kundiphunzitsa,+
Pakuti inu ndinu Mulungu wa chipulumutso changa.+
ו [Waw]
Chiyembekezo changa chili mwa inu tsiku lonse.+
ז [Zaʹyin]
6 Kumbukirani chifundo chanu,+ inu Yehova, ndi zochita zanu zosonyeza kukoma mtima kosatha.+
Pakuti munayamba kuchita zimenezo kale kwambiri.+
ח [Chehth]
7 Musakumbukire machimo a pa unyamata wanga ndi zolakwa zanga.+
Ndikumbukireni malinga ndi kukoma mtima kwanu kosatha,+
Ndiponso chifukwa cha ubwino wanu, inu Yehova.+
ט [Tehth]
8 Yehova ndi wabwino ndi wolungama.+
N’chifukwa chake amalangiza ochimwa kuti ayende m’njira yoyenera.+
י [Yohdh]
כ [Kaph]
10 M’njira zonse za Yehova muli kukoma mtima kosatha ndi choonadi
ל [Laʹmedh]
11 Chifukwa cha dzina lanu, inu Yehova,+
Mundikhululukire cholakwa changa ngakhale kuti n’chachikulu.+
מ [Mem]
נ [Nun]
13 Moyo wake udzasangalala ndi ubwino wa Mulungu,+
Mbadwa zake zidzatenga dziko lapansi kukhala lawo.+
ס [Saʹmekh]
14 Ubwenzi wolimba ndi Yehova ndi wa anthu amene amamuopa,+
Pangano lakenso ndi la anthu oterowo, ndipo iye amawadziwitsa panganolo.+
ע [ʽAʹyin]
15 Maso anga amayang’ana kwa Yehova nthawi zonse,+
Chifukwa iye ndi amene amawonjola phazi langa mu ukonde.+
פ [Peʼ]
צ [Tsa·dheh]
ר [Rehsh]
19 Onani mmene adani anga achulukira,+
Ndipo chifukwa cha chidani chawo chachikulu, amafuna kundichitira chiwawa.+
ש [Shin]
20 Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa.+
Musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndathawira kwa inu.+
ת [Taw]
21 Mtima wanga wosagawanika ndiponso wowongoka unditeteze,+
Pakuti chiyembekezo changa chili mwa inu.+
22 Inu Mulungu, wombolani Isiraeli m’masautso ake onse.+
Salimo la Davide.
26 Ndiweruzeni,+ inu Yehova, pakuti ine ndayenda mogwirizana ndi mtima wanga wosagawanika,+
Ndipo ndikudalira Yehova kuti ndisagwedezeke.+
4 Sindinakhale pansi pamodzi ndi anthu achinyengo.+
Ndipo sindinayanjane ndi anthu obisa umunthu wawo.+
6 Ndidzasamba m’manja mwanga kusonyeza kuti ndine wopanda cholakwa,+
Ndipo ndidzayenda mozungulira guwa lanu lansembe, inu Yehova,+
7 Kuti mawu anga oyamikira amveke kwambiri,+
Ndi kulengeza ntchito zanu zonse zodabwitsa.+
9 Musachotse moyo wanga pamodzi ndi anthu ochimwa,+
Kapena pamodzi ndi anthu a mlandu wamagazi.+
10 M’manja mwa anthu amenewa muli khalidwe lotayirira,+
Ndipo m’dzanja lawo lamanja mwadzaza ziphuphu.+
Salimo la Davide.
27 Yehova ndiye kuwala+ kwanga ndi chipulumutso changa.+
Ndingaopenso ndani?+
Yehova ndiye malo a chitetezo cha moyo wanga.+
Ndingachitenso mantha ndi ndani?+
2 Anthu ochita zoipa atandiyandikira kuti adye mnofu wanga,+
Popeza kuti iwo ndi ondiukira komanso adani anga,+
Anapunthwa ndi kugwa.+
3 Ngakhale gulu lankhondo litamanga msasa kuti lindiukire,+
Mtima wanga sudzachita mantha.+
Ngakhale nkhondo yolimbana ndi ine itayambika,+
Pameneponso ndidzadalira Mulungu.+
4 Chinthu chimodzi chimene ndapempha kwa Yehova,+
Chimenecho ndi chimene ndimachikhumba,+
N’chakuti, ndikhale m’nyumba ya Yehova masiku onse a moyo wanga,+
Kuti ndione ubwino wa Yehova,+
Komanso kuti ndiyang’ane kachisi wake moyamikira.+
5 Pakuti pa tsiku la tsoka, iye adzandibisa m’malo ake otetezeka.+
Adzandibisa m’malo obisika m’hema wake.+
Adzandiika pamwamba, pathanthwe.+
6 Pamenepo mutu wanga udzakwezeka pamwamba pa adani onse ondizungulira.+
Ndipo ndidzapereka nsembe za kufuula mokondwera pahema wake.+
Ndidzamuimbira nyimbo, ndithu ndidzaimba nyimbo zotamanda Yehova.+
8 Mtima wanga wanena lamulo lanu lakuti: “Ndifunefuneni anthu inu.”+
Ndidzakufunafunani, inu Yehova.+
Musabweze mtumiki wanu mutakwiya.+
Inu mukhale mthandizi wanga.+
Musanditaye ndi kundisiya, inu Mulungu wa chipulumutso changa.+
11 Ndilangizeni, inu Yehova, kuti ndiyende m’njira yanu.+
Nditsogolereni m’njira yowongoka kuti nditetezeke kwa adani anga.
12 Musandipereke kwa adani anga.+
Pakuti mboni zonama zandiukira,+
Chimodzimodzinso munthu wachiwawa.+
13 Ngati ndikanakhala wopanda chikhulupiriro poona ubwino wa Yehova m’dziko la anthu amoyo, ndikanataya chiyembekezo.+
Salimo la Davide.
Inu Thanthwe langa, musatseke makutu anu pamene ine ndikuitana,+
Kuti musakhale chete pamaso panga,+
Kutinso ine ndisafanane ndi amene akutsikira kudzenje la manda.+
2 Imvani mawu anga ochonderera pamene ndikufuulira inu kuti mundithandize,
Pamene ndikukweza manja anga,+ nditayang’ana kumene kuli chipinda chamkati cha m’malo anu opatulika.+
3 Musandikokolole pamodzi ndi anthu oipa komanso anthu amene amachita zopweteka anzawo,+
Anthu amene amalankhula mawu amtendere ndi anzawo+ koma m’mitima yawo muli zinthu zoipa.+
4 Muwabwezere mogwirizana ndi zochita zawo,+
Mogwirizana ndi kuipa kwa zochita zawo.+
Abwezereni mogwirizana ndi ntchito za manja awo.+
Abwezereni zochita zawo.+
5 Pakuti iwo salabadira zochita za Yehova,+
Kapena ntchito za manja ake.+
Mulungu sadzawamanga koma adzawapasula.
6 Adalitsike Yehova, chifukwa wamva kuchonderera kwanga.+
7 Yehova ndiye mphamvu yanga+ ndi chishango changa.+
Mtima wanga umam’khulupirira.+
Iye wandithandiza, moti mtima wanga ukukondwera.+
Ndidzamutamanda mwa kumuimbira nyimbo yanga.+
8 Yehova ndiye mphamvu kwa anthu ake,+
Iye ndi malo achitetezo odzetsa chipulumutso chachikulu kwa wodzozedwa wake.+
9 Pulumutsani anthu anu, ndipo dalitsani cholowa chanu.+
Mukhale m’busa wawo ndipo muwanyamule mpaka kalekale.+
Salimo la Davide.
29 M’patseni Yehova, inu amphamvu,*
M’patseni Yehova ulemerero ndipo vomerezani kuti iye ndi wamphamvu.+
2 M’patseni Yehova ulemerero woyenera dzina lake.+
Weramirani Yehova mutavala zovala zopatulika zokongola.+
3 Liwu la Yehova lili pamwamba pa madzi,*+
Liwu la Mulungu waulemerero+ lagunda ngati bingu.+
Yehova ali pamwamba pa madzi ambiri.+
5 Liwu la Yehova likuthyola mitengo ya mkungudza,
Yehova akuthyolathyola mitengo ya mkungudza ya ku Lebanoni.+
6 Iye akuichititsa kudumphadumpha ngati mwana wa ng’ombe,+
Lebanoni ndi Sirioni+ akudumphadumpha ngati ana a ng’ombe zakutchire.
7 Liwu la Yehova likutulutsa malawi a moto.+
8 Liwu la Yehova likuchititsa chipululu kuphiriphitha,+
Yehova akuchititsa chipululu cha Kadesi+ kuphiriphitha.
9 Liwu la Yehova likuchititsa mbawala zazikazi kuphiriphitha ndi ululu wa pobereka,+
Ndipo likufafaniza nkhalango.+
M’kachisi wake aliyense akunena kuti: “Ulemerero ndi wa Mulungu!”+
10 Yehova wakhala pampando wake wachifumu pamwamba pa chigumula,*+
Ndipo Yehova ndi mfumu mpaka kalekale.+
Nyimbo ndi Salimo la Davide lotsegulira nyumba.+
30 Ndidzakutamandani inu Yehova, pakuti mwandipulumutsa,+
Ndipo simunalole kuti adani anga akondwere ndi kusautsika kwanga.+
2 Inu Yehova Mulungu wanga, ndinafuulira kwa inu kuti mundithandize ndipo munandichiritsa.+
4 Imbani nyimbo zotamanda Yehova, inu okhulupirika ake,+
5 Chifukwa mkwiyo wa Mulungu sukhalitsa pa munthu,+
Koma kukoma mtima kwake ndi kwa moyo wonse.+
Usiku kumakhala kulira,+ koma m’mawa kumakhala kufuula ndi chisangalalo.+
7 Inu Yehova, chifukwa chakuti munandikomera mtima munakhazikitsa mwamphamvu phiri langa.+
Pamene munabisa nkhope yanu, ndinasokonezeka.+
9 Kodi magazi anga angakhale ndi phindu lanji ngati nditatsikira kudzenje la manda?+
Kodi fumbi lidzakutamandani?+ Kodi lidzalengeza kuti inu ndinu woona?+
11 Mwasintha kulira kwanga kuti kukhale kuvina.+
Mwandivula chiguduli* changa ndipo mwandiveka chisangalalo,+
12 Kuti mtima wanga uimbe nyimbo zokutamandani ndipo usakhale chete.+
Inu Yehova Mulungu wanga, ndidzakutamandani mpaka kalekale.+
Kwa wotsogolera nyimbo. Nyimbo ya Davide.
31 Ndathawira kwa inu Yehova.+
Musalole kuti ndichite manyazi.+
Ndipulumutseni chifukwa cha chilungamo chanu.+
2 Tcherani khutu lanu kwa ine.+
Ndilanditseni mofulumira.+
Mukhale thanthwe lolimba kwa ine,+
Mukhale nyumba ya mpanda wolimba kuti mundipulumutse.+
3 Pakuti inu ndinu thanthwe langa ndi malo anga achitetezo.+
Chifukwa cha dzina lanu+ mudzanditsogolera ndi kundilozera njira.+
7 Ndidzakondwera ndi kusangalala chifukwa cha kukoma mtima kwanu kosatha,+
Pakuti mwaona kusautsika kwanga.+
Mwadziwa zowawa zimene zandigwera,+
8 Simunandipereke m’manja mwa adani.+
Mwapondetsa phazi langa pamalo otakasuka.+
9 Ndikomereni mtima inu Yehova, pakuti ndasautsika kwambiri.+
Diso langa lafooka chifukwa cha chisoni,+ chimodzimodzinso moyo wanga ndi m’mimba mwanga.+
10 Chifukwa cha chisoni, moyo wanga watha,+
Ndipo chifukwa cha kuusa moyo kwanga, zaka zanga zafika kumapeto.+
Chifukwa cha zolakwa zanga, mphamvu zanga zafooka,+
Ndipo mafupa anga afooka.+
11 Ndakhala chitonzo+ pamaso pa onse odana nane,+
Ndipo kwa anthu oyandikana nawo ndakhala chitonzo chachikulu,+
Kwa anthu ondidziwa ndakhala woopsa.+
Akandiona ndili panja amandithawa.+
12 Ndaiwalidwa ngati munthu wakufa amene anthu sakumukumbukiranso.+
Ndakhala ngati chiwiya chosweka.+
13 Ndamva zinthu zoipa zimene anthu ambiri akunena,+
Ndamva zochititsa mantha kuchokera kumbali zonse.+
Akasonkhana pamodzi kundichitira upo,+
Amakonza chiwembu kuti achotse moyo wanga.+
14 Koma ine chikhulupiriro changa chili mwa inu Yehova.+
Ndipo ndikunena kuti: “Inu ndinu Mulungu wanga.”+
17 Inu Yehova, musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndaitana pa dzina lanu.+
Anthu oipa achite manyazi.+
Akhale chete m’Manda.+
18 Milomo yachinyengo isowe chonena,+
Milomo imene ikulankhula motsutsana ndi wolungama,+ yosadziletsa pa kudzikweza ndi kunyoza ena.+
19 Ubwino wanu,+ umene mwasungira anthu okuopani ndi wochuluka kwambiri!+
Ubwino umenewu mwapereka kwa anthu othawira kwa inu.
Mwaupereka kwa iwo, ana a anthu akuona.+
20 Mudzawabisa m’malo otetezeka pafupi ndi inu,+
Kuwachotsa pamaso pa anthu amene asonkhana pamodzi kuti awachitire chiwembu.+
Mudzawabisa mumsasa wanu kwa anthu ofuna kukangana nawo.+
22 Koma ine nditapanikizika ndinati:+
“Ndidzafafanizidwa kuchoka pamaso panu.”+
Ndithudi mwamva kuchonderera kwanga pamene ndinali kufuulira kwa inu kupempha thandizo.+
23 Kondani Yehova, inu nonse okhulupirika ake.+
Yehova amateteza okhulupirika,+
Koma aliyense wodzikuza adzamulanga mowirikiza.+
Salimo la Davide. Masikili.*
32 Wodala ndi munthu amene wakhululukidwa zolakwa zake, amene machimo ake aphimbidwa.+
3 Pamene ndinakhala chete osaulula machimo anga, mafupa anga anafooka, chifukwa tsiku lonse ndinali kuvutika mumtima mwanga.+
4 Pakuti dzanja lanu linali kundilemera usana ndi usiku.+
Mphamvu zanga zinauma ngati madzi m’nyengo yotentha ya chilimwe.+ [Seʹlah.]
5 Pamapeto pake ndinaulula tchimo langa kwa inu, ndipo sindinabise cholakwa changa.+
Ndinati: “Ndidzaulula kwa Yehova machimo anga.”+
Ndipo inu munandikhululukira zolakwa zanga ndi machimo anga.+ [Seʹlah.]
6 Pa chifukwa chimenechi, aliyense wokhulupirika adzapemphera kwa inu,+
Pa nthawi imene inu mungapezeke.+
Ndipo madzi ambiri osefukira sadzamukhudza ngakhale pang’ono.+
7 Ndinu malo anga obisalamo, mudzanditeteza ku masautso.+
Mudzachititsa kuti chisangalalo chindizungulire pamene mukundipulumutsa.+ [Seʹlah.]
8 Inu munati: “Ndidzakupatsa nzeru ndi kukulangiza njira yoti uyendemo.+
Ndidzakupatsa malangizo ndi kukuyang’anira.+
9 Anthu inu, musakhale ngati hatchi kapena nyulu* yosazindikira,+
Imene munthu amachita kuimanga chingwe chapakamwa ndi chapamutu kuti athetse kupulupudza kwake,+
Ndi kuti aiyandikire.”+
10 Zopweteka za woipa ndi zambiri.
Koma wokhulupirira Yehova+ amazunguliridwa ndi kukoma mtima kosatha.+
11 Inu olungama, kondwerani chifukwa cha zimene Yehova wachita ndipo sangalalani.+
Fuulani ndi chisangalalo inu nonse owongoka mtima.+
33 Fuulani mosangalala chifukwa cha Yehova, inu nonse olungama.+
M’poyenera kuti owongoka mtima atamande Mulungu.+
3 Muimbireni nyimbo yatsopano.+
Muimbireni choimbira cha zingwe ndi mtima wonse ndi kufuula mosangalala.+
5 Iye amakonda chilungamo ndi chiweruzo chosakondera.+
Dziko lapansi ladzaza ndi kukoma mtima kosatha kwa Yehova.+
6 Kumwamba kunalengedwa ndi mawu a Yehova,+
Ndipo makamu ake onse analengedwa ndi mpweya wa m’kamwa mwake.+
7 Anasonkhanitsa madzi a m’nyanja ngati wachita kuwatchinga ndi khoma,+
Anaika madzi amphamvu m’nyumba zosungiramo zinthu.
8 Onse okhala padziko lapansi aope Yehova.+
Anthu onse okhala panthaka ya dziko lapansi achite naye mantha.+
11 Zolinga za Yehova zidzakhalapo mpaka kalekale.+
Maganizo a mumtima mwake adzakhalapo ku mibadwomibadwo.+
12 Wodala ndi mtundu umene Mulungu wawo ndi Yehova,+
Anthu amene iye wawasankha kukhala cholowa chake.+
16 Palibe mfumu imene inapulumuka chifukwa cha kukula kwa gulu lake lankhondo.+
Munthu wamphamvu sapulumuka chifukwa cha kuchuluka kwa mphamvu zake.+
17 Hatchi siingabweretse chipulumutso,+
Siingapulumutse munthu chifukwa cha kuchuluka kwa mphamvu zake.+
18 Taonani! Diso la Yehova lili pa anthu amene amamuopa,+
Amene amayembekezera kukoma mtima kwake kosatha,+
19 Kuti apulumutse moyo wawo ku imfa,+
Ndi kuwasunga ndi moyo pa nthawi ya njala.+
Salimo la Davide, pa nthawi imene anachita zinthu ngati wamisala+ pamaso pa Abimeleki* moti anam’pitikitsa ndipo Davideyo anathawa.
א [ʼAʹleph]
ב [Behth]
ג [Giʹmel]
ד [Daʹleth]
ה [Heʼ]
ז [Zaʹyin]
ח [Chehth]
ט [Tehth]
8 Anthu inu, talawani ndipo muona kuti Yehova ndi wabwino.+
Wodala ndi munthu wamphamvu amene amathawira kwa iye.+
י [Yohdh]
כ [Kaph]
10 Mikango yamphamvu ingakhale ndi chakudya chochepa ndipo ingamve njala.+
Koma ofunafuna Yehova sadzasowa chilichonse chabwino.+
ל [Laʹmedh]
מ [Mem]
נ [Nun]
ס [Saʹmekh]
ע [ʽAʹyin]
פ [Peʼ]
16 Nkhope ya Yehova imakwiyira anthu ochita zoipa,+
Kuti dzina lawo lisatchulidwenso padziko lapansi.+
צ [Tsa·dhehʹ]
ק [Qohph]
18 Yehova ali pafupi ndi anthu a mtima wosweka.+
Ndipo odzimvera chisoni mumtima mwawo amawapulumutsa.+
ר [Rehsh]
ש [Shin]
ת [Taw]
22 Yehova amawombola moyo wa atumiki ake.+
Ndipo palibe aliyense wothawira kwa iye amene adzapezeka wolakwa.+
Salimo la Davide.
35 Weruzani mlandu wanga inu Yehova, motsutsana ndi adani anga.+
Menyani nkhondo ndi kugonjetsa amene akumenyana ndi ine.+
2 Tengani chishango chaching’ono ndi chishango chachikulu,+
Ndipo bwerani kuti mundithandize.+
3 Tengani mkondo ndi nkhwangwa ya pankhondo kuti mukumane ndi anthu amene akundilondalonda.+
Uzani moyo wanga kuti: “Ine ndine chipulumutso chako.”+
4 Amene akufunafuna moyo wanga achite manyazi ndi kunyozeka.+
Amene akundikonzera chiwembu muwabweze ndipo athedwe nzeru.+
7 Iwo andikumbira mbuna popanda chifukwa ndi kuikapo ukonde,+
Akumba mbunazo kuti ndigweremo ngakhale kuti sindinalakwe.+
8 Awonongeke pamene iwo sakuyembekezera,+
Akodwe mu ukonde umene atchera okha.+
Agweremo ndi kuwonongeka.+
10 Ndinene ndi mtima wanga wonse kuti:+
“Inu Yehova, ndani angafanane ndi inu,+
Amene mumalanditsa wosautsika m’manja mwa munthu wamphamvu kuposa iyeyo,+
Amene mumalanditsa wozunzika ndi wosauka m’manja mwa munthu amene akumulanda zinthu zake?”+
13 Iwo akadwala ndinali kuvala chiguduli,+
Ndinali kusautsa moyo wanga mwa kusala kudya.+
Ndipo mapemphero anga anali kubwerera kwa ine osayankhidwa.+
14 Chifukwa cha mnzanga ndiponso m’bale wanga,+
Ndinamva chisoni kwambiri ngati munthu wolira maliro a mayi ake.+
Ndinawerama chifukwa cha chisoni.
15 Atandiona ndikuyenda motsimphina anasangalala ndipo anasonkhana pamodzi.+
Anasonkhana pamodzi kuti alimbane nane.+
Anandimenya pamene sindinali kuyembekezera.+
Anandikhadzulakhadzula ndipo sanakhale chete.+
17 Inu Yehova, kodi mudzayang’anira zimenezi kufikira liti?+
Ndipulumutseni kwa anthu ofuna kundiwononga,+
Pulumutsani moyo wanga+ ku mikango yamphamvu.
19 Musalole kuti anthu amene amadana ndi ine popanda chifukwa akondwere ndi kusautsika kwanga.+
Ndipo musalole kuti anthu amene amandida popanda chifukwa anditsinzinire diso.+
20 Iwo salankhula mawu amtendere,+
Koma amakonzera chiwembu anthu ofatsa a padziko lapansi,
Kuti awachitire zachinyengo.+
23 Nyamukani ndi kukhala maso kuti mundichitire chilungamo,+
Chitani zimenezi inu Mulungu wanga Yehova, kuti muweruze mlandu wanga.+
24 Inu Yehova Mulungu wanga, mundiweruze mogwirizana ndi chilungamo chanu,+
Musalole kuti adani anga akondwere ndi kusautsika kwanga.+
25 Musalole kuti mumtima mwawo anene kuti: “Eya! Izi ndi zimene timafuna.”+
Ndipo asanene kuti: “Tamumeza.”+
26 Onse amene akukondwera ndi tsoka langa,+
Achite manyazi ndi kuthedwa nzeru.+
Onse odzikweza pamaso panga achite manyazi+ ndi kutsitsidwa.+
27 Onse amene amakonda chilungamo changa afuule mosangalala ndi kukondwera.+
Nthawi zonse azinena kuti:+
“Alemekezeke Yehova, amene amasangalala mtumiki wake akakhala pa mtendere.”+
Kwa wotsogolera nyimbo. Salimo la Davide, mtumiki wa Yehova.
3 Mawu a pakamwa pake ndi opweteka ndi achinyengo.+
Wasiya kugwiritsa ntchito nzeru zomuthandiza kuchita zinthu zabwino.+
4 Ali pabedi lake amakonza chiwembu kuti apweteke anzake.+
Amaima panjira yoipa.+
Sapewa kuchita zinthu zoipa.+
6 Inu Mulungu, chilungamo chanu chili ngati mapiri anu.+
Chiweruzo chanu ndi chozama kwambiri ngati madzi akuya.+
Inu Yehova, mumapulumutsa munthu ndiponso nyama.+
7 Inu Mulungu, kukoma mtima kwanu kosatha ndi kwamtengo wapatali!+
Ndipo ana a anthu amabisala mu mthunzi wa mapiko anu.+
8 Amadya ndi kukhuta chakudya chonona m’nyumba mwanu.+
Ndipo mumawamwetsa mumtsinje wa zosangalatsa zanu zambiri.+
10 Pitirizani kusonyeza kukoma mtima kwanu kosatha kwa anthu okudziwani,+
Ndiponso chilungamo chanu kwa anthu owongoka mtima.+
11 Musalole kuti phazi la anthu odzikweza lindipondereze.+
Ndipo musalole dzanja la anthu oipa kundipitikitsa kuti ndikhale wothawathawa.+
Salimo la Davide.
א [ʼAʹleph]
ב [Behth]
3 Khulupirira Yehova ndipo chita zabwino.+
Khala padziko lapansi, ndipo khala wokhulupirika m’zochita zako zonse.+
ג [Giʹmel]
6 Iye adzaonetsa poyera kulungama kwako kuti kuunike ngati kuwala,+
Adzaonetsa poyera chilungamo chako kuti chiwale ngati usana.+
ד [Daʹleth]
7 Khala chete pamaso pa Yehova,+
Ndipo umuyembekezere ndi mtima wako wonse.+
Usapse mtima ndi aliyense amene zinthu zikumuyendera bwino,+
Munthu amene akukwaniritsa zolinga zake zoipa.+
ה [Heʼ]
ו [Waw]
10 Patsala kanthawi kochepa, woipa sadzakhalakonso.+
Udzayang’ana pamene anali kukhala, ndipo sadzapezekapo.+
ז [Zaʹyin]
ח [Chehth]
14 Oipa asolola lupanga ndipo akunga uta wawo,+
Kuti agwetse osautsika ndi osauka,+
Kuti aphe anthu amene njira zawo ndi zowongoka.+
ט [Tehth]
16 Zinthu zochepa za munthu wolungama ndi zabwino+
Kusiyana ndi zinthu zochuluka za anthu ambiri oipa.+
י [Yohdh]
כ [Kaph]
20 Pakuti anthu oipa adzatheratu onse,+
Ndipo adani a Yehova adzafanana ndi busa la msipu wobiriwira mochititsa kaso.
ל [Laʹmedh]
21 Munthu woipa amakongola zinthu za ena koma osabweza,+
Koma wolungama amakomera mtima ena ndipo amapereka mphatso.+
22 Anthu amene Mulungu akuwadalitsa adzalandira dziko lapansi,+
Koma amene wawatemberera adzaphedwa.+
מ [Mem]
נ [Nun]
25 Ndinali mwana, ndipo tsopano ndakula,+
Koma sindinaonepo munthu aliyense wolungama atasiyidwa,+
Kapena ana ake akupemphapempha chakudya.+
26 Tsiku lililonse amakomera mtima ena ndi kuwakongoza zinthu,+
Ndipo ana ake adzalandira madalitso.+
ס [Saʹmekh]
פ [Peʼ]
30 Pakamwa pa munthu wolungama pamalankhula zinthu zanzeru,+
Ndipo lilime lake limalankhula zinthu zachilungamo.+
צ [Tsa·dhehʹ]
33 Koma Yehova sadzasiya wolungama m’manja mwa woipayo,+
Ndipo pamene wolungamayo akuweruzidwa, Mulungu sadzamuona monga wolakwa.+
ק [Qohph]
34 Yembekezera Yehova, ndi kusunga njira zake,+
Ndipo adzakukweza kuti ulandire dziko lapansi.+
Pamene oipa akuphedwa, iwe udzaona.+
ר [Rehsh]
35 Ine ndaona munthu woipa, wolamulira mwankhanza+
Zinthu zikumuyendera bwino ngati mtengo waukulu wa masamba obiriwira bwino panthaka yake.+
ש [Shin]
37 Ona munthu wosalakwa ndipo yang’anitsitsa munthu wolungama,+
Pakuti tsogolo la munthu ameneyu ndi lamtendere.+
ת [Taw]
39 Chipulumutso cha anthu olungama chimachokera kwa Yehova.+
Iye ndi malo awo achitetezo champhamvu pa nthawi ya nsautso.+
40 Yehova adzawathandiza ndi kuwapulumutsa.+
Adzawapulumutsa kwa anthu oipa ndi kuwalanditsa,+
Chifukwa athawira kwa iye.+
Nyimbo ya Davide ya chikumbutso.
3 Palibe pabwino m’thupi langa chifukwa cha chidzudzulo chanu.+
Ndipo m’mafupa anga mulibe mtendere chifukwa cha tchimo langa.+
6 Ndasokonezeka ndipo ndawerama kwambiri chifukwa cha chisoni changa.+
Ndayenda uku ndi uku tsiku lonse ndili wachisoni.+
11 Anthu amene anali kundikonda ndiponso anzanga aima patali chifukwa cha kuvutika kwanga,+
Ndipo mabwenzi anga apamtima anditalikira.+
12 Anthu amene akufuna kundiwononga anditchera misampha,+
Amene akufuna kundivulaza akulankhula motsutsana nane,+
Ndipo amakhala akukonza zachinyengo tsiku lonse.+
13 Koma ine ndakhala ngati munthu wogontha, sindikumvetsera,+
Ndakhala ngati munthu wosalankhula, sindikutsegula pakamwa.+
14 Ndakhala ngati munthu wosamva,
Sindikulankhula zotsutsana nawo.
20 Iwo anali kundibwezera choipa m’malo mwa chabwino,+
Ndikamayesetsa kuchita chabwino anali kunditsutsa.+
Kwa wotsogolera nyimbo pa Yedutuni.*+ Nyimbo ya Davide.
39 Ine ndinati: “Ndidzatchinjiriza njira zanga,+
Kuti ndisachimwe ndi lilime langa.+
Ndidzamanga pakamwa panga kuti patetezeke,+
Nthawi zonse pamene woipa ali pamaso panga.”+
2 Ndinakhala chete osalankhula kanthu.+
Ndinakhala phee osanena ngakhale zinthu zabwino,+
Ndipo ndinanyalanyaza ululu wanga.
4 “Inu Yehova, ndidziwitseni za kufulumira kwa chimaliziro changa,+
Ndiponso kuti masiku anga ndi ochepa motani,+
Kuti ndidziwe kufupika kwa moyo wanga.+
5 Taonani! Mwachepetsa masiku anga.+
Ndipo nthawi ya moyo wanga si kanthu pamaso panu.+
Ndithudi, munthu aliyense ngakhale atakhala wamphamvu bwanji, sali kanthu koma ali ngati mpweya wotuluka m’mphuno.+ [Seʹlah.]
6 Zoonadi, munthu amayenda ngati chithunzithunzi.+
Ndithudi, anthu amapokosera pachabe.+
Munthu amaunjika zinthu ndipo sadziwa amene adzazitute.+
11 Mwa kudzudzula cholakwa, mwawongolera munthu,+
Ndipo mwawononga zinthu zake zamtengo wapatali ngati mmene njenjete*+ imachitira.
Ndithudi, munthu aliyense ali ngati mpweya.+ [Seʹlah.]
12 Imvani pemphero langa, inu Yehova,
Ndipo tcherani khutu pamene ndikufuula kupempha thandizo.+
Musandinyalanyaze pamene ndikugwetsa misozi.+
Pakuti ndine mlendo wanu,+
Mlendo wokhala nanu monga anachitira makolo anga onse.+
Kwa wotsogolera nyimbo. Salimo la Davide.
40 Ndinayembekezera Yehova ndi mtima wonse,+
Choncho iye anatchera khutu kwa ine ndipo anamva kufuula kwanga kopempha thandizo.+
2 Iye ananditulutsanso m’dzenje la madzi a mkokomo,+
Ananditulutsa m’chithaphwi cha matope.+
Kenako anapondetsa phazi langa pathanthwe.+
Anandiyendetsa panthaka yolimba.+
3 Komanso anaika mawu a nyimbo yatsopano m’kamwa mwanga,
Nyimbo yotamanda Mulungu wathu.+
Ambiri adzaona zimenezi ndipo adzachita mantha,+
Iwo adzakhulupirira Yehova.+
4 Wodala ndi munthu wamphamvu amene amakhulupirira Yehova,+
Munthu amene sanacheukire anthu otsutsa,
Kapena anthu amene anapatukira m’njira za mabodza.+
5 Inu Yehova Mulungu wanga, mwatichitira zinthu zambiri zodabwitsa,+
Ndipo mumatiganizira.+
Palibe angafanane ndi inu.+
Ndikafuna kulankhula ndi kunena za zodabwitsazo,
Zimachuluka kwambiri moti sindingathe kuzifotokoza.+
6 Nsembe ndiponso zopereka, simunasangalale nazo.+
Inu munatsegula makutu anga.+
Simunapemphe nsembe yopsereza ndi nsembe yamachimo.+
8 Ndimakondwera ndi kuchita chifuniro chanu, inu Mulungu wanga,+
Ndipo chilamulo chanu chili mumtima mwanga.+
9 Ndanena za uthenga wabwino wachilungamo mumpingo waukulu.+
Onani! Sindinatseke pakamwa panga.+
Inu Yehova, mukudziwa bwino zimenezi.+
10 Chilungamo chanu sindinachibise mumtima mwanga.+
Ndinalengeza za kukhulupirika kwanu ndi chipulumutso chanu.+
Sindinabise kukoma mtima kwanu kosatha ndi choonadi chanu mumpingo waukulu.”+
11 Inu Yehova, musasiye kundimvera chisoni.+
Kukoma mtima kwanu kosatha komanso choonadi chanu zinditeteze nthawi zonse.+
12 Pakuti masoka anandizungulira moti sindinathe kuwawerenga.+
Zolakwa zanga zochuluka zinandifikira modzidzimutsa moti sindinathe kuziona mmene zinachulukira.+
Zinachuluka kwambiri kuposa tsitsi la kumutu kwanga,+
Ndipo ndinataya mtima.+
14 Onse amene akufunafuna moyo wanga kuti aufafanize+
Achite manyazi ndi kuthedwa nzeru.+
Amene akukondwera ndi tsoka langa abwerere ndipo anyazitsidwe.+
16 Onse amene akufunafuna inu,+
Akondwere ndi kusangalala mwa inu.+
Onse amene amakonda chipulumutso chanu,+
Nthawi zonse azinena kuti: “Yehova alemekezeke.”+
17 Koma ine ndasautsika ndipo ndasauka.+
Yehova amandiwerengera.+
Inu ndinu thandizo langa ndi Wopereka chipulumutso kwa ine.+
Inu Mulungu wanga musachedwe.+
Kwa wotsogolera nyimbo. Nyimbo ya Davide.
41 Wodala ndi munthu amene amachita zinthu moganizira munthu wonyozeka.+
Pa tsiku la tsoka, Yehova adzamupulumutsa.+
2 Yehova adzamuteteza ndi kumusunga ali wamoyo.+
Adzatchedwa wodala padziko lapansi.+
Ndipo Mulungu sangamupereke kwa adani ake.+
3 Yehova adzachirikiza wonyozekayo pamene akudwala pabedi lake.+
Mudzamusamalira bwino kwambiri pamene akudwala.+
5 Adani anga amanena zoipa zokhazokha za ine kuti:+
“Kodi ameneyu afa liti kuti dzina lake lifafanizike?”
6 Wina akabwera kudzandiona, amalankhula zabodza kuchokera mumtima mwake.+
Amasonkhanitsa nkhani zoipa.
Akatero amachoka, ndipo kunjako amauza ena zabodza zokhudza ine.+
7 Mogwirizana, onse amene amadana nane amanong’onezana kuti andiukire.+
Amandikonzera chiwembu kuti andichitire zinthu zoipa. Iwo amati:+
9 Koma munthu amene ndinali kukhala naye mwamtendere, amene ndinali kumukhulupirira,+
Munthu amene anali kudya chakudya changa,+ wakweza chidendene chake kundiukira.+
11 Mukatero ndidziwa kuti mwasangalala nane,
Chifukwa mdani wanga sadzafuula mosangalala kuti wandipambana.+
12 Koma ine mwandichirikiza chifukwa cha mtima wanga wosagawanika,+
Ndipo mudzandiika pamaso panu mpaka kalekale.+
BUKU LACHIWIRI
(Masalimo 42 – 72)
Kwa wotsogolera nyimbo. Masikili* ya ana a Kora.+
42 Monga mmene mbawala yaikazi imalakalakira mitsinje ya madzi,
Moyo wanganso ukulakalaka inu Mulungu wanga.+
2 Moyo wanga ukulakalaka Mulungu,+ ukulakalaka Mulungu wamoyo.+
Ndidzapita liti kunyumba ya Mulungu kukaonekera pamaso pake?+
3 Misozi yanga yasanduka chakudya changa usana ndi usiku,+
Pamene anthu akundifunsa tsiku lonse kuti: “Mulungu wako ali kuti?”+
4 Ndidzakumbukira zinthu zakale ndipo moyo wanga udzavutika pokumbukira zimenezo.+
Pakuti ndinali kuyenda ndi khwimbi la anthu,
Ndinali kuyenda pang’onopang’ono patsogolo pawo kupita kunyumba ya Mulungu,+
Tinali kufuula mosangalala ndi kuyamika Mulungu.+
Khamu la anthu okondwerera madyerero linali kunditsatira.+
5 N’chifukwa chiyani ukutaya mtima, moyo wangawe?+
Ndipo n’chifukwa chiyani ukusautsika mkati mwanga?+
Yembekezera Mulungu,+
Ndipo ndidzamutamanda pakuti iye ndiye mpulumutsi wanga wamkulu.+
6 Inu Mulungu wanga, ine ndataya mtima.+
N’chifukwa chake ndakumbukira inu,+
Pamene ndili m’dziko la Yorodano ndi m’mapiri a Herimoni,+
Pamene ndili m’phiri laling’ono.+
7 Madzi akuya akufuulira madzi akuya,
Kudzera mu mkokomo wa madzi otumphuka.
Mafunde anu onse amphamvu,+
Andimiza.+
8 Masana Yehova adzalamula kukoma mtima kwake kosatha kuti kufike pa ine,+
Ndipo usiku ndidzaimba za iye.+
Ndidzapemphera kwa Mulungu wondipatsa moyo.+
9 Ndidzauza Mulungu, thanthwe langa kuti:+
“N’chifukwa chiyani mwandiiwala?+
Ndikuyenderanji wachisoni chifukwa choponderezedwa ndi mdani wanga?”+
10 Odana nane akunditonza kwambiri moti zikungokhala ngati mafupa anga aphwanyidwa,+
Pakuti anthu akundifunsa tsiku lonse kuti: “Mulungu wako ali kuti?”+
11 N’chifukwa chiyani ukutaya mtima, moyo wangawe?+
Ndipo n’chifukwa chiyani ukusautsika mkati mwanga?+
Yembekezera Mulungu,+
Ndipo ndidzamutamanda pakuti iye ndiye mpulumutsi wanga wamkulu ndiponso ndiye Mulungu wanga.+
Weruzani mlandu wanga+ motsutsana ndi mtundu wosakhulupirika.
Ndipulumutseni kwa munthu wachinyengo ndi wochita zosalungama.+
2 Pakuti inu ndinu Mulungu wanga, ndinu malo anga achitetezo.+
N’chifukwa chiyani mwanditaya?
Ndikuyenderanji wachisoni chifukwa choponderezedwa ndi mdani wanga?+
3 Tumizani kuwala kwanu ndi choonadi chanu.+
Zimenezi zinditsogolere.+
Zindifikitse kuphiri lanu lopatulika ndi kuchihema chanu chachikulu.+
4 Ndidzapita paguwa lansembe la Mulungu,+
Kwa Mulungu amene amandikondweretsa ndi kundisangalatsa.+
Ndipo ndidzakutamandani ndi zeze, inu Mulungu, Mulungu wanga.+
5 N’chifukwa chiyani ukutaya mtima, moyo wangawe?+
Ndipo n’chifukwa chiyani ukusautsika mkati mwanga?
Yembekezera Mulungu,+
Ndipo ndidzamutamanda pakuti iye ndiye mpulumutsi wanga wamkulu ndi Mulungu wanga.+
Kwa wotsogolera nyimbo. Salimo la ana a Kora.+ Masikili.*
44 Inu Mulungu, ife tamva ndi makutu athu,
Makolo athu anatifotokozera+
Ntchito zimene inu munachita m’masiku awo,+
M’masiku akale.+
2 Munapitikitsa anthu a mitundu ina ndi dzanja lanu,+
Ndipo m’malo mwawo munakhazikitsa anthu anu.+
Munagonjetsa mitundu ya anthu ndi kuipitikitsa.+
3 Pakuti iwo sanatenge dzikolo chifukwa cha lupanga lawo,+
Ndipo si mkono wawo umene unawabweretsera chipulumutso.+
Koma chinabwera ndi dzanja lanu lamanja,+ mkono wanu ndi kuwala kwa nkhope yanu,
Chifukwa munakondwera nawo.+
7 Ndinu amene munatipulumutsa kwa adani athu,+
Ndipo munanyazitsa anthu amene amadana nafe kwambiri.+
10 Mwachititsa kuti tithawe pamaso pa adani athu,+
Ndipo anthu odana nafe kwambiri afunkha zinthu zathu.+
11 Mwatipereka kwa adani athu kuti atidye ngati nkhosa,+
Ndipo mwatimwaza pakati pa anthu a mitundu ina.+
13 Mwatisandutsa chitonzo kwa anthu oyandikana nafe,+
Mwatisandutsa chinthu chonyozeka ndi choseketsa kwa onse otizungulira.+
14 Mwatisandutsa mwambi pakati pa anthu a mitundu ina,+
Mwatisandutsa anthu amene anthu a mitundu inawo akuwapukusira mitu.+
15 Zondichititsa manyazi zili pamaso panga tsiku lonse,
Ndipo manyazi aphimba nkhope yanga,+
16 Chifukwa cha mawu a munthu wonditonza ndi wolankhula zachipongwe,
Ndiponso chifukwa cha mdani wanga ndi wofuna kundibwezera choipa.+
18 Mitima yathu sinakhale yosakhulupirika n’kuchoka panjira yanu,+
Ndipo mapazi athu sanapatuke panjira yanu.+
20 Ngati tikanaiwala dzina la Mulungu wathu,
Kapena kupemphera kwa mulungu wachilendo titakweza manja athu,+
21 Kodi Mulungu sakanafufuza zimenezi?+
Pakuti iye amadziwa zinsinsi za mumtima.+
24 N’chifukwa chiyani mukubisabe nkhope yanu?
N’chifukwa chiyani mukuiwala masautso athu ndi kuponderezedwa kwathu?+
Kwa wotsogolera nyimbo pa Maluwa.* Salimo la ana a Kora. Masikili.* Nyimbo yonena za akazi okondedwa.
45 Mtima wanga wagalamuka chifukwa cha nkhani yosangalatsa.+
Ine ndikuti: “Nyimbo yangayi ikunena za mfumu.”+
Lilime langa likhale ngati cholembera+ cha wokopera malemba waluso.+
2 Ndiwedi wokongola kwambiri kuposa ana a anthu.+
Mawu otuluka m’kamwa mwako ndi osangalatsadi.+
N’chifukwa chake Mulungu adzakupatsa madalitso mpaka kalekale.+
4 Ndipo upambane mu ulemerero wako.+
Kwera pahatchi yako chifukwa cha choonadi, kudzichepetsa ndi chilungamo,+
Ndipo dzanja lako lamanja lidzakulangiza mu zinthu zochititsa mantha.+
6 Mulungu ndiye mpando wako wachifumu mpaka kalekale, ndithu mpaka muyaya.+
Ndodo yako yachifumu ndiyo ndodo yachilungamo.+
7 Umakonda chilungamo+ ndipo umadana ndi zoipa.+
N’chifukwa chake Mulungu, Mulungu wako,+ wakudzoza+ ndi mafuta achikondwerero chachikulu+ kuposa cha mafumu ena.+
8 Zovala zako zonse ndi zonunkhira mafuta a mule, aloye ndi kasiya.*+
Umasangalala ndi nyimbo zoimbidwa ndi zipangizo za zingwe, kuchokera m’chinyumba chachikulu cha mfumu, chokongoletsedwa ndi minyanga ya njovu.+
9 Ana aakazi+ a mafumu ali m’gulu la akazi ako okondedwa.
Mkazi wamkulu wa mfumu+ waima kudzanja lako lamanja atavala zovala zagolide wa ku Ofiri.+
10 Iwe mwana wanga wamkazi, mvetsera ndipo ona ndi kutchera khutu.
Uiwale anthu ako ndi nyumba ya bambo ako.+
12 Mwana wamkazi wa ku Turo alinso komweko ndi mphatso,+
Olemera pakati pa anthu adzakhazika pansi mtima wako.+
14 Adzamubweretsa kwa mfumu atavala chovala choluka.+
Anamwali anzake omuperekeza akubwera nawo kwa iwe.+
15 Adzawabweretsa akusangalala ndi kukondwera.
Ndipo adzalowa m’nyumba ya mfumu.
17 Ndidzatchula dzina lanu m’mibadwo yonse yam’tsogolo.+
N’chifukwa chake mitundu ya anthu idzakutamandani mpaka kalekale, ndithu mpaka muyaya.
Kwa wotsogolera nyimbo. Salimo la ana a Kora+ mogwirizana ndi kaimbidwe ka Atsikana.
46 Mulungu ndiye pothawira pathu ndi mphamvu yathu,+
Thandizo lopezeka mosavuta pa nthawi ya masautso.+
2 N’chifukwa chake sitidzaopa, ngakhale dziko lapansi litasintha,+
Ndiponso ngakhale mapiri atagwedezeka ndi kumira m’nyanja yaikulu.+
3 Ngakhale madzi a m’nyanjayo atawinduka ndi kuchita thovu,+
Ndiponso ngakhale mapiri atagwedezeka chifukwa cha phokoso la nyanja yaikuluyo.+ [Seʹlah.]
4 Pali mtsinje womwe nthambi zake zimachititsa anthu a mumzinda wa Mulungu kukondwera,+
Chihema chachikulu chopatulika koposa cha Wam’mwambamwamba.+
6 Mitundu ya anthu inachita phokoso,+ maufumu anagwedezeka.
Iye anatulutsa mawu ndipo dziko lapansi linasungunuka.+
7 Yehova wa makamu ali ndi ife.+
Mulungu wa Yakobo ndiye malo athu okwezeka ndiponso achitetezo.+ [Seʹlah.]
8 Bwerani anthu inu, onani ntchito za Yehova,+
Onani mmene wakhazikitsira zinthu zodabwitsa padziko lapansi.+
9 Akuletsa nkhondo mpaka kumalekezero a dziko lapansi.+
Wathyola uta ndi kuduladula mkondo.+
Ndipo watentha magaleta pamoto.+
10 “Gonjerani anthu inu, ndipo dziwani kuti ine ndine Mulungu.+
Ndidzakwezedwa pakati pa anthu a mitundu ina,+
Ndidzakwezedwa padziko lapansi.”+
11 Yehova wa makamu ali ndi ife.+
Mulungu wa Yakobo ndiye malo athu okwezeka ndiponso achitetezo.+ [Seʹlah.]
Kwa wotsogolera nyimbo. Nyimbo ndi Salimo la ana a Kora.
2 Pakuti Yehova, Wam’mwambamwamba, ndi wochititsa mantha,+
Ndiye Mfumu yaikulu padziko lonse lapansi.+
3 Iye adzagonjetsa mitundu ya anthu ndi kuiika pansi pathu.+
Adzagonjetsa anthu a mitundu ina ndi kuwaika pansi pa mapazi athu.+
5 Mulungu wakwera kumalo ake, anthu akufuula mokondwera,+
Yehova wakwera kumalo ake, anthu akuliza lipenga la nyanga ya nkhosa.+
6 Imbani nyimbo zotamanda Mulungu, imbani nyimbo zotamanda.+
Imbani nyimbo zotamanda Mfumu yathu, imbani nyimbo zotamanda.
7 Pakuti Mulungu ndi Mfumu ya dziko lonse lapansi.+
Imbani nyimbo zotamanda ndi kuchita zinthu mozindikira.+
9 Atsogoleri a mitundu ya anthu asonkhana.+
Asonkhana pamodzi ndi anthu a Mulungu wa Abulahamu.+
Pakuti anthu onse omwe ali ngati zishango* za dziko lapansi ndi a Mulungu.+
Iye wakwera pamalo okwezeka kwambiri.+
Nyimbo ndi Salimo la ana a Kora.+
2 Phiri la Ziyoni limene lili m’dera lakutali la kumpoto,+
Ndi lokongola chifukwa lili pamalo okwezeka ndi osangalatsa padziko lonse lapansi,+
Mudzi wa Mfumu Yaikulu.+
3 Munsanja zokhalamo za m’mudzimo, Mulungu wadziwika kuti ndi malo okwezeka ndiponso achitetezo.+
7 Pogwiritsa ntchito mphepo yamphamvu ya kum’mawa, munaswa zombo za ku Tarisi.+
8 Ife taona zimene Mulungu anachita monga mmene tinamvera,+
Mumzinda wa Yehova wa makamu, mumzinda wa Mulungu wathu.+
Mulungu adzakhazikitsa mzindawo mpaka kalekale.+ [Seʹlah.]
10 Inu Mulungu, mofanana ndi dzina lanu,+ kukutamandani
Kwafika kumalire a dziko lapansi.
Dzanja lanu lamanja ladzaza ndi chilungamo.+
13 Ganizirani mofatsa za khoma lake lolimba.+
Yenderani nsanja zake zokhalamo,
Kuti mudzasimbire m’badwo wam’tsogolo.+
14 Pakuti Mulungu uyu ndi Mulungu wathu mpaka kalekale, ndithu mpaka muyaya.+
Iye adzatitsogolera kufikira imfa yathu.+
Kwa wotsogolera nyimbo. Nyimbo ndi Salimo la ana a Kora.+
49 Mvetserani izi, anthu nonsenu.
Tcherani khutu inu nonse a m’nthawi* ino,+
2 Inu mtundu wa anthu ndiponso inu ana a anthu,
Inu olemera pamodzi ndi inu osauka.+
3 Pakamwa panga padzalankhula zinthu zanzeru,+
Ndipo zosinkhasinkha za mtima wanga zidzakhala zinthu zakuya.+
6 Anthu amene akukhulupirira chuma chawo,+
Amene akudzitamandira chifukwa cha kuchuluka kwa chuma chawo,+
7 Palibe ngakhale mmodzi wa iwo amene angathe kuwombola m’bale wake,+
Kapena kumuperekera dipo* kwa Mulungu,
8 (Ndipo malipiro owombolera moyo wawo ndi amtengo wapatali,+
Moti munthu sangathe kuwapereka mpaka kalekale)
9 Kuti akhale ndi moyo mpaka muyaya osaona dzenje la manda.+
10 Pakuti amaona kuti ngakhale anthu anzeru amafa,+
Wopusa ndi wopanda nzeru, onsewo amawonongeka,+
Ndipo chuma chawo amasiyira anthu ena.+
11 Zokhumba za mtima wawo n’zakuti nyumba zawo zikhalebe mpaka kalekale,+
Mahema awo akhalebe ku mibadwomibadwo.+
Malo awo amawatcha mayina awo.+
12 Komabe munthu wochokera kufumbi, ngakhale atakhala wolemekezeka, sangakhale ndi moyo mpaka kalekale.+
Iye amangofanana ndi nyama zimene zaphedwa.+
13 Umu ndi mmene zimakhalira ndi zitsiru,+
Komanso amene amazitsanzira, omwe amasangalala ndi mawu awo odzitukumula. [Seʹlah.]
14 Awatsogolera ku Manda ngati nkhosa zopita kokaphedwa.+
Imfa idzakhala m’busa wawo.+
Ndipo m’mawa anthu owongoka mtima adzawalamulira.+
Matupi awo adzawonongeka.+
Aliyense wa iwo malo ake okhala ndi ku Manda, osati malo okwezeka.+
16 Musachite mantha chifukwa chakuti munthu wina akupeza chuma,+
Kapena chifukwa chakuti ulemerero wa nyumba yake ukuwonjezeka,+
17 Pakuti pa imfa yake sangatenge kena kalikonse.+
Ulemerero wake sudzapita naye pamodzi.+
18 Pakuti pamene anali moyo anali kutamanda moyo wake,+
(Ndipo anthu adzakutamanda chifukwa chakuti walemera)+
20 Munthu, ngakhale atakhala wolemekezeka, koma ngati ali wosazindikira,+
Amangofanana ndi nyama zimene zaphedwa.+
Nyimbo ya Asafu.+
50 Wamphamvuyo,+ Yehova, Mulungu,+ walankhula+
Ndipo akuitana dziko lapansi,+
Kuchokera kotulukira dzuwa mpaka kumene limalowera.+
2 Mulungu wawala ali ku Ziyoni,+ mzinda wokongola kwambiri.+
3 Mulungu wathu adzabwera ndipo sadzakhala chete.+
Pamaso pake pali moto wonyeketsa,+
Ndipo pamalo onse omuzungulira pali mkuntho wamphamvu.+
7 “Ndimvereni anthu anga, ndipo ine ndilankhula,+
Inu Aisiraeli, ine ndipereka umboni wotsutsana nanu.+
Ine ndine Mulungu, Mulungu wanu.+
8 Sindikukudzudzulani chifukwa cha nsembe zanu,+
Kapena chifukwa cha nsembe zanu zopsereza zathunthu zimene mumapereka kwa ine nthawi zonse.+
11 Ndikudziwa bwino zolengedwa zonse zouluka za m’mapiri,+
Ndipo magulu a nyama zakutchire ndi anga.+
12 Ngakhale nditakhala ndi njala, sindingakuuze,
13 Kodi ndiyenera kudya nyama ya ng’ombe zamphongo zonenepa,+
Kapena kumwa magazi a mbuzi zamphongo?+
14 Pereka nsembe zoyamikira kwa Mulungu,+
Ndipo pereka kwa Wam’mwambamwamba zimene walonjeza.+
15 Pa tsiku la nsautso undiitane.+
Ine ndidzakulanditsa, ndipo iwe udzandilemekeza.”+
16 Koma Mulungu adzauza woipa kuti:+
“Ndani wakupatsa udindo wofotokoza malangizo anga,+
Ndi wolankhula za pangano langa?+
18 Nthawi zonse ukaona wakuba unali kusangalala naye.+
Ndipo unali kugwirizana ndi anthu achigololo.+
19 Walekerera pakamwa pako kulankhula zinthu zoipa,+
Ndipo ukugwiritsa ntchito lilime lako kulankhula zachinyengo.+
20 Umakhala pansi ndi kunenera m’bale wako zinthu zoipa,+
Umapezera zifukwa mwana wamwamuna wa mayi ako.+
21 Wachita zinthu zonsezi, koma ine ndinakhala chete.+
Unali kuganiza kuti ine ndikhala ngati iwe.+
Ine ndidzakudzudzula,+ ndipo ndidzaika machimo ako onse poyera iwe ukuona.+
22 Zindikirani zimenezi, anthu oiwala Mulungu inu,+
Kuti ndisakukhadzulekhadzuleni popanda aliyense wokupulumutsani.+
23 Amene akupereka nsembe yoyamikira kwa ine ndi amene akundilemekeza.+
Ndipo amene akuyenda panjirayo motsimikiza,
Ndidzamuonetsa chipulumutso changa.”+
Kwa wotsogolera nyimbo. Nyimbo ya Davide. Pa nthawi imene mneneri Natani anapita kwa Davide atagona ndi Bati-seba.+
51 Ndikomereni mtima inu Mulungu, malinga ndi kukoma mtima kwanu kosatha.+
Malinga ndi kuchuluka kwa chifundo chanu, fafanizani zolakwa zanga.+
4 Ine ndakuchimwirani kwambiri,+
Ndipo ndachita chinthu choipa pamaso panu,+
Choncho mukamalankhula mumalankhula zachilungamo,+
Ndipo mukamaweruza, mumaweruza molungama.+
5 Taonani! Anandilandira mu zowawa za pobereka ndili wochimwa.+
Ndipo ndine wochimwa kuchokera pamene mayi anga anatenga pakati panga.+
6 Taonani! Mumakondwera ndi choonadi chochokera pansi pa mtima.+
Ndipo mundidziwitse nzeru mumtima mwanga.+
7 Ndiyeretseni ndi hisope ku machimo anga kuti ndikhale woyera.+
Ndisambitseni kuti ndiyere kwambiri kuposa chipale chofewa.+
12 Bwezeretsani mwa ine chisangalalo chifukwa cha chipulumutso chanu,+
Ndichirikizeni ndi mzimu wofunitsitsa.+
14 Inu Mulungu, ndilanditseni ku mlandu wa magazi,+ inu Mulungu wa chipulumutso changa,+
Kuti lilime langa linene za chilungamo chanu mokondwera.+
16 Pakuti nsembe singakusangalatseni, chifukwa ikanakusangalatsani ndikanaipereka kwa inu.+
Nsembe yopsereza yathunthu singakusangalatseni.+
17 Kudzimvera chisoni mumtima ndizo nsembe zimene Mulungu amavomereza.+
Inu Mulungu, simudzanyoza mtima wosweka ndi wophwanyika.+
19 Mukatero mudzakondwera ndi nsembe zachilungamo,+
Mudzakondwera ndi nsembe zopsereza ndi nsembe zathunthu.+
Pamenepo ng’ombe zamphongo zidzaperekedwa paguwa lanu la nsembe.+
Kwa wotsogolera nyimbo. Masikili.* Salimo la Davide, pa nthawi imene Doegi, Mwedomu, anapita kwa Sauli kukamuuza kuti Davide wapita kunyumba ya Ahimeleki.+
52 N’chifukwa chiyani ukudzitukumula chifukwa cha zinthu zoipa, wamphamvu iwe?+
Kukoma mtima kosatha kwa Mulungu n’kokhalitsa.+
3 Umakonda kwambiri zinthu zoipa kuposa zabwino,+
Umakonda kwambiri kulankhula chinyengo kuposa kulankhula chilungamo.+ [Seʹlah.]
5 Mulungu adzakupasula kosatha.+
Adzakugwetsa ndi kukukokera kunja kwa hema wako,+
Ndipo adzakuzula ndithu m’dziko la anthu amoyo.+ [Seʹlah.]
7 Munthu wamphamvu wotere sadalira Mulungu monga malo ake achitetezo,+
Koma amadalira kuchuluka kwa chuma chake,+
Ndipo chitetezo chake amachipeza m’mavuto amene iyeyo amawachititsa.+
8 Koma ine ndidzakhala ngati mtengo waukulu wa maolivi+ wa masamba obiriwira m’nyumba ya Mulungu.
Ndidzakhulupirira kukoma mtima kosatha kwa Mulungu mpaka kalekale, ndithu mpaka muyaya.+
9 Ndidzakutamandani mpaka kalekale, chifukwa cha zimene mwachita.+
Ndipo ndidzayembekezera dzina lanu pamaso pa okhulupirika anu, chifukwa ndi labwino.+
Kwa wotsogolera nyimbo pa Mahalati.*+ Masikili.* Salimo la Davide.
53 Wopusa amanena mumtima mwake kuti:
“Kulibe Yehova.”+
Anthu oterewa amachita zoipa, ndipo amachita zinthu zonyansa zogwirizana ndi kupanda chilungamo kwawo.+
Palibe amene akuchita zabwino.+
2 Koma kuchokera kumwamba, Mulungu wayang’ana ana a anthu padziko lapansi,+
Kuti aone ngati pali aliyense wozindikira, aliyense amene akufunafuna Yehova.+
3 Onse abwerera, ndipo onsewo ndi achinyengo.+
Palibe aliyense amene akuchita zabwino,+
Palibiretu ndi mmodzi yemwe.
4 Kodi palibe aliyense wozindikira mwa anthu ochita zopweteka anzawowa,+
Amene akudya anthu anga ngati chakudya?+
Iwo sanaitane pa Yehova.+
5 Nthawi yomweyo anagwidwa ndi mantha aakulu,+
Ngakhale kuti panalibe chochititsa mantha.+
Pakuti Mulungu adzamwaza mafupa a aliyense womanga msasa kuti akuukireni.+
Isiraeli adzawachititsa manyazi pakuti Yehova wawakana.+
6 Haa! Zikanakhala bwino m’Ziyoni mukanapezeka chipulumutso cha Isiraeli.+
Yehova akadzasonkhanitsa ndi kubwezeretsa anthu ake amene agwidwa ndi kutengedwa kupita kudziko lina,+
Yakobo adzasangalale, Isiraeli adzakondwere.+
Kwa wotsogolera nyimbo: Nyimboyi iimbidwe ndi zipangizo za zingwe. Masikili.* Salimo la Davide. Pa nthawi imene Zifi anabwera kudzauza Sauli kuti: “Kodi simukudziwa kuti Davide akubisala kwathu?”+
3 Pakuti pali anthu achilendo amene andiukira,
Ndipo pali olamulira ankhanza amene akufuna moyo wanga.+
Sanaike Mulungu patsogolo pawo.+ [Seʹlah.]
6 Ndidzapereka nsembe kwa inu mofunitsitsa.+
Inu Yehova, ndidzatamanda dzina lanu pakuti ndi labwino.+
Kwa wotsogolera nyimbo: Nyimboyi iimbidwe ndi zipangizo za zingwe. Masikili.* Salimo la Davide.
2 Ndimvetsereni mwatcheru ndi kundiyankha.+
Mtima wanga suli m’malo chifukwa cha mavuto anga,+
Sindingachitire mwina koma kusonyeza nkhawa zanga,
3 Chifukwa cha zimene adani akunena, ndiponso chifukwa chakuti oipa andipanikiza.+
Pakuti akundikhuthulira mavuto,+
Ndipo mwaukali akundisungira chidani.+
Ndikanapita kukakhala m’chipululu.+ [Seʹlah.]
8 Ndikanathawira kumalo opulumukirako,
Kuthawa mphepo yamphamvu, ndithu kuthawa mphepo yamkuntho.”+
9 Inu Yehova, sokonezani anthu oipa, ndipo sokonezani zonena zawo,+
Pakuti ndaona ziwawa ndi mikangano mumzinda.+
10 Usana ndi usiku amayenda pamwamba pa mpanda kuzungulira mzindawo.+
Ndipo mumzindawo muli zopweteka ndi masautso.+
12 Pakuti amene ananditonza si mdani.+
Akanakhala mdani ndikanapirira.
Amene anadzikweza pamaso panga si munthu wodana nane kwambiri.+
Akanakhala munthu wodana nane kwambiri ndikanabisala.+
13 Koma ndiwe, munthu wofanana ndi ine,+
Munthu amene ndimam’dziwa bwino ndiponso mnzanga weniweni,+
14 Chifukwa tinali mabwenzi apamtima.+
Tinali kuyenda limodzi ndi khwimbi la anthu kupita kunyumba ya Mulungu.+
17 Usiku, m’mawa ndi masana ndimakhala ndi nkhawa ndipo ndimakhala ndikulira,+
Choncho Mulungu amamva mawu anga.+
18 Iye adzandiwombola ndi kundikhazika pa mtendere, kundichotsa pankhondo,+
Pakuti khamu la anthu landiukira.+
19 Mulungu amene wakhala pampando wachifumu kuyambira kalekale,+
Adzandimvera ndipo adzawayankha,+ [Seʹlah.]
Anthu osafuna kusintha makhalidwe awo oipa,+
Ndiponso amene saopa Mulungu.+
21 Mawu a pakamwa pake ndi osalala ngati mafuta a mkaka,+
Koma mtima wake umakonda ndewu.+
Mawu ake ndi osalala ngati mafuta,+
Koma ali ngati lupanga lakuthwa.+
23 Koma inu Mulungu, mudzatsitsira oipa kumanda.+
Ndipo anthu amene ali ndi mlandu wa magazi komanso anthu achinyengo, sadzakwanitsa kukhala ngakhale hafu ya moyo wawo.+
Koma ine ndidzakhulupirira inu.+
Kwa wotsogolera nyimbo pa “Nkhunda Yosanena Kanthu” pakati pa okhala kutali. Salimo la Davide. Mikitamu.* Pa nthawi imene Afilisiti anamugwira ku Gati.+
56 Ndikomereni mtima inu Mulungu wanga, chifukwa munthu wopanda pake akufuna kundiwakha ndi pakamwa pake.+
Akulimbana nane tsiku lonse ndi kundipondereza.+
2 Tsiku lonse adani anga akufuna kundiwakha ndi pakamwa pawo,+
Pakuti anthu ambiri akumenyana nane modzikuza.+
3 Ine ndidzadalira inu, tsiku lililonse limene ndingachite mantha.+
4 Popeza kuti ndine wogwirizana ndi Mulungu, ndidzatamanda mawu ake.+
Ine ndimadalira Mulungu, sindidzaopa.+
Kodi munthu angandichite chiyani?+
6 Amandiukira ndi kundibisalira,+
Iwo nthawi zonse amaonetsetsa mmene ndikuyendera,+
Pamene akundidikirira kuti awononge moyo wanga.+
8 Inu mwalemba za kuthawathawa kwanga.+
Sungani misozi yanga m’thumba lanu lachikopa.+
Kodi misozi yanga sili m’buku lanu?+
9 Pa nthawi imeneyo adani anga adzabwerera pa tsiku limene ndidzaitana inu.+
Ndikudziwa bwino kuti Mulungu ali kumbali yanga.+
10 Popeza kuti ndine wogwirizana ndi Mulungu,+ ndidzatamanda mawu ake.
Popeza kuti ndine wogwirizana ndi Yehova, ndidzatamanda mawu ake.+
12 Inu Mulungu, ine ndikuyenera kukwaniritsa malonjezo anga kwa inu.+
Ndidzapereka kwa inu nsembe zoyamikira.+
13 Pakuti inu mwalanditsa moyo wanga ku imfa.+
Inu mwateteza phazi langa kuti lisapunthwe,+
Kuti ndiyendeyende pamaso pa Mulungu m’kuwala kumene kumaunikira anthu amoyo.+
Kwa wotsogolera nyimbo. “Musandiwononge.” Salimo la Davide. Mikitamu.* Pa nthawi imene anathawa Sauli n’kukalowa m’phanga.+
57 Ndikomereni mtima inu Mulungu, ndikomereni mtima,+
Pakuti ine ndathawira kwa inu.+
Ndipo ndathawira mumthunzi wa mapiko anu kufikira masoka atadutsa.+
2 Ndikufuulira Mulungu Wam’mwambamwamba, Mulungu woona amene akuthetsa masoka amenewa kuti zinthu zindiyendere bwino.+
3 Adzatumiza thandizo kuchokera kumwamba ndi kundipulumutsa.+
Adzasokoneza wofuna kundiwakha ndi pakamwa pake.+ [Seʹlah.]
Mulungu adzasonyeza kukoma mtima kwake kosatha ndi choonadi chake.+
4 Moyo wanga uli pakati pa mikango.+
Sindingachitire mwina koma kugona pakati pa ana a anthu, amene ali ngati nyama zoopsa zodya anthu,
Amene mano awo ali ngati mikondo ndi mivi,+
Ndipo lilime lawo lili ngati lupanga lakuthwa.+
5 Inu Mulungu, kwezekani kupitirira kumwamba.+
Ulemerero wanu ukhale pamwamba pa dziko lonse lapansi.+
6 Iwo anditchera ukonde panjira yanga.+
Moyo wanga wagwidwa ndi chisoni.+
Andikumbira mbuna.
Koma iwo agweramo.+ [Seʹlah.]
Iwe choimbira cha zingwe, galamuka, ndi iwenso zeze.+
Ndidzadzuka m’bandakucha usanafike.
9 Ndidzakutamandani pakati pa mitundu ya anthu, inu Yehova.+
Ndidzaimba nyimbo zokutamandani pakati pa mitundu ya anthu.+
10 Pakuti kukoma mtima kwanu kosatha n’kwakukulu ndipo kwafika kumwamba,+
Choonadi chanu chafika kuthambo.+
11 Inu Mulungu, kwezekani kupitirira kumwamba.+
Ulemerero wanu ukhale pamwamba pa dziko lonse lapansi.
Kwa wotsogolera nyimbo. “Musandiwononge.” Salimo la Davide. Mikitamu.*
58 Kodi mungalankhule bwanji za chilungamo mutakhala chete?+
Kodi mungaweruze molungama, inu ana a anthu?+
2 Ayi! Inu mukuchita zosalungama padziko lapansi mogwirizana ndi zimene mtima wanu ukufuna,+
Ndipo mukukonza njira zochitira chiwawa ndi manja anu.+
3 Oipa akhala opotoka maganizo kuyambira ali m’mimba.+
Iwo asochera kuyambira ali m’mimba,
Ndipo amalankhula zabodza.+
4 Iwo ali ndi poizoni ngati wa njoka,+
Ndipo ndi ogontha ngati njoka ya mamba imene yatseka makutu ake,+
5 Imene singamve mawu a munthu wamatsenga,+
Ngakhale wina wanzeru ataimanga ndi mphamvu zamatsenga.+
8 Woipayo amayenda ngati nkhono imene ikusungunuka.
Iwo sadzaona dzuwa ngati mwana wa mayi amene wapita padera.+
9 Miphika yanu isanayambe kumva kutentha kwa moto wa mitengo yaminga,+
Mulungu adzauluza ndi mphepo yamkuntho mitengo yaiwisi yaminga pamodzi ndi imene ikuyaka.+
10 Wolungama adzasangalala chifukwa chakuti waona oipa akupatsidwa chilango.+
Adzasambitsa mapazi ake m’magazi a anthu oipa.+
11 Ndipo mtundu wa anthu udzati:+ “Ndithudi wolungama adzalandira mphoto.+
Ndithudi pali Mulungu amene akuweruza dziko lapansi.”+
Kwa wotsogolera nyimbo. “Musandiwononge.” Salimo la Davide. Mikitamu.* Pa nthawi imene Sauli anatumiza anthu, ndipo anali kudikirira nyumba yake kuti amuphe.+
2 Ndilanditseni kwa anthu ochita zopweteka anzawo,+
Ndipo ndipulumutseni kwa anthu amene ali ndi mlandu wa magazi.
3 Pakuti, taonani! Iwo akundidikirira kuti awononge moyo wanga.+
Inu Yehova, anthu amphamvu akundiukira,+
Ngakhale kuti ine sindinapanduke kapena kuchita tchimo lililonse.+
4 Iwo akuthamanga ndi kukonzekera kundiukira, ngakhale kuti sindinalakwe chilichonse.+
Nyamukani pamene ine ndikuitana kuti muone zimene zikundichitikira.+
5 Inu Yehova, Mulungu wa makamu, ndinu Mulungu wa Isiraeli.+
Nyamukani ndi kuweruza mitundu yonse ya anthu.+
Musakomere mtima aliyense woipa ndi wachiwembu.+ [Seʹlah.]
7 Taonani! Amabwetuka ndi pakamwa pawo.+
Milomo yawo ili ngati malupanga,+
Pakuti iwo amati: “Ndani akumvetsera?”+
9 Inu Mphamvu yanga, ndidzayang’anabe kwa inu.+
Pakuti Mulungu ndiye malo anga okwezeka ndiponso achitetezo.+
10 Mulungu amene wandisonyeza kukoma mtima kosatha ndidzaonana naye maso ndi maso.+
Mulungu adzachititsa kuti ndione adani anga, adaniwo atagonja.+
11 Musawaphe, kuti anthu a mtundu wanga angaiwale.+
Ndi mphamvu zanu zochuluka achititseni kuyendayenda,+
Ndipo agwetseni, inu Yehova, chishango chathu,+
12 Chifukwa cha tchimo la pakamwa pawo, ndi mawu a pamilomo yawo.+
Agwidwe chifukwa cha kunyada kwawo,+
Chifukwa cha kutukwana ndi chinyengo zimene amachita mobwerezabwereza.
13 Afafanizeni mu mkwiyo wanu.+
Afafanizeni kuti asakhaleponso.
Ndipo adziwe kuti Mulungu akulamulira Yakobo mpaka kumalekezero a dziko lonse lapansi.+ [Seʹlah.]
16 Koma ine, ndidzaimba za mphamvu yanu,+
M’mawa ndidzanena mosangalala za kukoma mtima kwanu kosatha.+
Pakuti inu mwakhala malo anga okwezeka ndiponso achitetezo,+
Ndiponso malo anga othawirako pa nthawi ya masautso.+
17 Inu Mphamvu yanga, ine ndidzaimba nyimbo zokutamandani,+
Pakuti Mulungu ndiye malo anga okwezeka ndiponso achitetezo, Mulungu wandisonyeza kukoma mtima kosatha.+
Kwa wotsogolera nyimbo pa Duwa la Chikumbutso. Mikitamu.* Salimo la Davide. Nyimbo yophunzitsira.+ Pa nthawi imene Davide anali pankhondo ndi Aramu-naharaimu ndi Aramu-Zoba, ndipo Yowabu anabwerera ndi kukapha Aedomu 12,000 m’chigwa cha Mchere.+
60 Inu Mulungu, mwatitaya, ndipo mwasokoneza magulu athu ankhondo,+
Mwakwiya. Tiloleni tibwerere kwa inu.+
6 Pokhala woyera, Mulungu walankhula kuti:+
“Ndidzakondwa ndi kupereka Sekemu ngati gawo la cholowa.+
Ndipo ndidzayezera anthu anga chigwa cha Sukoti.+
7 Giliyadi ndi wanga ndipo Manase ndi wanganso.+
Efuraimu ndi malo otetezeka a mtsogoleri amene ine ndamuika.
Yuda ndi ndodo ya mtsogoleri wanga.+
8 Mowabu ndi beseni langa losambiramo.+
Ndidzaponyera Edomu nsapato zanga.+
Ndidzafuula mosangalala chifukwa chogonjetsa Filisitiya.”+
9 Ndani adzandibweretsa kumzinda wozunguliridwa ndi adani?+
Ndani adzanditsogolera mpaka kukafika ku Edomu?+
10 Ndinu Mulungu amene mungatichititse kupambana! Koma onani tsopano mwatitaya,+
Ndipo inu Mulungu wathu, simukupita kunkhondo pamodzi ndi magulu athu ankhondo.+
11 Tithandizeni kuti tichoke m’masautso,+
Pakuti chipulumutso chochokera kwa munthu wochokera kufumbi n’chopanda pake.+
Kwa wotsogolera nyimbo. Nyimboyi iimbidwe ndi zoimbira za zingwe. Salimo la Davide.
2 Mtima wanga ukalefuka, ndidzafuulira inu, kuchokera kumalekezero a dziko lapansi.+
Nditsogolereni ndi kundikweza pamwamba pa thanthwe lalitali kuposa msinkhu wanga.+
4 Ndidzakhala mlendo m’chihema chanu mpaka kalekale.+
Ndidzathawira m’malo obisalamo kunsi kwa mapiko anu.+ [Seʹlah.]
5 Pakuti inu Mulungu, mwamvetsera malonjezo anga.+
Mwandipatsa cholowa chimene mwasungira anthu oopa dzina lanu.+
7 Mfumuyo idzakhala pamaso pa Mulungu mpaka kalekale.+
Isonyezeni kukoma mtima kwanu kosatha ndi kuipatsa choonadi kuti zimenezi ziiteteze.+
8 Choncho ndidzaimba nyimbo zotamanda dzina lanu mpaka muyaya,+
Kuti ndikwaniritse malonjezo anga tsiku ndi tsiku.+
Kwa wotsogolera nyimbo pa Yedutuni.* Nyimbo ya Davide.
2 Iye ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa, malo anga okwezeka ndiponso achitetezo.+
Sindidzagwedezeka kwambiri.+
3 Kodi mudzayesayesa kufikira liti kuti muphe munthu amene mumadana naye?+
Nonsenu muli ngati khoma lopendekeka, khoma lamiyala limene akulikankha kuti ligwe.+
4 Iwo amapatsa munthu malangizo kuti amukope ndi kumutsitsa pamalo ake aulemu.+
Bodza limawasangalatsa.+
Iwo amadalitsa ndi pakamwa pawo, koma mumtima mwawo amatemberera.+ [Seʹlah.]
5 Ndithudi, yembekezera Mulungu modekha, iwe moyo wanga,+
Chifukwa chiyembekezo changa chichokera kwa iye.+
6 Ndithudi, iye ndi thanthwe langa ndi chipulumutso changa, malo anga okwezeka ndiponso achitetezo.+
Sindidzagwedezeka.+
7 Chipulumutso ndi ulemerero wanga zili mwa Mulungu.+
Iye ndi thanthwe langa lolimba ndi malo anga othawirako.+
8 Mukhulupirireni nthawi zonse, anthu inu.+
Mukhuthulireni za mumtima mwanu.+
Mulungu ndiye pothawirapo pathu.+ [Seʹlah.]
9 Ndithudi, ana a anthu ochokera kufumbi ali ngati mpweya,+
Ana a anthu ndi malo othawirako achinyengo.+
Onse pamodzi akaikidwa pasikelo ndi opepuka kuposa mpweya.+
10 Musadalire chizolowezi chobera ena mwachinyengo,+
Ndipo musakhale wachabechabe chifukwa chochita uchifwamba.+
Ngati chuma chanu chachuluka, mtima wanu wonse usakhale pachumacho.+
12 Komanso kukoma mtima kosatha ndi kwanu, inu Yehova,+
Pakuti inu mumabwezera aliyense mogwirizana ndi ntchito zake.+
Nyimbo ya Davide pamene anali m’chipululu cha Yuda.+
63 Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga, ine ndikukufunafunani.+
Moyo wanga ukulakalaka inu.+
Thupi langa lalefuka chifukwa cholakalaka inu
M’dziko louma ndi lopanda chonde, lopanda madzi.+
4 Choncho ndidzakutamandani pa nthawi yonse ya moyo wanga.+
Ndidzapemphera m’dzina lanu nditakweza manja anga.+
5 Moyo wanga wakhutira ndi gawo labwino kwambiri, wakhutira ndi zinthu zabwino kwambiri,+
Ndipo milomo yanga ikukutamandani ndi mfuu yachisangalalo.+
11 Ndipo mfumu idzakondwera mwa Mulungu.+
Aliyense wolumbira m’dzina la Mulungu adzam’tamanda,+
Pakuti pakamwa pa anthu olankhula chinyengo padzatsekedwa.+
Kwa wotsogolera nyimbo. Nyimbo ya Davide.
2 Ndibiseni kuti ndisamve zinsinsi za anthu ochita zoipa,+
Kuti ndisamve phokoso la anthu ochita zovulaza anzawo,+
3 Amene anola lilime lawo ngati lupanga,+
Amene alunjikitsa mivi yawo, imene ndi mawu awo owawa,+
4 Pa munthu wosalakwa, kuti amulase atamubisalira.+
Amamulasa modzidzimutsa ndipo saopa.+
6 Amafunafuna kuchita zinthu zosalungama,+
Abisa chiwembu chimene achikonza mochenjera,+
Ndipo zamkati, zamumtima mwa aliyense, n’zovuta kuzimvetsa.+
7 Koma Mulungu adzawalasa ndi muvi modzidzimutsa.+
Iwo adzakhala ndi zilonda,+
8 Ndipo iwo amakhumudwitsa munthu,+
Koma lilime lawo likutsutsana nawo.+
Onse owayang’ana adzapukusa mitu yawo,+
9 Anthu onse adzachita mantha,+
Ndipo adzanena za ntchito za Mulungu,+
Iwo adzamvetsa bwino ntchito zake.+
10 Wolungama adzakondwera mwa Yehova ndipo adzathawira kwa iye,+
Ndipo onse owongoka mtima adzatamanda Mulungu.+
Kwa wotsogolera nyimbo. Nyimbo ndi Salimo la Davide.
65 Inu Mulungu, anthu akukutamandani mu Ziyoni+ ndipo akhala chete pamaso panu,
Iwo adzakwaniritsa malonjezo awo kwa inu.+
2 Inu Wakumva pemphero, anthu a mitundu yonse adzabwera kwa inu.+
4 Wodala ndi munthu amene inu mwamusankha ndi kumuyandikizitsa kwa inu,+
Kuti akhale m’mabwalo anu.+
Tidzakhutira ndi zinthu zabwino za m’nyumba yanu,+
Malo anu oyera kapena kuti kachisi wanu woyera.+
5 Mudzatiyankha ndi zinthu zochititsa mantha zochitika mwachilungamo,+
Inu Mulungu wa chipulumutso chathu,+
Inu Chidaliro cha malire onse a dziko lapansi ndi anthu okhala pafupi ndi nyanja zakutali.+
7 Iye akutontholetsa phokoso la nyanja,+
Akutontholetsa phokoso la mafunde ake komanso chipwirikiti cha mitundu ya anthu.+
8 Ndipo anthu okhala m’madera akutali adzachita mantha ndi zizindikiro zanu,+
Mudzachititsa kulowa ndi kutuluka kwa dzuwa kufuula mokondwera.+
9 Inu mwatembenukira dziko lapansi kuti mulipatse zinthu zochuluka,+
Mwalilemeretsa kwambiri.
Mtsinje wochokera kwa Mulungu ndi wosefukira ndi madzi.+
Munalinganiza zinthu, kuti mbewu zawo zibale.+
Umu ndi mmene mumaperekera zinthu padziko lapansi.+
10 Mizere yawo imakhathamira, ndipo zibuma zake zimasalazidwa,+
Ndipo mumafewetsa nthaka ndi mvula yamvumbi. Mumadalitsa zomera m’nthakayo.+
12 Malo odyetserako ziweto a m’chipululu akukha mafuta,+
Ndipo zitunda zamangirira chisangalalo m’chiuno mwawo.+
13 Malo odyetserako ziweto adzaza ndi nkhosa,+
Ndipo zigwa zakutidwa ndi tirigu.+
Malo onsewa akufuula mosangalala ndi kuimba chifukwa cha kupambana.+
Kwa wotsogolera nyimbo. Nyimbo ndi Salimo.
66 Inu anthu nonse padziko lapansi, fuulirani Mulungu mosangalala chifukwa wapambana.+
3 Muuzeni Mulungu kuti: “Ntchito zanu ndi zochititsadi mantha!+
Chifukwa cha kuchuluka kwa mphamvu zanu, adani anu adzabwera kwa inu mogonjera.+
4 Anthu onse padziko lapansi adzakugwadirani,+
Ndipo adzaimba nyimbo zokutamandani, adzaimba nyimbo zotamanda dzina lanu.”+ [Seʹlah.]
5 Bwerani anthu inu, kuti muone ntchito za Mulungu.+
Zimene wachitira ana a anthu ndi zochititsa mantha.+
6 Anasandutsa nyanja kukhala malo ouma,+
Anthu anawoloka mtsinje mwa kuyenda ndi mapazi awo.+
Pamenepo tinayamba kusangalala mwa iye.+
7 Iye akulamulira ndi mphamvu zake mpaka kalekale.+
Maso ake akuyang’anitsitsa mitundu ya anthu.+
Koma anthu oumitsa khosi asadzikweze.+ [Seʹlah.]
12 Mwachititsa munthu wamba kutipondaponda.+
Tadutsa pamoto ndi pamadzi,+
Ndipo inu mwatipatsa mpumulo.+
13 Ndidzalowa m’nyumba yanu ndi nsembe zopsereza zathunthu.+
Ine ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa inu+
14 Amene milomo yanga inanena,+
Ndiponso amene pakamwa panga pananena nthawi imene ndinali m’masautso aakulu.+
15 Ndidzapereka kwa inu nsembe zathunthu zopsereza za nyama zonenepa,+
Pamodzi ndi nsembe zautsi wa nkhosa zamphongo.
Ndidzapereka ng’ombe yamphongo pamodzi ndi mbuzi zamphongo.+ [Seʹlah.]
20 Adalitsike Mulungu amene sananyalanyaze pemphero langa,
Kapena kundimana kukoma mtima kwake kosatha.+
Kwa wotsogolera nyimbo: Nyimboyi iimbidwe ndi zipangizo za zingwe. Nyimbo ndi Salimo.
67 Mulungu adzatiyanja ndi kutidalitsa.+
Iye adzatikomera mtima,+ [Seʹlah.]
2 Kuti njira zanu zidziwike padziko lapansi,+
Kuti chipulumutso chanu chidziwike pakati pa mitundu yonse ya anthu.+
4 Mitundu ya anthu isangalale ndi kufuula mokondwera,+
Pakuti inu mudzaweruza anthu molungama.+
Ndipo mudzatsogolera mitundu ya anthu padziko lapansi. [Seʹlah.]
Kwa wotsogolera nyimbo. Salimo la Davide. Nyimbo ndi Salimo.
2 Monga mmene mphepo imauluzira utsi, inunso muwauluze chimodzimodzi.+
Ngati mmene phula limasungunukira chifukwa cha moto,+
Anthu oipa awonongeke ndi kuchotsedwa pamaso pa Mulungu.+
4 Anthu inu, imbirani Mulungu, muimbireni nyimbo zotamanda dzina lake.+
Muimbireni nyimbo Iye amene akudutsa m’chipululu,+
Amene dzina lake ndi Ya,*+ ndipo kondwerani pamaso pake.
5 Tate wa ana amasiye* ndi woweruzira akazi amasiye milandu,+
Ndi Mulungu amene amakhala m’malo ake oyera.+
6 Mulungu akuchititsa osungulumwa kukhala m’nyumba.+
Akumasula akaidi ndi kuwathandiza kuti zinthu ziwayendere bwino.+
Koma anthu osamvera adzakhala m’dziko lowonongeka ndi kutentha kwa dzuwa.+
7 Inu Mulungu, pamene munatsogolera anthu anu,+
Pamene munadutsa m’chipululu,+ [Seʹlah.]
8 Dziko lapansi linagwedezeka,+
Kumwamba kunagwa mvula chifukwa cha inu Mulungu,+
Phiri ili la Sinai linagwedezeka chifukwa cha inu Mulungu,+ Mulungu wa Isiraeli.+
9 Inu Mulungu, munayamba kugwetsa mvula yamphamvu,+
Ngakhale pamene anthu anu anali ofooka, inu munawalimbitsa.+
10 Iwo anakhala mumsasa wanu wa mahema,+
Inu Mulungu, chifukwa chakuti ndinu wabwino munakonzera munthu wosautsika msasa wa mahema.+
12 Mafumu enieniwo okhala ndi magulu a asilikali amathawa, ndithu amathawadi.+
Mkazi wongokhala pakhomo, nayenso amagwira nawo ntchito yofunkha.+
13 Ngakhale anthu inu mutagona pakati pa milu ya phulusa mumsasawo,
Mudzaona mapiko a njiwa okutidwa ndi siliva,
Ndipo nthenga za kumapeto a mapiko ake zidzakhala zagolide wobiriwira monkera ku chikasu.+
15 Dera lamapiri la ku Basana+ ndilo phiri la Mulungu.+
Dera lamapiri la ku Basana ndilo phiri la nsonga zitalizitali.+
16 N’chifukwa chiyani inu mapiri a nsonga zitalizitali mumayang’ana mwanjiru
Phiri limene Mulungu wafuna kukhalamo?+
Yehova adzakhala m’phiri limenelo mpaka muyaya.+
17 Magaleta ankhondo a Mulungu ali m’magulu a masauzande makumimakumi, ali m’magulu a masauzande osawerengeka.+
Yehova walowa m’malo oyera kuchokera kuphiri la Sinai.+
18 Mwakwera pamalo apamwamba,+
Mwatenga anthu ogwidwa,+
Mwatenga mphatso za amuna,+
Ndithu inu Yehova* Mulungu, mwatenga ngakhale anthu osamvera,+ kuti inu mukhale pakati pawo.+
19 Adalitsike Yehova, amene amanyamula katundu wathu tsiku ndi tsiku,+
Mulungu woona wa chipulumutso chathu.+ [Seʹlah.]
20 Mulungu woona ndi Mulungu amene amatipulumutsa.+
Ndipo njira zopulumukira ku imfa ndi za Yehova,+ Ambuye Wamkulu Koposa.+
21 Ndithudi, Mulungu adzaphwanya mitu ya adani ake kukhala zibenthuzibenthu,+
Adzaphwanya liwombo latsitsi la aliyense woyenda m’njira yochimwa.+
22 Yehova wanena kuti: “Ndidzawabweza kuchokera ku Basana,+
Ndidzawatulutsa m’nyanja yakuya,+
23 Kuti musambitse mapazi anu m’magazi,+
Kuti malilime a agalu anu anyambite magazi a adani anu.”+
24 Iwo aona magulu anu a anthu opambana akuyendera pamodzi, inu Mulungu,+
Magulu a anthu oyendera pamodzi a Mulungu wanga, Mfumu yanga, akukalowa kumalo oyera.+
25 Oimba nyimbo anali patsogolo, oimba zoimbira za zingwe anali pambuyo pawo,+
Pakati panali atsikana akuimba maseche.+
26 Pamisonkhano tamandani Mulungu,+
Tamandani Yehova, inu nonse amene moyo wanu ukuchokera mu Kasupe wa Isiraeli.+
27 Pali fuko laling’ono la Benjamini limene likugonjetsa anthu,+
Pali akalonga a Yuda pamodzi ndi makamu awo amene akufuula,
Palinso akalonga a Zebuloni ndi akalonga a Nafitali.+
28 Mulungu wanu walamula mphamvu zanu kuti zionekere.+
Inu Mulungu, sonyezani mphamvu monga mmene mwachitira kwa ife.+
30 Dzudzulani nyama yakutchire yokhala m’mabango,+ gulu la ng’ombe zamphongo,+
Pamodzi ndi mitundu ya anthu imene ili ngati ana a ng’ombe amphongo, aliyense amene akupondaponda ndalama zasiliva.+
Iye wabalalitsa mitundu ya anthu yokonda ndewu.+
31 Zinthu zopangidwa ndi mkuwa wosakaniza ndi zitsulo zina* zidzabwera kuchokera ku Iguputo,+
Mwamsanga Kusi adzatambasula dzanja lake ndi kupereka mphatso kwa Mulungu.+
32 Inu maufumu a dziko lapansi, imbirani Mulungu,+
Imbani nyimbo zotamanda Yehova [Seʹlah.]
33 Imbirani Iye wokwera kumwamba kwa kumwamba kwakale.+
Tamverani! Iye akulankhula ndi mawu amphamvu.+
34 Vomerezani kuti Mulungu ndi wamphamvu zochuluka.+
Iye akulamulira Isiraeli ndipo mphamvu zake zili m’mitambo.+
35 Mulungu akamatuluka m’malo ake opatulika aulemerero, amachititsa mantha.+
Iye ndi Mulungu wa Isiraeli, wopereka mphamvu ndi nyonga kwa anthu.+
Mulungu adalitsike.+
Kwa wotsogolera nyimbo pa Maluwa.*+ Salimo la Davide.
69 Ndipulumutseni, inu Mulungu, pakuti madzi afika m’khosi.+
2 Ndamila m’matope akuya, mmene mulibe malo oponda.+
Ndalowa m’madzi akuya,
Ndipo mtsinje wa madzi othamanga wandikokolola.+
3 Ndatopa ndi kufuula kwanga,+
Mawu asasa pammero panga.
Maso anga achita mdima poyembekezera Mulungu wanga.+
4 Anthu amene amadana nane popanda chifukwa achuluka kuposa tsitsi la m’mutu mwanga.+
Amene akufuna kunditsitsira kuli chete, chifukwa chodana nane popanda chifukwa, achuluka kwambiri.+
Ngakhale kuti sindine wakuba, anandikakamiza kubweza zinthu zimene zinabedwa.
6 Onse amene akuyembekezera inu asachite manyazi chifukwa cha ine,+
Inu Ambuye Wamkulu Koposa, Yehova wa makamu.+
Onse amene akufunafuna inu, asanyazitsidwe chifukwa cha ine,+
Inu Mulungu wa Isiraeli.+
9 Pakuti kudzipereka kwambiri panyumba yanu kwandidya,+
Ndipo mnyozo wa anthu amene akukutonzani wagwa pa ine.+
10 Ndipo ndinalira ndi kusala kudya chifukwa cha moyo wanga,+
Koma anthu anali kungonditonza chifukwa cha zimenezo.+
12 Anthu okhala kuchipata anayamba kundidera nkhawa,+
Ndipo anthu amene anali kumwa zakumwa zoledzeretsa anali kundinena mu nyimbo zawo.+
13 Koma ine ndinali kupemphera kwa inu Yehova,+
Pa nthawi yovomerezedwa, inu Mulungu.+
Ndiyankheni mwa kuchuluka kwa kukoma mtima kwanu kosatha, ndipo sonyezani kuti ndinudi mpulumutsi.+
14 Ndipulumutseni m’matope kuti ndisamire.+
Ndipulumutseni kwa anthu odana nane+ ndiponso ku madzi akuya.+
16 Ndiyankheni inu Yehova, pakuti kukoma mtima kwanu kosatha ndi kwabwino.+
Ndicheukireni chifukwa chifundo chanu ndi chochuluka,+
17 Ndipo ine mtumiki wanu musandibisire nkhope yanu.+
Ndiyankheni mwamsanga, chifukwa ndasautsika kwambiri.+
19 Inu mwadziwa chitonzo changa, manyazi anga ndi kunyazitsidwa kwanga.+
Onse odana nane ali pamaso panu.+
20 Mtima wanga wasweka chifukwa cha chitonzo, ndipo chilonda chake ndi chosachiritsika.+
Ndinali kuyembekezera kuti wina andimvere chifundo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe,+
Ndinali kuyembekezera onditonthoza, koma sanapezeke ngakhale mmodzi.+
21 Koma anandipatsa chomera chakupha kuti ndidye,+
Ndipo anayesa kundimwetsa vinyo wowawasa pamene ndinali ndi ludzu.+
26 Pakuti iwo amalondalonda munthu amene inu mwamulanga,+
Ndipo amakamba za ululu wa anthu amene inu mwawalasa.
31 Zimenezinso zidzasangalatsa kwambiri Yehova kuposa ng’ombe yamphongo,+
Kuposa ng’ombe yamphongo yaing’ono imene ili ndi nyanga, komanso yogawanika ziboda.+
32 Anthu ofatsa adzaona zimenezi ndipo adzakondwera.+
Inu amene mukutumikira Mulungu, mtima wanu ukhalenso ndi moyo.+
34 Kumwamba ndi dziko lapansi zimutamande,+
Chimodzimodzinso nyanja ndi chilichonse choyenda mmenemo.+
35 Pakuti Mulungu adzapulumutsa Ziyoni,+
Ndipo adzamanga mizinda ya Yuda,+
Iwo adzakhala mmenemo ndi kutenga dzikolo kukhala lawo.+
36 Ana a atumiki ake adzalandira dzikolo monga cholowa chawo,+
Ndipo anthu okonda dzina lake adzakhala mmenemo.+
Kwa wotsogolera nyimbo. Salimo la Davide. Nyimbo ya chikumbutso.+
2 Amene akufunafuna moyo wanga achite manyazi ndi kuthedwa nzeru.+
Amene akukondwera ndi tsoka langa abwerere ndipo anyazitsidwe.+
3 Amene akunena kuti: “Eyaa! Eyaa!” abwerere chifukwa cha manyazi awo.+
4 Onse amene akufunafuna inu akondwere ndi kusangalala mwa inu,+
Ndipo onse amene amakonda chipulumutso chanu, nthawi zonse azinena kuti: “Mulungu alemekezeke!”+
5 Koma ine ndasautsika ndipo ndasauka.+
Inu Mulungu, chitanipo kanthu mwamsanga kuti zinthu zindiyendere bwino.+
Inu ndinu thandizo langa ndi Wopereka chipulumutso kwa ine.+
Inu Yehova musachedwe.+
2 Mundilanditse chifukwa cha chilungamo chanu ndipo mundipulumutse.+
Tcherani khutu lanu kwa ine ndi kundipulumutsa.+
3 Mukhale thanthwe lachitetezo loti ndizilowamo nthawi zonse.+
Lamulani kuti ndipulumutsidwe,+
Pakuti inu ndinu thanthwe langa ndi malo anga achitetezo.+
4 Inu Mulungu wanga, ndipulumutseni m’manja mwa woipa,+
Ndipulumutseni m’manja mwa munthu wochita zinthu mopanda chilungamo komanso mopondereza.+
5 Pakuti chiyembekezo changa ndinu,+ Yehova Ambuye Wamkulu Koposa, ndimadalira inu kuyambira pa unyamata wanga.+
6 Kuyambira ndili m’mimba mwa mayi anga inu mwandithandiza.+
Inu ndi amene munanditulutsa m’mimba mwa mayi anga.+
Ndimatamanda inu nthawi zonse.+
8 M’kamwa mwanga mwadzaza mawu otamanda inu,+
Ndipo pakamwa panga pakunena za ulemerero wanu tsiku lonse.+
10 Pakuti adani anga anena za ine,+
Ndipo anthu olondalonda moyo wanga, onse pamodzi achita upo,+
11 Iwo akunena kuti: “Mulungu wamusiya.+
Mulondoleni ndi kumugwira pakuti palibe womulanditsa.”+
13 Anthu otsutsana nane achite manyazi, iwo awonongedwe.+
Amene akufunafuna kundigwetsera tsoka adziphimbe ndi chitonzo ndiponso manyazi.+
15 Pakamwa panga padzanena za chilungamo chanu,+
Padzanena za chipulumutso chanu tsiku lonse,+
Pakuti ntchito za chilungamo ndi chipulumutso chanu ndi zochuluka ndipo sindinathe kuziwerenga.+
16 Ndidzabwera ndi kunena za mphamvu zanu zazikulu,+ inu Yehova Ambuye Wamkulu Koposa.+
Ndidzanena za chilungamo chanu, osati cha wina aliyense.+
17 Inu Mulungu, mwandiphunzitsa kuyambira pa unyamata wanga,+
Ndipo mpaka pano ndikunena za ntchito zanu zodabwitsa.+
18 Ngakhale nditakalamba ndi kumera imvi, inu Mulungu musandisiye,+
Kufikira nditanena za dzanja lanu lamphamvu ku m’badwo wotsatira,+
Kufikira nditanena za mphamvu zanu kwa onse obwera m’tsogolo.+
19 Chilungamo chanu, inu Mulungu chafika kumwamba.+
Tikanena za zinthu zazikulu zimene munachita,+
Inu Mulungu, ndani angafanane ndi inu?+
20 Chifukwa chakuti mwandionetsa masautso ndi masoka ambiri,+
Nditsitsimutseni.+
Nditulutseninso m’madzi akuya, pansi pa nthaka.+
22 Inenso ndidzakutamandani ndi chipangizo cha zingwe,+
Ndidzatamanda choonadi chanu, inu Mulungu.+
Ndidzaimba nyimbo zokutamandani ndi zeze, Inu Woyera wa Isiraeli.+
23 Ndikafuna kuimba nyimbo zokutamandani, pakamwa panga padzafuula mokondwera,+
Ngakhalenso moyo wanga umene mwauwombola+ udzakutamandani.
24 Ngakhalenso lilime langa lidzalankhula chapansipansi za chilungamo chanu tsiku lonse,+
Pakuti ofunafuna kundigwetsera tsoka achita manyazi ndipo athedwa nzeru.+
Salimo lonena za Solomo.
72 Inu Mulungu, dziwitsani mfumu za zigamulo zanu,+
Ndipo dziwitsani mwana wa mfumu za chilungamo chanu.+
2 Aweruzire anthu milandu mwachilungamo,+
Ndipo aweruze milandu ya osautsika ndi ziweruzo zolungama.+
3 Mapiri atenge mtendere ndi kupita nawo kwa anthu,+
Komanso zitunda zitenge mtendere wopezeka mwachilungamo.
4 Aweruze osautsika pakati pa anthu,+
Apulumutse ana a anthu osauka,
Ndipo aphwanye wobera anzake mwachinyengo.
5 Iwo adzakuopani nthawi zonse pamene dzuwa likuwala,+
Adzakuopani ku mibadwomibadwo pamene mwezi uli kuthambo.+
6 Adzatsika ngati mvula pa udzu umene wadulidwa,+
Ngati mvula yambiri yamvumbi imene imanyowetsa kwambiri nthaka.+
7 M’masiku ake, wolungama adzaphuka,+
Ndipo padzakhala mtendere wochuluka kwa nthawi yonse pamene mwezi udzakhalepo.+
8 Ndipo adzakhala ndi anthu omugonjera kuchokera kunyanja kukafika kunyanja,+
Komanso kuchokera ku Mtsinje*+ kukafika kumalekezero a dziko lapansi.+
10 Mafumu a ku Tarisi ndi m’zilumba+
Adzapereka msonkho.+
Mafumu a ku Sheba ndi Seba
Adzapereka mphatso.+
12 Pakuti adzalanditsa wosauka amene akufuula popempha thandizo,+
Komanso wosautsika ndi aliyense wopanda womuthandiza.+
14 Adzawombola miyoyo yawo ku chipsinjo ndi chiwawa,
Ndipo adzaona magazi awo kukhala amtengo wapatali.+
15 Iye akhale ndi moyo wautali,+ ndipo apatsidwe wina mwa golide wa ku Sheba.+
Nthawi zonse anthu azimupempherera.
Adalitsike tsiku lililonse.+
16 Padziko lapansi padzakhala tirigu wambiri.+
Pamwamba pa mapiri padzakhala tirigu wochuluka.+
Zokolola za mfumu zidzachuluka ngati mitengo ya ku Lebanoni,+
Ndipo anthu ochokera mumzinda adzaphuka ngati udzu wa panthaka.+
17 Dzina lake likhalebe mpaka kalekale.+
Nthawi zonse pamene dzuwa latuluka, dzina lake lizitchuka,
Ndipo kudzera mwa iye, anthu apeze madalitso.*+
Mitundu yonse ya anthu imutche wodala.+
19 Lidalitsike dzina lake laulemerero mpaka kalekale,+
Ndipo ulemerero wake udzaze dziko lonse lapansi.+
Ame! Ame!*
20 Mapemphero a Davide mwana wa Jese,+ athera pamenepa.
BUKU LACHITATU
(Masalimo 73 – 89)
Nyimbo ya Asafu.+
73 Mulungu ndi wabwinodi kwa Isiraeli, kwa anthu oyera mtima.+
2 Koma ine phazi langa linangotsala pang’ono kupatuka,+
Mapazi anga anangotsala pang’ono kuterereka.+
5 Iwo sakumana ndi mavuto amene anthu onse amakumana nawo,+
Ndipo sakumana ndi masoka mofanana ndi anthu ena onse.+
9 Kudzikweza kwawo kwafika kumwamba,+
Akuyendayenda padziko lapansi ndipo lilime lawo likunena zilizonse zimene akufuna.+
10 Choncho woipa amatengera anthu a Mulungu kumalo omwewo,
Ndipo amamwa madzi m’kapu yodzaza bwino.
12 Onani! Awa ndi anthu oipa, amene akukhala mosatekeseka mpaka kalekale.+
Iwo achulukitsa chuma chawo.+
13 Ndithudi, ndayeretsa mtima wanga pachabe,+
Ndipo ndasamba m’manja mwanga pachabe posonyeza kuti ndine wopanda cholakwa.+
15 Ngati ndikananena kuti: “Ndidzalankhula za zinthu zimenezi,”
Pamenepo ndikanachitira chinyengo
M’badwo wa ana anu aamuna.+
16 Ndipo ndinali kuganizira nkhani imeneyi kuti ndiimvetse.+
Zinali zopweteka kwa ine,
17 Kufikira pamene ndinalowa m’malo opatulika aulemerero a Mulungu.+
Ndinafuna kudziwa za tsogolo lawo.+
19 Haa! M’kanthawi kochepa, iwo akhala chinthu chodabwitsa.+
Afika pamapeto awo ndipo atha chifukwa cha masoka owagwera modzidzimutsa!
20 Inu Yehova, anthu amenewa ali ngati maloto amene aiwalika podzuka.+
Choncho pamene mukuimirira mudzawakana mochititsa manyazi.+
21 Pakuti mtima unandipweteka+
Ndipo ndinamva ululu mu impso zanga.+
22 Ndinakhala wopanda nzeru ndipo sindinadziwe kanthu.+
Ndinakhala ngati nyama yakuthengo pamaso panu.+
25 Winanso ndani kumwambako amene ali kumbali yanga?+
Palibe wina wondisangalatsa padziko lapansi koma inu nokha.+
26 Thupi langa ndi mtima wanga zalefuka.+
Mulungu ndiye thanthwe la mtima wanga ndiponso cholowa changa mpaka kalekale.+
27 Pakuti onse okhala kutali ndi inu adzatheratu.+
Mudzawononga ndithu aliyense wochita chigololo mwa kukusiyani.+
28 Koma kwa ine kuyandikira kwa Mulungu ndi chinthu chabwino.+
Yehova Ambuye Wamkulu Koposa ndiye pothawirapo panga,+
Kuti ndilengeze za ntchito zanu zonse.+
74 Inu Mulungu, n’chifukwa chiyani mwatitaya?+
N’chifukwa chiyani mkwiyo wanu ukuyakira nkhosa zimene mukuweta?+
2 Kumbukirani anthu amene munawatenga kukhala anu kalelo,+
Fuko limene munaliwombola monga cholowa chanu,+
Ndi phiri la Ziyoni ili mmene inu mukukhala.+
4 Anthu amene akukuchitirani zoipa afuula mosangalala kuti apambana m’malo anu olambiriramo.+
Aikamo mbendera zawo monga zizindikiro.+
5 Iwo amatchuka ngati munthu amene amagwetsa mitengo ndi nkhwangwa m’nkhalango.
6 Ndipo tsopano zojambula mochita kugoba za m’makoma a malo opatulika, onse amazichotsa ndi nkhwangwa komanso ndodo zokhala ndi chitsulo kumutu kwake.+
8 Iwo, ngakhalenso ana awo, onse pamodzi anena mumtima mwawo kuti:
“Malo onse olambiriramo a Mulungu ayenera kutenthedwa m’dzikoli.”+
9 Zizindikiro zathu sitinazione, ndipo palibenso mneneri amene watsala,+
Pakati pathu palibe amene akudziwa kuti zikhala choncho mpaka liti.
10 Inu Mulungu, kodi mdani adzakuchitirani mopanda ulemu kufikira liti?+
Kodi mdani adzanyoza dzina lanu kwamuyaya?+
11 N’chifukwa chiyani mwachotsa dzanja lanu, dzanja lanu lamanja,+
Pachifuwa panu koma osachitapo kanthu? Kodi mukatero ife sitiwonongedwa?
12 Koma Mulungu ndi Mfumu yanga kuyambira kalekale,+
Iye ndiye wondipatsa chipulumutso chachikulu padziko lapansi.+
14 Inu munaphwanya mitu ya Leviyatani*+ kukhala zidutswazidutswa.
Munaipereka kwa anthu monga chakudya, munaipereka kwa anthu okhala m’madera opanda madzi.+
15 Ndinu amene munang’amba nthaka ndi kupanga akasupe ndi makwawa.+
Inu munaumitsa mitsinje imene inali kukhala ndi madzi nthawi zonse.+
17 Ndinu amene munaika malire onse a dziko lapansi.+
Munapanga nyengo yachilimwe ndi nyengo yachisanu.+
18 Kumbukirani izi: Inu Yehova, mdani wakuchitirani mopanda ulemu,+
Ndipo anthu opusa anyoza dzina lanu.+
19 Musapereke moyo wa njiwa yanu kwa chilombo chakuthengo.+
Musaiwale kwamuyaya moyo wa anthu anu osautsika.+
20 Kumbukirani pangano limene munachita nafe,+
Pakuti malo a mdima a dziko lapansi adzaza ndi chiwawa.+
21 Musalole kuti munthu woponderezedwa achite manyazi.+
Munthu wosautsika ndi wosauka atamande dzina lanu.+
22 Nyamukani inu Mulungu, weruzani mlandu wanu.+
Kumbukirani mmene munthu wopusa wakunyozerani tsiku lonse.+
23 Musaiwale mawu a anthu amene akukuchitirani zoipa.+
Phokoso la anthu okuukirani likukwera kumwamba nthawi zonse.+
Kwa wotsogolera nyimbo. “Musandiwononge.” Nyimbo ndi Salimo la Asafu.+
75 Timakuyamikani, inu Mulungu, timakuyamikani,+
Ndipo dzina lanu lili pafupi ndi ife.+
Anthu ayenera kulengeza ntchito zanu zodabwitsa.+
3 Dziko lapansi ndi onse okhala mmenemo anayamba kusungunuka chifukwa cha mantha,+
Ndine amene ndinakonzanso zipilala zake.”+ [Seʹlah.]
6 Pakuti kukwezeka kwa munthu sikuchokera kum’mawa,
Kumadzulo kapena kum’mwera.
8 M’dzanja la Yehova muli kapu.+
Kapuyo yadzaza ndi vinyo wosakaniza ndi zokometsera ndipo akuchita thovu.
Ndithudi, iye adzatsanula vinyo yense amene ali m’kapuyo kuphatikizapo nsenga zake.
Anthu onse oipa padziko lapansi adzamwa ndi kugugudiza nsengazo.”+
10 Mulungu akuti:* “Ndidzadula nyanga zonse za anthu oipa.”+
Koma nyanga za munthu wolungama zidzakwezedwa.+
Kwa wotsogolera nyimbo: Iimbidwe ndi zipangizo za zingwe. Nyimbo ndi Salimo la Asafu.+
4 Inu Mulungu, mwazunguliridwa ndi kuwala, ndipo ndinu wochititsa nthumanzi kuposa mapiri amene muli nyama zodya zinzake.+
5 Anthu olimba mtima alandidwa zinthu zawo,+
Iwo awodzera ndi kugona tulo,+
Ndipo palibe ngakhale mmodzi mwa anthu onse olimba mtimawo amene ali ndi mphamvu zotsutsa.+
6 Hatchi komanso wokwera galeta agona tulo tofa nato chifukwa cha kudzudzula kwanu, inu Mulungu wa Yakobo.+
8 Munachititsa ziweruzo zanu kumveka kuchokera kumwambako.+
Dziko lapansi linachita mantha ndipo linakhala duu+
9 Pamene Mulungu ananyamuka ndi kupereka chiweruzo,+
Kuti apulumutse anthu onse ofatsa padziko lapansi.+ [Seʹlah.]
11 Inu nonse amene mwazungulira Mulungu, lonjezani ndi kukwaniritsa malonjezo anuwo kwa Yehova Mulungu wanu.+
Bweretsani mphatso mwamantha.+
Kwa wotsogolera nyimbo pa Yedutuni. Nyimbo ndi Salimo la Asafu.+
2 Pa tsiku la zowawa zanga ndafunafuna Yehova.+
Ndakweza dzanja langa kumwamba usiku wonse, ndipo silinachite dzanzi.
Koma sindinatonthozeke.+
3 Ndidzakumbukira Mulungu ndipo ndidzavutika maganizo.+
Ine ndasautsika. N’chifukwa chake ndafooka.+ [Seʹlah.]
6 Usiku ndidzakumbukira nyimbo zanga zoimbidwa ndi chipangizo cha zingwe.+
Ndidzasonyeza kudera nkhawa mumtima mwanga,+
Ndipo ndidzasinkhasinkha zinthu zonse mozama.
8 Kodi kukoma mtima kwake kosatha wakusiya mpaka muyaya?+
Kodi malonjezo ake sadzakwaniritsidwa+ ku mibadwomibadwo?
10 Kodi ndizingonena kuti: “Zimene zikundisautsa n’zakuti,+
Wam’mwambamwamba wasiya kutipatsa thandizo”?+
13 Inu Mulungu, njira yanu ili m’malo oyera.+
Kodi ndi Mulungu wamkulu uti amene angafanane ndi Mulungu wathu?+
14 Inu ndinu Mulungu woona amene mukuchita zodabwitsa.+
Mphamvu zanu mwazidziwikitsa pakati pa mitundu ya anthu.+
16 Madzi akuonani, inu Mulungu,
Madzi akuonani, ndipo ayamba kumva ululu woopsa.+
Komanso madzi akuya ayamba kuwinduka.+
17 Mitambo yatulutsa mabingu ndi kugwetsa madzi.+
Thambo latulutsa mkokomo.
Mphezi zanu zinawala paliponse ngati mivi.+
18 Phokoso la bingu lanu linali ngati la mawilo a galeta.+
Mphezi zinaunika padziko.+
Ndipo dziko lapansi linagwedezeka ndi kuyamba kunjenjemera.+
19 Msewu wanu unadutsa panyanja,+
Ndipo njira yanu inadutsa pamadzi ambiri.
Mmene mapazi anu anaponda simunaoneke.
2 Ndidzatsegula pakamwa panga ndi kunena mwambi.+
Ndidzanena mawu ophiphiritsa akalekale,+
3 Amene tinamva ndipo tikuwadziwa,+
Komanso amene makolo athu anatifotokozera.+
4 Mbadwa zawo sitikuzibisira mawu ophiphiritsawa,+
Ndipo tidzawasimba ngakhale ku mibadwo ya m’tsogolo.+
Tidzasimba ntchito zotamandika za Yehova ndi mphamvu zake,+
Komanso zinthu zodabwitsa zimene wachita.+
5 Mulungu anaika chikumbutso pakati pa ana a Yakobo,+
Iye anaika chilamulo mu Isiraeli,+
Zinthu zimene analamula makolo athu,+
Kuti auze ana awo.+
6 Kuti m’badwo wa m’tsogolo, ana amene adzabadwe m’tsogolo, adzadziwe zimenezi,+
Kuti nawonso adzanyamuke ndi kusimbira ana awo.+
7 Kuti anawo azidzadalira Mulungu,+
Ndi kuti asadzaiwale zochita za Mulungu+ koma kuti azidzasunga malamulo ake.+
8 Ndipo asadzakhale ngati makolo awo,+
M’badwo wosamva ndi wopanduka,+
M’badwo umene sunakonze mtima wawo,+
Ndipo maganizo awo sanali okhulupirika kwa Mulungu.+
14 Iye anapitiriza kuwatsogolera ndi mtambo masana,+
Ndipo usiku wonse anali kuwatsogolera ndi kuwala kwa moto.+
17 Koma iwo anapitiriza kumuchimwira+
Mwa kupandukira Wam’mwambamwamba m’dera lopanda madzi.+
18 Iwo anapitiriza kuyesa Mulungu m’mitima yawo+
Mwa kupempha chakudya china chimene mtima wawo unalakalaka.+
19 Pamenepo anayamba kulankhula mawu oipa kwa Mulungu.+
Iwo anati: “Kodi Mulungu angathe kutipatsa chakudya m’chipululu muno?”+
20 Taonani! Kodi Mulungu si uja anamenya thanthwe+
Kuti madzi atuluke, kutinso patuluke mitsinje yodzaza madzi?+
Koma iwo anati: “Kodi angathenso kutipatsa chakudya,+
Kapena kodi angakonzere anthu ake chakudya?”+
21 Choncho Yehova anamva zimenezo ndipo anakwiya.+
Moti moto unayakira Yakobo,+
Ndipo mkwiyo unatsikira pa Isiraeli.+
24 Ndipo anapitiriza kuwagwetsera mana ngati mvula kuti adye.+
Iye anawapatsa tirigu wochokera kumwamba.+
26 Anachititsa mphepo ya kum’mawa kuwomba m’mlengalenga,+
Ndipo mwa mphamvu zake anachititsa mphepo ya kum’mwera kuwomba.+
27 Iye anagwetsa chakudya pa iwo ngati fumbi.+
Anawagwetsera zolengedwa zamapiko zouluka, zochuluka ngati mchenga wakunyanja.+
30 Iwo anafunabe chakudya china,
Pamene china chinali m’kamwa.+
31 Nthawi yomweyo, mkwiyo wa Mulungu unatsikira pa iwo.+
Iye anayamba kupha anthu awo amphamvu.+
Ndipo anakomola anyamata a mu Isiraeli.
32 Ngakhale zinali choncho, iwo anawonjezera machimo awo,+
Ndipo sanakhulupirire ntchito zake zodabwitsa.+
33 Choncho anathetsa masiku a moyo wawo ngati mpweya wotuluka m’mphuno.+
Anadula zaka za moyo wawo ndi masoka.
34 Nthawi zonse akayamba kuwapha, iwo anali kumufunafuna.+
Anali kutembenuka ndi kuyamba kufunafuna Mulungu.+
35 Iwo anali kukumbukira kuti Mulungu anali Thanthwe lawo,+
Ndiponso kuti Mulungu Wam’mwambamwamba anali Wowabwezerera.+
36 Koma iwo anali kufuna kum’pusitsa ndi pakamwa pawo.+
Ndi lilime lawo anali kufuna kunena bodza kwa iye.+
38 Koma anawamvera chifundo.+ Anali kukhululukira* machimo awo+ ndipo sanali kuwawononga.+
Nthawi zambiri anali kubweza mkwiyo wake,+
Ndipo sanali kuwasonyeza ukali wake wonse.
39 Iye anali kukumbukira nthawi zonse kuti iwo ndi anthu athupi la nyama,+
Anali kukumbukira kuti moyo wawo umachoka ndipo subwereranso.+
42 Iwo sanakumbukire dzanja la Mulungu,+
Sanakumbukire tsiku limene anawawombola kwa mdani wawo,+
43 Iwo sanakumbukire mmene anaikira zizindikiro zake mu Iguputo,+
Ndi zozizwitsa zimene anachita m’dera la Zowani,+
44 Mmene anasinthira mitsinje ing’onoing’ono yotuluka mumtsinje wa Nailo kukhala magazi,+
Moti sanathe kumwa madzi ake.+
49 Anawasonyeza mkwiyo wake woyaka moto,+
Ukali, ziweruzo zamphamvu ndi masautso.+
Anawatumizira makamu a angelo obweretsa masoka.+
51 Pamapeto pake anapha ana onse oyamba kubadwa mu Iguputo,+
Amene ndi chiyambi cha mphamvu zawo zobereka m’mahema a Hamu.+
52 Kenako anachititsa anthu ake kuchoka m’dzikolo ngati gulu la nkhosa,+
Anawayendetsa m’chipululu ngati gulu la ziweto.+
54 Kenako anawalowetsa m’dziko lake lopatulika,+
M’dera lamapiri ili limene dzanja lake lamanja linatenga.+
55 Chifukwa cha iwo anachotsa mitundu ina pang’onopang’ono m’dzikoli,+
Ndipo anayesa dzikoli ndi kuligawa kwa iwo kukhala cholowa chawo,+
Moti anachititsa mafuko a Isiraeli kukhala m’nyumba zawozawo.+
56 Koma iwo anayamba kuyesa Mulungu Wam’mwambamwamba ndi kum’pandukira,+
Ndipo sanasunge zikumbutso zake.+
57 Iwo anali kubwerera ndi kuchita zinthu mwachinyengo ngati makolo awo.+
Anapotoka maganizo ngati uta wosakunga kwambiri.+
58 Iwo anapitiriza kumukhumudwitsa ndi malo awo okwezeka,+
Ndipo anamuchititsa nsanje ndi zifaniziro zawo zogoba.+
60 Pamapeto pake anasiya chihema chopatulika cha ku Silo,+
Hema limene anali kukhalamo pakati pa anthu ochokera kufumbi.+
61 Analola kuti chizindikiro cha mphamvu zake chitengedwe ndi adani ake,+
Iye analola kuti chizindikiro cha kukongola kwake chikhale m’manja mwa adani.+
65 Pamenepo Yehova anagalamuka ngati akudzuka kutulo,+
Ngati munthu wamphamvu amene akugalamuka pambuyo pomwa vinyo wambiri.+
69 Anayamba kumanga malo opatulika ngati malo okwera a paphiri,+
Ngati dziko lapansi limene analikhazikitsa mpaka kalekale.+
71 Anamutenga kumene anali kuweta nkhosa zoyamwitsa,+
Anamutenga kuti akhale m’busa wa ana a Yakobo amene ndi anthu ake,+
Ndi Isiraeli, amene ndi cholowa chake.+
72 Iye anayamba kuwaweta malinga ndi mtima wake wosagawanika,+
Ndipo anayamba kuwatsogolera mwaluso.+
Nyimbo ya Asafu.
79 Inu Mulungu, anthu a mitundu ina alowa m’dziko limene ndilo cholowa chanu.+
Aipitsa kachisi wanu woyera.+
Awononga Yerusalemu ndi kumusandutsa bwinja.+
2 Apereka mitembo ya atumiki anu kwa mbalame kuti chikhale chakudya chawo.+
Matupi a okhulupirika anu awapereka kwa zilombo zakutchire.+
5 Haa! Inu Yehova, mukhala wokwiya mpaka liti? Kwamuyaya?+
Kodi mkwiyo wanu udzakhala ukuyaka ngati moto mpaka liti?+
6 Tsanulirani mkwiyo wanu pa mitundu ya anthu amene akukunyalanyazani,+
Ndi pa maufumu amene sakuitana pa dzina lanu.+
8 Musatiimbe mlandu chifukwa cha zolakwa za makolo athu.+
Fulumirani! Tisonyezeni chifundo chanu,+
Chifukwa tasautsika koopsa.+
9 Tithandizeni inu Mulungu wa chipulumutso chathu,+
Kuti dzina lanu lilemekezedwe.+
Tipulumutseni ndi kutikhululukira* machimo athu chifukwa cha dzina lanu.+
10 Musalole kuti anthu a mitundu ina azinena kuti: “Mulungu wawo ali kuti?”+
Pamene mukubwezera anthu a mitundu inawo chifukwa cha magazi a atumiki anu amene anakhetsedwa,+
Ife tidzaone ndi maso athu.+
12 Bwezerani anthu oyandikana nafe mwa kuwatsanulira chitonzo pachifuwa pawo maulendo 7,+
Inu Yehova, muwabwezere chitonzo chimene anachita pa inu.+
13 Koma ife, anthu anu, nkhosa zimene mukuweta,+
Tidzakuyamikani mpaka kalekale.
Tidzakutamandani ku mibadwomibadwo.+
Kwa wotsogolera nyimbo pa Maluwa.*+ Chikumbutso.* Nyimbo ndi Salimo la Asafu.+
4 Inu Yehova Mulungu wa makamu, mudzakwiyira mapemphero a anthu anu mpaka liti?+
6 Mwachititsa kuti anthu oyandikana nafe azimenyana polimbirana ifeyo.+
Ndipo adani athu akupitirizabe kutinyoza mmene akufunira.+
8 Munachititsa mtengo wa mpesa kuchoka mu Iguputo.+
Munapitikitsa mitundu ya anthu kuti mubzalemo mtengowo.+
9 Munalambula malo obzalapo mtengo wa mpesawo+ kuti uzike mizu ndi kudzaza dziko.+
12 N’chifukwa chiyani mwagwetsa mpanda wake wamiyala?+
Ndipo n’chifukwa chiyani anthu onse odutsa mumsewu akuthyola zipatso zake?+
14 Inu Mulungu wa makamu, chonde bwererani.+
Yang’anani pansi pano muli kumwambako, ndipo onani ndi kusamalira mtengo wa mpesa uwu.+
15 Onani muzu umene dzanja lanu lamanja linabzala.+
Muonenso mwana wanu amene munamulimbitsa kuti inu mulemekezeke.+
17 Dzanja lanu likhale pa munthu wa kudzanja lanu lamanja,+
Ndipo likhale pa mwana wa munthu amene mwamulimbitsa kuti mulemekezeke.+
18 Ndipo ife sitidzabwerera kukusiyani.+
Tisungeni amoyo kuti tiitane pa dzina lanu.+
19 Inu Yehova Mulungu wa makamu, tibwezeretseni mwakale.+
Walitsani nkhope yanu kuti tipulumutsidwe.+
Kwa wotsogolera nyimbo pa Gititi.*+ Salimo la Asafu.
81 Anthu inu, fuulani mosangalala kwa Mulungu amene ndi mphamvu yathu,+
Fuulirani Mulungu wa Yakobo mosangalala chifukwa wapambana.+
2 Yambani kuimba nyimbo+ ndipo tengani maseche,+
Zeze womveka mosangalatsa pamodzi ndi choimbira cha zingwe.+
3 Pa tsiku lokhala mwezi, imbani lipenga la nyanga ya nkhosa.+
Pa tsiku looneka mwezi wathunthu, imbani lipenga la nyanga ya nkhosa, loimba pa tsiku la chikondwerero.+
5 Anaika chigamulocho monga chikumbutso kwa Yosefe,+
Pamene anali kutuluka m’dziko la Iguputo.+
Ndinali kumva chilankhulo chimene sindinali kuchidziwa.+
7 Pa nthawi ya nsautso unaitana ndipo ine ndinakupulumutsa.+
Ndinayamba kukuyankha m’malo obisika a bingu.+
Ndinakusanthula pamadzi a Meriba.+ [Seʹlah.]
8 Imvani anthu anga, ndipo ndidzakulangizani ndi kukuchenjezani.+
Zikanakhala bwino ngati mukanandimvera, inu Aisiraeli.+
10 Ine Yehova, ndine Mulungu wanu,+
Amene ndinakutulutsani m’dziko la Iguputo.+
Tsegulani pakamwa panu ndipo ndidzaikamo chakudya.+
11 Koma anthu anga sanamvere mawu anga.+
Ndipo Isiraeli sanasonyeze kuti ndi wofunitsitsa kundimvera.+
13 Haa! Zikanakhala bwino ngati anthu anga akanandimvera,+
Zikanakhala bwino ngati Isiraeli akanayenda m’njira zanga.+
15 Koma odana kwambiri ndi Yehova adzabwera kwa iye akunjenjemera ndi mantha,+
Ndipo nthawi yawo idzakhala mpaka kalekale.
16 Ine ndidzadyetsa Aisiraeli tirigu wabwino koposa,+
Ndipo ndidzawapatsa uchi wochokera pathanthwe+ kuti adye ndi kukhuta.”
Nyimbo ya Asafu.
3 Chitirani chilungamo anthu onyozeka ndi ana amasiye.*+
Chitirani chilungamo anthu osautsika ndi osauka.+
5 Milunguyo siikudziwa kanthu ndipo siikuzindikira.+
Ikuyendayenda mu mdima,+
Ndipo maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.+
8 Nyamukani inu Mulungu, weruzani dziko lapansi.+
Pakuti inu nokha muyenera kutenga mitundu yonse kukhala yanu.+
Nyimbo ndi Salimo la Asafu.+
83 Inu Mulungu, musakhale chete.+
Musakhale phee osalankhulapo kanthu ndipo musakhale duu osachitapo kanthu, inu Mulungu.+
3 Iwo amakumana mwachinsinsi kuti akambirane zochitira chiwembu anthu anu.+
Ndipo amakonzera chiwembu anthu anu obisika.+
4 Iwo anena kuti: “Bwerani tiwafafanize kuti asakhalenso mtundu,+
Ndi kuti dzina la Isiraeli lisakumbukikenso.”+
5 Pakuti ndi mtima wonse, iwo amagawana nzeru,+
Ndipo anapangana pangano lotsutsana ndi inu.+
6 Amenewa ndi anthu okhala m’mahema a Edomu+ ndi m’mahema a Isimaeli, Amowabu+ ndi Ahagara,+
9 Muwachitire zimene munachitira Midiyani+ ndi Sisera.+
Muwachitirenso zimene munachitira Yabini+ kuchigwa cha Kisoni.+
11 Atsogoleri awo muwachititse kukhala ngati Orebi ndi Zeebi.+
Ndipo mafumu awo onse muwachititse kukhala ngati Zeba ndi Zalimuna.+
12 Iwo anena kuti: “Tiyeni tilande malo amene Mulungu amakhalako kuti akhale athu.”+
13 Inu Mulungu wanga, achititseni kukhala ngati udzu wouma wouluzika ndi mphepo,+
Ngati mapesi otengeka ndi mphepo.+
14 Mofanana ndi moto wotentha nkhalango,+
Ndiponso malawi a moto woyaka m’mapiri,+
15 Muwathamangitse ndi mphepo yanu yamphamvu,+
Ndipo muwasokoneze ndi mphepo yanu yamkuntho.+
17 Achite manyazi ndi kusokonezeka nthawi zonse.+
Athedwe nzeru ndi kutheratu,+
18 Kuti anthu adziwe+ kuti inu, amene dzina lanu ndinu Yehova,+
Inu nokha ndinu Wam’mwambamwamba,+ wolamulira dziko lonse lapansi.+
Kwa wotsogolera nyimbo pa Gititi.*+ Nyimbo ndi Salimo la ana a Kora.
2 Ndimalakalaka mabwalo a Yehova ndipo ndafookeratu chifukwa cholakalaka mabwalowo.+
Mtima wanga ndi thupi langa zikufuula mosangalala kwa Mulungu wamoyo.+
3 Inu Yehova wa makamu, Mfumu yanga ndi Mulungu wanga,
Ngakhale mbalame zapeza malo okhala pafupi ndi guwa lanu lansembe lalikulu.
Namzeze* wadzimangira chisa chake pamenepo,
Ndi kuikamo ana ake!
5 Odala ndi anthu amene amapeza mphamvu kuchokera kwa inu,+
Amene mtima wawo umalakalaka misewu yaikulu yopita kunyumba yanu.+
6 Poyenda m’chigwa chouma mmene muli zitsamba za baka,*+
Amasandutsa chigwacho kukhala choyenda madzi ochokera pakasupe,
Mlangizi wafunda mawu otamanda.+
7 Mphamvu zawo zidzapitiriza kuwonjezeka pamene akuyenda.+
Aliyense wa iwo amaonekera kwa Mulungu mu Ziyoni.+
8 Yehova Mulungu wa makamu, imvani pemphero langa,+
Tcherani khutu, inu Mulungu wa Yakobo.+ [Seʹlah.]
10 Pakuti kukhala tsiku limodzi m’mabwalo anu n’kwabwino kuposa kukhala masiku 1,000 kwina.+
Ndasankha kuima pakhomo la nyumba ya Mulungu wanga+
Kuposa kukhala m’mahema a anthu oipa.+
11 Pakuti Yehova Mulungu ndi dzuwa+ ndiponso chishango.+
Iye amatikomera mtima ndi kutipatsa ulemerero.+
Yehova samana anthu oyenda mosalakwa chinthu chilichonse chabwino.+
12 Inu Yehova wa makamu, wodala ndi munthu amene amakhulupirira inu.+
Kwa wotsogolera nyimbo. Nyimbo ndi Salimo la ana a Kora.
85 Inu Yehova, mwasangalala ndi dziko lanu.+
Mwabwezeretsa ana a Yakobo amene anagwidwa ndi kutengedwa kupita kudziko lina.+
4 Tisonkhanitseni ndi kutibwezeretsa mwakale, inu Mulungu wa chipulumutso chathu,+
Ndipo tichotsereni mkwiyo wanu.+
8 Ndidzamvetsera zimene Mulungu woona Yehova adzanena,+
Pakuti adzanena za mtendere kwa anthu ake+ ndi kwa okhulupirika ake.
Koma iwo asadzidalire kwambiri ngati kale.+
9 Ndithudi, chipulumutso chake chili pafupi ndi amene amamuopa,+
Kuti ulemerero ukhale m’dziko lathu.+
Pemphero la Davide.
2 Tetezani moyo wanga pakuti ndine wokhulupirika.+
Inu ndinu Mulungu wanga, pulumutsani mtumiki wanu amene amakukhulupirirani.+
5 Pakuti inu Yehova ndinu Mulungu wabwino+ ndipo ndinu wokonzeka kukhululuka.+
Kukoma mtima kosatha kumene mumawasonyeza onse oitana pa inu ndi kwakukulu.+
8 Inu Yehova, palibe mulungu wina amene angafanane ndi inu.+
Ndipo palibe ntchito zilizonse zofanana ndi ntchito zanu.+
9 Mitundu yonse imene munapanga idzabwera kwa inu,+
Ndipo idzagwada pamaso panu, inu Yehova,+
Ndi kulemekeza dzina lanu.+
11 Inu Yehova, ndilangizeni za njira yanu.+
Ndidzayenda m’choonadi chanu.+
Ndipatseni mtima wosagawanika kuti ndiope dzina lanu.+
12 Ndikukutamandani inu Yehova Mulungu wanga ndi mtima wanga wonse,+
Ndipo ndidzalemekeza dzina lanu mpaka kalekale,
13 Pakuti kukoma mtima kosatha kumene mwandisonyeza ndi kwakukulu,+
Ndipo mwapulumutsa moyo wanga ku Manda, kumalo apansi penipeni.+
14 Inu Mulungu, anthu odzitukumula andiukira.+
Khamu la anthu opondereza anzawo likufunafuna moyo wanga,+
Ndipo sanakuikeni patsogolo pawo.+
15 Koma inu Yehova, ndinu Mulungu wachifundo ndi wachisomo,+
Wosakwiya msanga+ ndiponso wodzaza ndi kukoma mtima kosatha ndi choonadi.+
16 Ndicheukireni ndi kundikomera mtima.+
Patsani mtumiki wanu mphamvu,+
Ndipo pulumutsani mwana wa kapolo wanu wamkazi.+
17 Ikani chizindikiro cha ubwino wanu pa ine,
Kuti anthu odana nane aone zimenezi ndi kuchita manyazi,+
Pakuti inu Yehova mwandithandiza ndi kundilimbikitsa.+
Nyimbo ndi Salimo la ana a Kora.
87 Maziko a mzinda wa Mulungu ali m’mapiri opatulika.+
3 Iwe mzinda wa Mulungu woona, anthu akunena za ulemerero wako.+ [Seʹlah.]
4 Ine ndidzatchula Rahabi*+ ndi Babulo+ monga ena mwa amene akundidziwa.
Ponena za Filisitiya,+ Turo ndi Kusi ine ndidzati:
“Amenewa anabadwira m’Ziyoni.”+
7 Kudzakhalanso oimba komanso ovina gule wovina mozungulira amene adzati:+
“Akasupe anga onse ali mwa iwe.”+
Nyimbo ndi Salimo la ana a Kora. Kwa wotsogolera nyimbo pa Mahalati.* Iimbidwe molandizana. Masikili* ya Hemani+ wa m’banja la Zera.
88 Inu Yehova, Mulungu wa chipulumutso changa,+
Masana ndimafuula kwa inu,+
Usikunso ndimafuula pamaso panu.+
4 Anandiika m’gulu la anthu otsikira kudzenje.+
Ndakhala ngati mwamuna wanyonga zake koma wopanda mphamvu.+
5 Ndakhala womasuka ngati anthu akufa,+
Ngati anthu ophedwa amene agona m’manda,+
Anthu amene simukuwakumbukiranso
Komanso amene sakulandira thandizo kuchokera m’manja mwanu.+
8 Anzanga mwawaika kutali ndi ine.+
Mwandisandutsa chinthu chonyansa kwa iwo.+
Ndatsekerezedwa ndipo sindingathenso kuchoka.+
9 Diso langa lafooka chifukwa cha kusautsika kwanga.+
Ndaitana inu Yehova tsiku lonse.+
Ndapemphera kwa inu nditakweza manja anga.+
10 Kodi anthu akufa mudzawachitira zodabwitsa?+
Kapena kodi anthu akufa, anthu amene sangachite kanthu, adzauka?+
Kodi adzakutamandani?+ [Seʹlah.]
11 Kodi adzalengeza za kukoma mtima kwanu kosatha m’manda?
Kodi adzalengeza za kukhulupirika kwanu m’malo a chiwonongeko?+
12 Kodi zodabwitsa zimene inu mukuchita zidzadziwika mu mdima?+
Kapena kodi chilungamo chanu chidzadziwika m’dziko la anthu oiwalika?+
13 Koma ine ndafuulira inu Yehova kupempha thandizo,+
Ndipo m’mawa mapemphero anga amafika kwa inu nthawi zonse.+
15 Kuyambira pa unyamata wanga ndakhala ndikusautsika komanso kutsala pang’ono kufa.+
Ndapirira kwambiri zinthu zoopsa zochokera kwa inu.+
16 Mafunde a mkwiyo wanu woyaka moto andimiza.+
Zinthu zochititsa mantha zochokera kwa inu zandisowetsa chonena.+
Masikili.* Salimo la Etani wa m’banja la Zera.+
89 Ndidzaimba mpaka kalekale za ntchito za Yehova zosonyeza kukoma mtima kwake kosatha.+
Ndidzalengeza ndi pakamwa panga ku mibadwomibadwo za kukhulupirika kwanu.+
2 Pakuti ndanena kuti: “Kukoma mtima kwanu kosatha kudzakhazikika mpaka kalekale.+
Ndipo mwakhazikitsa kukhulupirika kwanu kumwamba.”+
3 Mulungu anati: “Ndachita pangano ndi wosankhidwa wanga.+
Ndalumbira kwa Davide mtumiki wanga,+
4 ‘Ndidzakhazikitsa mbewu yako mpaka kalekale,+
Ndipo ndidzalimbitsa mpando wako wachifumu+ ku mibadwomibadwo.’” [Seʹlah.]
5 Inu Yehova, kumwamba kudzatamanda ntchito zanu zodabwitsa.+
Mpingo wa oyera anu udzatamanda kukhulupirika kwanu.
6 Pakuti ndani kumwamba angayerekezeredwe ndi Yehova?+
Ndani angafanane ndi Yehova pakati pa ana a Mulungu?+
7 Mulungu ayenera kuopedwa pakati pa gulu lake la oyera.+
Iye ndi wamkulu ndi wochititsa mantha kuposa onse omuzungulira.+
8 Inu Yehova Mulungu wa makamu,+
Ndani ali ndi mphamvu ngati inu Ya?+
Ndinu wokhulupirika pa chilichonse.+
10 Mwaphwanya Rahabi*+ ndi kumuchititsa kukhala ngati munthu amene waphedwa.+
Mwabalalitsa adani anu ndi dzanja lanu lamphamvu.+
11 Kumwamba ndi kwanu,+ dziko lapansi nalonso ndi lanu.+
Nthaka ya dziko lapansi ndiponso zinthu zimene zili mmenemo+ munazipanga ndinu.+
12 Munapanga kumpoto ndi kum’mwera.+
Mapiri a Tabori+ ndi Herimoni+ amafuula mokondwera ndi kutamanda dzina lanu.+
14 Chilungamo ndi chiweruzo ndizo maziko a mpando wanu wachifumu.+
Kukoma mtima kosatha ndi choonadi zili pamaso panu.+
15 Odala ndi anthu amene amafuula mosangalala.+
Iwo amayendabe m’kuwala kwa nkhope yanu, inu Yehova.+
18 Pakuti chishango chathu ndi chochokera kwa Yehova,+
Ndipo mfumu yathu ndi yochokera kwa Woyera wa Isiraeli.+
19 Pa nthawi imeneyo munalankhula ndi okhulupirika anu mwa masomphenya,+
Ndipo munati:
“Ndapereka thandizo kwa wamphamvu.+
Ndakweza wosankhidwa mwapadera pakati pa anthu.+
20 Ndapeza Davide mtumiki wanga,+
Ndipo ndamudzoza ndi mafuta anga opatulika.+
21 Dzanja langa lolimba lidzakhala pa iye.+
Mkono wanga udzamulimbitsa.+
22 Palibe mdani amene adzamupondereza,+
Ndipo palibe mwana aliyense wa anthu oipa amene adzamusautsa.+
23 Ndinaphwanya adani ake zidutswazidutswa ndi kuwachotsa pamaso pake,+
Ndipo odana naye kwambiri ndinapitirizabe kuwamenya.+
24 Kukhulupirika kwanga ndi kukoma mtima kwanga kosatha kuli pa iye,+
Ndipo nyanga yake imakwezedwa m’dzina langa.+
27 Inenso ndidzamuika kukhala mwana woyamba kubadwa,+
Ndiponso mfumu yaikulu pa mafumu onse a padziko lapansi.+
28 Ndidzamusonyeza kukoma mtima kwanga kosatha mpaka kalekale,+
Ndipo pangano limene ndinachita naye silidzaphwanyidwa.+
29 Ndidzakhazikitsa mbewu yake kwamuyaya,+
Ndipo mpando wake wachifumu udzakhalapo kwa masiku ochuluka ngati masiku a kumwamba.+
30 Ana ake akadzasiya chilamulo changa,+
Ndi kuleka kutsatira zigamulo zanga,+
31 Akadzanyoza mfundo zanga,
Ndi kusasunga malamulo anga,
32 Ine ndidzawaimba mlandu ndi kuwalanga ndi ndodo,+
Ndipo ndidzawalanga ndi zikoti chifukwa cha zolakwa zawo.+
33 Koma kukoma mtima kwanga kosatha sindidzakuchotsa pa iye,+
Ndipo sindidzasiya kukhulupirika kwanga.+
36 Mbewu yake idzakhala mpaka kalekale,+
Ndipo mpando wake wachifumu udzakhala ngati dzuwa pamaso panga.+
37 Udzakhazikika ngati mwezi mpaka kalekale,
Udzakhala ngati mboni yokhulupirika ya m’mlengalengayo.” [Seʹlah.]
39 Mwakana moipidwa pangano la mtumiki wanu.
Mwanyoza chisoti chake chachifumu mwa kuchiponyera pansi.+
41 Onse oyenda njira imeneyo afunkha zinthu zake.+
Iye wakhala chinthu chotonzedwa kwa anthu oyandikana naye.+
43 Kuwonjezera apo, mukuonanso lupanga lake ngati mdani,+
Ndipo mwachititsa kuti iye asapambane pa nkhondo.+
46 Inu Yehova, kodi mudzadzibisa kufikira liti? Ku nthawi zonse?+
Kodi mkwiyo wanu udzakhalabe ukuyaka ngati moto?+
48 Kodi pali mwamuna wamphamvu aliyense amene sadzaona imfa?+
Kodi angathe kupulumutsa moyo wake m’dzanja la Manda?+ [Seʹlah.]
49 Kodi zochita zanu zakale zija zosonyeza kukoma mtima kosatha zili kuti, inu Yehova?
Zija zimene munalumbira kwa Davide chifukwa cha kukhulupirika kwanu?+
50 Inu Yehova, kumbukirani chitonzo chimene chagwera atumiki anu.+
Kumbukirani kuti ndanyamula pachifuwa panga chitonzo cha mitundu yambiri ya anthu.+
51 Inu Yehova, kumbukirani mmene adani anu alankhulira motonza,+
Mmene atonzera paliponse pamene mapazi a wodzozedwa wanu aponda.+
52 Adalitsike Yehova mpaka kalekale. Ame! Ame!*+
BUKU LACHINAYI
(Masalimo 90 – 106)
Pemphero la Mose, munthu wa Mulungu woona.+
Kapena musanakhazikitse dziko lapansi+ ndi malo okhalapo anthu,*+
Inu ndinu Mulungu kuyambira kalekale mpaka kalekale.+
5 Mwawawonongeratu,+ ndipo amangozimiririka ngati maloto.+
M’mawa amakhala ngati msipu wobiriwira umene watsitsimuka.+
8 Zolakwa zathu mwaziika patsogolo panu,+
Ndipo machimo athu obisika* ali patsogolo pa nkhope yanu yowala.+
9 Pakuti masiku athu onse atha chifukwa cha mkwiyo wanu.+
Zaka zathu zafika kumapeto ngati mpweya wotuluka m’mphuno pousa moyo.+
10 Masiku a moyo wathu amangokwana zaka 70,+
Ndipo ngati tili ndi mphamvu yapadera amakwana zaka 80.+
Koma ngakhale zili choncho, amangodzaza ndi mavuto ndi zopweteka.+
Pakuti masiku amene timakhala ndi moyo amatha mwamsanga ndipo timachoka mofulumira.+
11 Ndani angadziwe kukula kwa ukali wanu,+
Ndi kukula kwa mkwiyo wanu kumene kumafanana ndi ulemu umene muyenera kulandira?+
13 Bwererani kwa ife, inu Yehova!+ Kodi mudzatenga nthawi yaitali bwanji musanabwerere kwa ife?+
Timvereni chisoni ife atumiki anu.+
14 M’mawa mutikhutiritse ndi kukoma mtima kwanu kosatha,+
Kuti tifuule mokondwera ndi kuti tikhale osangalala masiku onse a moyo wathu.+
15 Tichititseni kusangalala kwa masiku ofanana ndi masiku amene mwatisautsa,+
Kwa masiku ofanana ndi zaka zimene taona masoka.+
17 Ubwino wa Yehova Mulungu wathu ukhale pa ife,+
Ndipo mukhazikitse ntchito ya manja athu.+
Muidalitse ntchito ya manja athu.+
91 Aliyense wokhala m’malo otetezeka+ a Wam’mwambamwamba+
Adzakhala wosungika mumthunzi wa Wamphamvuyonse.+
2 Ndidzauza Yehova kuti: “Inu ndinu pothawirapo panga ndi malo anga achitetezo,+
Mulungu wanga amene ndimamukhulupirira.”+
4 Adzakutchinjiriza ndi mapiko ake,+
Udzathawira pansi pa mapiko ake.+
Choonadi chake+ chidzakhala chishango chako+ chachikulu ndi malo ako achitetezo.
5 Usiku sudzaopa choopsa chilichonse,+
Ndipo sudzaopanso muvi+ woponyedwa masana,
6 Sudzaopa mliri umene umayenda mu mdima,+
Kapena chiwonongeko chimene chimachitika dzuwa lili paliwombo.+
7 Anthu 1,000 adzagwa pambali pako,
Ndipo anthu 10,000 adzagwa kudzanja lako lamanja.
Koma palibe zoterezi zimene zidzakuchitikira.+
9 Popeza wanena kuti: “Yehova ndiye pothawirapo panga,”+
Wapanga Wam’mwambamwamba kukhala malo ako okhalamo.+
10 Palibe tsoka limene lidzakugwera,+
Ndipo ngakhale mliri sudzayandikira hema wako.+
13 Udzapondaponda mkango wamphamvu ndi njoka ya mamba,+
Ndipo udzapondaponda mkango wamphamvu kwambiri ndi chinjoka.+
14 Mulungu wanena kuti: “Popeza wasonyeza kuti amandikonda,+
Inenso ndidzamupulumutsa.+
Ndidzamuteteza chifukwa wadziwa dzina langa.+
15 Adzandiitana ndipo ndidzamuyankha.+
Ndidzakhala naye m’nthawi ya masautso.+
Ndidzamupulumutsa ndi kumupatsa ulemerero.+
Nyimbo ndi Salimo la pa tsiku la sabata.
92 Ndi bwino kuyamika inu Yehova,+
Ndi kuimba nyimbo zotamanda dzina lanu, inu Wam’mwambamwamba.+
2 Ndi bwino kunena za kukoma mtima kwanu kosatha m’mawa,+
Ndi za kukhulupirika kwanu usiku,+
3 Ndipo ndidzatero pogwiritsa ntchito choimbira cha zingwe 10 ndi choimbira cha zingwe zitatu.+
Ndidzaimba nyimbo yomveka bwino ndi zeze.+
4 Pakuti mwandichititsa kusangalala, inu Yehova, chifukwa cha zochita zanu.
Ndimafuula mosangalala chifukwa cha ntchito ya manja anu.+
7 Anthu oipa akamaphuka ngati msipu,+
Ndipo anthu onse ochita zopweteka anzawo akamaphuka ngati maluwa,
Amatero kuti awonongeke kwamuyaya.+
8 Koma inu Yehova, ndinu wokwezeka mpaka kalekale.+
9 Pakuti taonani adani anu, inu Yehova!+
Adani anu onse adzatha!+
Anthu onse ochita zopweteka anzawo adzamwazikana.+
10 Koma inu mudzakweza nyanga* yanga ngati nyanga ya ng’ombe yam’tchire yamphongo.*+
Ndidzadzola mafuta abwino.+
11 Diso langa lidzayang’ana adani anga atagonja,+
Makutu anga adzamva za anthu ondiukira, anthu ochita zoipa.
12 Wolungama adzakula ngati mtengo wa kanjedza,+
Ndipo adzakula kwambiri ngati mtengo wa mkungudza wa ku Lebanoni.+
14 Zinthu zidzapitiriza kuwayendera bwino ngakhale atachita imvi,+
Adzakhalabe onenepa ndi athanzi,+
Iye wavala ulemerero.+
Yehova wavala mphamvu ngati chovala, ndipo wamangirira mphamvuzo m’chiuno mwake.+
Dziko lapansi lakhazikika, moti silingagwedezeke.+
3 Inu Yehova, mitsinje ikufuula.
Ikufuula ndi mawu amphamvu.+
Mitsinje ikupitiriza kufuula ndi mawu amkokomo.+
4 Ulemerero wa Yehova ndi waukulu+ kumwamba,
Kuposa mkokomo wa madzi ambiri, kuposanso mafunde amphamvu a m’nyanja.+
5 Zikumbutso zanu ndi zodalirika zedi.+
Chiyero ndi choyenera nyumba yanu+ mpaka muyaya, inu Yehova.+
4 Iwo amalankhula zopanda pake, ndipo amalankhula mosasamala.+
Onse ochita zopweteka anzawo amadzitukumula.+
10 Kodi amene amalangiza mitundu ya anthu,+
Amene amaphunzitsa anthu kuti akhale ozindikira, sangathe kudzudzula?+
11 Yehova amadziwa kuti maganizo a anthu ali ngati mpweya wotuluka m’mphuno.+
12 Wodala ndi munthu wamphamvu amene inu Ya mumamudzudzula,+
Komanso amene inu mumamuphunzitsa chilamulo chanu,+
13 Kuti mum’patse mtendere pa nthawi ya masoka,+
Kufikira dzenje la munthu woipa litakumbidwa.+
16 Ndani adzanyamuka kuti amenye nkhondo ndi anthu ochita zoipa m’malo mwa ine?+
Ndani adzaima m’malo mwa ine kulimbana ndi anthu ochita zopweteka anzawo?+
18 Pamene ndinanena kuti: “Phazi langa literereka,”+
Kukoma mtima kwanu kosatha, inu Yehova, kunandichirikiza.+
19 Malingaliro osautsa atandichulukira mumtima mwanga,+
Mawu anu otonthoza anayamba kusangalatsa moyo wanga.+
21 Iwo amaukira koopsa munthu wolungama,+
Ndipo munthu wosalakwa amamuweruza kuti ndi woipa. Amachita zimenezi kuti akhetse magazi ake.+
22 Koma Yehova adzakhala malo anga okwezeka ndiponso achitetezo,+
Ndipo Mulungu wanga adzakhala thanthwe langa lothawirako.+
23 Iye adzawabwezera zoipa zawo,+
Ndipo adzawakhalitsa chete mwa kuwadzetsera masoka okonza okha.+
Yehova Mulungu wathu adzawakhalitsa chete.+
95 Bwerani tifuule kwa Yehova mokondwera!+
Iye amene ndi Thanthwe la chipulumutso chathu, timufuulire mosangalala chifukwa wapambana.+
2 Tiyeni tionekere pamaso pake ndi chiyamiko.+
Tiyeni tiimbe nyimbo zomutamanda ndi kumufuulira mosangalala chifukwa wapambana.+
3 Pakuti Yehova ndi Mulungu wamkulu,+
Ndiponso ndi Mfumu yaikulu kuposa milungu ina yonse.+
4 Malo ozama kwambiri a dziko lapansi ali m’manja mwake,+
Mapiri aatali nawonso ndi ake.+
5 Nyanja imene anapanga ndi yake,+
Iye amenenso anapanga mtunda ndi manja ake.+
7 Pakuti iye ndi Mulungu wathu ndipo ife ndife anthu ake. Iye amatisamalira ngati nkhosa zimene akuweta.+
Lero anthu inu mukamvera mawu a Mulungu,+
8 Musaumitse mitima yanu monga mmene makolo anu anachitira pa Meriba,+
Monga mmene anachitira pa Masa m’chipululu,+
9 Pamene makolo anu anandiyesa.+
Iwo anandisanthula, ndipo anaonanso ntchito zanga.+
10 Kwa zaka 40, m’badwo umenewo unali kundinyansa,+
Ndipo ndinati:
“Anthu awa mitima yawo imasochera,+
Ndipo sadziwa njira zanga.”+
11 Kunena za anthu amenewa ndinalumbira mu mkwiyo wanga kuti:+
“Sadzalowa mu mpumulo wanga.”+
2 Imbirani Yehova, tamandani dzina lake.+
Tsiku ndi tsiku lengezani uthenga wabwino wa chipulumutso chake.+
3 Lengezani ulemerero wake pakati pa anthu a mitundu ina,+
Ndiponso ntchito zake zodabwitsa pakati pa mitundu yonse ya anthu.+
4 Pakuti Yehova ndi wamkulu+ ndi woyenera kutamandidwa kwambiri.
Iye ndi wochititsa mantha kuposa milungu ina yonse.+
5 Chifukwa milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi milungu yopanda pake,+
Koma Yehova ndiye anapanga kumwamba.+
7 Vomerezani Yehova, inu mabanja a mitundu ya anthu,+
M’patseni Yehova ulemerero ndi kuvomereza kuti iye ndi wamphamvu.+
9 Gwadirani Yehova mutavala zovala zokongola ndi zopatulika.+
Njenjemerani ndi mantha aakulu* pamaso pake, inu anthu nonse okhala padziko lapansi.+
10 Nenani pakati pa anthu a mitundu ina kuti: “Yehova wakhala mfumu.+
Dziko lapansi nalonso lakhazikika moti silingagwedezeke.+
Iye adzaweruzira mitundu ya anthu milandu yawo mwachilungamo.”+
11 Kumwamba kukondwere, ndipo dziko lapansi lisangalale.+
Nyanja ichite mkokomo ndi zonse zimene zili mmenemo.+
12 Mtunda ukondwere ndi zonse zimene zili kumeneko.+
Pa nthawi imodzimodziyo, mitengo ya m’nkhalango ifuule mokondwera pamaso pa Yehova.+
Iye wabwera kudzaweruza dziko lapansi.+
Adzaweruza dziko mwachilungamo,+
Ndipo adzaweruza mitundu ya anthu mokhulupirika.+
2 Mitambo ndi mdima wandiweyani zamuzungulira.+
Chilungamo ndi chiweruzo ndizo malo okhazikika a mpando wake wachifumu.+
7 Onse amene akupembedza chifaniziro chilichonse achite manyazi.+
Amene amadzitama chifukwa cha milungu yopanda pake achite manyazi.+
Muweramireni, inu milungu yonse.+
8 Ziyoni anamva ndipo anayamba kusangalala,+
Midzi yozungulira Yuda inayamba kukondwera+
Chifukwa cha zigamulo zanu, inu Yehova.+
9 Pakuti inu Yehova, ndinu Wam’mwambamwamba wolamulira dziko lonse lapansi.+
Mwakwera pamwamba kwambiri kuposa milungu ina yonse.+
10 Inu okonda Yehova+ danani nacho choipa.+
Iye amateteza moyo wa anthu ake okhulupirika.+
Amawalanditsa m’manja mwa anthu oipa.+
Nyimbo.
98 IMBIRANI Yehova nyimbo yatsopano,+
Pakuti zimene wachita ndi zodabwitsa.+
Dzanja lake lamanja, ndithu mkono wake woyera, wabweretsa chipulumutso.+
2 Yehova wachititsa chipulumutso chake kudziwika.+
Chilungamo chake wachisonyeza ku mitundu ya anthu.+
3 Iye wakumbukira lonjezo lake losonyeza kukoma mtima kosatha ndi kukhulupirika kwake ku nyumba ya Isiraeli.+
Malekezero onse a dziko lapansi aona chipulumutso cha Mulungu wathu.+
4 Fuulirani Yehova mosangalala chifukwa wapambana, inu nonse anthu a padziko lapansi.+
Kondwerani, fuulani mosangalala ndi kuimba nyimbo zomutamanda.+
5 Imbirani Yehova nyimbo zomutamanda ndi zeze,+
Muimbireni nyimbo ndi zeze ndi kumutamanda ndi nyimbo zokoma.+
6 Fuulani mwa kuimba malipenga ndi mphalasa.*+
Fuulani mosangalala pamaso pa Mfumu Yehova, chifukwa wapambana.
7 Nyanja ndi zonse zili mmenemo zichite mkokomo,+
Chimodzimodzinso mtunda ndi zonse zokhala kumeneko.+
8 Mitsinje iwombe m’manja,
Mapiri onse afuule pamodzi mokondwera pamaso pa Yehova.+
9 Pakuti iye wabwera kudzaweruza dziko lapansi.+
Adzaweruza dziko mwachilungamo,+
Ndipo adzaweruza mitundu ya anthu molungama.+
2 Yehova wasonyeza mu Ziyoni kuti ndi wamkulu,+
Ndipo ndi wokwezeka pamwamba pa mitundu yonse ya anthu.+
4 Iye amakonda chilungamo ngati mmene mfumu yamphamvu imachitira.+
Inu mwakhazikitsa kulungama.+
Mwakhazikitsa chiweruzo ndi chilungamo pakati pa ana a Yakobo.+
6 Mose ndi Aroni anali pakati pa ansembe ake,+
Samueli anali pakati pa anthu amene anali kuitana pa dzina lake.+
Iwo anali kuitana Yehova, ndipo iye anali kuwayankha.+
7 Mulungu anapitiriza kulankhula nawo mumtambo woima njo ngati chipilala.+
Iwo anasunga zikumbutso zake ndi malangizo amene anawapatsa.+
8 Inu Yehova Mulungu wathu munawayankha.+
Kwa iwo munasonyeza kuti ndinu Mulungu wokhululuka,+
Ndiponso wopereka chilango chifukwa cha zochita zawo zoipa.+
9 Kwezani Yehova Mulungu wathu,+
Ndipo weramani paphiri lake loyera.+
Pakuti Yehova Mulungu wathu ndi woyera.+
Nyimbo yoyamikira.+
100 Fuulirani Yehova mosangalala inu nonse anthu a padziko lapansi chifukwa wapambana.+
3 Dziwani kuti Yehova ndi Mulungu.+
Iye ndi amene anatipanga, sitinadzipange tokha.+
Ndife anthu ake ndi nkhosa zimene akuweta.+
4 Lowani pazipata zake ndi mawu oyamikira,+
Lowani m’mabwalo ake ndi mawu otamanda.+
Muyamikeni, tamandani dzina lake.+
Kukoma mtima kwake kosatha kudzakhalapo mpaka kalekale,+
Ndipo kukhulupirika kwake kudzakhalapo ku mibadwomibadwo.+
Nyimbo ndi Salimo la Davide.
101 Ndidzaimba za kukoma mtima kwanu kosatha ndi chiweruzo chanu.+
Inu Yehova, ndidzakuimbirani nyimbo zokutamandani.+
2 Ndidzachita zinthu mwanzeru m’njira yowongoka.+
Kodi inu mudzandithandiza liti?+
Ndidzayendayenda m’nyumba yanga ndi mtima wanga wosagawanika.+
3 Sindidzaika maso anga pa chinthu chilichonse chopanda pake.+
Ndimadana ndi zochita za opatuka pa choonadi.+
Sindilola kuti zochita zawozo zindikhudze.+
5 Aliyense wonenera mnzake miseche,+
Ndimamukhalitsa chete.+
Sindingathe kupirira zochita za+
Aliyense wodzikweza ndi wamtima wonyada.+
6 Maso anga ali pa okhulupirika a padziko lapansi,+
Kuti akhale ndi ine.+
Woyenda m’njira yowongoka,+
Ndi amene adzanditumikira.+
7 M’nyumba yanga simudzakhala wochita chinyengo.+
Ndipo aliyense wolankhula zachinyengo sadzapitiriza kukhala+
Pamaso panga.+
8 M’mawa uliwonse ndidzawononga oipa onse a padziko lapansi.+
Ndidzapha ndi kuchotsa mumzinda wa Yehova anthu onse ochita zinthu zopweteka anzawo.+
Pemphero la munthu wosautsika pamene walefuka ndipo akutula nkhawa zake kwa Yehova.+
2 Musandibisire nkhope yanu pa tsiku limene ndili m’masautso aakulu.+
Tcherani khutu lanu kwa ine.+
Fulumirani kundiyankha pa tsiku limene ndikuitana.+
3 Pakuti masiku a moyo wanga atha ndi kuzimiririka ngati utsi,+
Ndipo mafupa anga atentha kwambiri ngati ng’anjo.+
8 Tsiku lonse adani anga amanditonza.+
Anthu ondinyoza amagwiritsa ntchito dzina langa potemberera ena.+
9 Pakuti ndadya phulusa ngati chakudya.+
Ndipo zakumwa zanga ndazisakaniza ndi misozi,+
10 Chifukwa cha kudzudzula kwanu kwamphamvu ndi mkwiyo wanu.+
Inu mwandikweza m’mwamba kuti munditaye.+
11 Masiku a moyo wanga ali ngati chithunzithunzi chimene chimazimiririka dzuwa likalowa,+
Ndipo ndauma ngati udzu.+
13 Inu mudzanyamuka ndi kusonyeza Ziyoni chifundo,+
Pakuti imeneyi ndi nyengo yomukomera mtima,
Chifukwa nthawi yoikidwiratu yakwana.+
15 Mitundu ya anthu idzaopa dzina lanu, inu Yehova,+
Ndipo mafumu onse a padziko lapansi adzaopa ulemerero wanu.+
17 Iye adzamvetsera pemphero la anthu amene alandidwa chilichonse,+
Ndipo sadzapeputsa pemphero lawo.+
19 Iye wayang’ana pansi ali kumalo oyera, okwezeka,+
Yehova wayang’ana dziko lapansi ali kumwambako,+
20 Kuti amve kuusa moyo kwa akaidi,+
Ndi kumasula anthu opita kukaphedwa.+
21 Wachita izi kuti dzina la Yehova lilengezedwe m’Ziyoni,+
Ndi kuti atamandidwe mu Yerusalemu,+
22 Pamene mitundu ya anthu idzasonkhanitsidwa pamodzi,+
Komanso maufumu, kuti atumikire Yehova.+
24 Ine ndinati: “Inu Mulungu wanga,
Musadule pakati masiku a moyo wanga.+
Mudzakhalapo ku mibadwomibadwo.+
26 Zimenezi zidzatha, koma inu mudzakhalapobe.+
Ndipo zonsezi zidzatha ngati chovala.+
Mofanana ndi zovala zimene zatha, mudzapezerapo zina ndipo nazonso zidzatha.+
27 Koma inu simudzasintha, ndipo mudzakhalapo kwamuyaya.+
28 Ana a atumiki anu adzapitiriza kukhala motetezeka pamaso panu.+
Ndipo ana awo adzakhazikika pamaso panu.”+
Salimo la Davide.
2 Tamanda Yehova, iwe moyo wanga,
Ndipo usaiwale zochita zake zonse.+
3 Tamanda amene akukukhululukira zolakwa zako zonse,+
Iye amene akukuchiritsa matenda ako onse.+
4 Tamanda amene akuwombola moyo wako kudzenje,+
Amene akukuveka kukoma mtima kosatha ndi chifundo ngati chisoti chachifumu,+
5 Amene akukukhutiritsa pa nthawi ya moyo wako ndi zinthu zabwino.+
Mulungu akukuchititsa kukhalabe wachinyamata ndi wamphamvu ngati chiwombankhanga.+
9 Iye sadzakhalira kutiimba mlandu nthawi zonse chifukwa cha zolakwa zathu,+
Kapena kutisungira mkwiyo mpaka kalekale.+
10 Sanatichitire mogwirizana ndi machimo athu,+
Kapena kutipatsa chilango chogwirizana ndi zolakwa zathu.+
11 Pakuti monga mmene kumwamba kulili pamwamba kwambiri kuposa dziko lapansi,+
Kukoma mtima kwake kosatha nakonso ndi kwapamwamba kwa onse omuopa.+
13 Monga mmene bambo amasonyezera chifundo kwa ana ake,+
Yehova wasonyezanso chifundo kwa onse omuopa.+
15 Masiku a moyo wa munthu ali ngati masiku a udzu wobiriwira.+
Iye amaphuka ngati mmene duwa lakutchire limaphukira.+
17 Koma Yehova adzapitiriza kusonyeza kukoma mtima kwake kosatha mpaka kalekale,+
Kwa anthu amene amamuopa.+
Ndipo adzapitiriza kusonyeza chilungamo chake kwa ana a ana awo.+
18 Adzapitiriza kuchita zimenezi kwa anthu osunga pangano lake,+
Ndi kwa anthu okumbukira malamulo ake ndi kuwatsatira.+
22 Tamandani Yehova inu ntchito zake zonse,+
M’malo onse amene iye akulamulira.+
Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.+
104 Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.+
Inu Yehova Mulungu wanga, mwasonyeza kuti ndinu wamkulu koposa.+
Mwadziveka ulemu ndi ulemerero.+
2 Mwadzifunditsa kuwala ngati chofunda,+
Mwatambasula kumwamba ngati nsalu ya chihema.+
3 Inu munamanga zipinda za m’mwamba pamadzi pogwiritsa ntchito mitanda,+
Munapanga mitambo kukhala galeta lanu,+
Mumayenda pamapiko a mphepo.+
4 Inu mumapanga angelo anu kukhala mizimu,+
Ndipo atumiki anu kukhala moto wonyeketsa.+
7 Chifukwa cha kudzudzula kwanu, madziwo anayamba kuthawa.+
Atamva mabingu anu anayamba kuthamanga mopanikizika kwambiri,
8 Kupita kumalo amene munawakonzera.
Mapiri anakwera,+
Zigwa zinatsika.
11 Akasupewo amapereka madzi kwa zilombo zonse zakutchire.+
Nthawi zonse mbidzi+ zimapha ludzu lawo mmenemo.
12 Zolengedwa zouluka m’mlengalenga zimamanga zisa zawo pafupi ndi akasupewo,+
Ndipo zimalira m’mitengo ya masamba ambiri obiriwira.+
13 Mulungu amathirira mapiri kuchokera m’zipinda zake za m’mwamba.+
Dziko lapansi ladzaza ndi zipatso za ntchito yake.+
14 Amameretsa msipu kuti nyama zidye,+
Ndipo amameretsa mbewu kuti anthu agwiritse ntchito.+
Amachita zimenezi kuti chakudya chituluke m’nthaka,+
15 Komanso kuti mutuluke vinyo amene amasangalatsa mtima wa munthu.+
Amachita zonsezi kuti nkhope ya munthu isalale ndi mafuta,+
Komanso kuti apereke chakudya chimene chimakhutiritsa mtima wa munthu.+
16 Mitengo ya Yehova imathiriridwa bwino,
Mikungudza ya ku Lebanoni imene iye anabzala.+
17 Mbalame zimamanga zisa zawo mmenemo.+
Dokowe nyumba yake ndiyo mitengo ya mlombwa.+
19 Wapanga mwezi kuti uzisonyeza nthawi yoikidwiratu.+
Dzuwa nalo limadziwa bwino kumene limalowera.+
24 Ntchito zanu ndi zochuluka, inu Yehova!+
Zonsezo munazipanga mwanzeru zanu.+
Dziko lapansi ladzaza ndi zinthu zimene munapanga.+
25 M’nyanja yakuya iyi ndiponso yotambalala,+
Muli zinthu zoyenda zosawerengeka,+
Muli zamoyo zazikulu ndi zazing’ono zomwe.+
29 Mukaphimba nkhope yanu, zimasokonezeka.+
Mukachotsa mzimu wawo, zimafa,+
Ndipo zimabwerera kufumbi.+
33 Ndidzaimbira Yehova moyo wanga wonse.+
Ndidzaimba nyimbo zotamanda Mulungu wanga nthawi yonse ya moyo wanga.+
5 Kumbukirani ntchito zodabwitsa zimene wachita,+
Kumbukirani zozizwitsa zake ndi zigamulo zotuluka m’kamwa mwake,+
6 Inu mbewu ya Abulahamu mtumiki wake,+
Inu ana a Yakobo, osankhidwa mwapadera.+
8 Wakumbukira pangano lake mpaka kalekale,+
Wakumbukira lonjezo limene anapereka ku mibadwo 1,000,+
9 Wakumbukira pangano limene anapangana ndi Abulahamu,+
Ndi lonjezo limene analumbira kwa Isaki,+
10 Lonjezo limeneli analikhazikitsa monga lamulo kwa Yakobo,
Monga pangano lokhalapo mpaka kalekale kwa Isiraeli,+
11 Pamene anati: “Ndidzakupatsa dziko la Kanani+
Kuti likhale gawo la cholowa chako.”+
12 Pamene ananena zimenezi, n’kuti iwo ali ochepa.+
N’kuti ali ochepa kwambiri komanso ali alendo m’dzikolo.+
13 Iwo anapitiriza kuyendayenda pakati pa mitundu yosiyanasiyana,+
Anali kuchoka mu ufumu wina ndi kupita kukakhala ndi anthu a mtundu wina.+
14 Mulungu sanalole kuti munthu aliyense awachitire zachinyengo,+
Koma anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo.+
15 Iye anati: “Anthu inu musakhudze odzozedwa anga,+
Ndipo aneneri anga musawachitire choipa chilichonse.”+
16 Iye anadzetsa njala yaikulu m’dzikomo,+
Ndipo anathyola ndodo zonse zopachikapo mkate wozungulira woboola pakati.+
17 Mulungu anatsogoza munthu kuti anthu akewo abwere pambuyo pake,
Anatumiza Yosefe amene anagulitsidwa kuti akhale kapolo.+
18 Kumeneko anasautsa mapazi ake ndi matangadza,+
Anam’manga ndi maunyolo.+
Kufikira pamene lonjezo la Mulungu linakwaniritsidwa.+
20 Mfumu inalamula kuti amutulutse m’ndende.+
Wolamulira mitundu ya anthu analamula kuti Yosefe amasulidwe.
21 Anamuika kukhala mkulu woyang’anira banja lake,+
Komanso wolamulira chuma chake chonse.+
22 Anamupatsa ulamuliro womanga kalonga aliyense wa mfumu,+
Komanso kuphunzitsa zinthu za nzeru anthu achikulire.+
24 Mulungu anachititsa anthu ake kuberekana,+
Ndipo pang’onopang’ono anawasandutsa anthu amphamvu kuposa adani awo.+
25 Analola adaniwo kusintha mitima yawo ndi kudana ndi anthu ake,+
Anawalola kuchitira atumiki ake zachinyengo.+
31 Analamula kuti pagwe tizilombo touluka toyamwa magazi,+
Komanso ntchentche zoluma m’madera awo onse.+
36 Mulungu anapha mwana aliyense woyamba kubadwa m’dziko lawo,+
Chiyambi cha mphamvu zawo zonse zobereka.+
37 Ndiyeno anayamba kuwatulutsa atatenga siliva ndi golide.+
Pakati pa mafuko ake panalibe amene anapunthwa panjira.
41 Anatsegula thanthwe ndipo panatuluka madzi ambiri.+
Madziwo anayenda ngati mtsinje kudutsa m’dera lopanda madzi.+
42 Iye anakumbukira lonjezo lake loyera limene analonjeza mtumiki wake Abulahamu.+
43 Choncho Mulungu anatulutsa anthu ake m’dzikomo anthuwo akusangalala,+
Anatulutsa osankhidwa ake akufuula mokondwera.+
44 Pang’onopang’ono anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina,+
Ndipo zipatso za ntchito imene mitundu ya anthu inagwira mwakhama, anazitenga kukhala zawo,+
45 Anachita zimenezi kuti asunge malangizo ake,+
Ndi kusunga malamulo ake.+
Tamandani Ya, anthu inu!+
Yamikani Yehova, chifukwa iye ndi wabwino.+
Pakuti kukoma mtima kwake kosatha kudzakhalapobe mpaka kalekale.+
4 Ndikumbukireni inu Yehova, ndipo ndisonyezeni kukoma mtima kumene mumasonyeza anthu anu.+
Ndisamalireni ndi kundipulumutsa,+
5 Kuti ndione ubwino umene mumapereka kwa osankhidwa anu,+
Kuti ndikondwere pamene mtundu wanu ukukondwera,+
Ndiponso kuti ndinyadire pamodzi ndi cholowa chanu.+
7 Makolo athu ku Iguputo,
Sanasonyeze kuzindikira kulikonse ntchito zanu zodabwitsa.+
Sanakumbukire kuchuluka kwa kukoma mtima kwanu kosatha,+
Koma anapanduka panyanja, pafupi ndi Nyanja Yofiira.+
9 Choncho anadzudzula Nyanja Yofiira, ndipo pang’onopang’ono nyanjayo inauma.+
Pamenepo anawayendetsa kudutsa pakati pa madzi akuya ngati akuwayendetsa m’chipululu.+
10 Chotero anawapulumutsa m’manja mwa wodana nawo,+
Ndipo anawawombola m’manja mwa mdani.+
15 Mulungu anawapatsa zimene anali kupempha,+
Ndipo anawagwetsera matenda a kaliwondewonde pakati pawo.+
19 Iwo anapanganso mwana wa ng’ombe ku Horebe,+
Ndipo anaweramira chifaniziro chopangidwa ndi chitsulo chosungunula.+
20 Choncho anasinthanitsa ulemerero wanga+
Ndi chifaniziro cha ng’ombe yamphongo yodya udzu.+
21 Iwo anaiwala Mulungu, Mpulumutsi wawo,+
Amene anachita zinthu zazikulu ku Iguputo,+
22 Amene anachita zodabwitsa m’dziko la Hamu,+
Amene anachita zochititsa mantha pa Nyanja Yofiira.+
23 Iye anangotsala pang’ono kulamula kuti awawononge,+
Koma Mose wosankhidwa wake,
Anaima pamalo ogumuka pamaso pa Mulungu,+
Ndi kubweza mkwiyo wake kuti usawawononge.+
26 Choncho Mulungu anawalumbirira atakweza dzanja lake,+
Kuti adzawapha m’chipululu,+
27 Ndiponso kuti adzachititsa ana awo kuphedwa ndi mitundu ina,+
Ndi kuti adzawamwaza m’mayiko osiyanasiyana.+
32 Kuwonjezera pamenepo, iwo anaputa mkwiyo pa madzi a ku Meriba,+
Moti Mose sizinamuyendere bwino chifukwa cha anthu amenewa.+
38 Choncho anali kukhetsa magazi a anthu osalakwa,+
Magazi a ana awo aamuna ndi a ana awo aakazi,
Amene anawapereka nsembe kwa mafano a ku Kanani.+
Ndipo dzikolo linaipa ndi magazi amene iwo anakhetsa.+
41 Mobwerezabwereza anali kuwapereka m’manja mwa anthu a mitundu ina,+
Kuti anthu odana nawo awalamulire,+
42 Ndi kuti adani awowo awapondereze,
Komanso kuti awagonjetse.+
43 Nthawi zambiri anali kuwalanditsa,+
Koma iwo anali kumupandukira chifukwa sanali kumumvera,+
Ndipo anali kuwatsitsa chifukwa cha zolakwa zawo.+
45 Zikatero anali kukumbukira pangano limene anachita ndi iwo,+
Ndipo anali kuwamvera chisoni chifukwa cha kuchuluka kwa kukoma mtima kwake kosatha.+
47 Tipulumutseni inu Yehova Mulungu wathu,+
Tisonkhanitseni pamodzi kuchokera m’mitundu ina,+
Kuti titamande dzina lanu loyera,+
Ndi kuti tilankhule mokondwa pokutamandani.+
48 Adalitsike Yehova Mulungu wa Isiraeli,+
Kuyambira kalekale mpaka kalekale.
Ndipo anthu onse anene kuti, Ame.*+
Tamandani Ya, anthu inu!+
BUKU LACHISANU
(Masalimo 107 – 150)
107 Yamikani Yehova anthu inu, pakuti iye ndi wabwino.+
Kukoma mtima kwake kosatha kudzakhalapobe mpaka kalekale.+
2 Anthu owomboledwa a Yehova anene zimenezi,+
Anthu amene iye wawawombola m’manja mwa mdani,+
3 Anthu amene anawasonkhanitsa pamodzi kuchokera m’mayiko osiyanasiyana,+
Kuchokera kotulukira dzuwa kukafika kolowera dzuwa,+
Kuchokera kumpoto kukafika kum’mwera.+
4 Iwo anayendayenda m’chipululu+ mopanda kanthu.+
Sanapeze njira iliyonse yopita kumzinda woti azikhalamo.+
6 Iwo anapitiriza kufuulira Yehova m’masautso awo,+
Ndipo anawalanditsa ku mavuto awo.+
7 Anawayendetsa m’njira yabwino,+
Kuti akafike kumzinda woti azikhalamo.+
8 Anthu ayamike Yehova chifukwa cha kukoma mtima kwake kosatha,+
Ndiponso chifukwa cha ntchito zake zodabwitsa zimene wachitira ana a anthu.+
10 Ena anali kukhala mu mdima, mu mdima wandiweyani,+
Anali akaidi osautsika ndi omangidwa maunyolo,+
11 Chifukwa anachita zinthu mopandukira+ mawu a Mulungu,+
Ndipo ananyoza malangizo a Wam’mwambamwamba.+
12 Choncho mwa kuwadzetsera mavuto, Mulungu anagonjetsa mitima yawo.+
Iwo anapunthwa ndipo panalibe wowathandiza.+
13 Iwo anayamba kuitana Yehova kuti awathandize m’masautso awo,+
Ndipo iye anawapulumutsa ku mavuto awo monga mwa nthawi zonse.+
15 Anthu ayamike Yehova chifukwa cha kukoma mtima kwake kosatha,+
Ndiponso chifukwa cha ntchito zake zodabwitsa zimene wachitira ana a anthu.+
17 Anthu amene anali opusa chifukwa cha njira yawo yophwanya malamulo,+
Komanso chifukwa cha zolakwa zawo, pamapeto pake anadzibweretsera masautso.+
19 Iwo anayamba kuitana Yehova kuti awathandize m’masautso awo.+
Ndipo iye anawapulumutsa ku mavuto awo monga mwa nthawi zonse.+
21 Anthu ayamike Yehova chifukwa cha kukoma mtima kwake kosatha,+
Ndiponso chifukwa cha ntchito zake zodabwitsa zimene wachitira ana a anthu.+
23 Anthu amene amayenda m’zombo panyanja,+
Amene amachita malonda pamadzi ambiri,+
24 Amenewa ndi amene aona ntchito za Yehova,+
Ndiponso ntchito zake zodabwitsa m’madzi akuya.+
25 Aona mmene amautsira mphepo yamkuntho mwa kungonena mawu,+
Moti nyanjayo imachita mafunde.+
27 Amadzandira ndipo amayenda peyupeyu ngati munthu woledzera,+
Ndipo ngakhale nzeru zawo zonse zimasokonezeka.+
30 Iwo amasangalala chifukwa mafundewo atha,
Ndipo Mulungu amawatsogolera kudoko limene iwo akufuna.+
31 Anthu ayamike Yehova chifukwa cha kukoma mtima kwake kosatha,+
Ndiponso chifukwa cha ntchito zake zodabwitsa zimene wachitira ana a anthu.+
33 Amasandutsa mitsinje kukhala chipululu,+
Ndiponso akasupe a madzi kukhala malo opanda madzi.+
34 Nthaka yobala zipatso amaisandutsa dziko lamchere,+
Chifukwa cha kuipa kwa anthu okhala mmenemo.
35 Amasandutsa chipululu kukhala dambo la madzi,+
Ndipo dziko lopanda madzi amalisintha kukhala dera la akasupe amadzi.+
40 Mulungu akutsanulira mnyozo pa anthu olemekezeka,+
Moti iye akuwachititsa kuyendayenda m’chipululu, mmene mulibe njira.+
41 Koma akuteteza munthu wosauka ku nsautso,+
Ndipo akumuchulukitsa kukhala mabanja ambiri ngati gulu la nkhosa.+
43 Wanzeru ndani? Iye aona zimenezi,+
Ndi kuchita chidwi ndi ntchito za Yehova zosonyeza kukoma mtima kwake kosatha.+
Nyimbo ndi Salimo la Davide.
108 Mtima wanga wakhazikika, Inu Mulungu,+
Ndidzaimba nyimbo zokutamandani,+
Mtima wanga udzachitanso chimodzimodzi.+
3 Ndidzakutamandani pakati pa mitundu ya anthu, inu Yehova.+
Ndidzaimba nyimbo zokutamandani pakati pa mitundu ya anthu.+
4 Pakuti kukoma mtima kwanu kosatha n’kwakukulu ndipo kwafika kumwamba,+
Choonadi chanu chafika kuthambo.+
5 Inu Mulungu, kwezekani kupitirira kumwamba.+
Ulemerero wanu ukhale pamwamba pa dziko lonse lapansi.+
7 Pokhala woyera, Mulungu walankhula kuti:+
“Ndidzakondwa ndi kupereka Sekemu+ ngati gawo la cholowa.+
Ndipo ndidzayezera anthu anga chigwa cha Sukoti.+
8 Giliyadi+ ndi wanga ndipo Manase+ ndi wanganso.
Efuraimu ndi malo otetezeka a mtsogoleri amene ine ndamuika.+
Yuda ndi ndodo yanga ya mtsogoleri wa asilikali.+
10 Ndani adzandibweretsa kumzinda wokhala ndi mpanda wolimba kwambiri?+
Ndani adzanditsogolera mpaka kukafika ku Edomu?+
11 Ndinu Mulungu amene mungatichititse kupambana! Koma onani tsopano mwatitaya,+
Ndipo inu Mulungu wathu, simukupita kunkhondo pamodzi ndi magulu athu ankhondo.+
12 Tithandizeni kuti tichoke m’masautso,+
Pakuti chipulumutso chochokera kwa munthu wochokera kufumbi n’chopanda pake.+
Kwa wotsogolera nyimbo. Nyimbo ndi Salimo la Davide.
109 Inu Mulungu amene ndimakutamandani,+ musakhale chete.+
2 Munthu woipa ndiponso munthu wachinyengo andinenera zoipa ndi pakamwa pawo.+
Iwo anena za ine ndi lilime lonama.+
3 Andizungulira ndi mawu achidani,+
Ndipo akulimbana nane popanda chifukwa.+
10 Ana ake azingoyendayenda ndithu,+
Ndipo azipemphapempha.
Azichoka m’mabwinja mmene akukhala, n’kupita kukafunafuna chakudya.+
11 Wopereka ngongole yakatapira* atchere msampha pa zonse zimene ali nazo,+
Ndipo anthu achilendo+ afunkhe zinthu zimene wakhetsera thukuta.+
15 Tchimo ndi cholakwacho zikhale pamaso pa Yehova nthawi zonse,+
Ndipo achotse dzina lawo padziko lapansi kuti lisakumbukiridwenso,+
16 Chifukwa chakuti sanakumbukire kusonyeza kukoma mtima kosatha,+
M’malomwake anapitiriza kuthamangitsa wosautsika ndi wosauka,+
Komanso munthu wa mtima wachisoni kuti amuphe.+
17 Iye anakonda kutemberera ena,+ mwakuti matemberero anabwera kwa iye.+
Koma kudalitsa ena sikunali kumusangalatsa,+
Moti madalitso anali patali ndi iye,+
18 Iye anali kuvala matemberero ngati chovala.+
Matembererowo analowa mwa iye ngati madzi,+
Ndiponso analowa m’mafupa ake ngati mafuta.
19 Kwa iye matembererowo akhale ngati chovala chimene amadziphimba nacho,+
Komanso ngati lamba amene amamanga m’chiuno mwake nthawi zonse.+
20 Amenewa ndi malipiro a Yehova kwa aliyense amene amalimbana nane,+
Ndi kwa amene amakamba zondichitira zinthu zoipa.+
21 Koma inu ndinu Yehova Ambuye Wamkulu Koposa.+
Ndikomereni mtima chifukwa cha dzina lanu.+
Ndilanditseni,+ popeza kukoma mtima kwanu kosatha ndi kwakukulu.
23 Ine ndiyenera kuchoka mofanana ndi chithunzithunzi chimene chimazimiririka dzuwa likalowa.+
Ndakutumulidwa ngati dzombe.
Koma inu mundipatse madalitso.+
Iwo aimirira kuti andiukire koma inu muwachititse manyazi,+
Ndipo ine mtumiki wanu ndisangalale.+
29 Amene akulimbana ndi ine avale manyazi,+
Ndipo adziphimbe ndi manyaziwo ngati akudziphimba ndi malaya akunja odula manja.+
31 Pakuti adzaima kudzanja lamanja la munthu wosauka,+
Kuti am’pulumutse kwa omuweruza mopanda chilungamo.
Salimo la Davide.
110 Yehova wauza Ambuye wanga kuti:+
“Khala kudzanja langa lamanja+
Kufikira nditaika adani ako monga chopondapo mapazi ako.”+
2 Yehova adzatambasula ndodo+ yako yachifumu yamphamvu kuchokera m’Ziyoni+ ndi kunena kuti:
“Pita ukagonjetse anthu pakati pa adani ako.”+
3 Anthu ako+ adzadzipereka mofunitsitsa+ pa tsiku limene udzatsogolera asilikali ako kunkhondo.+
Wadzikongoletsa ndi ulemerero,+
Ndipo gulu la achinyamata amene ali ngati mame a m’bandakucha lili pamodzi ndi iwe.+
4 Yehova walumbira+ (ndipo sadzasintha maganizo). Iye wati:+
“Iwe ndiwe wansembe mpaka kalekale,+
Monga mwa unsembe wa Melekizedeki!”+
6 Adzapereka chiweruzo pakati pa anthu a mitundu ina.+
Adzachititsa mitembo ya anthu kupezeka paliponse.+
Adzaphwanyaphwanya mtsogoleri wa dziko la anthu ambiri.+
ג [Giʹmel]
ה [Heʼ]
ז [Zaʹyin]
4 Iye wakonza zoti ntchito zake zodabwitsa zizikumbukiridwa.+
ח [Chehth]
Yehova ndi wachisomo ndiponso wachifundo.+
ט [Tehth]
5 Wapereka chakudya kwa anthu omuopa.+
י [Yohdh]
Iye adzakumbukira pangano lake nthawi zonse.+
כ [Kaph]
6 Wafotokozera anthu ake mphamvu za ntchito zake,+
ל [Laʹmedh]
Mwa kuwapatsa cholowa cha mitundu ina ya anthu.+
מ [Mem]
7 Ntchito za manja ake zimadziwika ndi choonadi ndiponso chiweruzo.+
נ [Nun]
Malamulo onse amene amapereka ndi odalirika.+
ס [Saʹmekh]
8 Ndi ochirikizika bwino mpaka muyaya, ndithu mpaka kalekale,+
ע [ʽAʹyin]
Ndipo amawapereka m’choonadi ndiponso molungama.+
פ [Peʼ]
צ [Tsa·dhehʹ]
Wakhazikitsa pangano lake mpaka kalekale.+
ק [Qohph]
Dzina lake ndi loyera ndi lochititsa mantha.+
ר [Rehsh]
10 Chiyambi cha nzeru ndicho kuopa Yehova.+
ש [Sin]
Onse otsatira malamulo a Mulungu ndi ozindikira.+
ת [Taw]
Iye ayenera kutamandidwa mpaka muyaya.+
ג [Giʹmel]
2 Ana ake adzakhala amphamvu padziko lapansi.+
ד [Daʹleth]
Ndipo m’badwo wa anthu olungama udzadalitsidwa.+
ה [Heʼ]
3 Zinthu zamtengo wapatali ndiponso chuma zili m’nyumba yake,+
ו [Waw]
Ndipo chilungamo chake chidzakhalapo kwamuyaya.+
ז [Zaʹyin]
4 Waunika mu mdima kuti anthu owongoka mtima aone kuwala.+
ח [Chehth]
Iye ndi wachisomo, wachifundo ndi wolungama.+
ט [Tehth]
5 Munthu wachisomo+ komanso wokongoza ena zinthu ndi wabwino.+
י [Yohdh]
Amachita zinthu mwachilungamo.+
כ [Kaph]
6 Ndithudi munthu wotero sadzagwedezeka ngakhale pang’ono.+
ל [Laʹmedh]
Wolungama adzakumbukiridwa mpaka kalekale.+
מ [Mem]
ס [Saʹmekh]
8 Mtima wake sungagwedezeke,+ ndipo sadzachita mantha,+
ע [ʽAʹyin]
Pamapeto pake adzayang’ana adani ake atagonjetsedwa.+
פ [Peʼ]
9 Iye wagawira ena mowolowa manja, wapereka kwa anthu aumphawi.+
צ [Tsa·dhehʹ]
Chilungamo chake chidzakhalapo kwamuyaya.+
ר [Rehsh]
10 Woipa adzaona zimenezi ndipo adzasautsika.+
ש [Shin]
Adzakukuta mano ndi kusungunuka.+
ת [Taw]
Chikhumbo cha anthu oipa chidzatha.+
6 Iye amatsika m’munsi kuti aone kumwamba ndi dziko lapansi.+
7 Amadzutsa munthu wonyozeka kumuchotsa m’fumbi.+
Amakweza munthu wosauka kumuchotsa padzala,+
8 Kuti amukhazike pamodzi ndi anthu olemekezeka,+
Pamodzi ndi anthu olemekezeka pakati pa anthu a Mulungu.+
9 Akuchititsa mkazi wosabereka kukhala m’nyumba+
Monga mayi wosangalala wa ana aamuna.+
Tamandani Ya, anthu inu!+
114 Pamene Isiraeli anatuluka mu Iguputo,+
Pamene nyumba ya Yakobo inatuluka pakati pa anthu olankhula zosamveka,+
2 Yuda anakhala malo ake oyera,+
Ndipo Isiraeli anakhala ufumu wake waukulu.+
5 Kodi chinavuta n’chiyani nyanja iwe kuti uthawe?+
Kodi iwe Yorodano chinavuta n’chiyani kuti ubwerere m’mbuyo?+
6 Nanga inu mapiri, chinavuta n’chiyani kuti mudumphedumphe ngati nkhosa zamphongo?+
Inunso zitunda, chinavuta n’chiyani kuti mudumphedumphe ngati ana a nkhosa?+
7 Chifukwa cha Ambuye, chita mantha aakulu dziko lapansi iwe,+
Chita mantha aakulu chifukwa cha Mulungu wa Yakobo,
8 Amene amasintha thanthwe kukhala dambo la madzi,+
Ndiponso amasintha mwala wa nsangalabwi kukhala kasupe.+
115 Ife sitikuyenerera kalikonse, inu Yehova, ife sitikuyenerera kalikonse,+
Koma dzina lanu ndi loyenera kulemekezedwa+
Malinga ndi kukoma mtima kwanu kosatha, malinganso ndi choonadi chanu.+
5 Pakamwa ali napo koma salankhula,+
Maso ali nawo koma saona.+
6 Makutu ali nawo koma satha kumva.+
Mphuno ali nayo koma sanunkhiza.+
7 Manja ali nawo, koma sakhudza kanthu.+
Mapazi ali nawo koma sayenda.+
Satulutsa mawu ndi mmero wawo.+
12 Yehova watikumbukira, ndipo adzapereka madalitso,+
Adzadalitsa nyumba ya Isiraeli,+
Adzadalitsa nyumba ya Aroni.+
3 Zingwe za imfa zinandizungulira+
Ndipo ndinasautsika ngati kuti ndili m’Manda.+
Ndinapitiriza kusautsika ndi kukhala wachisoni,+
8 Pakuti inu mwapulumutsa moyo wanga ku imfa,+
Mwateteza maso anga kuti asakhetse misozi ndiponso phazi langa kuti lisapunthwe.+
9 Ndidzayenda+ pamaso pa Yehova m’dziko la anthu amoyo.+
Inetu ndine mtumiki wanu.+
Ndine mtumiki wanu, mwana wa kapolo wanu wamkazi.+
Mwamasula zingwe zimene anandimanga nazo.+
18 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova,+
Ndidzawakwaniritsa pamaso pa anthu ake onse,+
19 M’mabwalo a nyumba ya Yehova,+
Pakati pa iwe Yerusalemu.+
Tamandani Ya, anthu inu!+
2 Pakuti kukoma mtima kosatha kumene watisonyeza ndi kwakukulu.+
Ndipo choonadi+ cha Yehova chidzakhalapobe mpaka kalekale.
Tamandani Ya, anthu inu!+
118 Yamikani Yehova anthu inu, pakuti iye ndi wabwino.+
Kukoma mtima kwake kosatha kudzakhalapobe mpaka kalekale.+
7 Yehova ali kumbali yanga pamodzi ndi anthu amene akundithandiza,+
Ndipo ine ndidzayang’ana anthu odana nane atagonja.+
11 Mitunduyo inandizungulira, ndithu inandizungulira kumbali zonse.+
Koma ndinali kuikankhira kutali m’dzina la Yehova.
12 Inandizungulira ngati njuchi,+
Koma inazima ngati moto wa zitsamba zaminga.+
Ndinali kuikankhira kutali m’dzina la Yehova.+
Mumamveka mfuu yachisangalalo ndipo muli chipulumutso.+
Dzanja lamanja la Yehova limachita zamphamvu.+
25 Haa! Inu Yehova, chonde tipulumutseni.+
Haa! Inu Yehova, chonde tithandizeni kuti zinthu zitiyendere bwino.+
Ndipo amatipatsa kuwala.+
Kongoletsani gulu la anthu amene ali pachikondwerero+ ndi nthambi za mitengo,+ anthu inu.
Likongoletseni mpaka kukafika panyanga za guwa lansembe.+
29 Yamikani Yehova anthu inu, pakuti iye ndi wabwino.+
Kukoma mtima kwake kosatha kudzakhalapobe mpaka kalekale.+
א [ʼAʹleph]
ב [Behth]
9 Kodi wachinyamata+ angakhale bwanji woyera pa moyo wake?
Mwa kudziyang’anira ndi kuchita zinthu mogwirizana ndi mawu anu.+
10 Ndayesetsa kukufunafunani ndi mtima wanga wonse.+
Musandichititse kusochera ndi kuchoka pa malamulo anu.+
14 Ndimakondwera kuyenda m’njira ya zikumbutso zanu,+
Ngati mmene anthu amachitira akapeza chuma chilichonse chamtengo wapatali.+
ג [Giʹmel]
23 Akalonga asonkhana pamodzi kuti akambirane zondiukira.+
Koma ine mtumiki wanu, ndimasinkhasinkha malangizo anu.+
ד [Daʹleth]
27 Ndithandizeni kumvetsa njira zofotokozedwa m’malamulo anu,+
Kuti ndisinkhesinkhe ntchito zanu zodabwitsa.+
ה [Heʼ]
33 Ndilangizeni inu Yehova, kuti ndiyende motsatira malangizo anu,+
Kuti nditsatire malangizo anu moyo wanga wonse.+
34 Ndithandizeni kukhala wozindikira kuti nditsatire chilamulo chanu,+
Ndiponso kuti ndichisunge ndi mtima wonse.+
37 Chititsani maso anga kuti asaone zinthu zopanda pake.+
Ndiyendetseni m’njira yanu kuti ndikhalebe wamoyo.+
ו [Waw]
41 Monga mwa mawu anu, inu Yehova, ndipatseni chipulumutso chanu.+
Ndipatseni zochita zanu zosonyeza kukoma mtima kosatha,+
42 Kuti ndipeze choyankha kwa wonditonza,+
Pakuti ine ndakhulupirira mawu anu.+
48 Ndidzapemphera kwa inu nditakweza manja anga chifukwa ndimakonda malamulo anu,+
Ndipo ndidzasinkhasinkha malangizo anu.+
ז [Zaʹyin]
49 Kumbukirani mawu amene munandiuza ine mtumiki wanu,+
Mawu amene ndikuwayembekezera malinga ndi lonjezo lanu.+
54 Kwa ine, malangizo anu akhala ngati nyimbo zokutamandani,+
M’nyumba zimene ndimakhala m’mayiko achilendo.+
ח [Chehth]
64 Inu Yehova, kukoma mtima kwanu kosatha kwadzaza dziko lonse lapansi.+
Ndiphunzitseni malamulo anu.+
ט [Tehth]
66 Ndiphunzitseni kuchita zabwino,+ kulingalira bwino+ ndi kudziwa zinthu,+
Pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.+
69 Anthu odzikuza andinenera mabodza ambiri,+
Koma ine ndidzasunga malamulo anu ndi mtima wanga wonse.+
72 Chilamulo+ chotuluka pakamwa panu n’chabwino kwa ine,+
N’chabwino kwambiri kuposa ndalama masauzande zagolide ndi zasiliva.+
י [Yohdh]
73 Manja anu anandipanga, ndipo anandiumba.+
Ndithandizeni kukhala wozindikira, kuti ndiphunzire malamulo anu.+
75 Inu Yehova, ndikudziwa bwino kuti zigamulo zanu ndi zolungama,+
Ndiponso kuti mwandilanga chifukwa chakuti ndinu wokhulupirika.+
78 Odzikuza achite manyazi, chifukwa andisocheretsa popanda chifukwa,+
Koma ine ndimasinkhasinkha malamulo anu.+
כ [Kaph]
82 Maso anga alefuka chifukwa cholakalaka mawu anu,+
Ndipo ndikunena kuti: “Kodi mudzandilimbikitsa liti?”+
85 Anthu amene sachita zinthu mogwirizana ndi chilamulo chanu,+
Anthu odzikuza akumba mbuna kuti andigwire.+
88 Ndisungeni wamoyo monga mwa kukoma mtima kwanu kosatha,+
Kuti ndisunge zikumbutso zotuluka pakamwa panu.+
ל [Laʹmedh]
90 Kukhulupirika kwanu kudzakhalapobe ku mibadwomibadwo.+
Mwakhazikitsa mwamphamvu dziko lapansi, kuti lisagwedezeke.+
91 Chilengedwe chonse chakhalapobe kufikira lero chifukwa cha zigamulo zanu,+
Pakuti chilengedwe chonse chimakutumikirani.+
93 Sindidzaiwala malamulo anu mpaka kalekale,+
Chifukwa mwandisungabe wamoyo kudzera m’malamulo amenewo.+
96 Ndaona kuti zinthu zonse zabwino kwambiri zili ndi malire.+
Koma malamulo anu amakhudza mbali zonse.
מ [Mem]
98 Malamulo anu amandichititsa kukhala wanzeru kuposa adani anga,+
Chifukwa ndi anga mpaka kalekale.+
99 Ndakhala wozindikira kwambiri kuposa aphunzitsi anga,+
Chifukwa ndimasinkhasinkha zikumbutso zanu.+
104 Chifukwa cha malamulo anu ndimachita zinthu mozindikira.+
N’chifukwa chake ndimadana ndi njira iliyonse yachinyengo.+
נ [Nun]
108 Inu Yehova, chonde kondwerani ndi nsembe zaufulu za pakamwa panga,+
Ndipo ndiphunzitseni zigamulo zanu.+
111 Ndatenga zikumbutso zanu kukhala chuma changa mpaka kalekale,+
Pakuti zimakondweretsa mtima wanga.+
ס [Saʹmekh]
116 Inu Mulungu, ndithandizeni monga mwa mawu anu kuti ndikhalebe ndi moyo,+
Ndipo musandichititse manyazi chifukwa cha chiyembekezo changa.+
118 Onse osochera ndi kuchoka pa malangizo anu mwawataya kutali,+
Pakuti ndi achinyengo komanso onama.+
119 Anthu onse oipa mwawachotsa padziko lapansi ngati zonyansa.*+
N’chifukwa chake ine ndimakonda zikumbutso zanu.+
120 Chifukwa choopa inu, thupi langa linagwidwa nthumanzi,+
Ndipo chifukwa cha zigamulo zanu, ndinachita mantha.+
ע [ʽAʹyin]
121 Ndapereka ziweruzo zolungama ndipo ndachita zinthu mwachilungamo.+
Musandipereke kwa anthu ondichitira chinyengo.+
122 Khalani ngati chikole kwa ine mtumiki wanu kuti mudzandichitira zabwino.+
Anthu odzikuza asandichitire chinyengo.+
124 Ndichitireni zabwino ine mtumiki wanu monga mwa kukoma mtima kwanu kosatha,+
Ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.+
126 Ino ndi nthawi yakuti inu Yehova muchitepo kanthu,+
Chifukwa anthu odzikuzawo aphwanya chilamulo chanu.+
128 Choncho ndaona kuti malamulo anu onse okhudza chilichonse ndi olungama.+
Ndimadana ndi njira iliyonse yachinyengo.+
פ [Peʼ]
130 Kuululidwa kwa mawu anu kumapereka kuwala,+
Kumathandiza anthu osadziwa zambiri kukhala ozindikira.+
131 Ndatsegula kwambiri pakamwa panga kuti ndipume mofulumira,+
Chifukwa ndikulakalaka malamulo anu.+
132 Ndicheukireni ndi kundikomera mtima,+
Mogwirizana ndi zigamulo zimene mumapereka kwa anthu okonda dzina lanu.+
133 Mwapondetsa mwamphamvu mapazi anga pa mawu anu,+
Ndipo musalole kuti choipa chilichonse chindilamulire.+
136 Misozi yatsika m’maso mwanga ngati mitsinje ya madzi,+
Chifukwa chakuti iwo sanasunge chilamulo chanu.+
צ [Tsa·dhehʹ]
138 M’chilungamo chanu ndiponso kukhulupirika kwanu kosaneneka+
Mwatilamula kuti tisunge zikumbutso zanu.+
144 Zikumbutso zanu zidzakhalabe zolungama mpaka kalekale.+
Ndithandizeni kukhala wozindikira kuti ndikhalebe ndi moyo.+
ק [Qohph]
149 Imvani mawu anga mwa kukoma mtima kwanu kosatha.+
Inu Yehova, ndisungenibe wamoyo mogwirizana ndi zigamulo zanu.+
150 Okonda kuchita khalidwe lotayirira+ abwera pafupi ndi ine.
Iwo atalikirana kwambiri ndi chilamulo chanu.+
ר [Rehsh]
159 Onani kuti ndimakonda malamulo anu.+
Inu Yehova, ndisungenibe wamoyo mwa kukoma mtima kwanu kosatha.+
160 Mawu anu onse ndi choonadi chokhachokha,+
Ndipo chigamulo chanu chilichonse cholungama chidzakhalapo mpaka kalekale.+
ש [Sin] kapena kuti [Shin]
ת [Taw]
169 Inu Yehova, imvani kulira kwanga kochonderera.+
Ndithandizeni kuti ndikhale wozindikira, monga mwa mawu anu.+
176 Ndayendayenda ngati nkhosa yosochera.+ Ndifunefuneni ine mtumiki wanu,+
Pakuti sindinaiwale malamulo anu.+
Nyimbo Yokwerera Kumzinda.
5 Tsoka kwa ine! Chifukwa ndakhala mlendo m’dziko la Meseke.+
Ndakhala muhema pakati pa mahema a Kedara.+
Nyimbo Yokwerera Kumzinda.
Nyimbo ya Davide Yokwerera Kumzinda.
3 Mzinda wa Yerusalemu unamangidwa+
Ngati chinthu chimodzi chogwirizana,+
Mafuko a Ya,+
Amapita kumeneko kukatamanda dzina la Yehova+
Mogwirizana ndi lamulo loperekedwa kwa Isiraeli.+
6 Pemphererani mtendere wa Yerusalemu, anthu inu.+
Amene amakukonda, mzinda iwe, sadzakhala ndi nkhawa iliyonse.+
7 M’malo ako otchingidwa ndi khoma lolimba mupitirizebe kukhala mtendere,+
Anthu okhala munsanja zako apitirizebe kukhala opanda nkhawa iliyonse.+
9 Chifukwa cha nyumba ya Yehova Mulungu wathu,+
Ndidzapitiriza kukupempherera kuti zinthu zikuyendere bwino.+
Nyimbo Yokwerera Kumzinda.
2 Taonani! Monga mmene maso a atumiki amayang’anira dzanja la mbuye wawo,+
Mmene maso a kapolo wamkazi amayang’anira dzanja la mbuye wake wamkazi,+
Momwemonso, maso athu adzayang’ana kwa Yehova Mulungu wathu,+
Kufikira atatikomera mtima.+
4 Moyo wathu wasautsika kwambiri chifukwa cha kunyoza kwa anthu amene akukhala mosatekeseka,+
Ndiponso chifukwa cha kunyoza kwa anthu odzikuza.+
Nyimbo ya Davide Yokwerera Kumzinda.
124 “Yehova akanapanda kukhala kumbali yathu,”+
Isiraeli anene kuti,+
2 “Yehova akanapanda kukhala kumbali yathu,+
Pamene anthu anatiukira,+
Pamene mkwiyo wawo unatiyakira.+
7 Moyo wathu uli ngati mbalame imene yathawa+
Pamsampha wa munthu wogwiritsa ntchito nyambo.+
Msamphawo wathyoka,+
Ndipo ife tapulumuka.+
Nyimbo Yokwerera Kumzinda.
2 Yehova wazungulira anthu ake+
Ngati mmene mapiri azungulirira Yerusalemu,+
Kuyambira tsopano mpaka kalekale.+
3 Ndodo yachifumu ya oipa sidzapitiriza kukhala+ padziko limene olungama analandira monga cholowa chawo,
Kuti olungamawo asatambasule dzanja lawo ndi kuchita choipa.+
5 Koma anthu obwerera kunjira zawo zokhotakhota,+
Yehova adzawapereka ku chilango pamodzi ndi ochita zopweteka anzawo.+
Ndipo mu Isiraeli mudzakhala mtendere.+
Nyimbo Yokwerera Kumzinda.
126 Pamene Yehova anasonkhanitsa ndi kubwezeretsa ogwidwa ukapolo a Ziyoni,+
Tinakhala ngati tikulota.+
2 Pa nthawiyo tinaseka kwambiri,+
Ndipo lilime lathu linatulutsa mawu okondwa.+
Pamenepo anthu a mitundu ina anayamba kuuzana kuti:+
“Yehova wachitira anthu amenewa zinthu zazikulu.”+
4 Sonkhanitsani ndi kubwezeretsa gulu lathu logwidwa ukapolo inu Yehova,+
Ngati mmene mumabwezeretsera madzi m’mitsinje ya ku Negebu.+
6 Amene akupita kumunda akulira,+
Atasenza thumba lodzaza mbewu,+
Adzabwerako akufuula mosangalala,+
Atasenza mtolo wake wa zokolola.+
Nyimbo ya Solomo Yokwerera Kumzinda.
127 Yehova akapanda kumanga nyumba,+
Omanga nyumbayo amagwira ntchito pachabe.+
Yehova akapanda kulondera mzinda,+
Alonda amakhala maso pachabe.+
2 Anthu inu mukudzuka m’mawa pachabe,+
Mukungovutika kugwira ntchito mpaka usiku,+
Mukudya chakudya chimene mwachipeza movutikira.+
Koma Mulungu amapereka tulo kwa wokondedwa wake.+
5 Wodala ndi mwamuna wamphamvu amene wadzaza+ kachikwama kake ka mivi ndi mivi imeneyo.
Abambo oterowo sadzachita manyazi,+
Pakuti anawo adzalankhula ndi adani pachipata.
Nyimbo Yokwerera Kumzinda.
2 Pakuti udzadya zipatso za ntchito ya manja ako.+
Udzakhala wodala ndipo zinthu zidzakuyendera bwino.+
3 Mkazi wako adzakhala ngati mtengo wa mpesa wobala zipatso+
Mkati mwa nyumba yako.
Ana ako adzakhala ngati mphukira za mitengo ya maolivi+ kuzungulira tebulo lako.
5 Yehova adzakudalitsa ali ku Ziyoni.+
Komanso usangalale ndi zinthu zabwino za mu Yerusalemu masiku onse a moyo wako,+
Mtendere ukhale pa Isiraeli.+
Nyimbo Yokwerera Kumzinda.
129 “Andisonyeza chidani mokwanira kuyambira ndili mnyamata,”+
Isiraeli anene kuti,+
2 “Andisonyeza chidani mokwanira kuyambira ndili mnyamata,+
Koma sanandigonjetse.+
6 Adzakhala ngati udzu wanthete womera padenga,+
Umene umauma asanauzule,+
7 Umene wokolola sanadzaze nawo manja ake,+
Ngakhalenso aliyense amene akunyamula mitolo ya zokolola sanadzaze nawo thumba lake la pachifuwa.
8 Anthu odutsa nawonso sananene kuti:
“Madalitso a Yehova akhale nanu anthu inu.+
Takudalitsani m’dzina la Yehova.”+
Nyimbo Yokwerera Kumzinda.
130 Inu Yehova, pa nthawi imene zinthu zinandivuta kwambiri ndinaitana pa inu.+
5 Ndayembekezera thandizo lanu, inu Yehova. Moyo wanga wayembekezera thandizo lanu.+
Ine ndayembekezera mawu anu.+
Kuposa alonda amene akuyembekezera kuti kuche,+
Ndithu kuposa alonda amene akuyembekezera kuti kuche.+
7 Isiraeli ayembekezere Yehova,+
Pakuti Yehova amasonyeza kukoma mtima kosatha.+
Iye ali ndi mphamvu zochuluka zowombolera anthu ake.+
8 Iye adzawombola Isiraeli ku zolakwa zake zonse.+
Nyimbo ya Davide Yokwerera Kumzinda.
131 Inu Yehova, mtima wanga sunadzikweze,+
Maso anga si onyada.+
Sindinafune zinthu zapamwamba kwambiri,+
Kapena zinthu zodabwitsa kwambiri.+
2 Ine ndadzitonthoza ndipo ndakhazika mtima wanga pansi.+
Ndakhala ngati mwana amene wangosiya kumene kuyamwa, amene ali m’manja mwa mayi ake.+
Ndakhala ngati mwana amene wangosiya kumene kuyamwa.+
Nyimbo Yokwerera Kumzinda.
132 Inu Yehova, kumbukirani Davide,+
Kumbukirani masautso ake onse.+
Sindigona pabedi langa.+
Ndipo sindilola maso anga owala kuwodzera,+
5 Kufikira Yehova nditamupezera nyumba,+
Kufikira nditapeza chihema chachikulu cha Wamphamvu wa Yakobo.”+
11 Yehova walumbira kwa Davide,+
Ndithudi sadzabweza mawu ake akuti:+
“Ndidzaika pampando wako wachifumu+
Chipatso cha mimba yako.+
12 Ana ako akadzasunga pangano langa+
Ndi zikumbutso zanga zimene ndidzawapatsa,+
Ngakhalenso ana awo+
Adzakhala pampando wako wachifumu kwamuyaya.”+
14 “Awa ndi malo anga okhalamo mpaka muyaya.+
Ndidzakhala mmenemu, pakuti ndimafunitsitsa kukhala m’malo amenewa.+
Nyimbo ya Davide Yokwerera Kumzinda.
2 Zili ngati mafuta abwino amene athiridwa pamutu,+
Amene akutsikira kundevu,
Ndevu za Aroni,+
Amenenso akuyenderera mpaka m’khosi la zovala zake.+
3 Zili ngati mame+ a ku Herimoni,+
Amene akutsikira pamapiri a ku Ziyoni.+
Pakuti Yehova analamula dalitso kukhala kumeneko,+
Walamulanso kuti kukhale moyo mpaka kalekale.+
Nyimbo Yokwerera Kumzinda.
Tamandani dzina la Yehova,+
Mutamandeni, inu atumiki a Yehova,+
2 Inu amene mukuimirira m’nyumba ya Yehova,+
M’mabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.+
3 Tamandani Ya, pakuti Yehova ndi wabwino.+
Muimbireni nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti kuchita zimenezi n’kosangalatsa.+
6 Chilichonse chimene Yehova anafuna kuchita anachita.+
Anachita zimenezi kumwamba, padziko lapansi, m’nyanja ndi m’madzi onse akuya.+
7 Amachititsa nthunzi kukwera kuchokera kumalekezero a dziko lapansi.+
Iye anapanganso zipata zotulukirapo mvula.+
Amachititsa mphepo kutuluka m’nkhokwe zake.+
8 Wochita zimenezi ndiye anapha ana oyamba kubadwa a ku Iguputo,+
Anapha ana a anthu ngakhalenso ana a nyama.+
9 Anasonyeza zizindikiro ndi kuchita zozizwitsa pakati pako Iguputo iwe,+
Anachita zimenezo kwa Farao ndi kwa atumiki ake onse.+
10 Amene anachita zimenezi ndi amene anakantha mitundu yambiri+
Ndi kupha mafumu amphamvu.+
11 Anaphanso Sihoni mfumu ya Aamori+
Ndi Ogi mfumu ya Basana,+
Ndipo anafafaniza maufumu onse a ku Kanani.+
12 Dziko lawo analipereka kukhala cholowa,+
Cholowa cha anthu ake Aisiraeli.+
15 Mafano a anthu a mitundu ina ndi opangidwa ndi siliva ndi golide,+
Ntchito ya manja a munthu wochokera kufumbi.+
16 Pakamwa ali napo koma salankhula.+
Maso ali nawo koma saona.+
17 Makutu ali nawo koma satha kumva.+
Komanso m’mphuno mwawo mulibe mpweya.+
136 Yamikani Yehova anthu inu, pakuti iye ndi wabwino:+
Kukoma mtima kwake kosatha kudzakhalapobe mpaka kalekale.+
2 Yamikani Mulungu wa milungu:+
Pakuti kukoma mtima kwake kosatha kudzakhalapobe mpaka kalekale.+
Pakuti kukoma mtima kwake kosatha kudzakhalapobe mpaka kalekale.+
4 Yamikani Wochita zodabwitsa ndiponso ntchito zazikulu:+
Pakuti kukoma mtima kwake kosatha kudzakhalapobe mpaka kalekale.+
5 Yamikani amene anapanga kumwamba mwanzeru:+
Pakuti kukoma mtima kwake kosatha kudzakhalapobe mpaka kalekale.+
6 Yamikani woyala dziko lapansi pamwamba pa madzi:+
Pakuti kukoma mtima kwake kosatha kudzakhalapobe mpaka kalekale.+
7 Yamikani wopanga zounikira zazikulu:+
Pakuti kukoma mtima kwake kosatha kudzakhalapobe mpaka kalekale.+
8 Amenenso anapanga dzuwa kuti lizilamulira masana:+
Pakuti kukoma mtima kwake kosatha kudzakhalapobe mpaka kalekale.+
9 Amene anapanga mwezi ndi nyenyezi kuti zizilamulira pamodzi usiku:+
Pakuti kukoma mtima kwake kosatha kudzakhalapobe mpaka kalekale.+
10 Yamikani amene anakantha Aiguputo mwa kupha ana awo oyamba kubadwa:+
Pakuti kukoma mtima kwake kosatha kudzakhalapobe mpaka kalekale.+
11 Yamikani amene anatulutsa Aisiraeli pakati pawo:+
Pakuti kukoma mtima kwake kosatha kudzakhalapobe mpaka kalekale.+
12 Anawatulutsa ndi dzanja lamphamvu ndi mkono wotambasula:+
Pakuti kukoma mtima kwake kosatha kudzakhalapobe mpaka kalekale.
13 Yamikani amene anagawa pakati Nyanja Yofiira:+
Pakuti kukoma mtima kwake kosatha kudzakhalapobe mpaka kalekale.+
14 Amenenso anachititsa Isiraeli kudutsa pakati pake:+
Pakuti kukoma mtima kwake kosatha kudzakhalapobe mpaka kalekale.+
15 Amenenso anakutumulira Farao ndi gulu lake lankhondo m’Nyanja Yofiira:+
Pakuti kukoma mtima kwake kosatha kudzakhalapobe mpaka kalekale.+
16 Yamikani amene anayendetsa anthu ake m’chipululu:+
Pakuti kukoma mtima kwake kosatha kudzakhalapobe mpaka kalekale.+
17 Yamikani amene anapha mafumu amphamvu:+
Pakuti kukoma mtima kwake kosatha kudzakhalapobe mpaka kalekale.+
18 Amenenso anapha mafumu olemekezeka:+
Pakuti kukoma mtima kwake kosatha kudzakhalapobe mpaka kalekale.+
19 Iye anapha Sihoni mfumu ya Aamori:+
Pakuti kukoma mtima kwake kosatha kudzakhalapobe mpaka kalekale.+
20 Anaphanso Ogi mfumu ya Basana:+
Pakuti kukoma mtima kwake kosatha kudzakhalapobe mpaka kalekale.+
21 Ndipo dziko lawo analipereka kwa anthu ake kukhala cholowa:+
Pakuti kukoma mtima kwake kosatha kudzakhalapobe mpaka kalekale.+
22 Cholowa cha Isiraeli mtumiki wake:+
Pakuti kukoma mtima kwake kosatha kudzakhalapobe mpaka kalekale.+
23 Iye amene anatikumbukira pamene adani anatinyazitsa:+
Pakuti kukoma mtima kwake kosatha kudzakhalapobe mpaka kalekale.+
24 Amene anatipulumutsa mobwerezabwereza kuchokera m’manja mwa adani athu:+
Pakuti kukoma mtima kwake kosatha kudzakhalapobe mpaka kalekale.+
25 Amenenso amapereka chakudya kwa zamoyo zonse:+
Pakuti kukoma mtima kwake kosatha kudzakhalapobe mpaka kalekale.+
26 Yamikani Mulungu wakumwamba:+
Pakuti kukoma mtima kwake kosatha kudzakhalapobe mpaka kalekale.+
3 Kumeneko, amene anatigwira ukapolo anatiuza kuti tiwaimbire nyimbo,+
Ndipo otinyozawo anatipempha kuti tiwasangalatse.+ Iwo anati:
“Tiimbireni imodzi mwa nyimbo za ku Ziyoni.”+
6 Lilime langa limamatire m’kamwa mwanga+
Ngati sindingakukumbukire,+
Ngati sindingakweze iwe Yerusalemu
Pamwamba pa chilichonse chimene chimandikondweretsa.+
7 Inu Yehova, kumbukirani+ zimene ana a Edomu+ ananena pa tsiku limene Yerusalemu anawonongedwa,+
Iwo anati: “Fafanizani mzindawo! Ufafanizeni mpaka pamaziko ake!”+
8 Iwe mwana wamkazi wa Babulo, amene udzafunkhidwa,+
Wodala ndi amene adzakubwezera+
Zimene iwe watichitira.+
9 Wodala ndi iye amene adzagwira ana ako ndi kuwaphwanya zidutswazidutswa+
Mwa kuwawombetsa pathanthwe.
Salimo la Davide.
138 Ndidzakutamandani ndi mtima wanga wonse.+
Ndidzakuimbirani nyimbo zokutamandani pamaso pa milungu ina.+
2 Ndidzawerama nditayang’ana kukachisi wanu woyera,+
Ndipo ndidzatamanda dzina lanu+
Chifukwa cha kukoma mtima kwanu kosatha+ ndi choonadi chanu.+
Pakuti malonjezo+ amene munawachita m’dzina lanu ndi aakulu ndithu. Koma kukwaniritsidwa kwa malonjezowo n’kwakukulu koposa.+
4 Mafumu onse a padziko lapansi adzakutamandani, inu Yehova,+
Pakuti adzakhala atamva mawu a pakamwa panu.
7 Ndikakhala pa masautso, inu mudzandisunga wamoyo.+
Mudzatambasula dzanja lanu chifukwa cha mkwiyo wa adani anga,+
Ndipo dzanja lanu lamanja lidzandipulumutsa.+
8 Yehova adzakwaniritsa zolinga zimene ali nazo pa ine.+
Inu Yehova, kukoma mtima kwanu kosatha kudzakhalapobe mpaka kalekale.+
Musasiye ntchito ya manja anu.+
Kwa wotsogolera nyimbo. Nyimbo ndi Salimo la Davide.
139 Inu Yehova, mwandifufuza ndipo mukundidziwa.+
3 Mumandidziwa bwino pamene ndikuyenda komanso pamene ndikugona,+
Ndipo njira zanga zonse mukuzidziwa bwino.+
5 Mwandizungulira,
Ndipo mwaika dzanja lanu pa ine.
6 Kwa ine ndi zovuta kwambiri kuti ndidziwe zinthu zonsezi.+
Ndi zapamwamba kwambiri moti sindingathe kuzifikira.+
8 Ngati ndingakwere kumwamba, inu mudzakhala komweko.+
Ndipo ngati ndingayale bedi langa ku Manda, taonani! inunso mudzakhala komweko.+
9 Ngati ndingakwere pamapiko+ a m’bandakucha,
Kuti ndikakhale m’nyanja ya kutali kwambiri,+
10 Kumenekonso dzanja lanu lidzanditsogolera,+
Dzanja lanu lamanja lidzandigwira.+
11 Ngati ndinganene kuti: “Ndithudi mdima undipeze mofulumira!”+
Pamenepo mdima udzasanduka kuwala pa ine.+
12 Ndipo mdimawo sudzakhala mdima wandiweyani kwa inu,+
Koma usiku udzakuwalirani ngati masana.+
Mdima udzangokhala ngati kuwala.+
14 Ndidzakutamandani chifukwa munandipanga modabwitsa ndipo zimenezi zimandichititsa mantha.+
Ntchito zanu ndi zodabwitsa,+
Ndipo ine ndimadziwa bwino zimenezi.+
15 Mafupa anga sanali obisika kwa inu+
Pamene munali kundipanga m’malo obisika,+
Pamene munali kundiwomba ngati nsalu m’malo apansi kwambiri+ padziko lapansi.
16 Maso anu anandiona pamene ndinali mluza,+
Ndipo ziwalo zanga zonse zinalembedwa m’buku lanu.
M’bukumo munalembamo za masiku amene zinapangidwa+
Koma panalibe ngakhale chiwalo chimodzi chimene chinali chitapangidwa.
18 Nditati ndiyese kuwawerenga, angakhale ochuluka kwambiri kuposa mchenga.+
Podzuka ndingakhale ndikuwawerengabe.+
19 Inu Mulungu, zikanakhala bwino mukanapha woipa.+
Pamenepo anthu amene ali ndi mlandu wa magazi+ akanandichokera,
21 Inu Yehova, pajatu ine ndimadana ndi anthu amene amadana nanu kwambiri,+
Ndipo anthu okupandukirani ndimanyansidwa nawo.+
23 Ndifufuzeni, inu Mulungu, ndi kudziwa mtima wanga.+
Ndisanthuleni ndi kudziwa malingaliro anga amene akundisowetsa mtendere,+
24 Ndipo muone ngati mwa ine muli chilichonse chimene chikundichititsa kuyenda m’njira yoipa,+
Ndipo munditsogolere m’njira+ yamuyaya.
Kwa wotsogolera nyimbo. Nyimbo ya Davide.
140 Inu Yehova, ndilanditseni kwa anthu oipa.+
Nditetezeni kwa munthu wochita zachiwawa,+
2 Anthu amene amakonza chiwembu mumtima mwawo,+
Amene amandiukira tsiku lonse ngati mmene zimakhalira pankhondo.+
4 Inu Yehova, ndithandizeni kuti manja a munthu woipa asandikhudze.+
Nditetezeni kwa munthu wochita zachiwawa.+
Nditetezeni kwa anthu amene andikonzera chiwembu kuti andikankhe ndi kundigwetsa.+
5 Anthu odzikweza anditchera msampha.+
Iwo aika zingwe ponseponse ngati ukonde m’mphepete mwa njira,+
Ndipo anditchera makhwekhwe.+ [Seʹlah.]
6 Ndauza Yehova kuti: “Inu ndinu Mulungu wanga.+
Tcherani khutu, inu Yehova, ku mawu anga ochonderera.”+
7 Inu Yehova Ambuye Wamkulu Koposa,+ mpulumutsi wanga wamphamvu,+
Mwatchinga ndi kuteteza mutu wanga pa tsiku lankhondo.+
8 Inu Yehova, munthu woipa musam’patse zimene mtima wake umafuna.+
Musalole kuti chiwembu chawo chitheke chifukwa angadzikweze.+ [Seʹlah.]
10 Muwakhuthulire makala oyaka moto pamutu pawo.+
Muwachititse kugwera m’moto+ ndi m’madzi akuya kuti asanyamukenso.+
11 Munthu wolankhula zazikulu* asakhazikike padziko lapansi.+
Zoipa zisakesake munthu wochita zachiwawa ndipo zimukanthe mobwerezabwereza.+
12 Ndikudziwa bwino kwambiri kuti Yehova adzazengera+
Mlandu anthu osautsika. Iye adzachitira chilungamo anthu osauka.+
Nyimbo ya Davide.
141 Inu Yehova, ine ndakuitanani.+
Bwerani kwa ine mofulumira.+
Tcherani khutu pamene ndikukuitanani.+
2 Pemphero langa likhale lokonzedwa ngati zofukiza+ pamaso panu,+
Mapembedzero anga akhale ngati nsembe yambewu yamadzulo.+
4 Musachititse mtima wanga kukonda choipa chilichonse,+
Kuti ndisamachite zinthu zoipa zonditchukitsa,+
Pamodzi ndi amene amachita zinthu zopweteka anzawo,+
Kuti ndisadye chakudya chawo chapamwamba.+
5 Wolungama akandimenya ndiye kuti wandisonyeza kukoma mtima kosatha,+
Ndipo akandidzudzula ndiye kuti wandidzoza mafuta pamutu panga,+
Mafuta amene mutu wanga sungawakane.+
Pakuti ndidzapemphererabe anthu olungama ngakhale pamene masoka awagwera.+
6 Oweruza awo awagwetsera pansi m’mphepete mwa thanthwe,+
Koma anthu awo amva zonena zanga ndipo aona kuti ndi zabwino.+
7 Mafupa athu amwazika pakamwa pa Manda,
Mofanana ndi zidutswa zimene zimamwazika pansi pamene munthu akuwaza ndi kung’amba mtengo.+
8 Koma ine maso anga ali pa inu+ Yehova Ambuye Wamkulu Koposa.+
Ndathawira kwa inu.+
Musalole kuti moyo wanga uwonongeke.+
9 Nditetezeni kuti ndisagwidwe pamsampha umene anditchera,+
Kuti ndisakodwe ndi makhwekhwe a anthu ochita zopweteka anzawo.+
Masikili.* Salimo ndiponso pemphero la Davide, pamene anali kukhala kuphanga.+
2 Ndinapitirizabe kumukhuthulira nkhawa zanga.+
Ndinapitirizabe kumuuza masautso anga.+
3 Ndinachita zimenezi pamene mtima wanga+ unalefuka.
Pamenepo, munadziwa njira yanga.+
Adani anga anditchera msampha+
M’njira imene ndikuyenda.+
4 Yang’anani kudzanja lamanja ndipo muone
Kuti palibe aliyense amene akufuna kundithandiza.+
Ndilibenso malo othawirako,+
Ndipo palibe amene akufunsa za moyo wanga.+
6 Mvetserani kulira kwanga kochonderera,+
Pakuti ndasautsika koopsa.+
Ndipulumutseni kwa anthu amene akundizunza,+
Pakuti iwo ndi amphamvu kuposa ine.+
7 Nditulutseni mundende ya mdima+
Kuti nditamande dzina lanu.+
Chititsani kuti anthu olungama asonkhane ndi kundizungulira,+
Chifukwa mumandichitira zabwino.+
Nyimbo ya Davide.
143 Inu Yehova, imvani pemphero langa.+
Tcherani khutu pamene ndikuchonderera.+
Ndiyankheni mogwirizana ndi kukhulupirika kwanu ndi chilungamo chanu.+
2 Musandiimbe mlandu ine mtumiki wanu,+
Pakuti palibe aliyense wamoyo amene angakhale wolungama pamaso panu.+
3 Mdani akufunafuna moyo wanga,+
Iye waupondaponda pafumbi.+
Wandichititsa kukhala m’malo a mdima ngati anthu amene anafa kalekale.+
Ndasinkhasinkha zochita zanu zonse,+
Ndipo ndakhala ndikuganizira ntchito ya manja anu ndi mtima wonse.+
6 Ine ndikupemphera nditakweza manja anga kwa inu.+
Moyo wanga uli ngati dziko louma limene likulakalaka kuti muthetse ludzu lake.+ [Seʹlah.]
7 Fulumirani, ndiyankheni inu Yehova.+
Mphamvu zanga zatha.+
Musandibisire nkhope yanu,+
Chifukwa mukatero ndikhala ngati anthu amene akutsikira kudzenje la manda.+
8 M’mawa ndichititseni kumva za kukoma mtima kwanu kosatha,+
Pakuti ndimadalira inu.+
Ndidziwitseni njira imene ndiyenera kuyendamo,+
Pakuti ndapereka moyo wanga kwa inu.+
10 Ndiphunzitseni kuchita chifuniro chanu,+
Pakuti inu ndinu Mulungu wanga.+
Mzimu wanu ndi wabwino.+
Unditsogolere m’dziko la olungama.+
11 Inu Yehova, ndisungenibe wamoyo+ chifukwa cha dzina lanu.+
Chotsani moyo wanga m’masautso+ monga mwa chilungamo chanu.+
12 Adani anga muwakhalitse chete monga mwa kukoma mtima kwanu kosatha.+
Ndipo muwononge onse ondichitira zoipa,+
Pakuti ine ndine mtumiki wanu.+
Salimo la Davide.
144 Atamandike Yehova Thanthwe langa,+
Amene akuphunzitsa manja anga kumenya nkhondo,+
Amenenso akuphunzitsa zala zanga kumenyana ndi adani anga.
2 Iye amandisonyeza kukoma mtima kwake kosatha ndipo ndiye malo anga achitetezo,+
Malo anga okwezeka ndi Wopereka chipulumutso,+
Chishango+ changa ndi malo anga othawirako.+
Iye amandigonjetsera mitundu ya anthu.+
3 Inu Yehova, munthu ndani kuti mumuganizire?+
Kodi mwana wa munthu wochokera kufumbi+ ndani kuti mumuwerengere?
7 Tambasulani manja anu kuchokera kumwamba.+
Ndimasuleni ndi kundilanditsa m’madzi ambiri.+
Mundilanditse m’manja mwa anthu achilendo,+
8 Anthu amene amalankhula zinthu zonama,+
Amenenso dzanja lawo lamanja limachita zachinyengo.+
9 Inu Mulungu, ine ndidzakuimbirani nyimbo yatsopano.+
Ndidzaimba nyimbo yokutamandani ndi choimbira cha zingwe 10.+
10 Ndidzaimbira inu amene mumapulumutsa mafumu,+
Amene mumalanditsa ine Davide mtumiki wanu ku lupanga lovulaza.+
11 Ndimasuleni ndi kundilanditsa m’manja mwa anthu achilendo,+
Anthu amene amalankhula zinthu zonama,+
Amenenso dzanja lawo lamanja limachita zachinyengo.+
12 Anthuwo amanena kuti: “Ana athu aamuna, mu unyamata wawo, ali ngati mitengo imene yangokhwima kumene,+
Ndipo ana athu aakazi ali ngati mizati yapakona yosemedwa mwaluso ya m’nyumba ya mfumu.
13 Nkhokwe zathu ndi zodzaza ndi zakudya zosiyanasiyana.+
Nkhosa zathu zikuswana kukhala masauzandemasauzande. Nkhosa imodzi ikukhala masauzande 10 m’misewu.
14 Ng’ombe zathu zili ndi bere, sizikuvulala kapena kubereka ana akufa,+
Ndipo palibe munthu amene akulira m’mabwalo athu.+
15 Odala ndi anthu amene zimenezi zikuwachitikira.”
Ayi, koma odala ndi anthu amene Mulungu wawo ndi Yehova.+
Nyimbo yotamanda Mulungu. Salimo la Davide.
א [ʼAʹleph]
145 Ndidzakukwezani, inu Mfumu ndi Mulungu wanga,+
Ndipo ndidzatamanda dzina lanu mpaka kalekale, ndithu mpaka muyaya.+
ב [Behth]
ג [Giʹmel]
ד [Daʹleth]
ה [Heʼ]
ו [Waw]
6 Anthu adzanena za zochita zanu zamphamvu ndi zochititsa mantha.+
Ndipo ine ndidzalengeza za ukulu wanu.+
ז [Zaʹyin]
7 Iwo adzalankhula mosefukira za kuchuluka kwa ubwino wanu,+
Ndipo adzafuula mokondwera chifukwa cha chilungamo chanu.+
ח [Chehth]
8 Yehova ndi wachisomo ndi wachifundo,+
Wosakwiya msanga ndi wosonyeza kukoma mtima kosatha komanso kwakukulu.+
ט [Tehth]
י [Yohdh]
כ [Kaph]
מ [Mem]
13 Ufumu wanu ndi ufumu umene udzakhalapobe mpaka kalekale.+
Ulamuliro wanu udzakhalapobe ku mibadwo yonse.+
ס [Saʹmekh]
14 Yehova amachirikiza amene ali pafupi kugwa,+
Ndipo amaweramutsa onse amene awerama chifukwa cha masautso.+
ע [ʽAʹyin]
15 Zolengedwa zonse zimayang’ana kwa inu mwachiyembekezo,+
Ndipo mumazipatsa chakudya pa nyengo yake.+
פ [Peʼ]
צ [Tsa·dhehʹ]
ק [Qohph]
18 Yehova ali pafupi ndi onse oitanira pa iye.+
Iye ali pafupi ndi onse amene amamuitana m’choonadi,+
ר [Rehsh]
19 Ndipo anthu amene amamuopa adzawachitira zokhumba zawo,+
Adzamva kufuula kwawo kopempha thandizo ndipo adzawapulumutsa.+
ש [Shin]
ת [Taw]
21 Pakamwa panga padzalankhula zotamanda Yehova,+
Ndipo anthu onse atamande dzina lake loyera mpaka kalekale, ndithu mpaka muyaya.+
2 Ndidzatamanda Yehova pamene ndili moyo.+
Ndidzaimbira Mulungu wanga nyimbo zomutamanda kwa moyo wanga wonse.+
3 Musamakhulupirire anthu olemekezeka,+
Kapena mwana wa munthu wina aliyense wochokera kufumbi amene alibe chipulumutso.+
4 Mzimu* wake umachoka,+ ndipo iye amabwerera kunthaka.+
Pa tsiku limenelo zonse zimene anali kuganiza zimatheratu.+
5 Wodala ndi munthu amene thandizo lake limachokera kwa Mulungu wa Yakobo,+
Amene chiyembekezo chake chili mwa Yehova Mulungu wake,+
6 Wopanga kumwamba ndi dziko lapansi,+
Nyanja ndi zonse zili mmenemo.+
Wosunga choonadi mpaka kalekale.+
7 Iye ndi Woperekera chiweruzo anthu ochitiridwa chinyengo,+
Wopereka chakudya kwa anthu anjala.+
Yehova amamasula anthu omangidwa.+
8 Yehova amatsegula maso a anthu akhungu.+
Yehova amaweramutsa anthu owerama chifukwa cha masautso.+
Yehova amakonda anthu olungama.+
9 Yehova amayang’anira alendo okhala m’dziko la eni.+
Amathandiza mwana wamasiye* ndi mkazi wamasiye.+
Koma njira+ ya anthu oipa amaichititsa kukhala yovuta kuyendamo.+
10 Yehova adzakhala mfumu mpaka kalekale,+
Mulungu wako, iwe Ziyoni, adzakhala mfumu ku mibadwomibadwo.+
Tamandani Ya, anthu inu!+
Pakuti kuimbira Mulungu wathu nyimbo zomutamanda n’kwabwino,+
Ndipo n’kosangalatsa. Kumutamanda n’koyenera.+
2 Yehova akumanga Yerusalemu.+
Anthu okhala mu Isiraeli amene anabalalika akuwasonkhanitsanso pamodzi.+
7 Imbirani Yehova molandizana mawu nyimbo zomuyamikira anthu inu.+
Imbirani Mulungu wathu nyimbo zomutamanda ndi zeze.+
8 Muimbireni Iye amene amaphimba mapiri ndi mitambo,+
Amene amakonza mvula kuti igwe padziko lapansi,+
Amenenso amameretsa udzu wobiriwira m’mapiri.+
14 Iye akukhazikitsa mtendere m’dziko lako.+
Ndipo akupitirizabe kukukhutiritsa ndi tirigu wabwino koposa.+
16 Iye amapereka chipale chofewa kuti chikhale ngati ubweya wa nkhosa.+
Amamwaza mame oundana ngati kuti ndi phulusa.+
18 Amatumiza mawu ake+ ndi kusungunula madzi oundanawo.
Amachititsa mphepo yake kuwomba,+
Ndipo madzi amayenda.
20 Sanachite zimenezi ndi mtundu wina uliwonse,+
Ndipo mitundu inayo sikudziwa zigamulo zake.+
Tamandani Ya, anthu inu!+
6 Amazichititsa kukhalapobe kwamuyaya, ngakhalenso mpaka kalekale.+
Iye wazikhazikitsira lamulo, ndipo silidzatha.+
7 Tamandani Yehova, inu okhala padziko lapansi,+
Inu zilombo za m’nyanja ndi inu nonse madzi akuya,+
8 Inu moto ndi matalala, chipale chofewa ndi utsi wakuda bii,+
Iwe mphepo yamkuntho yokwaniritsa mawu ake.+
9 Mutamandeni inu mapiri ndi inu nonse zitunda,+
Inu mitengo ya zipatso ndi inu nonse mitengo ya mkungudza.+
10 Inu nyama zakutchire ndi inu nonse nyama zoweta,+
Inu zinthu zokwawa ndi mbalame zamapiko.+
11 Mutamandeni inu mafumu a padziko lapansi+ ndi inu nonse mitundu ya anthu,
Inunso akalonga+ ndi inu nonse oweruza a padziko lapansi,+
13 Onse, anthu ndi nyama, atamande dzina la Yehova,+
Pakuti dzina lake lokhalo lili pamwamba posafikirika.+
Ulemerero wake uli pamwamba kuposa dziko lapansi ndi kumwamba.+
14 Iye adzakweza nyanga* ya anthu ake.+
Adzachititsa kuti anthu ake onse okhulupirika atamandike,+
Amene ndi ana a Isiraeli, anthu amene ali pafupi ndi iye.+
Tamandani Ya, anthu inu!+
Imbirani Yehova nyimbo yatsopano,+
Muimbireni nyimbo zomutamanda mu mpingo wa anthu ake okhulupirika.+
6 Pakamwa pawo patuluke nyimbo zotamanda Mulungu,+
Ndipo lupanga lakuthwa konsekonse likhale m’manja mwawo,+
7 Kuti abwezere anthu a mitundu ina,+
Ndi kudzudzula mitundu ya anthu,+
8 Ndiponso kuti amange mafumu awo maunyolo,+
Ndi kumanga anthu awo olemekezeka m’matangadza achitsulo.
9 Kuti awaweruze motsatira chigamulo cholembedwa.+
Ulemerero umenewu ndi wa anthu onse okhulupirika a Mulungu.+
Tamandani Ya, anthu inu!+
2 Mutamandeni chifukwa cha ntchito zake zamphamvu.+
Mutamandeni mogwirizana ndi ukulu wake wosaneneka.+
3 Mutamandeni mwa kuliza lipenga la nyanga ya nkhosa.+
Mutamandeni ndi choimbira cha zingwe ndi zeze.+
Mawu akuti “Masalimo” amatanthauza “Nyimbo Zotamanda.”
“Mankhusu” ndi makoko amene amachotsa ku mbewu ngati mpunga popuntha, ndipo amatha kuwauluza ndi mphepo.
“Seʹlah” ndi mawu achiheberi amene anali kuwagwiritsa ntchito polemba nyimbo kapena ndakatulo. Tanthauzo lake lenileni silikudziwika.
“Nehiloti” ndi mawu achiheberi ndipo tanthauzo lake lenileni silikudziwika. N’kutheka kuti ndi dzina la chipangizo choimbira mochita kuuziramo mpweya kapena dzina la nyimbo yoimba motsagana ndi zipangizo zoimbira.
Onani Matanthauzo a Mawu Ena.
N’kutheka kuti mawu amene tawamasulira kuti “chapansipansi” akutanthauza kuti anali kuimba nyimbo imeneyi motsitsa kapena mwabesi.
Onani Zakumapeto 5.
Onani Matanthauzo a Mawu Ena.
Tanthauzo la mawu achiheberi amene tawamasulira kuti “nyimbo yoimba polira” silikudziwika, koma mwina mawu amenewo angatanthauze nyimbo yoimba mokhudzidwa mtima kwambiri. Kaimbidwe kake kangasonyeze kuti moyo wa munthuyo uli pangozi, akufuula kupempha thandizo, kapena akukondwera ndipo akutamanda winawake.
“Gititi” ndi mawu achiheberi amene anali kuwagwiritsa ntchito polemba nyimbo, koma tanthauzo lake lenileni silikudziwika.
Kapena kuti “angelo.”
“Mutilabeni” ndi mawu achiheberi amene tanthauzo lake lenileni silikudziwika. Koma omasulira ena anamasulira mawuwa kuti, “yonena za imfa ya mwana wamwamuna.”
“Higayoni” ndi mawu achiheberi amene anali kuwagwiritsa ntchito polemba nyimbo, koma tanthauzo lake lenileni silikudziwika.
Mawu ake enieni, “mwana wamwamuna wopanda bambo.”
Onani mawu a m’munsi pa Sl 6:Kamutu.
Mawu ake enieni, “m’badwo.”
“Mikitamu” ndi mawu amene anali kuwagwiritsa ntchito polemba nyimbo, koma tanthauzo lake lenileni silikudziwika.
Mawu ake enieni, “adzikuta ndi mafuta awo omwe.”
Onani Matanthauzo a Mawu Ena.
Onani mawu a m’munsi pa 1Sa 2:1.
Kapena kuti “mapiko a mphepo.”
Mawu ake enieni, “amamangirira zolimba mphamvu m’chiuno mwanga.”
Kapena kuti “Mudzandipatsa kumbuyo kwa khosi la adani anga.”
Ena amati “n’zonzuna.”
Onani Matanthauzo a Mawu Ena.
Ena amati “mahosi” kapena “akavalo.”
Mawu ake enieni, “ana a amphamvu.”
“Madzi” amenewa akutanthauza “mvula yamkuntho.”
Kapena kuti “pamwamba pa nyanja yaikulu ya kumwamba.”
Mawu ake enieni, “chikumbutso chake choyera.”
Ena amati “saka.”
Onani Zakumapeto 4.
“Masikili” ndi mawu achiheberi amene tanthauzo lake silikudziwika. N’kutheka kuti amatanthauza “ndakatulo imene munthu amanena posinkhasinkha.”
Onani mawu a m’munsi pa 2Sa 13:29.
Zikuoneka kuti ili ndi dzina laudindo la Mfumu Akisi. Yerekezerani ndi mawu a m’munsi pa Ge 20:2.
“Yedutuni” ndi mawu achiheberi amene tanthauzo lake silikudziwika.
Mawu achiheberi amene tawamasulira kuti “njenjete” amatanthauza mtundu wa kachilombo kotchedwa kadziwotche kooneka ngati gulugufe, kamene kamadya zovala ngati mmene njenjete imachitira.
Mawu ake enieni, “chinthu chopanda pake.”
Kapena kuti “Zikhale momwemo! Zikhale momwemo!”
Onani mawu a m’munsi pa Sl 32:Kamutu.
Onani mawu a m’munsi pa Sl 32:Kamutu.
N’kutheka kuti “Maluwa” chinali chipangizo choimbira cha zingwe 6.
Onani mawu a m’munsi pa Sl 32:Kamutu.
Onani Matanthauzo a Mawu Ena.
N’kutheka kuti mawu akuti “zishango” akunena olamulira kapena oteteza anthu.
Onani Matanthauzo a Mawu Ena.
Onani Matanthauzo a Mawu Ena.
Onani mawu a m’munsi pa Miy 1:2.
Mawu ake enieni, “mafupa.”
Kapena kuti “mzimu.”
Onani mawu a m’munsi pa Sl 32:Kamutu.
“Mahalati” ndi mawu achiheberi. N’kutheka kuti ndi mawu okhudzana ndi nyimbo, mwina okhudzana ndi luso la kaimbidwe.
Onani mawu a m’munsi pa Sl 32:Kamutu.
Onani mawu a m’munsi pa Sl 32:Kamutu.
Onani mawu a m’munsi pa Sl 32:Kamutu.
Onani mawu a m’munsi pa Sl 16:Kamutu.
Onani mawu a m’munsi pa Sl 16:Kamutu.
Onani mawu a m’munsi pa Sl 16:Kamutu.
Onani mawu a m’munsi pa Sl 16:Kamutu.
Onani mawu a m’munsi pa Sl 16:Kamutu.
Onani mawu a m’munsi pa Sl 39:Kamutu.
Pa nthawi ya Mfumu Davide, Aisiraeli anali ndi maulonda a usiku atatu. Ulonda woyamba unkayamba 6 koloko madzulo mpaka 10 koloko usiku. Ulonda wachiwiri unkayamba 10 koloko usiku mpaka 2 koloko usiku, ndipo ulonda wachitatu unkayamba 2 koloko usiku mpaka 6 koloko m’mawa.
Mawu ake enieni, “mudzaphimba.”
Onani mawu a m’munsi pa Eks 15:2.
Mawu ake enieni, “ana aamuna opanda bambo.”
Mawu ake enieni, “Ya.” Onani mawu a m’munsi pa Eks 15:2.
Tanthauzo la mawu achiheberi amene tawamasulira kuti “zinthu zopangidwa ndi mkuwa wosakaniza ndi zitsulo zina” silidziwika. Ena amati tanthauzo lake ndi “akazembe.”
Onani mawu a m’munsi pa Sl 45:Kamutu.
Zikuoneka kuti “dzenje” limeneli ndi manda.
Mawu ake enieni, “chiuno.”
Umenewu ndi mtsinje wa Firate.
Kapena kuti “adzadzidalitsa okha,” kusonyeza kuti akufunika kuchitapo kanthu kuti alandire madalitso amenewo.
Kapena kuti “Zikhale momwemo! Zikhale momwemo!”
Onani mawu a m’munsi pa Sl 32:Kamutu.
Kapena kuti “ng’ona.”
M’Malemba achiheberi mulibe mawu akuti “Mulungu akuti,” koma aikidwapo pofuna kusonyeza amene akulankhula m’mavesi 2 ndi 3.
Onani mawu a m’munsi pa 1Sa 2:1.
Onani mawu a m’munsi pa vesi 2.
Onani mawu a m’munsi pa Sl 32:Kamutu.
Mawu ake enieni, “kuphimba.”
Mawu ake enieni, “kuphimba.”
Onani mawu a m’munsi pa Sl 45:Kamutu.
Onani Sl 60:Kamutu.
Umenewu ndi mtsinje wa Firate.
Onani mawu a m’munsi pa Sl 8:Kamutu.
Mawu ake enieni, “ana aamuna opanda bambo.”
Onani mawu a m’munsi pa Sl 8:Kamutu.
Mbalame imeneyi ena amati “kaluweluwe” kapena “kamembe.”
Dzina lakuti “baka” ndi lochokera ku Chiheberi. Chitsamba chimenechi sichikudziwika kuti chinali chotani.
Zikuoneka kuti dzina lakuti “Rahabi” likuimira dziko la Iguputo.
Onani mawu a m’munsi pa Sl 53:Kamutu.
Onani mawu a m’munsi pa Sl 32:Kamutu.
Onani mawu a m’munsi pa Sl 32:Kamutu.
Zikuoneka kuti dzina lakuti “Rahabi” likuimira dziko la Iguputo kapena Farao.
Onani mawu a m’munsi pa 1Sa 2:1.
Kapena kuti “Zikhale momwemo! Zikhale momwemo!”
Kapena kuti “musanamve zowawa ngati za pobereka pokhazikitsa dziko lapansi.”
Zikuoneka kuti usiku anali kuugawa zigawo zitatu za ulonda, kuyambira pamene dzuwa lalowa mpaka kutuluka. Ulonda uliwonse unali pafupifupi maola anayi malinga ndi nyengo ya pachaka.
Kapena kuti “machimo amene tinachita mosadziwa.”
Onani mawu a m’munsi pa 1Sa 2:1.
Mwina nyama imeneyi inali yooneka ngati njati.
Mawu ake enieni, “ana aamuna opanda bambo.”
Kapena kuti “imvani kupweteka kwambiri.”
Mawu ake enieni, “chikumbutso chake choyera.”
“Mphalasa” ndi lipenga lopangidwa ndi nyanga ya nkhosa.
Kapena kuti “patsindwi.”
Mawu ake enieni, “chikumbutso chanu.”
Mawu ake enieni, “anthu amene adzalengedwe.”
Kapena kuti “ng’ona.”
Kapena kuti “Aleluya.”
Kapena kuti “Zikhale momwemo!”
Mawu ake enieni, “ana aamuna opanda bambo.”
Onani mawu a m’munsi pa Eks 22:25.
Onani mawu a m’munsi pa 1Sa 2:1.
Kapena kuti “phindu lopezeka mwachinyengo pamalonda.”
Mawu ake enieni, “ndafewetsa nkhope yanu.”
Mawu ake enieni, “moyo wanga uli m’dzanja langa.”
Zimenezi ndi zonyansa zotsalira poyenga zitsulo.
Zikuoneka kuti apa akunena za nkhanza zimene mitundu ina yodana nawo inawachitira.
Kapena “Chihema.”
Onani mawu a m’munsi pa 1Sa 2:1.
Mawu ake enieni, “chisoti chachifumu.”
Mawu ake enieni, “chikumbutso chanu.”
Kapena kuti “woneneza.” Mawu ake enieni ndi “munthu wa lilime.”
Onani mawu a m’munsi pa Sl 32:Kamutu.
Onani Zakumapeto 4.
Mawu ake enieni, “mwana wamwamuna wopanda bambo.”
Onani mawu a m’munsi pa 1Sa 2:1.